< اعمال رسولان 13 >
در کلیسای انطاکیهٔ سوریه، تعدادی نبی و معلم وجود داشت که عبارت بودند از: برنابا، شمعون که به او «سیاه» نیز میگفتند، لوکیوس اهل قیروان، منائن که برادرخواندۀ هیرودیس پادشاه بود، و سولس. | 1 |
Mu mpingo wa ku Antiokeya munali aneneri ndi aphunzitsi awa: Barnaba, Simeoni, Lukia wa ku Kurene, Manayeni (amene analeredwa pamodzi ndi mfumu Herode), ndiponso Saulo.
یک روز، وقتی این اشخاص روزه گرفته بودند و خدا را عبادت میکردند، روحالقدس به ایشان فرمود: «برنابا و سولس را برای من جدا کنید تا به خدمت مخصوصی که ایشان را بدان فرا خواندهام، مشغول شوند.» | 2 |
Iwo pamene ankapembedza Ambuye ndi kusala kudya, Mzimu Woyera anati, “Mundipatulire Barnaba ndi Saulo kuti akagwire ntchito imene ndinawayitanira.”
پس به روزه و دعا ادامه داده، دستها بر سر آن دو گذاشتند و آنان را روانه ساختند. | 3 |
Ndipo atasala kudya ndi kupemphera anasanjika manja awo pa iwo nawatumiza.
برنابا و پولس با هدایت روحالقدس سفر خود را آغاز کردند. نخست به بندر سُلوکیه رفتند و از آنجا با کشتی عازم جزیرهٔ قبرس شدند. | 4 |
Barnaba ndi Saulo motumidwa ndi Mzimu Woyera, anapita ku Selukeya ndipo kuchokera kumeneko anakwera sitima ya pamadzi kupita ku Kupro.
در قبرس به شهر سَلامیس رفتند و در کنیسهٔ یهودیان کلام خدا را موعظه کردند. یوحنا معروف به مرقس نیز بهعنوان دستیار، آنها را همراهی میکرد. | 5 |
Pamene anafika ku Salamisi, analalikira Mawu a Mulungu mʼMasunagoge a Ayuda. Iwo anali ndi Yohane monga wowatumikira.
در آن جزیره، شهر به شهر گشتند و پیغام خدا را به مردم رساندند، تا اینکه به شهر پافُس رسیدند. در آنجا به یک جادوگر یهودی برخوردند به نام باریشوع که ادعای پیغمبری میکرد. | 6 |
Iwo anayenda pa chilumba chonse mpaka anafika ku Pafo, kumeneko anapezanako ndi Myuda, wamatsenga amene analinso mneneri wonama dzina lake Barayesu.
وی با «سرجیوس پولس» که فرماندار رومی قبرس و شخصی فرهیخته و دانا بود، طرح دوستی ریخته بود. فرماندار برنابا و سولس را به حضور خود فراخواند، چون میخواست پیغام خدا را از زبان آنان بشنود. | 7 |
Iyeyu, amathandiza mkulu wa boma, Sergio Paulo. Mkulu wa bomayu, munthu wanzeru, anayitana Barnaba ndi Saulo chifukwa anafuna kumva Mawu a Mulungu.
ولی عِلیما، همان جادوگر (زیرا معنی نامش همین است)، مزاحم میشد و نمیگذاشت فرماندار به پیغام برنابا و پولس گوش دهد و سعی میکرد نگذارد به خداوند ایمان بیاورد. | 8 |
Koma Elima wamatsengayo, (Elima tanthauzo lake ndi wamatsenga), anatsutsana nawo ndipo anafuna kumuletsa mkulu wa bomayo kuti asakhulupirire.
آنگاه سولُس که پولُس نیز خوانده میشد، پُر از روحالقدس شده، مستقیم به چشمان عِلیما نگاه کرد و گفت: | 9 |
Koma Saulo, amenenso amatchedwa Paulo, wodzazidwa ndi Mzimu Woyera anamuyangʼanitsitsa Elima ndipo anati,
«ای فرزند ابلیس، ای حیلهگر بدذات، ای دشمن تمام خوبیها، آیا از مخالفت کردن با خدا دست برنمیداری؟ | 10 |
“Iwe ndiwe mwana wa mdierekezi ndiponso mdani wa chilungamo! Ndiwe wodzaza ndi chinyengo cha mtundu uliwonse ndi kuchenjera konse. Kodi sudzaleka kupotoza njira zolungama za Ambuye?
