< Maluko 7 >

1 Kangi Vafalisayu vangi na Vawula va Malagizu vevahumili ku Yelusalemu valundumini palongolo ya Yesu.
Afarisi ndi ena mwa aphunzitsi amalamulo omwe anachokera ku Yerusalemu anasonkhana momuzungulira Yesu ndipo
2 Vavaweni vawuliwa vangi va Yesu vilya chakulya kwa mawoko changasamba ngati cheyiganikiwa na malagizu.
iwo anaona ophunzira ake akudya chakudya ndi mʼmanja mwakuda kapena kuti mʼmanja mosasamba.
3 Muni Vafalisayu na Vayawudi vangi vayovalili kulanda mivelu ya vagogo wavi, muni valyayi lepi changasamba mawoko bwina.
(Afarisi ndi Ayuda onse sadya pokhapokha atasamba mʼmanja, kusunga mwambo wa makolo awo.
4 Kavili vakagula chakulya kuhuma pandu pakugulisila vindu, vilya lepi mbaka vasanja hoti. Mewa vavi na mivelu yingi ya namuna ya kusanja vikombi na viviga na vyombo ya shaba.
Akabwera kuchokera ku msika samadya pokhapokha atasamba. Ndipo amasunga miyambo ina yambiri monga, kutsuka zikho, mitsuko ndi maketulo).
5 Hinu, Vafalisayu na Vawula va Malagizu vangi vakamkota Yesu, “Ndava kyani vawuliwa vaku vilanda lepi mambu ga kadeni kuhuma kwa vagogo vitu, ndava vilya changasamba mawoko?”
Choncho Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo anafunsa Yesu kuti, “Nʼchifukwa chiyani ophunzira anu satsatira mwambo wa makolo, mʼmalo mwake amangodya chakudya ndi mʼmanja mwakuda?”
6 Yesu akavayangula, “Vandu mwavahomela! Isaya mweavi Mlota wa Chapanga, alotili chakaka kuvavala nyenye peayandiki, ‘Chapanga ijova, vandu venava vakunitopesa kwa malovi ndu, nambu mitima yavi yivii kutali na nene.
Iye anayankha kuti, “Yesaya ananena zoona pamene ananenera za inu achiphamaso; monga kunalembedwa kuti: “Anthu awa amandilemekeza Ine ndi milomo yawo, koma mitima yawo ili kutali ndi Ine.
7 Kunigundamila kwavi chindu lepi, muni mambu geviwula ndi malagizu ga vandu ndu. Ngati malagizu ga Chapanga.’”
Amandilambira Ine kwachabe; ndi kuphunzitsa malamulo ndi malangizo a anthu.
8 “Nyenye mulekili mihilu ya Chapanga na kukamulila mawuliwu ga vandu.”
Mwasiya malamulo a Mulungu ndipo mwagwiritsitsa miyambo ya anthu.”
9 Yesu akayendelela kujova, “Nyenye mumanyili kuyepa cha kuchenjela mihilu ya Chapanga na kulanda mivelu yinu!
Ndipo anawawuzanso kuti, “Inu muli ndi njira yabwino yokankhira kumbali malamulo a Mulungu kuti mukatsatire miyambo yanuyo!
10 Muni Musa alagizi, ‘Muvatopesa dadi waku na nyina waku,’ Na, ‘Mweakumliga dadi waki amala nyina waki, yikumugana akomiwa.’
Pakuti Mose anati, ‘Lemekeza abambo ako ndi amayi ako,’ ndipo, ‘aliyense amene atemberera abambo ake kapena amayi ake ayenera kuphedwa.’
11 Nambu nyenye muwula, ngati mundu avi na chindu chakumtangatila dadi waki amala nyina waki, nambu akajova, chindu chenicho ndi ‘Kolibani,’ Mana yaki njombi kwa Chapanga,
Koma inu mumati, ngati munthu anena kwa abambo ake kapena amayi ake kuti, ‘Thandizo lililonse mukanayenera kulandira kuchokera kwa ine ndi Korobani’ (kutanthauza kuti, mphatso yoperekedwa kwa Mulungu),
12 hinu yikumugana lepi kumtangatila dadi waki amala nyina waki.
pamenepo inu simumalola kuti achitire kanthu kalikonse abambo kapena amayi ake.
13 Chenichi ndi chemukulivevesa Lilovi la Chapanga ndava ya mawuliwu ga kuhalilana. Kangi mkita mambu gamahele ngati genago.”
Potero mumachepetsa mawu a Mulungu kukhala wopanda mphamvu ndi miyambo yanu imene mumapatsirana. Ndipo mumachita zinthu zina zambiri monga zimenezi.”
14 Yesu aukemili kangi msambi wa vandu, akavajovela, “Muniyuwanilayi mwavoha na kumanya malovi aga.
Yesu anayitananso gulu la anthu ndipo anati, “Tandimverani nonsenu, ndipo zindikirani izi.
15 Kawaka chakulya cheilya mundu chechihotola kumuhakasa palongolo ya Chapanga. Nambu mambu gegihuma mugati ya mundu ndi gegihotola kumuhakasa.
Palibe kanthu kunja kwa munthu kamene kakalowa mwa iye kangamusandutse wodetsedwa. Koma zimene zituluka mwa munthu ndizo zimupanga kukhala wodetsedwa.”
16 Mweavi na makutu ga kuyuwana na amanyayi!”
(Ngati wina ali ndi makutu akumva amve).
