< Objawienie 21 >

1 Potemem widział niebo nowe i ziemię nową; albowiem pierwsze niebo i pierwsza ziemia przeminęła, a morza już więcej nie było.
Kenaka ndinaona kumwamba kwatsopano ndi dziko lapansi latsopano pakuti kumwamba koyamba ndi dziko lapansi loyamba zinapita ndipo kunalibenso nyanja ina iliyonse.
2 A ja Jan widziałem ono święte miasto, Jeruzalem nowe, zstępujące z nieba od Boga zgotowane, jako oblubienicę ubraną mężowi swemu.
Ndinaona mzinda wopatulika, Yerusalemu watsopano, ukutsika kuchokera kumwamba kwa Mulungu, utakonzedwa ngati mkwatibwi wovala zokongola kukonzekera mwamuna wake.
3 I słyszałem głos wielki z nieba mówiący: Oto przybytek Boży z ludźmi, i będzie mieszkał z nimi; a oni będą ludem jego, a sam Bóg będzie z nimi, będąc Bogiem ich.
Ndipo ndinamva mawu ofuwula kuchokera ku Mpando Waufumu kuti, “Taonani! Malo wokhalapo Mulungu ali pakati pa anthu, ndipo Iye adzakhala ndi anthuwo. Iwo adzakhala anthu ake ndipo Mulungu mwini adzakhala nawo nakhala Mulungu wawo.
4 I otrze Bóg wszelką łzę z oczów ich; a śmierci więcej nie będzie, ani smutku, ani krzyku, ani boleści nie będzie; albowiem pierwsze rzeczy pominęły.
‘Mulungu adzapukuta misozi yonse mʼmaso mwawo. Sikudzakhalanso imfa kapena kukhuza maliro kapena kulira kapena ululu popeza zakale zapita.’”
5 I rzekł ten, który siedział na stolicy: Oto wszystko nowe czynię. I rzekł mi: Napisz: bo te słowa są wierne i prawdziwe.
Amene anakhala pa mpando waufumuyo anati, “Ndikulenga zinthu zonse zikhale zatsopano!” Ndipo anati, “Lemba izi, pakuti mawu awa ndi okhulupirika ndi woona.”
6 I rzekł mi: Stało się. Jam jest Alfa i Omega, początek i koniec. Ja pragnącemu dam darmo ze źródła wody żywej.
Iye anandiwuza kuti, “Kwatha. Ine ndine Alefa ndi Omega, Woyamba ndi Wotsiriza. Kwa onse akumva ludzu, ndidzawapatsa zakumwa zaulere zochokera ku kasupe wamadzi amoyo.
7 Kto zwycięży, odziedziczy wszystko i będę mu Bogiem, a on mi będzie synem.
Iye amene adzapambane adzalandira zonsezi, ndipo ndidzakhala Mulungu wake ndi Iye adzakhala mwana wanga.
8 Lecz bojaźliwym i niewiernym, i obmierzłym, i mężobójcom, i wszetecznikom, i czarownikom, i bałwochwalcom, i wszystkim kłamcom część ich dana będzie w jeziorze gorejącem ogniem i siarką: Tać jest śmierć wtóra. (Limnē Pyr g3041 g4442)
Koma amantha, osakhulupirira, okonda zonyansa, opha anthu, achiwerewere, amatsenga, opembedza mafano ndi abodza, malo awo adzakhala nyanja yamoto ya sulufule wotentha. Iyi ndi imfa yachiwiri.” (Limnē Pyr g3041 g4442)
9 Tedy przyszedł do mnie jeden z onych siedmiu Aniołów, którzy mieli siedm czasz napełnionych siedmioma plagami ostatecznemi, i mówił ze mną, i rzekł: Chodź sam, okażę ci oblubienicę, małżonkę Barankową.
Mmodzi wa angelo asanu ndi awiri aja, anali ndi mbale zisanu ndi ziwiri zodzaza ndi miliri yotsiriza isanu ndi iwiri anandiwuza kuti, “Bwera, ine ndidzakuonetsa mkwatibwi wa Mwana Wankhosa.”
10 I zaniósł mię w duchu na górę wielką i wysoką, i okazał mi miasto wielkie, ono święte Jeruzalem, zstępujące z nieba od Boga,
Ndipo anandinyamula mwa Mzimu Woyera kupita nane ku phiri lalikulu ndi lalitali nandionetsa mzinda wopatulika, Yerusalemu ukutsika kuchokera kumwamba kwa Mulungu.
11 Mające chwałę Bożą, którego światłość podobna była kamieniowi najkosztowniejszemu, jako kamieniowi jaspisowi, na kształt kryształu przezroczystemu;
Unawala ndi ulemerero wa Mulungu, ndipo kuthwanima kwake kunali ngati mwala wamtengowapatali, ngati jasipa; woyera ngati krustalo.
12 I mające mur wielki i wysoki, mające bram dwanaście, a na onych bramach dwanaście Aniołów i imiona napisane, które są dwanaście pokoleń synów Izraelskich.
Mzindawo unali ndi mpanda waukulu ndi wautali, unali ndi zipata khumi ndi ziwiri, ndipo panali angelo khumi ndi awiri. Pa chipata chilichonse panayima mngelo. Pa chipata chilichonse panalembedwa dzina la fuko la Israeli.
