< Hioba 26 >

1 A Ijob odpowiadając rzekł:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 Jakożeś ratował tego, który nie ma mocy? a jakoś wybawił ramię, które nie ma siły?
“Wamuthandizadi munthu wopanda mphamvu! Walimbitsadi dzanja la munthu wofowoka!
3 Jakążeś dał radę temu, co nie ma mądrości? Azaś go samej rzeczy gruntownie nie wyuczył?
Wapereka malangizo kwa munthu amene alibe nzeru! Ndipotu waonetsadi nzeru zochuluka!
4 Komużeś powiedział te słowa? Czyjże duch wyszedł od ciebie?
Kodi wakuthandiza ndani kuti uyankhule mawu awa? Ndipo ndi mzimu wa yani umene unayankhula pakamwa pako?
5 I martwe rzeczy rodzą się pod wodami, i obywatele ich.
“Mizimu ya anthu akufa ikunjenjemera pansi pa madzi, ndi zonse zokhala mʼmadzimo.
6 Odkryte są przepaści przed nim, a nie ma przykrycia zatracenie. (Sheol h7585)
Dziko la anthu akufa ndi lapululu pamaso pa Mulungu; chiwonongeko ndi chosaphimbidwa. (Sheol h7585)
7 Rozciągnął północy nad miejscem próżnem, a ziemię zawiesił na niczem.
Mulungu anayala thambo la kumpoto pa phompho; Iye anakoloweka dziko lapansi mʼmalo mwake pamene panali popanda nʼkanthu komwe.
8 Zawiązuje wody na obłokach swoich, a nie rwie się obłok pod nimi.
Amasunga madzi ambiri mʼmitambo yake, koma mitamboyo siphulika chifukwa cha kulemera kwa madziwo.
9 Zatrzymuje stolicę swoję, rozpostarłszy nad nią obłok swój.
Iye amaphimba mwezi wowala, amawuphimba ndi mitambo yake.
10 Położył granice wodom, aż weźmie koniec światłość i ciemność.
Mulungu anawalembera madzi malire wonga uta, kukhala malire pakati pa kuwunika ndi mdima.
11 Słupy niebieskie trzęsą się, i chwieją się na gromienie jego.
Mizati yochirikiza mitambo yakumwamba imanjenjemera, ndi kudabwa pa kudzudzula kwake.
12 Mocą swą dzieli morze, a roztropnością swą uśmierza nawałności jego.
Ndi mphamvu zake anatontholetsa nyanja; ndi nzeru zake anakantha chirombo cha mʼmadzi chija chotchedwa Rahabe.
13 Duchem swym niebiosa przyozdobił, a ręka jego stworzyła węża skrętnego.
Ndi mpweya wake anayeretsa zamumlengalenga, dzanja lake linapha chinjoka chothawa chija.
14 Oto teć są tylko części dróg jego, lecz i ta trocha niewybadana, cośmy słyszeli o nim, a grzmot wielkiej możności jego któż zrozumie?
Zimenezi ndi pangʼono chabe mwa ntchito yake; tingomva pangʼono za Iye ngati kunongʼona! Kodi ndani angathe kudziwa kukula kwa mphamvu zake?”

< Hioba 26 >