< Ezechiela 18 >

1 I stało się słowo Pańskie do mnie, mówiąc:
Yehova anandiyankhula nati:
2 Cóż wam po tem, iż używacie tej przypowieści o ziemi Izraelskiej mówiąc: Ojcowie jedli jagodę cierpką, a synów zęby drętwieją.
“Kodi anthu inu mumatanthauza chiyani mukamabwerezabwereza kunena mwambi uwu wokhudza dziko la Israeli kuti: “‘Nkhuyu zodya akulu zimapota ndi ana omwe?’”
3 Jako żyję Ja, mówi panujący Pan, że wy nie będziecie więcej mogli używać tej przypowieści w Izraelu.
“Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, simudzanenanso mwambi umenewu mu Israeli.
4 Oto dusze wszystkie moje są, jako dusza ojcowska tak i dusza synowska moje są; dusza, która grzeszy, ta umrze.
Pakuti moyo uliwonse ndi wanga. Moyo wa abambo ndi wanga, wamwananso ndi wanga. Munthu wochimwa ndi amene adzafe.
5 Bo byłliby mąż sprawiedliwy, a czyniłby sąd i sprawiedliwość,
“Tiyerekeze kuti pali munthu wolungama amene amachita zolungama ndi zolondola.
6 Któryby na górach nie jadał, a oczówby swych nie podnosił do plugawych bałwanów domu Izraelskiego, a żonyby bliźniego swego nie zmazał, i do niewiasty dla nieczystoty oddalonej nie przystąpił;
Iye sadyera nawo pa mapiri a chipembedzo kapena kupembedza mafano a Aisraeli. Iye sayipitsa mkazi wa mnzake kapena kugonana ndi mkazi pamene akusamba.
7 Któryby nikogo nie uciskał, zastawby dłużnikowi swemu wracał, cudzegoby gwałtem nie brał, chlebaby swego łaknącemu udzielał, a nagiegoby szatą przyodziewał;
Iye sapondereza munthu wina aliyense, koma amabwezera wangongole nʼchigwiriro chake. Iye salanda zinthu za osauka, koma amapereka chakudya kwa anthu anjala, ndipo amapereka zovala kwa anthu ausiwa.
8 Któryby na lichwę nie dawał, i płatuby nie brał, od nieprawościby odwracał rękę swoję, a sądby sprawiedliwy czynił między mężem a mężem;
Iye sakongoletsa ndalama mwa katapira, kapena kulandira chiwongoladzanja chachikulu. Amadziletsa kuchita zoyipa ndipo sakondera poweruza milandu.
9 Któryby w ustawach moich chodził, a sądówby moich przestrzegał, czyniąc, co jest prawego: ten sprawiedliwy pewnie żyć będzie, mówi panujący Pan.
Iye amatsatira malangizo anga, ndipo amasunga malamulo anga mokhulupirika. Munthu ameneyo ndi wolungama; iye adzakhala ndithu ndi moyo, akutero Ambuye Yehova.
10 A gdyby spłodził syna łotra, krew wylewającego, któryby czemkolwiek z tych rzeczy bratu szkodził,
“Tiyerekeze kuti munthu wolungama chotere wabala mwana chimbalangondo amene amakhalira kupha anthu ndi kuchita zinthu zina zotere.
11 A tegoby wszystkiego nie czynił, owszemby i na górach jadał, i żonęby bliźniego swego zmazał,
Iye nʼkumachita zinthu zimene ngakhale abambo ake sanachitepo. “Amadyera nawo ku mapiri achipembedzo. Amayipitsa mkazi wa mnzake.
12 Ubogiegoby i nędznego uciskał, co cudzego jest, gwałtemby zabierał, zastawuby nie wracał, a do plugawych bałwanów podnosiłby oczy swoje, i obrzydliwościby czynił,
Iye amapondereza munthu wosauka ndi wosowa. Amalanda zinthu za osauka. Sabweza chikole cha munthu wa ngongole. Iye amatembenukira ku mafano nachita zonyansa.
13 Na lichwęby dawał, i płat brał, izali żyć będzie? Nie będzie żył; ponieważ te wszystkie obrzydliwości czynił: śmiercią umrze, krew jego na nim będzie.
