< اعمال رسولان 12 >
در همین زمانها بود که هیرودیس پادشاه به آزار و شکنجهٔ عدهای از پیروان مسیح پرداخت. | 1 |
Inali nthawi yomweyi imene mfumu Herode anamanga ena a mu mpingo ndi cholinga chakuti awazunze.
به دستور او یعقوب برادر یوحنا با شمشیر کشته شد. | 2 |
Iye analamula kuti Yakobo mʼbale wa Yohane, aphedwe ndi lupanga.
وقتی هیرودیس دید که این کارش موجب خرسندی سران یهود شده، پطرس را نیز در ایام عید پِسَح یهود دستگیر کرد، | 3 |
Ataona kuti zimenezi zinakondweretsa Ayuda, anawonjeza ndi kugwiranso Petro. Izi zinachitika pa nthawi ya Chikondwerero cha Buledi wopanda Yisiti.
و او را به زندان انداخت و دستور داد شانزده سرباز، زندان او را نگهبانی کنند. هیرودیس قصد داشت بعد از عید پِسَح، پطرس را بیرون آورد تا در ملاء عام محاکمه شود. | 4 |
Atamugwira Petro, namutsekera mʼndende, anamupereka kwa magulu anayi a asilikali kuti amuyangʼanire, gulu lililonse linali ndi asilikali anayi. Herode anafuna kumuzenga mlandu pamaso pa anthu onse chikondwerero cha Paska chitapita.
ولی در تمام مدتی که پطرس در زندان بود، کلیسا با جدیّتِ تمام برای او دعا میکردند. | 5 |
Kotero Petro anasungidwa mʼndende, koma mpingo unamupempherera kolimba kwa Mulungu.
شبِ قبل از روزی که قرار بود پطرس توسط هیرودیس محاکمه شود، او به دو زنجیر بسته و بین دو سرباز خوابیده بود. سربازان دیگر نیز کنار در زندان کشیک میدادند. | 6 |
Usiku woti mmawa mwake Herode amuzenga mlandu, Petro amagona pakati pa asilikali awiri, atamangidwa maunyolo awiri, ndiponso alonda atayima pa khomo.
ناگهان محیط زندان نورانی شد و فرشتهٔ خداوند آمد و کنار پطرس ایستاد! سپس به پهلوی پطرس زد و او را بیدار کرد و گفت: «زود برخیز!» همان لحظه زنجیرها از مچ دستهایش باز شد و بر زمین فرو ریخت! | 7 |
Mwadzidzidzi mngelo wa Ambuye anaonekera ndipo kuwala kunawunika mʼchipindamo. Mngeloyo anamugwedeza Petro mʼnthiti ndi kumudzutsa. Iye anati, “Fulumira, imirira!” Ndipo maunyolo anagwa kuchoka mʼmanja a Petro.
فرشته به او گفت: «لباسها و کفشهایت را بپوش.» پطرس نیز پوشید. آنگاه فرشته به او گفت: «ردایت را بر دوش خود بینداز و به دنبال من بیا!» | 8 |
Kenaka mngelo anati kwa iye, “Vala zovala ndi nsapato.” Ndipo Petro atachita izi mngeloyo anamuwuzanso kuti, “Funda chovala chako ndipo unditsate.”
به این ترتیب، پطرس از زندان بیرون آمد و به دنبال فرشته به راه افتاد. ولی در تمام این مدت تصور میکرد که خواب میبیند و باور نمیکرد که بیدار باشد. | 9 |
Petro anatsatira natuluka mʼndende, koma sanazindikire kuti zimene mngeloyo amachita zimachitikadi; iye amaganiza kuti amaona masomphenya.
سپس از نگهبانان اول و دوم گذشتند تا به دروازهٔ آهنی زندان رسیدند که به کوچهای باز میشد. این در نیز خودبهخود باز شد! پس، از آنجا هم رد شدند تا به آخر کوچه رسیدند، و ناگهان فرشته او را ترک کرد. | 10 |
Iwo anadutsa gulu loyamba ndi lachiwiri la asilikali ndipo anafika pa chitseko chachitsulo cholowera mu mzinda. Chitsekocho chinatsekuka chokha ndipo anadutsa. Pamene anayenda kutalika kwa msewu umodzi, mwadzidzidzi mngelo uja anachoka.
پطرس که تازه متوجهٔ ماجرا شده بود، به خود گفت: «پس حقیقت دارد که خداوند فرشتهٔ خود را فرستاده، مرا از چنگ هیرودیس و نقشهای که رهبران یهود برای من کشیده بودند، رهانیده است!» | 11 |
Pamenepo Petro anazindikira nati, “Tsopano ndikudziwa mosakayika kuti Ambuye anatuma mngelo wake kudzandipulumutsa mʼmanja mwa Herode, ndi ku zoyipa zonse zimene Ayuda amafuna kundichitira.”
آنگاه، پس از لحظهای تأمل، به خانهٔ مریم مادر یوحنا معروف به مرقس رفت. در آنجا عدهٔ زیادی برای دعا گرد آمده بودند. | 12 |
Atazindikira zimenezi anapita ku nyumba ya Mariya amayi ake a Yohane, wotchedwanso Marko, kumene kunasonkhana anthu ambiri ndipo amapemphera.