حال که چنین است، خدا تو را چنان میزند که تا مدتی کور شوی و نور خورشید را نبینی!» در دَم، چشمان عِلیما تیره و تار شد و کورکورانه به این سو و آن سو میرفت و التماس میکرد کسی دست او را بگیرد و راه را به او نشان دهد. | 11 |
Tsopano dzanja la Ambuye likukutsutsa iwe. Udzakhala wosaona ndipo kwa kanthawi sudzatha kuona kuwala kwa dzuwa.” Nthawi yomweyo khungu ndi mdima zinamugwera ndipo anafunafuna munthu woti amugwire dzanja kuti amutsogolere.
وقتی فرماندار این را دید، از قدرت پیام خدا متحیر شد و ایمان آورد. | 12 |
Pamene mkulu wa bomayo anaona zimene zinachitika anakhulupirira pakuti anadabwa ndi chiphunzitso cha Ambuye.
پولس و همراهانش پافُس را ترک کردند و با کشتی عازم ایالت پامْفیلیا شدند و در بندر پِرجه پیاده شدند. در آنجا یوحنا معروف به مرقس از ایشان جدا شد و به اورشلیم بازگشت. | 13 |
Kuchokera ku Pafo, Paulo ndi anzake anayenda pa sitima ya pamadzi kupita ku Perga wa ku Pamfiliya, kumeneko Yohane anawasiya nabwerera ku Yerusalemu.
ولی برنابا و پولس به شهر انطاکیه در ایالت پیسیدیه رفتند. ایشان روز شَبّات برای پرستش خدا به کنیسهٔ یهود وارد شدند. | 14 |
Kuchokera ku Perga anapita ku Pisidiya wa ku Antiokeya. Pa tsiku la Sabata analowa mʼsunagoge, nakhala pansi.
وقتی قرائت تورات و کتب انبیا به پایان رسید، رؤسای کنیسه برایشان پیام فرستاده، گفتند: «برادران، اگر سخن آموزندهای دارید، لطفاً برایمان بیان کنید.» | 15 |
Atawerenga mawu a mʼMalamulo ndi Aneneri, akulu a sunagoge anawatumizira mawu ndi kuti, “Abale ngati muli ndi mawu olimbikitsa nawo anthuwa, nenani.”
پولس از جا برخاست و با دست اشاره کرد تا ساکت باشند و گفت: «ای مردان اسرائیل، و ای غیریهودیانِ خداپرست، به من گوش فرا دهید. | 16 |
Atayimirira, Paulo anakweza dzanja lake ndi kuti, “Inu Aisraeli ndiponso inu a mitundu ina amene mumapembedza Mulungu, tandimverani!
«خدای بنیاسرائیل، اجداد ما را انتخاب کرد و باشکوه و جلال تمام از چنگ مصریها رهایی بخشید و ایشان را سرافراز نمود. | 17 |
Mulungu wa Aisraeli anasankha makolo athu ndipo anawapatsa chuma chambiri pamene amakhala ku Igupto. Anawatulutsa mʼdzikomo ndi dzanja lake lamphamvu.
در آن چهل سالی که در بیابان سرگردان بودند، او آنان را تحمل کرد. | 18 |
Ndipo Iye anapirira khalidwe lawo mʼchipululu kwa zaka makumi anayi.
سپس، هفت قوم ساکن کنعان را از بین برد و سرزمین آنان را به اسرائیل به میراث بخشید. | 19 |
Mulungu anawagonjetsera mitundu isanu ndi iwiri ya ku Kanaani ndipo anapereka dzikolo kwa Israeli kuti likhale lawo.
پس از آن، چهارصد و پنجاه سال، یعنی تا زمان سموئیل نبی، رهبران گوناگون، این قوم را اداره کردند. | 20 |
Izi zonse zinatenga zaka 450. “Zitatha izi, Mulungu anawapatsa oweruza mpaka nthawi ya mneneri Samueli.
