< Provérbios 23 >

1 Quando te assentares a comer com um governador, attenta bem para o que se te poz diante,
Ngati ukhala pansi kuti udye pamodzi ndi wolamulira, uyangʼane bwino zimene zili pamaso pako,
2 E põe uma faca á tua garganta, se és homem de grande appetite.
ngati ndiwe munthu wadyera udziletse kuti usaonetse dyera lakolo.
3 Não cubices os seus manjares gostosos, porque são pão de mentiras.
Usasirire zakudya zake, pakuti zimenezo ndi zakudya zachinyengo.
4 Não te cances para enriqueceres; dá de mão á tua prudencia.
Usadzitopetse wekha ndi kufuna chuma, ukhale ndi nzeru ya kudziretsa.
5 Porventura fitarás os teus olhos n'aquillo que não é nada? porque certamente se fará azas e voará ao céu como a aguia
Ukangoti wachipeza chumacho uwona posachedwa kuti palibepo. Chumacho chimachita ngati chamera mapiko mwadzidzidzi ndi kuwuluka kunka kumwamba ngati chiwombankhanga.
6 Não comas o pão d'aquelle que tem o olho maligno, nem cubices os seus manjares gostosos.
Usadye chakudya cha munthu waumbombo, usalakalake zakudya zake zokoma;
7 Porque, como imaginou na sua alma, te dirá: Come e bebe; porém o seu coração não estará comtigo.
paja iye ndi munthu amene nthawi zonse amaganizira za mtengo wake ngakhale amati kwa iwe, “Idya ndi kumwa,” koma sakondweretsedwa nawe.
8 Vomitarias o bocado que comeste, e perderias as tuas suaves palavras.
Udzasanza zimene wadyazo ndipo mawu ako woyamikira adzapita pachabe.
9 Não falles aos ouvidos do tolo, porque desprezará a sabedoria das tuas palavras.
Usayankhule munthu wopusa akumva, pakuti adzanyoza mawu ako anzeru.
10 Não removas os limites antigos, nem entres nas herdades dos orphãos,
Usasunthe mwala wa mʼmalire akalekale kapena kulowerera mʼminda ya ana amasiye,
11 Porque o seu redemptor é o Forte, que pleiteará a sua causa contra ti.
paja Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu; iye adzawateteza pa milandu yawo kutsutsana nawe.
12 Applica á disciplina o teu coração, e os teus ouvidos ás palavras do conhecimento.
Mtima wako uzikhala pa malangizo ndipo makutu ako azimvetsera mawu a chidziwitso.
13 Não retires a disciplina da creança, quando a fustigares com a vara; nem por isso morrerá.
Usaleke kumulangiza mwana; ngati umulanga ndi chikwapu sadzafa.
14 Tu a fustigarás com a vara, e livrarás a sua alma do inferno. (Sheol h7585)
Ukamukwapula ndi tsatsa udzapulumutsa moyo wake. (Sheol h7585)
15 Filho meu, se o teu coração fôr sabio, alegrar-se-ha o meu coração, sim, o meu proprio,
Mwana wanga, ngati mtima wako ukhala wanzeru, inenso mtima wanga udzakondwera.
16 E exultarão os meus rins, quando os teus labios fallarem coisas rectas.
Mtima wanga udzakondwera pamene ndidzakumva ukuyankhula zolungama.
17 Não inveje aos peccadores o teu coração; antes sê no temor do Senhor todo o dia
Mtima wako usachite nsanje ndi anthu ochimwa, koma uziopa Yehova tsiku ndi tsiku.
18 Porque devéras ha um bom fim: não será cortada a tua expectação.
Ndithu za mʼtsogolo zilipo ndipo chiyembekezo chakocho sichidzalephereka.
19 Ouve tu, filho meu, e sê sabio, e dirige no caminho o teu coração.
Tamvera mwana wanga, ndipo ukhale wanzeru, mtima wako uwuyendetse mʼnjira yabwino.
20 Não estejas entre os beberrões de vinho, nem entre os comilões de carne.
Usakhale pakati pa anthu amene amaledzera kapena pakati pa anthu amene amadya nyama mwadyera.
21 Porque o beberrão e o comilão empobrecerão; e a somnolencia faz trazer os vestidos rotos.
Paja anthu oledzera ndi adyera amadzakhala amphawi ndipo aulesi adzavala sanza.
22 Ouve a teu pae, que te gerou, e não desprezes a tua mãe, quando vier a envelhecer.
Mvera abambo ako amene anakubala, usanyoze amayi ako pamene akalamba.
23 Compra a verdade, e não a vendas: a sabedoria, e a disciplina, e a prudencia.
Gula choonadi ndipo usachigulitse; ugulenso nzeru, mwambo ndiponso kumvetsa zinthu bwino.
24 Grandemente se regozijará o pae do justo, e o que gerar a um sabio se alegrará n'elle.
Abambo a munthu wolungama ali ndi chimwemwe chachikulu; Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.
25 Alegrem-se teu pae e tua mãe, e regozije-se a que te gerou.
Abambo ndi amayi ako asangalale; amene anakubereka akondwere!
26 Dá-me, filho meu, o teu coração, e os teus olhos observem os meus caminhos.
Mwana wanga, undikhulupirire ndipo maso ako apenyetsetse njira zanga.
27 Porque cova profunda é a prostituta, e poço estreito a estranha.
Paja mkazi wachiwerewere ali ngati dzenje lozama; ndipo mkazi woyendayenda ali ngati chitsime chopapatiza.
28 Tambem ella, como um salteador, se põe a espreitar, e multiplica entre os homens os iniquos.
Amabisala ngati mbala yachifwamba, ndipo amuna amakhala osakhulupirika chifukwa cha iyeyu.
29 Para quem são os ais? para quem os pezares? para quem as pelejas? para quem as queixas? para quem as feridas sem causa? e para quem os olhos vermelhos?
Ndani ali ndi tsoka? Ndani ali ndi chisoni? Ndani ali pa mkangano? Ndani ali ndi madandawulo? Ndani ali ndi zipsera zosadziwika uko zachokera? Ndani ali ndi maso ofiira?
30 Para os que se demoram perto do vinho, para os que andam buscando bebida misturada.
Ndi amene amakhalitsa pa mowa, amene amapita nalawa vinyo osakanizidwa.
31 Não olhes para o vinho quando se mostra vermelho, quando resplandece no copo e se escoa suavemente.
Usatengeke mtima ndi kufiira kwa vinyo, pamene akuwira mʼchikho pamene akumweka bwino!
32 No seu fim morderá como a cobra, e como o basilisco picará.
Potsiriza pake amaluma ngati njoka, ndipo amajompha ngati mphiri.
33 Os teus olhos olharão para as mulheres estranhas, e o teu coração fallará perversidades.
Maso ako adzaona zinthu zachilendo ndipo maganizo ndi mawu ako adzakhala osokonekera.
34 E serás como o que dorme no meio do mar, e como o que dorme no topo do mastro.
Udzakhala ngati munthu amene ali gone pakati pa nyanja, kapena ngati munthu wogona pa msonga ya mlongoti ya ngalawa.
35 E dirás: Espancaram-me, e não me doeu; maçaram-me, e não o senti; quando virei a despertar? ainda tornarei a buscal-a outra vez
Iwe udzanena kuti, “Anandimenya, koma sindinapwetekedwe! Andimenya koma sindinamve kanthu! Kodi ndidzuka nthawi yanji? Ndiye ndifunefunenso vinyo wina.”

< Provérbios 23 >