Iye amakongoletsa mwa katapira ndipo amalandira chiwongoladzanja chachikulu. Kodi munthu wotereyu nʼkukhala ndi moyo? Ayi ndithu! Chifukwa wachita zinthu zonyansa zonsezi, adzaphedwa ndipo adzalandira chilango chomuyenera.
14 A oto jeżeliby spłodził syna, któryby widział wszystkie grzechy ojca swego, które czynił, a widząc nie czyniłby tak;
“Tsono tiyerekeze kuti munthu woyipa uyu wabala mwana amene amaona machimo onse amene abambo ake ankachita. Ngakhale amaona koma osatsanzira ntchito zake zoyipazo.
15 Na górachby nie jadał, a oczówby swych nie podnosił do plugawych bałwanów domu Izraelskiego, żonyby bliźniego swego nie zmazał,
“Sadyera nawo pa mapiri achipembedzo. Sapembedza mafano a ku Israeli. Sayipitsa mkazi wa mnzake.
16 I nikogoby nie uciskał, zastawuby nie zatrzymywał, a cudzegoby gwałtem nie brał, chlebaby swego łaknącemu udzielał, a nagiegoby szatą przyodział,
Sapondereza munthu wina aliyense. Satenga chikole akabwereketsa chinthu. Salanda zinthu za osauka. Salanda zinthu za munthu. Amapereka chakudya kwa anthu anjala. Amapereka zovala kwa anthu aumphawi.
17 Od nieprawegoby odwrócił rękę swoję, lichwyby i płatu nie brał, sądyby moje czynił, w ustawachby moich chodził: ten nie umrze dla nieprawości ojca swego, ale pewnie żyć będzie.
Amadziletsa kuchita zoyipa. Sakongoletsa kuti apezepo phindu. Salandira chiwongoladzanja. Amasunga malangizo anga ndi kumvera malamulo anga. Munthu wotereyo sadzafa chifukwa cha machimo a abambo ake. Adzakhala ndi moyo ndithu.
18 Lecz ojciec jego, przeto, że czynił krzywdę, co jest cudzego, bratu gwałtem brał, a to, co jest dobrego, nie czynił w pośrodku ludu swego: przetoż oto umrze dla nieprawości swojej.
Koma abambo ake, popeza kuti anazunza anthu ena ndi kubera mʼbale wawo ndiponso popeza kuti sanachitire zabwino anansi ake, adzafera machimo ake omwe.
19 Ale mówicie: Czemuż? Izali nie poniesie syn nieprawości ojcowskiej? Gdy syn sąd i sprawiedliwość czyni, wszystkich ustaw moich strzeże i czyni je, pewnie żyć będzie.
“Mwina inu mukhoza kufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani mwana salangidwa chifukwa cha kulakwa kwa abambo ake? Ayi, mwanayo adzakhala ndi moyo chifukwa ankachita zolungama ndi zolondola ndipo ankasamala kumvera malamulo anga onse.
20 Dusza, która grzeszy, ta umrze; ale syn nie poniesie nieprawości ojcowskiej, ani ojciec poniesie nieprawości synowskiej; sprawiedliwość sprawiedliwego przy nim zostanie, a niepobożność niepobożnego nań przypadnie.
Munthu wochimwa ndiye amene adzafe. Mwana sadzapezeka wolakwa chifukwa cha abambo ake, kapena abambo kupezeka wolakwa chifukwa cha mwana wawo. Chilungamo cha munthu wolungama ndicho chidzamupulutse, ndipo kuyipa kwa munthu wochimwa ndiko kudzamuwonongetse.
21 A jeźliby się niepobożny odwrócił od wszystkich grzechów swoich, które czynił, a strzegłby wszystkich ustaw moich, i czyniłby sąd i sprawiedliwość, pewnie żyć będzie, nie umrze;
“‘Munthu woyipa akatembenuka mtima ndi kusiya machimo amene ankachita ndi kuyamba kumvera malamulo anga ndi kumachita zolungama ndi zokhulupirika, ndiye kuti adzakhala ndi moyo. Sadzafa ayi.
22 Żadne przestępstwa jego, których się dopuścił, nie będą mu przypominane; w sprawiedliwości swej, którąby czynił, żyć będzie.