پطرس در زد و خادمهای به نام رُدا آمد تا در را باز کند. | 13 |
Petro anagogoda pa chitseko cha panja, ndipo mtsikana wantchito dzina lake Roda anabwera kuti adzatsekule chitseko.
وقتی صدای پطرس را شنید، از فرط شادی، بدون اینکه در را باز کند، برگشت تا به همه مژده دهد که پطرس در میزند. | 14 |
Atazindikira mawu a Petro anakondwa kwambiri ndipo anabwerera osatsekula ndipo anafuwula kuti, “Petro ali pa khomopa!”
ولی آنان حرف او را باور نکردند و گفتند: «مگر دیوانه شدهای؟» اما وقتی دیدند اصرار میکند، گفتند: «لابد فرشتۀ اوست.» | 15 |
Anthuwo anati kwa iye, “Wopenga iwe!” Atalimbikira kunena kuti zinali zoona, iwo anati, “Ameneyo ndi mngelo wake.”
ولی پطرس بیوقفه در میزد. سرانجام رفتند و در را باز کردند. وقتی دیدند خود پطرس است، مات و مبهوت ماندند. | 16 |
Koma Petro anapitiriza kugogoda ndipo atatsekula chitseko ndi kumuona, anthuwo anadabwa kwambiri.
پطرس اشاره کرد که آرام باشند و تعریف کرد که چه اتفاقی افتاده و چطور خداوند او را از زندان بیرون آورده است. پیش از رفتن نیز از ایشان خواست تا یعقوب و سایر برادران را آگاه سازند. بعد به جای امنتری رفت. | 17 |
Petro anakweza dzanja ndi kuwawuza kuti akhale chete ndipo anawafotokozera mmene Ambuye anamutulutsira mʼndende. Iye anati, “Uzani Yakobo ndi abale ena za zimenezi.” Kenaka anachoka napita kumalo ena.
صبح در زندان غوغایی بپا شد. همه پطرس را جستجو میکردند. | 18 |
Pamene kunacha kunali phokoso lalikulu pakati pa asilikali, iwo anafunsa kuti, “Kodi chamuchitikira Petro ndi chiyani?”
وقتی هیرودیس به دنبال او فرستاد و آگاه شد که در زندان نیست، هر شانزده نگهبان را بازداشت کرده، حکم اعدامشان را صادر کرد. آنگاه یهودیه را ترک کرده، به قیصریه رفت و مدتی در آنجا ماند. | 19 |
Herode atamufunafuna ndipo wosamupeza, anawafunsa asilikali ndipo analamulira kuti asilikaliwo aphedwe. Kenaka Herode anachoka ku Yudeya ndi kupita ku Kaisareya ndipo anakhala kumeneko kwa kanthawi
وقتی هیرودیس در قیصریه بود، گروهی از نمایندگان شهرهای صور و صیدون به دیدن او آمدند. هیرودیس نسبت به اهالی این دو شهر خصومت عمیقی داشت. پس ایشان حمایت بلاستوس وزیر دربار او را به دست آوردند و از هیرودیس تقاضای صلح کردند، زیرا اقتصاد شهرهای آنان به داد و ستد با سرزمین او بستگی داشت. | 20 |
Herode anakwiyira anthu a ku Turo ndi Sidoni; anthuwo anagwirizana zoti akambirane naye. Atapeza thandizo kuchokera kwa Blasito, wantchito wokhulupirika wa mfumu, anapempha kuti pakhale mtendere, chifukwa dziko lawo limadalira dziko la mfumuyo pa chakudya chawo.
در روز مقرر، هیرودیس لباس شاهانهای پوشید و بر تخت سلطنت نشست و نطقی ایراد کرد. | 21 |
Pa tsiku limene anasankha Herode, atavala zovala zake zaufumu, anakhala pa mpando wake ndipo anayankhula kwa anthuwo.
مردم فریاد برآوردند: «این صدای خداست، نه صدای انسان!» | 22 |
Anthuwo anafuwula nati, “Amenewa ndi mawu a mulungu osati a munthu ayi.”
همان لحظه فرشتهٔ خداوند هیرودیس را چنان زد که بدنش پر از کرم شد و مرد، زیرا به جای اینکه خدا را تمجید کند، گذاشت مردم او را پرستش کنند. | 23 |
Nthawi yomweyo mngelo wa Mulungu anamukantha chifukwa sanapereke ulemu kwa Mulungu ndipo anadyedwa ndi mphutsi nafa.
اما پیغام خدا به سرعت به همه میرسید و تعداد ایمانداران روزبهروز بیشتر میشد. | 24 |
Koma Mawu a Mulungu anapitirirabe kufalikirafalikira.
برنابا و سولس نیز به اورشلیم رفتند و هدایای مسیحیان را به کلیسا دادند و بعد به شهر انطاکیه بازگشتند. در این سفر یوحنا معروف به مرقس را نیز با خود بردند. | 25 |
Barnaba ndi Saulo atamaliza ntchito yawo anachoka ku Yerusalemu, atatenga Yohane wotchedwanso Marko.