13 Od wschodu bramy trzy, od północy bramy trzy, od południa bramy trzy, od zachodu bramy trzy.
Kummawa kunali zipata zitatu, kumpoto zitatu, kummwera zitatu ndi kumadzulo zitatu.
14 A mur miasta miał gruntów dwanaście, a na nich dwanaście imion dwunastu Apostołów Barankowych.
Mpanda wa mzindawu unali ndi maziko khumi ndi awiri ndipo pa mazikopo panali mayina khumi ndi awiri a atumwi a Mwana Wankhosa.
15 A ten, co mówił ze mną, miał trzcinę złotą, a zmierzył miasto i bramy jego, i mur jego.
Mngelo amene ankayankhula nane uja anali ndi ndodo yagolide yoyezera mzindawo, zipata zake ndi mpanda wake.
16 A położenie miasta onego jest czworograniaste, a długość jego taka jest, jako i szerokość. I pomierzył miasto ono trzciną na dwanaście tysięcy stajan; a długość i szerokość i wysokość jego równe są.
Mzindawo unamangidwa mofanana kutalika kwake, mulitali ndi mulifupi munali mofanana. Anayeza mzindawo ndi ndodo ija ndipo anapeza kuti mulitali, mulifupi ndi msinkhu wake kutalika kwake kunali makilomita 2,200.
17 I zmierzył mur jego na sto czterdzieści cztery łokcie miary człowieczej, która jest miara Aniołowa.
Anayesa mpanda uja ndipo kuchindikala kwake kunali kopitirirapo mamita 65 monga mwa muyeso wa anthu umene mngelo anagwiritsa ntchito.
18 A było budowanie muru jego z jaspisu; a samo miasto było złoto czyste, podobne szkłu czystemu.
Mpandawo unapangidwa ndi yasipa, ndipo mzindawo unali wagolide oyengeka owala ngati galasi.
19 A grunty muru miasta ozdobione były wszelkim kamieniem drogim. Pierwszy grunt był jaspis, wtóry szafir, trzeci chalcedon, czwarty szmaragd.
Maziko a mpanda wa mzindawo anali okongoletsedwa ndi miyala yamtengowapatali ya mtundu uliwonse. Maziko oyamba anali yasipa, achiwiri anali safiro, achitatu ndi kalikedo, achinayi ndi simaragido,
20 Piąty sardoniks, szósty sardyjusz, siódmy chrysolit, ósmy beryllus, dziewiąty topazyjusz, dziesiąty chrysopras, jedenasty hijacynt, dwunasty ametyst.
achisanu ndi sardiyo, achisanu ndi chiwiri ndi krusolito, achisanu ndi chitatu ndi berulo, achisanu ndi chinayi ndi topaziyo, a khumi ndi krusoprazo, a khumi ndi chimodzi ndi huakito, a khumi ndi chiwiri ndi emetusto.
21 A dwanaście bram jest dwanaście pereł: a każda brama była z jednej perły, a rynek miasta złoto czyste jako szkło przezroczyste.
Zipata khumi ndi ziwiri zija zinapangidwa ndi ngale, chipata chilichonse chinapangidwa ndi ngale imodzi. Misewu ya mzindawo inali yopangidwa ndi golide oyengeka, owala ngati galasi.
22 Alem kościoła nie widział w niem; albowiem Pan, Bóg wszechmogący, jest kościołem jego, i Baranek.
Ine sindinaone Nyumba ya Mulungu iliyonse mu mzindawo chifukwa Ambuye Mulungu Wamphamvuzonse ndi Mwana Wankhosa ndiwo Nyumba yake.
23 A nie potrzebuje to miasto słońca ani księżyca, aby świeciły w niem; albowiem chwała Boża oświeciła je, a świecą jego jest Baranek.
Palibe chifukwa choti dzuwa kapena mwezi ziwale popeza mu mzindawo ulemerero wa Mulungu ndiwo umawalamo ndipo nyale yake ndi Mwana Wankhosa uja.
24 A narody, które będą zbawione, będą chodziły w świetle jego, a królowie ziemscy chwałę i cześć swoję do niego przyniosą.
Mitundu ya anthu idzayenda mʼkuwala kwake ndipo mafumu a dziko lapansi adzabweretsa ulemerero wawo mu mzindamo.
25 A bramy jego nie będą zamknięte we dnie; albowiem tam nocy nie będzie.
Zipata zake sizidzatsekedwa ngakhale tsiku limodzi lomwe pakuti sikudzakhala usiku kumeneko.
26 I wniosą do niego chwałę i cześć narodów.
Ulemerero ndi ulemu wa mitundu ya anthu adzapita nazo kumeneko.
27 I nie wnijdzie do niego nic nieczystego i czyniącego obrzydliwość i kłamstwo, tylko ci, którzy są napisani w księgach żywota Barankowych.
Kanthu kosayeretsedwa sikadzalowamo, kuphatikizanso aliyense wochita zinthu zochititsa manyazi ndi zachinyengo, koma okhawo amene mayina awo alembedwa mʼbuku lamoyo la Mwana Wankhosa.

< Objawienie 21 >