Zoyipa zake zonse zidzakhululukidwa. Chifukwa cha zinthu zolungama zimene anazichita adzakhala ndi moyo.
23 Azaż Ja się kocham w śmierci niepobożnego? mrwi panujący Pan. Izali nie raczej, gdy się odwróci od dróg swoich, aby żył?
Kodi Ine ndimakondwera ndi imfa ya munthu woyipa? Ayi, ndimakondwera pamene woyipa watembenuka mtima kuti akhale ndi moyo. Akutero Ambuye Yehova.
24 Ale jeźliby się odwrócił sprawiedliwy od sprawiedliwości swojej, a czyniłby nieprawość, czyniąc według wszystkich obrzydliwości, które czyni niezbożny, izali taki żyć będzie? Wszystkie sprawiedliwości jego, które czynił, nie będą wspominane; dla przestępstwa swego, które popełniał, i dla grzechu swego, którego się dopuścił, dla tych rzeczy umrze.
“‘Koma ngati munthu wolungama apatuka kusiya zachilungamo ndi kuyamba kuchita tchimo ndi zonyansa za mtundu uliwonse zimene amachita anthu oyipa, kodi munthu wotereyu nʼkukhala ndi moyo? Ayi ndithu, zolungama zake zonse sizidzakumbukiridwa. Iye adzayenera kufa chifukwa cha machimo amene anachita.
25 A iż mówicie: Nie prosta jest droga Pańska; słuchajcież teraz, o domie Izraelski! izali droga moja nie jest prosta? Izali drogi wasze nie są krzywe?
“Komabe inu mukunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Tamvani tsono inu Aisraeli: Kodi zochita zanga ndizo zosalungama? Kodi si zochita zanu zimene ndi zosalungama?
26 Gdyby się odwrócił sprawiedliwy od sprawiedliwości swojej, a czyniąc nieprawość w temby umarł, dla nieprawości swojej, którą czynił, umrze.
Ngati munthu wolungama atembenuka kusiya chilungamo chake ndi kuchita tchimo, iye adzafa chifukwa cha tchimolo.
27 Ale gdyby się odwrócił niezbożny od niezbożności swojej, której się dopuścił, a czyniłby sąd i sprawiedliwość, ten duszę swoję zachowa.
Koma ngati munthu woyipa aleka zoyipa zake zimene anazichita ndi kuyamba kuchita zimene ndi zolungama ndi zolondola, iye adzapulumutsa moyo wake.
28 Bo obaczywszy się odwrócił się od wszystkich występków swoich, których się dopuszczał, pewnie żyć będzie, nie umrze.
Popeza waganizira za zolakwa zonse ankachita ndipo wazileka, iye adzakhala ndi moyo ndithu; sadzafa.
29 A przecie mówi dom Izraelski: Nie prosta jest droga Pańska; izali drogi moje nie są proste, o domie Izraelski? Izali nie raczej drogi wasze są krzywe?
Komabe Aisraeli akunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Kodi zochita zanga ndizo zopanda chilungamo, inu Aisraeli? Kodi si zochita zanu zimene ndi zopanda chilungamo?
30 A przetoż każdego z was według dróg jego sądzić będę, o domie Izraelski! mówi panujący Pan. Nawróćcież się, a odwróćcie się od wszystkich występków waszych, aby wam nieprawość nie była na obrażenie.
“Chifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: inu Aisraeli, Ine ndidzakuweruzani aliyense wa inu molingana ndi ntchito zake. Lapani! Lekani zoyipa zanu kuti musawonongeke nazo.
31 Odrzućcie od siebie wszystkie przestępstwa wasze, którycheście się dopuszczali, a uczyńcie sobie serce nowe i ducha nowego. I przeczże macie umrzeć, o domie Izraelski?
Tayani zolakwa zanu zonse zimene munandichimwira nazo ndipo khalani ndi mtima watsopano ndi mzimu watsopano. Kodi muferanji inu Aisraeli?
32 Albowiem się Ja nie kocham w śmierci umierającego, mówi panujący Pan; nawróćcież się tedy, a żyć będziecie.
Ine sindikondwera ndi imfa ya munthu aliyense, akutero Ambuye Yehova. Chifukwa chake, lapani kuti mukhale ndi moyo.”

< Ezechiela 18 >