< Habakuka 3 >

1 Modlitwa proroka Habakuka na Syggajon.
Pemphero la mneneri Habakuku potsata mayimbidwe a Sigionoti.
2 PANIE, usłyszałem twoją wieść i uląkłem się. PANIE, ożyw swoje dzieło w środku lat, objaw je w środku lat; w gniewie pamiętaj o miłosierdziu.
Inu Yehova, ndamva za kutchuka kwanu; Inu Yehova, ntchito zanu zandiopsa. Muzichitenso masiku athu ano, masiku athu ano zidziwike; mu ukali wanu mukumbukire kuchita chifundo.
3 Bóg szedł z Temanu, Święty z góry Paran, (Sela) Jego majestat okrył niebiosa, ziemia była pełna jego chwały.
Mulungu anabwera kuchokera ku Temani, Woyerayo kuchokera ku Phiri la Parani. (Sela) Ulemerero wake unaphimba mlengalenga ndipo dziko lapansi linadzaza ndi matamando ake.
4 Jego blask był jak światłość, rogi wychodziły z jego rąk, a tam była ukryta jego moc.
Kuwala kwa ulemerero wake kunali ngati kutuluka kwa dzuwa; kunyezimira kunkatuluka mʼdzanja lake, mʼmene anabisamo mphamvu zake.
5 Przed nim szła zaraza, płonące węgle szły przed jego nogami.
Patsogolo pake pankagwa mliri; nthenda yoopsa inkagwa kumbuyo kwake.
6 Stanął i zmierzył ziemię, spojrzał i rozproszył narody; góry wieczyste zostały skruszone, skłoniły się pagórki dawne. Jego drogi są wieczne.
Iye anayimirira ndi kugwedeza dziko lapansi; anayangʼana ndipo mitundu ya anthu inanjenjemera. Mapiri okhazikika anagumuka ndipo zitunda zakalekale zinatitimira. Njira zake ndi zachikhalire.
7 Widziałem namioty Kuszanu dotknięte uciskiem, a zasłony ziemi Midian drżały.
Ndinaona matenti a ku Kusani ali pa mavuto, mokhala a ku Midiyani muli ululu waukulu.
8 Czy PAN rozgniewał się przeciwko rzekom? Czy [skierowałeś] przeciwko rzekom swój gniew? Czy przeciwko morzu zwróciło się twoje oburzenie, gdy jechałeś na swoich koniach [i na] swoich rydwanach zbawienia?
Inu Yehova, kodi munakwiyira mitsinje? Kodi munakalipira timitsinje? Kodi munapsera mtima nyanja pamene munakwera pa akavalo anu ndiponso magaleta anu achipulumutso?
9 Twój łuk został obnażony [z powodu] przysięgi wypowiedzianej pokoleniom. (Sela) Podzieliłeś ziemię rzekami.
Munasolola uta wanu mʼchimake, munayitanitsa mivi yambiri. (Sela) Munagawa dziko lapansi ndi mitsinje;
10 Widziały cię góry [i] zadrżały, ulewa wód przeminęła. Przepaść wydała swój głos, wysoko podniosła swoje ręce.
mapiri anakuonani ndipo anagwedezeka. Madzi amphamvu anasefukira; nyanja yozama inakokoma ndipo mafunde ake anakwera kwambiri.
11 Słońce i księżyc zatrzymały się w swoim przybytku, szli przy blasku [twoich] strzałów [i] przy blasku twojej lśniącej włóczni.
Dzuwa ndi mwezi zinayima chilili mlengalenga, pa kungʼanima kwa mivi yanu yowulukayo, pa kunyezimira kwa mkondo wanu.
12 W gniewie deptałeś ziemię, w zapalczywości młóciłeś pogan.
Munayendayenda mʼdziko lapansi muli ndi ukali, ndipo munapondereza mitundu ya anthu muli ndi mkwiyo.
13 Wyruszyłeś, aby wybawić swój lud, by ze swoim pomazańcem [go] wybawić; zraniłeś głowę z domu niegodziwego, odkrywając fundament aż do szyi. (Sela)
Munapita kukalanditsa anthu anu, kukapulumutsa wodzozedwa wanu. Munakantha mtsogoleri wa dziko la anthu oyipa, munawononga anthu ake onse. (Sela)
14 Jego oszczepami przebiłeś głowę jego wsi; burzyli się jak wicher, aby mnie rozproszyć; cieszyli się, jakby mieli potajemnie pożreć ubogiego.
Ndi mkondo wake womwe munalasa mtsogoleri wake pamene ankhondo ake anabwera mwamphamvu kudzatibalalitsa, ankasangalala ngati kuti akudzawononga osauka amene akubisala.
15 Jechałeś przez morze na swoich koniach, [przez] skupisko wielkich wód.
Munapondaponda pa nyanja ndi akavalo anu, kuvundula madzi amphamvu.
16 Gdy to usłyszałem, zatrzęsło się moje wnętrze, na ten głos zadrżały moje wargi. Zgnilizna przeniknęła moje kości i cały się trząsłem, słysząc, że mam odpocząć w dniu utrapienia. Gdy nadciągnie na ten lud, zgładzi ich swoim wojskiem.
Ndinamva ndipo mtima wanga unagunda kwambiri, milomo yanga inanjenjemera pakumva phokosolo; mafupa anga anaguluka, ndipo mawondo anga anawombana. Komabe ndikuyembekezera mofatsa, tsiku la masautso limene lidzafike pa mtundu wa anthu umene ukutithira nkhondo.
17 Choćby drzewo figowe nie zakwitło i nie było plonu w winnicach, choćby i owoc oliwy zawiódł, i pola nie przyniosły żywności, trzoda zniknęła z owczarni, i nie było bydła w oborach;
Ngakhale mtengo wa mkuyu usachite maluwa, ndipo mipesa ikhale yopanda mphesa. Ngakhale mitengo ya olivi isabereke zipatso, ndipo mʼminda musatuluke kanthu. Ngakhale nkhosa ndi ngʼombe zithe mʼkhola,
18 Ja jednak będę się radował w PANU, rozraduję się w Bogu mojego zbawienia.
komabe ine ndidzakondwera mwa Yehova, ndidzasangalala mwa Mulungu Mpulumutsi wanga.
19 Pan BÓG jest moją siłą i uczyni moje nogi jak [nogi] łań, i sprawi, że będę chodzić po wyżynach. Przewodnikowi chóru, na moje instrumenty strunowe.
Ambuye Yehova ndiye mphamvu yanga; amalimbitsa miyendo yanga ngati ya mbawala yayikazi, amandithandiza kukafika pamwamba pa phiri. Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za nsambo.

< Habakuka 3 >