< Objawienie 22 +

1 I ukazał mi rzekę czystą wody żywota, jasną jako kryształ, wychodzącą z stolicy Bożej i Barankowej.
Ndipo mngeloyo anandionetsa mtsinje wamadzi amoyo, oyera ngati mwala wa krustalo ukutuluka ku mpando waufumu wa Mulungu ndi wa Mwana Wankhosa,
2 A w pośród rynku jego z obu stron rzeki było drzewo żywota, przynoszące owoc dwanaścioraki, na każdy miesiąc wydawające owoc swój, a liście drzewa służyły ku uzdrowieniu pogan.
Ukuyenda pakati pa msewu waukulu wa mu mzindawo. Mbali iliyonse ya mtsinjewo kunali mtengo wamoyo, utabala zipatso khumi ndi ziwiri. Kubereka zipatso mwezi uliwonse. Ndipo masamba a mtengowo ndi mankhwala wochiritsa anthu a mitundu ina.
3 I nie będzie więcej żadnego przeklęstwa, ale stolica Boża i Barankowa w niem będzie, a słudzy jego służyć mu będą,
Sipadzakhalanso temberero lililonse. Mpando waufumu wa Mulungu ndi wa Mwana Wankhosa udzakhala mu mzindawo, ndipo atumiki ake adzamutumikira.
4 I patrzyć będą na oblicze jego, a imię jego na czołach ich będzie.
Iwo adzaona nkhope yake ndipo dzina lake lidzalembedwa pa mphumi zawo.
5 I nocy tam nie będzie i nie będą potrzebować świecy i światłości słonecznej; bo je Pan Bóg oświeca, i królować będą na wieki wieków. (aiōn g165)
Sipadzakhalanso usiku. Sadzafuna kuwala kwa nyale kapena kwa dzuwa pakuti Ambuye Mulungu adzakhala kuwala kwawo. Ndipo adzalamulira kwamuyaya. (aiōn g165)
6 I rzekł mi: Te słowa wierne są i prawdziwe, a Pan, Bóg świętych proroków, posłał Anioła swego, aby ukazał sługom swoim, co się ma stać w rychle.
Mngeloyo anandiwuza kuti, “Mawu awa ndi okhulupirika ndi owona. Ambuye Mulungu wa mizimu ya aneneri anatumiza mngelo wake kudzaonetsa atumiki ake zinthu zimene ziyenera kuchitika posachedwapa.”
7 Oto przychodzę rychło: Błogosławiony, który zachowuje słowa proroctwa księgi tej.
“Taonani, ndikubwera posachedwa! Wodala ndi amene asunga mawu oneneratu za kutsogolo a mʼbuku ili.”
8 A ja Jan widziałem i słyszałem te rzeczy. A gdym słyszał i widział, upadłem, abym się pokłonił przed nogami Anioła onego, który mi to pokazywał.
Ine Yohane, ndine amene ndinamva ndi kuona zinthu izi. Ndipo pamene ndinamva ndi kuona izi ndinagwa pansi kuti ndipembedze mngelo amene amandionetsa zimenezi.
9 Ale mi on rzekł: Patrz, abyś tego nie czynił; bom jest spółsługa twój i braci twoich proroków, i tych, co chowają słowa księgi tej; Bogu się kłaniaj.
Koma mngeloyo anandiwuza kuti, “Usatero ayi! Ine ndine wotumikira monga iwe pamodzi ndi abale ako aneneri ndi onse amene amasunga mawu a mʼbuku pembedzani Mulungu.”
10 Potem mi rzekł: Nie pieczętuj słów proroctwa księgi tej; albowiem czas blisko jest.
Kenaka anandiwuza kuti, “Usabise mawu onena zamʼtsogolo a mʼbuku ili chifukwa nthawi yayandikira.
