< Psalmów 72 >
1 Salomonowi. Boże! daj królowi sądy twoje, a sprawiedliwość twoję synowi królewskiemu;
Salimo la Solomoni. Patsani mwana wa mfumu nzeru zanu zoweruzira mwa chilungamo, Inu Mulungu mupatseni mwana wa mfumu chilungamo chanu.
2 Aby sądził lud twój w sprawiedliwości, a ubogich twoich w prawości.
Iye adzaweruza anthu anu mwachilungamo, anthu anu ozunzika mosakondera.
3 Przyniosą góry ludowi pokój, a pagórki sprawiedliwość.
Mapiri adzabweretsa chuma kwa anthu anu, timapiri tidzabweretsa zipatso zachilungamo.
4 Będzie sądził ubogich z ludu, a wybawi synów ubogiego; ale gwałtownika pokruszy.
Iye adzateteza ozunzika pakati pa anthu ndi kupulumutsa ana a anthu osowa; adzaphwanya ozunza anzawo.
5 Będą się bać ciebie, póki słońce i miesiąc trwać będzie, od narodu aż do narodu.
Adzakhala ndi moyo pa mibado yonse, nthawi zonse pamene dzuwa ndi mwezi zikuwala.
6 Jako zstępuje deszcz na pokoszoną trawę, a deszcz kroplisty skrapiający ziemię:
Iye adzakhala kugwa kwa mvula pa minda yolimidwa ngati mivumbi yothirira dziko lapansi.
7 Tak sprawiedliwy zakwitnie za dni jego, a będzie obfitość pokoju, dokąd miesiąca staje.
Mʼmasiku a munthu wolungama adzakhazikika; chuma chidzachuluka mpaka mwezi utaleka kuwala.
8 Będzie panował od morza aż do morza, i od rzeki aż do kończyn ziemi.
Iye adzalamulira kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina ndiponso kuchokera ku mtsinje mpaka ku malekezero a dziko lapansi.
9 Przed nim padać będą mieszkający na pustyniach, a nieprzyjaciele jego proch lizać będą.
Mafuko a mʼchipululu adzawerama pamaso pake ndipo adani ake adzanyambita fumbi.
10 Królowie od morza i z wysep dary mu przyniosą; królowie Sebejscy i Sabejscy upominki oddadzą.
Mafumu a ku Tarisisi ndi a ku zilumba zakutali adzabweretsa mitulo kwa iye, mafumu a ku Seba ndi Seba adzapereka mphatso kwa iyeyo.
11 I będą mu się kłaniać wszyscy królowie; wszystkie narody służyć mu będą.
Mafumu onse adzamuweramira ndipo mitundu yonse idzamutumikira.
12 Albowiem wyrwie ubogiego wołającego, i nędznego, który nie ma pomocnika.
Pakuti iye adzawombola wosowa amene akulira, wozunzika amene alibe wina womuthandiza.
13 Zmiłuje się nad ubogim, i nad niedostatecznym, a duszę nędznych wybawi.
Iye adzachitira chifundo anthu ofowoka ndi anthu osowa ndi kupulumutsa osowa ku imfa.
14 Od zdrady i gwałtu wybawi duszę ich; bo droga jest krew ich przed oczyma jego.
Iye adzalanditsa iwo ku mazunzo ndi chiwawa pakuti magazi awo ndi amtengo wapatali pamaso pake.
15 I będzie żył, a dawać mu będą złoto sabejskie, i ustawicznie się za nim modlić będą, cały dzień błogosławić mu będą.
Iye akhale ndi moyo wautali; golide ochokera ku Seba apatsidwe kwa iye. Anthu amupempherere nthawi zonse ndi kumudalitsa tsiku lonse.
16 Gdy się wrzuci garść zboża do ziemi na wierzchu gór, zaszumi jako Liban urodzaj jego, a mieszczanie zakwitną jako zioła polne.
Mulole kuti tirigu achuluke mʼdziko lonse; pamwamba pa mapiri pakhale tirigu. Zipatso zake zichuluke ngati za ku Lebanoni; zichuluke ngati udzu wakuthengo
17 Imię jego będzie na wieki; pokąd słońce trwa, dziedziczyć będzie imię jego, a błogosławiąc sobie w nim wszystkie narody wielbić go będą.
Dzina lake likhazikike kwamuyaya, lipitirire kukhala monga momwe limakhalira dzuwa. Mitundu yonse idzadalitsika kudzera mwa iye ndipo iwo adzamutcha iye wodala.
18 Błogosławiony Pan Bóg, Bóg Izraelski, który sam cuda czyni.
Matamando akhale kwa Yehova Mulungu, Mulungu wa Israeli amene Iye yekha amachita ntchito zodabwitsa.
19 I błogosławione imię chwały jego na wieki, a niech będzie napełniona chwałą jego wszystka ziemia. Amen, Amen.
Matamando akhale ku dzina lake laulemerero kwamuyaya dziko lonse lapansi lidzaze ndi ulemerero wake. Ameni ndi Ameni.
20 A tuć się kończą modlitwy Dawida, syna Isajego.
Uku ndiko kumaliza kwa mapemphero a Davide mwana wa Yese.