«پس از آن، قوم خواستند برای خود پادشاهی داشته باشند؛ و خدا شائول، پسر قیس از قبیلهٔ بنیامین را به ایشان داد که چهل سال بر آنان سلطنت کرد. | 21 |
Kenaka anthu anapempha kuti awapatse mfumu, ndipo anawapatsa Sauli mwana wa Kisi, wa fuko la Benjamini amene analamulira zaka makumi anayi.
ولی خدا او را برکنار نمود و داوود را به جای وی پادشاه ساخت و فرمود: داوود، پسر یَسا، مرد دلخواه من است. او کسی است که هر چه بگویم اطاعت، میکند. | 22 |
Mulungu atamuchotsa Sauli, anayika Davide kukhala mfumu yawo. Mulungu anamuchitira umboni kuti, ‘Ndapeza Davide mwana wa Yese munthu wa pamtima panga; iye adzachita zonse zimene ine ndikufuna kuti iye achite.’
و عیسی، آن نجاتدهندهای که خدا وعدهاش را به اسرائیل داد، از نسل همین داوود پادشاه است. | 23 |
“Kuchokera mwa zidzukulu za munthu ameneyu, Mulungu anawutsa Yesu kukhala Mpulumutsi wa Aisraeli, monga analonjezera.
«ولی پیش از آمدن او، یحیی موعظه میکرد که لازم است تمامی قوم اسرائیل از گناهان خود دست بکشند، به سوی خدا بازگشت نمایند و تعمید بگیرند. | 24 |
Yesu asanabwere, Yohane analalikira kwa anthu onse Aisraeli za kutembenuka mtima ndi ubatizo.
وقتی یحیی دورهٔ خدمت خود را به پایان رساند، به مردم گفت: آیا تصور میکنید که من مسیح هستم؟ نه، من مسیح نیستم. مسیح بهزودی خواهد آمد. من حتی شایسته نیستم که بند کفشهایش را باز کنم. | 25 |
Pamene Yohane amatsiriza ntchito yake anati: ‘Mukuganiza kuti ine ndine yani? Ine sindine ameneyo ayi, koma Iye akubwera pambuyo panga, amene ine sindine woyenera kumasula zingwe za nsapato zake.’
«برادران، خدا این نجات را به همهٔ ما هدیه کرده است. این نجات هم برای شماست که از نسل ابراهیم میباشید، و هم برای شما غیریهودیان که خداپرست هستید. | 26 |
“Abale, ana a Abrahamu, ndiponso inu a mitundu ina amene mumaopa Mulungu, Iye watumiza uthenga wachipulumutsowo kwa ife.
«ولی یهودیانِ شهر اورشلیم، با سران قوم خود عیسی را کشتند، و به این ترتیب پیشگویی پیامبران را تحقق بخشیدند. ایشان او را نپذیرفتند و پی نبردند که او همان کسی است که پیامبران دربارهاش پیشگویی کردهاند، با اینکه هر شَبّات نوشتههای آن پیامبران را میخواندند و میشنیدند. | 27 |
Anthu a ku Yerusalemu ndi atsogoleri awo sanazindikire Yesu, komabe pomuweruza Yesu anakwaniritsa mawu a Aneneri amene amawerengedwa Sabata lililonse.
هر چند عیسی بیگناه بود، ولی به پیلاتُس اصرار کردند که او را بکشد. | 28 |
Ngakhale sanapeze chifukwa choti afe, anapempha Pilato kuti amuphe.
سرانجام وقتی تمام بلاهای پیشگوییشده را بر سر او آوردند، او را از صلیب پایین آورده، در مقبره گذاشتند. | 29 |
Atachita zonse zimene zinalembedwa za Iye, iwo anamuchotsa pa mtengo ndipo anamuyika mʼmanda.
