< Ezechiela 17 >

1 Stało się zaś słowo Pańskie do mnie, mówiąc:
Yehova anayankhula nane kuti,
2 Synu człowieczy! zadaj zagadkę, a mów w podobieństwie o domu Izraelskim,
“Iwe mwana wa munthu, aphere mwambi anthu a Israeli ndi kuwawuza fanizo.
3 I rzecz: Tak mówi panujący Pan: Orzeł wielki z wielkiemi skrzydłami i z długiemi pióry, pełen pierza pstrego, przyleciał na Liban, i wziął wierzch cedru.
Uwawuze kuti Ambuye Yehova akuti, chiwombankhanga chachikulu, cha mapiko amphamvu, nthenga zitalizitali zamathothomathotho chinabwera ku Lebanoni. Chinagwira nthambi ya pamwamba pa mtengo wa mkungudza.
4 Wierzch młodocianych latorośli jego ułamał, i zaniósł go do ziemi kupieckiej, a w mieście kupieckiem położył go.
Chinabudula msonga yeniyeni ya nthambiyo nʼkupita nayo ku dziko lamalonda ndipo anakayika mu mzinda wa anthu amalonda.
5 Wziął też nasienia onej ziemi, a wsadził je na polu urodzajnem, a wsadził je bardzo ostrożnie przy wodach wielkich;
“‘Kenaka chinatenga mbewu ina ya mʼdziko ndi kukayidzala ku malo a chonde kumene kunali madzi ambiri. Anayidzala ngati mmene amadzalira mtengo wa msondozi.
6 Które weszłoby było, i byłoby winną macicą bujną, choć niskiego wzrostu; i byłyby latorośli jej ku niemu, a korzenie jej byłyby mu poddane. A tak byłoby było macicą winną, któraby była wydała latorośli, i wypuściła gałązki.
Ndipo inaphuka nisanduka mtengo wa mpesa wotambalala chamʼmunsi. Nthambi zake zinaloza mmwamba kumene kunali chiwombankhangacho, koma mizu yake inalowa pansi. Kotero unakhala mtengo wamphesa ndipo unasanduka wa nthambi ndiponso wa masamba ambiri.
7 Ale był orzeł jeden wielki z wielkiemi skrzydłami i z gęstem pierzem, a oto ona winna macica przypoiła korzenie swoje ku niemu, i gałązki swe rozciągnęła do niego, aby ją odwilżał z brózd sadu swego.
“‘Koma panali chiwombankhanga chinanso chachikulu, cha mapiko amphamvu ndi cha nthenga zambiri. Tsopano mtengo wamphesa uja unakhotetsera mizu yake kwa chiwombankhangacho kuchokera pa malo amene unadzalidwa ndipo unatambalitsa nthambi zake kwa chiwombankhangacho kufuna kuthiridwa madzi.
8 Choć na polu dobrem przy wodach wielkich wsadzona była, aby wypuściła latorośli, i przyniosła owoce, i była macicą winną wspaniałą.
Koma mtengowo unadzalidwa kale pa nthaka yabwino mʼmbali mwa madzi kuti ukhale ndi nthambi zambiri, ubereke zipatso ndi kukhala wokongola.’
9 Rzeczże tedy: Tak mówi panujący Pan: Izali się jej poszczęści? Izali orzeł korzenia jej nie wyrwie, i owocu jej nie oberwie, i nie posuszy? Izali wszystkich latorośli wyrosłych z niej nie ususzy? Izali z wielką mocą a z obfitym ludem jej nie wygładzi z korzenia jej?
“Ukawawuze Aisraeli kuti, ‘Ambuye Wamphamvuzonse akuti: Kodi udzakula bwino? Kodi chiwombankhanga chija sichidzawuzula mizu ndi kubudula nthambi zake kuti ufote? Masamba ake onse anthete adzafota. Sipadzafunika dzanja lamphamvu kapena anthu ambiri kuti awuzule.
10 Oto jakożkolwiek wsadzona jest, izali się jej poszczęści? Izali do szczętu nie uschnie, skoro się jej dotknie wiatr wschodni? Izali przy brózdach, przy którch się przyjęła, nie uschnie?
Ngakhale utawokedwa pena, kodi udzaphuka? Kodi sudzafoteratu mphepo ya kummawa ikadzawomba, kufotera pa malo pamene anawuwokerapo?’”
11 Zatem stało się słowo Pańskie do mnie, mówiąc:
Kenaka Yehova anandiyankhula nati:
12 Mów teraz do domu odpornego: Azaż nie wiecie, co to jest? Zatem mów: Oto przyciągnął król Babiloński do Jeruzalemu, i zabrał króla jego, i książąt jego, i zawiódł ich z sobą do Babilonu.
“Tawafunsa anthu owukirawa kuti, ‘kodi mukudziwa tanthauzo la zinthu zimenezi?’ Uwafotokozere kuti, ‘Mfumu ya Babuloni inapita ku Yerusalemu ndikukatengako mfumu ndi anthu ake otchuka ndi kubwera nawo ku Babuloni.