11 Kto szkodzi, niech jeszcze szkodzi; a kto jest plugawy, niech jeszcze będzie plugawszy; a kto jest sprawiedliwy, niech się jeszcze usprawiedliwi; a kto święty, niech jeszcze będzie poświęcony.
Wochita zoyipa apitirire kuchita zoyipazo; wochita zonyansa apitirire kuchita zonyansazo; wochita zabwino apitirire kuchita zabwinozo; ndipo woyera mtima apitirire kukhala woyera mtima.”
12 A oto przychodzę rychło, a zapłata moja jest ze mną, abym oddał każdemu według uczynków jego.
“Taonani, ndikubwera posachedwa! Ndikubwera ndi mphotho zanga kuti ndidzapereke kwa aliyense malinga ndi zimene anachita.
13 Jam jest Alfa i Omega, początek i koniec, pierwszy i ostateczny.
Ine ndine Alefa ndi Omega, Woyamba ndi Wotsiriza, Chiyambi ndi Chimaliziro ndine.
14 Błogosławieni, którzy czynią przykazania jego, aby mieli prawo do drzewa żywota, i aby weszli bramami do miasta.
“Odala amene achapa mikanjo yawo, kuti akhale ndi ufulu wopita ku mtengo wamoyo ndi kuti akalowe mʼzipata za mu mzindawo.
15 A na dworze będą psy i czarownicy, i wszetecznicy, i mężobójcy, i bałwochwalcy, i każdy, który miłuje i czyni kłamstwo.
Kunja kuli agalu, amatsenga, achiwerewere, akupha anthu, opembedza mafano ndi aliyense amene amakonda bodza ndi kulichita.
16 Ja Jezus posłałem Anioła mojego, aby wam świadczył o tych rzeczach we zborach. Jam jest korzeń i rodzaj on Dawidowy, gwiazda jasna i poranna.
“Ine Yesu, ndatuma mngelo wanga kuti achitire umboni uwu ku mipingo. Ine ndine Muzu ndi Chipatso cha Davide ndipo ndine Nthanda Yonyezimira.”
17 A Duch i oblubienica mówią: Przyjdź! A kto słyszy, niech rzecze: Przyjdź! A kto pragnie, niech przyjdzie; a kto chce, niech bierze wodę żywota darmo.
Mzimu Woyera ndi mkwatibwi akuti, “Bwerani!” Ndipo amene akumva anena kuti Bwerani! Iye amene ali ndi ludzu abwere, ndipo aliyense amene afuna alandire mphatso yaulere ya madzi amoyo.
18 A oświadczam się każdemu słuchającemu słów proroctwa księgi tej: Jeźliby kto przydał do tego, przyda mu też Bóg plag opisanych w tej księdze;
Ndikuchenjeza aliyense amene akumva mawu onena zamʼtsogolo a mʼbukuli kuti, “Ngati wina awonjezerapo kalikonse, Mulungu adzamuwonjezera miliri imene yalembedwa mʼbuku ili.
19 A jeźliby kto ujął ze słów księgi proroctwa tego, odejmie też Bóg część jego z księgi żywota i z miasta świętego, i z tych rzeczy, które są napisane w tej księdze.
Ndipo wina akachotsapo mawu onena zamʼtsogolo a mʼbuku ili, Mulungu adzachotsa gawo lake pa mtengo wamoyo ndi la mu mzinda woyera zimene zanenedwa mʼbuku ili.”
20 Tak mówi ten, który świadectwo daje o tych rzeczach: Zaiste, przyjdę rychło. Amen. I owszem przyjdź, Panie Jezusie!
Iye amene akuchitira umboni pa zinthu izi akuti, “Inde, Ine ndikubwera posachedwa.” Ameni. Bwerani Ambuye Yesu.
21 Łaska Pana naszego, Jezusa Chrystusa, niech będzie z wami wszystkimi. Amen.
Chisomo cha Ambuye Yesu chikhale ndi anthu onse. Ameni.

< Objawienie 22 +