ولی خدا او را زنده کرد! | 30 |
Koma Mulungu anamuukitsa,
و کسانی که همراه او از جلیل به اورشلیم آمده بودند، بارها او را زنده دیدند. ایشان اکنون شاهدان او نزد قوم ما، یعنی قوم اسرائیل هستند. | 31 |
ndipo kwa masiku ambiri anaonekera kwa amene anayenda naye kuchokera ku Galileya mpaka ku Yerusalemu. Iwowa tsopano ndi mboni zake kwa anthu a Israeli.
«من و برنابا برای همین به اینجا آمدهایم تا این خبر خوش را به شما نیز برسانیم. این وعده به اجداد ما داده شد | 32 |
“Ife tikukuwuzani Uthenga Wabwino; umene Mulungu analonjeza makolo athu.
و خدا آن را با زنده کردن عیسی، برای ما که فرزندان ایشانیم، وفا کرد. این است آنچه در مزمور دوم دربارۀ عیسی نوشته شده است: «”تو پسر من هستی! امروز من پدر تو شدهام.“ | 33 |
Iye wakwaniritsa zimenezi kwa ife ana awo, poukitsa Yesu kuchokera kwa akufa. Monga zinalembedwa mu Salimo lachiwiri kuti, “Iwe ndiwe mwana wanga; lero ine ndakhala Atate ako.”
«زیرا خدا وعده داده بود که او را از مردگان برخیزاند تا در قبر نپوسد، چنانکه در کتب مقدّس آمده:”آن برکات مقدّسی را که به داوود وعده دادم، برای تو انجام خواهم داد.“ | 34 |
Zakuti Mulungu anamuukitsa kuti asawole konse, zinanenedwa mʼmawu awa: “‘Ine, ndidzakupatsa madalitso opatulika ndi odalirika amene ndinalonjeza Davide.’
مزمور دیگری به طور مفصل شرح میدهد که:”تو نخواهی گذاشت قُدّوسِ تو در قبر بپوسد.“ | 35 |
Nʼchifukwa chakenso zinalembedwa mu Salimo lina kuti, “‘Simudzalekerera woyera wanu kuti awole.’
این آیه اشاره به داوود نیست چون داوود، در زمان خود مطابق میل خدا خدمت کرد و بعد مرد، دفن شد و بدنش نیز پوسید. | 36 |
“Pakuti pamene Davide anatsiriza kutumikira Mulungu mu mʼbado wake, anamwalira, iye anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake ndipo thupi lake linawola.
پس این اشاره به شخص دیگری است، یعنی به کسی است که خدا او را دوباره زنده کرد و بدنش از مرگ ضرر و زیانی ندید. | 37 |
Koma amene Mulungu anamuukitsa kwa akufa sanawole ayi.
«برادران، توجه کنید! در این مرد، یعنی عیسی برای گناهان شما امید آمرزش هست. | 38 |
“Nʼchifukwa chake, abale anga, dziwani kuti mwa Yesu chikhululukiro cha machimo chikulalikidwa.
هر که به او ایمان آورد، از قید تمام گناهانش آزاد خواهد شد و خدا او را خوب و شایسته به حساب خواهد آورد؛ و این کاری است که شریعت موسی هرگز نمیتواند برای ما انجام دهد. | 39 |
Kudzera mwa Iye aliyense amene akhulupirira, alungamitsidwa kuchoka ku tchimo lililonse limene silingachoke ndi Malamulo a Mose.
پس مواظب باشید مبادا گفتههای پیامبران شامل حال شما نیز بشود که میگویند: | 40 |
Samalani kuti zimene aneneri akunena zisakuchitikireni inu:
شما که حقیقت را خوار میشمارید، ببینید و تعجب کنید و نابود شوید! زیرا در روزگار شما کاری میکنم که حتی وقتی خبرش را به شما دهند، باور نکنید!» | 41 |
“‘Onani, inu anthu onyoza, dabwani ndipo wonongekani, chifukwa ine ndidzachita china chake mʼmasiku anu, inu simudzazikhulupirira ngakhale wina atakufotokozerani!’”
آن روز وقتی پولس و برنابا کنیسه را ترک میگفتند، مردم از ایشان خواهش کردند که هفتهٔ بعد نیز دربارۀ این امور برای ایشان صحبت کنند. | 42 |
Pamene Paulo ndi Barnaba amatuluka mʼSunagoge, anthu anawapempha kuti adzapitirize kuyankhula zinthu zimenezi Sabata linalo.