13 Wziął też z nasienia królewskiego, a uczyniwszy z nim przymierze, zawiązał go przysięgą, i mocnych z onej ziemi zabrał,
Ndipo anatenga mmodzi wa banja laufumu ndi kuchita naye mgwirizano, ndipo anamulumbiritsa kuti akhale womvera. Inatenganso akulu onse a mʼdzikomo
14 Aby było królestwo zniżone, przeto, żeby się nie wyniosło, żeby tak strzegąc przymierza jego, stało.
kuti ufumu wa dzikolo utsitsidwe, usadzaphukenso, koma kuti ukhalepobe posunga pangano limene unachita.
15 Ale mu się sprzeciwił, posławszy posłów swych do Egiptu, aby mu dał koni i wiele ludu. Izali się to poszczęści? Izali pomsty ujdzie ten, co tak uczynił? Ten, który wzrusza przymierze, izali pomsty ujdzie?
Koma mfumu inawukira mfumu ya ku Babuloni potumiza nthumwi ku dziko la Igupto kukatenga akavalo ndi gulu lalikulu la nkhondo. Kodi mfumu yotereyi ingapambane? Kodi wochita zinthu zoterezi angapulumuke? Kodi angaphwanye mgwirizano ndi kupulumuka?
16 Jako żyję Ja, mówi panujący Pan, że na miejscu króla tego, który go królem uczynił, którego przysięgą wzgardził, a którego przymierze wzruszył, u niego w Babilonie umrze.
“‘Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, mfumuyo idzafera ku Babuloni, mʼdziko la mfumu imene inayika pa mpando waufumu. Inapeputsa lumbiro lake nʼkuphwanya pangano limene inachita ndi mfumu inayo.
17 Ani mu Farao z wielkim wojskiem i z ludem gęstym co pomoże na wojnie, gdy usypie wał, i porobi szańce, aby wykorzenił mnóstwo ludu,
Farao ndi gulu lake lankhondo lamphamvu sadzatha kumuthandiza pa nkhondo, pamene mfumu ya Babuloni idzapanga mitumbira ya nkhondo ndi nsanja za nkhondo kuti iwononge miyoyo yambiri.
18 Ponieważ pogardził przysięgą, zrzuciwszy przymierze; bo oto dał na to rękę swą, a przecie to wszystko uczyni; nie ujdzie pomsty.
Mfumu ya ku Yuda inanyoza lumbiro lake pophwanya pangano. Inalonjeza komabe sinatsatire malonjezo ake. Choncho sidzapulumuka.
19 Dlatego tak mówi panujący Pan: Jako żyję Ja, że przysięgę swoję, którą wzgardził, i przymierze moje, które wzruszył, pewnie obrócę na głowę jego.
“‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndithu pali Ine wamoyo, Ine ndidzalanga mfumu imeneyi chifukwa inanyoza lumbiro langa, ndi kuphwanya pangano langa.
20 Bo rozciągnę nań sieć moję, a będzie niewodem moim pojmany, i zawiodę go do Babilonu, a tam się z nim rozsądzę o występek jego, którym wystąpił przeciwko mnie.
Ndidzayitchera ukonde ndipo idzakodwa mu msampha wanga. Ndidzapita nayo ku Babuloni ndi kuyilanga kumeneko chifukwa inali yosakhulupirika kwa Ine.
21 A wszyscy też, którzy uciekli od niego ze wszystkiemi hufami jego, od miecza polegną, a pozostali na wszystkie strony rozproszeni będą, a dowiecie się, że Ja Pan mówiłem to.
Asilikali ake onse amene akuthawa adzaphedwa ndi lupanga, ndipo opulumuka adzabalalitsidwa ku mbali zonse. Ndipo iwo adzadziwa kuti Ine Yehova ndayankhula.
22 Tak mówi panujący Pan: Wszakże wezmę z wierzchu tego wysokiego cedru, i wsadzę; z wierzchu młodocianych latorośli jego młodą latorostkę ułamię, a wszczepię ją na górze wysokiej i wyniosłej;
“‘Ambuye Yehova akuti: Ine mwini ndidzatenga nthambi pamwamba penipeni pa mkungudza ndi kuyidzala; ndidzathyola nthambi yanthete kuchokera pa nthambi zapamwamba penipeni ndi kuyidzala pamwamba pa phiri lalitali.
23 Na wysokiej górze Izraelskiej wszczepię ją, i wypuści gałązki, i wyda owoc, i będzie cedrem zacnym; i będzie pod nim mieszkać wszelkie ptastwo, i wszystko, co ma skrzydła, pod cieniem gałęzia jego mieszkać będzie.
Ndidzayidzaladi pa phiri lalitali la Israeli. Idzaphuka nthambi ndi kubereka zipatso. Choncho idzasanduka mkungudza wamphamvu. Mbalame za mtundu uliwonse zidzamanga zisa zawo mʼmenemo; zidzapeza malo okhala mu mthunzi wa nthambi zake.
24 A tak poznają wszystkie drzewa polne, żem Ja Pan poniżył drzewo wysokie, a wywyższyłem drzewo niskie, ususzyłem drzewo zielone, a uczyniłem, że zakwitło drzewo suche. Ja Pan rzekłem to, i uczynię.
Mitengo yonse yakuthengo idzadziwa kuti Ine ndine Yehova amene ndimafupikitsa mitengo yayitali ndi kutalikitsa mitengo yayifupi. Ndimawumitsa mitengo yabiriwiri ndi kubiriwitsa mitengo yowuma. “‘Ine Yehova ndayankhula zimenezi, ndipo ndidzazichita.’”

< Ezechiela 17 >