< Nahuma 1 >

1 Brzemię Niniwy. Księga widzenia Nahuma Elkoszyty.
Uthenga wonena za Ninive. Buku la masomphenya a Nahumu wa ku Elikosi.
2 PAN jest Bogiem zazdrosnym i mściwym; PAN jest mściwy i pełen gniewu; PAN mści się nad swoimi przeciwnikami i zachowuje gniew wobec swoich wrogów.
Yehova ndi Mulungu wansanje ndiponso wobwezera; Yehova amabwezera ndipo ndi waukali. Yehova amabwezera adani ake ndipo ukali wake umakhala nthawi zonse pa adani akewo.
3 PAN jest nieskory do gniewu i wielki w mocy, a winnego nie uniewinni. Droga PANA [jest] w wichrze i w burzy, a obłok jest prochem pod jego stopami.
Yehova sakwiya msanga koma ndi wa mphamvu yayikulu; ndipo sadzalola kuti munthu wolakwa asalangidwe. Iye amayenda mʼkamvuluvulu ndi mʼnamondwe, ndipo mitambo ndi fumbi la ku mapazi ake.
4 On gromi morze i je wysusza, wysusza też wszystkie rzeki. Przed nim Baszan i Karmel mdleje, a kwiat Libanu więdnie;
Amalamulira nyanja ndipo imawuma; amawumitsa mitsinje yonse. Zomera za ku Basani ndi Karimeli zimawuma ndipo maluwa a ku Lebanoni amafota.
5 Góry drżą przed nim, a pagórki się rozpływają; ziemia płonie przed jego obliczem, okrąg [ziemi] i wszyscy jej mieszkańcy.
Mapiri amagwedera pamaso pake ndipo zitunda zimasungunuka. Dziko lapansi limanjenjemera pamaso pake, dziko lonse ndi zonse zokhala mʼmenemo.
6 Któż się ostoi przed jego oburzeniem? Kto wytrzyma zapalczywość jego gniewu? Jego gniew wylewa się jak ogień, a skały rozpadają się przed nim.
Ndani angathe kuyima pamaso pake Iye akalusa? Ndani angapirire mkwiyo wake woopsa? Ukali wake ukuyaka ngati moto; matanthwe akunyeka pamaso pake.
7 Dobry jest PAN – warownia w dniu ucisku; zna tych, którzy mu ufają.
Yehova ndi wabwino, ndiye kothawirako nthawi ya masautso. Amasamalira amene amamudalira,
8 Ale gwałtowną powodzią zniszczy jej miejsce, ciemność będzie ścigała jego wrogów.
koma ndi madzi achigumula choopsa Iye adzawononga adani ake (Ninive); adzapirikitsira adani ake ku malo a mdima.
9 Co zamierzacie przeciwko PANU? On dokona zniszczenia, ucisk nie powstanie po raz drugi.
Chiwembu chilichonse chimene akukonzekera kumuchitira Yehova adzachiwononga kotheratu; msautso sudzabweranso kachiwiri.
10 Gdy bowiem będą jak splecione ciernie i jak pijacy upojeni [winem], jak suche ściernisko do szczętu spłoną.
Iwo adzakodwa mu ziyangoyango za minga ndipo adzaledzera ndi vinyo wawo; adzatenthedwa ngati ziputu zowuma.
11 Z ciebie wyszedł ten, który obmyślił zło przeciwko PANU, doradca nikczemny.
Kwa iwe, Ninive, kunachokera munthu wa cholinga choyipa, wofuna kuchitira Yehova chiwembu, amene amapereka uphungu woyipa.
12 Tak mówi PAN: Chociaż są spokojni i tak liczni, będą jednak skoszeni, gdy przejdzie. Chociaż cię trapiłem, już więcej nie będę cię trapił.
Yehova akuti, “Ngakhale Asiriyawo ali ndi abwenzi, kaya iwowo ndi ambiri, koma adzawonongedwa ndi kutheratu. Ngakhale ndinakuzunza iwe Yuda, sindidzakuzunzanso.
13 Teraz bowiem złamię jego jarzmo, aby na tobie nie leżało, a rozerwę twoje więzy.
Tsopano ndidzathyola goli lake pa khosi lako ndipo ndidzadula maunyolo ako.”
14 O tobie PAN rozkazał, że twoje imię już nie będzie miało więcej potomstwa. Wyniszczę z domu twoich bogów rzeźbione i lane posągi. Przygotuję ci grób, gdyż jesteś nikczemny.
Yehova walamulira za iwe, Ninive kuti, “Sudzakhala ndi zidzukulu zimene zidzadziwike ndi dzina lako. Ndidzawononga zifanizo zosema ndi mafano owumba amene ali mʼnyumba ya milungu yako. Ine ndidzakukumbira manda chifukwa ndiwe woyipitsitsa.”
15 Oto na górach nogi opowiadającego dobre wieści, zwiastującego pokój. Obchodź, Judo, swoje uroczyste święta, wypełniaj swoje śluby. Nikczemnik bowiem już nie przejdzie przez ciebie, został doszczętnie zgładzony.
Taonani, pa phiripo, mapazi a munthu amene akubweretsa nkhani yabwino, amene akulengeza za mtendere! Inu anthu a ku Yuda, chitani madyerero anu ndipo kwaniritsani malumbiro anu. Anthu oyipa sadzakuthiraninso nkhondo; iwo adzawonongedwa kotheratu.

< Nahuma 1 >