وقتی جماعت مرخص شدند، بسیاری از یهودیان و غیریهودیان خداپرست به دنبال پولس و برنابا رفتند. این دو با ایشان سخن گفتند و ترغیبشان کردند تا در فیض خدا ثابتقدم بمانند. | 43 |
Atatha mapemphero, Ayuda ambiri ndi anthu odzipereka otembenukira ku Chiyuda anatsatira Paulo ndi Barnaba, iwo anayankhula ndi anthuwo ndipo anawapempha kuti apitirire mʼchisomo cha Mulungu.
هفتهٔ بعد تقریباً همهٔ مردم شهر آمدند تا کلام خدا را از زبان آنان بشنوند. | 44 |
Pa Sabata linalo pafupifupi anthu onse a mu mzindawo anasonkhana kudzamva Mawu a Ambuye.
اما وقتی سران یهود دیدند که مردم اینچنین از پیغام رسولان استقبال میکنند، از روی حسادت از آنان بدگویی کردند و هر چه پولس میگفت، ضد آن را میگفتند. | 45 |
Pamene Ayuda anaona gulu la anthu, anachita nsanje ndipo anayankhula zamwano kutsutsana ndi zimene Paulo amanena.
آنگاه پولس و برنابا با دلیری گفتند: «لازم بود که پیغام خدا را اول به شما یهودیان برسانیم. ولی حالا که شما آن را رد کردید، آن را به غیریهودیان اعلام خواهیم کرد، چون شما نشان دادید که لایق حیات جاودانی نیستید. (aiōnios ) | 46 |
Ndipo Paulo ndi Barnaba anawayankha molimba mtima kuti, “Ife tinayenera kuyankhula Mawu a Mulungu kwa inu poyamba. Popeza inu mwawakana ndi kudziyesa nokha osayenera moyo wosatha, ife tsopano tikupita kwa anthu a mitundu ina. (aiōnios )
و این درست همان دستوری است که خداوند به ما داد و فرمود:”تو را برای قومهای جهان نور ساختم تا نجات را به کرانهای زمین برسانی.“» | 47 |
Pakuti izi ndi zimene Ambuye anatilamula ife: “‘Ine ndakuyika iwe ukhale kuwunika kwa anthu a mitundu ina, kuti ukafikitse chipulumutso ku malekezero a dziko lapansi!’”
وقتی غیریهودیان این را شنیدند، بسیار شاد شدند و خداوند را برای پیامش سپاس گفتند، و آنان که برای حیات جاودانی تعیین شده بودند، ایمان آوردند. (aiōnios ) | 48 |
Anthu a mitundu ina atamva izi, anakondwa ndipo analemekeza Mawu Ambuye; ndipo onse amene anawasankha kuti alandire moyo osatha anakhulupirira. (aiōnios )
به این ترتیب، پیام خدا به تمام آن ناحیه رسید. | 49 |
Mawu a Ambuye anafalikira mʼchigawo chonse.
آنگاه سران قوم یهود، زنان دیندار و متشخص و بزرگان شهر را بر ضد پولس و برنابا تحریک کردند، و بههمراه جمعی از مردم بر سر ایشان ریختند و آنان را از آنجا راندند. | 50 |
Koma Ayuda anawutsa mitima ya akazi otchuka opembedza Mulungu ndi akulu a mu mzindamo. Iwo anabweretsa mazunzo kwa Paulo ndi Barnaba ndipo anawathamangitsa mʼchigawo chawo.
پولس و برنابا نیز در مقابل این عمل، گرد و خاک آن شهر را از پاهای خود تکاندند و از آنجا به شهر قونیه رفتند. | 51 |
Tsono iwo anasasa fumbi la ku mapazi awo powatsutsa, ndipo anapita ku Ikoniya.
اما کسانی که در اثر پیغام آنان ایمان آوردند، سرشار از شادی و روحالقدس شدند. | 52 |
Ndipo ophunzira anadzazidwa ndi chimwemwe ndiponso ndi Mzimu Woyera.