< Psalmów 113 >
1 Alleluja. Chwalcie, słudzy PANA, chwalcie imię PANA.
Tamandani Yehova. Mutamandeni, inu atumiki a Yehova, tamandani dzina la Yehova.
2 Niech imię PANA będzie błogosławione, odtąd aż na wieki.
Yehova atamandidwe, kuyambira tsopano mpaka muyaya.
3 Od wschodu słońca aż do jego zachodu, niech imię PANA będzie pochwalone.
Kuyambira ku matulukiro a dzuwa mpaka ku malowero ake, dzina la Yehova liyenera kutamandidwa.
4 PAN jest wywyższony ponad wszystkie narody, jego chwała ponad niebiosa.
Yehova wakwezeka pa anthu a mitundu yonse, ulemerero wake ndi woposa mayiko akumwamba.
5 Któż jak PAN, nasz Bóg, który mieszka na wysokości;
Ndani wofanana ndi Yehova Mulungu wathu, Iye amene amakhala mwaufumu mmwamba?
6 Który zniża się, aby patrzeć na to, co jest na niebie i na ziemi?
amene amawerama pansi kuyangʼana miyamba ndi dziko lapansi?
7 Podnosi nędznego z prochu, a z gnoju podnosi ubogiego;
Iye amakweza munthu wosauka kuchoka pa fumbi ndi kutukula munthu wosowa kuchoka pa dzala;
8 Aby go posadzić z książętami, z książętami swego ludu;
amawakhazika pamodzi ndi mafumu, pamodzi ndi mafumu a anthu ake.
9 On sprawia, że niepłodna staje się matką domu, cieszącą się dziećmi. Alleluja.
Amakhazikitsa mayi wosabereka mʼnyumba yake monga mayi wa ana wosangalala. Tamandani Yehova.