17 Paaulekili msambi wa vandu na kuyingila mu nyumba, vawuliwa vaki vakamkota mana ya luhumu lula.
Atalisiya gulu la anthu ndi kulowa mʼnyumba, ophunzira ake anamufunsa za fanizoli
18 Mwene akavajovela, “Wu, hati nyenye mwimanya lepi? Kawaka chakulya chechikumyingila mundu chihotola lepi, kumuhakasa mundu palongolo ya Chapanga.
Iye anawafunsa kuti, “Kodi nanunso simumvetsetsa? Kodi simukuona kuti palibe kanthu kamene kakalowa mwa munthu kochokera kunja kakhoza kumudetsa?
19 Ndava muni chikumyingila lepi mumtima, nambu mulileme, kangi chihumiswa kundindima.” Ndava ya kujova chenicho Yesu ayidikili vyakulya vyoha viliwayi.
Pakuti sikalowa mu mtima wake koma mʼmimba mwake, ndipo kenaka kamatuluka kunja.” (Ndi mawu amenewa, Yesu anayeretsa zakudya zonse).
20 Yesu akayendelela kujova, “Chechihuma mumtima wa mundu chihotola kumuhakasa palongolo ya Chapanga.
Anapitiriza kuti, “Chimene chichokera mwa munthu ndi chomwe chimamudetsa.
21 Muni mugati ya mumtima wa mundu, gihuma maholo gahakau, ukemi na kuyiva na kukoma,
Pakuti kuchokera mʼkati mwa mitima ya anthu, mumatuluka maganizo oyipa, chiwerewere, kuba, kupha, chigololo,
22 ugoni na unota na udese na uhakau na kuyiva na kunogela vindu vya vangi na luhonda na wihu na ng'omo na uyimu na maligu.
dyera, nkhwidzi, chinyengo, machitidwe onyansa, kaduka, chipongwe, kudzikuza ndi kupusa.
23 Gahakau goha ago gihuma mumtima wa mundu, genago ndi gakumhakasa mundu palongolo ya Chapanga.”
Zoyipa zonsezi zimatuluka mʼkati ndipo zimadetsa munthu.”
24 Yesu awukili penapo akahamba kumuji wa Tilo. Kwenuko ayingili munyumba yimonga, mwene aganili lepi mundu amanyayi kuvya avili mugati, nambu ahotwili lepi kujifiya.
Yesu anachoka kumalo amenewo napita ku madera a Turo. Iye analowa mʼnyumba ndipo sanafune wina kuti adziwe zimenezi; komabe sanathe kudzibisa.
25 Mdala mmonga, msikana waki avili na mzuka, peayuwini malovi ga Yesu, kanyata akabwela akafugama palongolo ya magendelu ga Yesu.
Kunena zoona, amayi amene kamwana kawo kakakazi kanali kogwidwa ndi mzimu woyipa, atangomva za Iye, anabwera nagwada pa mapazi ake.
26 Mdala mwenuyo, avi Mgiliki, ndi mkolonjinji wa muji wa Foinike mulima wa ku Silia. Hinu akamuyupa Yesu amuwusa mzuka msikana waki.
Mayiyu anali Mhelene, wobadwira ku Fonisia wa ku Siriya. Anamupempha Yesu kuti atulutse chiwanda mwa mwana wake.
27 Yesu akavajovela, vana vayukuta hoti, “Chabwina lepi kutola chakulya cha kuvayukutisa vana na kugatagila mabwa.”
Iye anamuwuza kuti, “Choyamba asiye ana adye zimene akuzifuna, pakuti si kwabwino kutenga buledi wa ana ndi kuponyera agalu awo.”
28 Nambu mdala yula akamyangula, “Chakaka, Bambu, hati mabwa gegavi pahi ya meza gilya masigalilu ga chakulya cha vana.”
Mayiyo anayankha kuti, “Inde Ambuye, koma ngakhale agalu amadya zomwe zimagwa pansi kuchokera pa tebulo la ana.”
29 Yesu akamjovela, “Ndava ya lilovi lenilo, wuyayi kunyumba yaku. Mzuka umuwukili msikana waku!”
Ndipo Iye anamuwuza kuti, “Chifukwa cha yankholi, ukhoza kupita; chiwanda chachoka mwa mwana wako wamkazi.”
30 Hinu, akahamba kunyumba yaki, amkolili msikana waki agonili palusongwani, na mzuka wamali kumuwuka.
Atapita kwawo anakapeza mwana wake aligone pa bedi, chiwanda chitatuluka.
31 Kangi Yesu akawuka kumuji wa Tilo, akapitila pagati ya ku Sidoni, akahamba mbaka kunyanja ya Galilaya kuvedukila pamulima wa Dekapoli mana yaki miji kumi.
Ndipo Yesu anachoka ku dera la Turo nadutsa pakati pa Sidoni, kutsikira ku nyanja ya Galileya kupita ku dera la Dekapoli.
32 Ndi vakamletela ngayuwa nambu mewawa avi ngajova kwa Yesu, vakamuyupa amvikilayi mawoko muni amlamisa.
Kumeneko anthu ena anabweretsa kwa Iye munthu amene anali wosamva ndi wosayankhula, ndipo anamupempha kuti asanjike dzanja pa iye.
33 Yesu akamvika pamuhana na msambi wa vandu mundu uyo. Akamsopa ngonji mumakutu. Kangi akahunya mata mulungoji lwaki na kumpamisa mululimi lwa mundu yula.
Atamutengera iye pambali, patali ndi gulu la anthu, Yesu analowetsa zala zake mʼmakutu a munthuyo. Kenaka anapaka malovu pachala ndi kukhudza lilime la munthuyo.
34 Kangi Yesu akalola kunani kwa Chapanga, akakeka kwa likakala, akamjovela, “Efata,” Mana yaki “Dindukayi.”
Iye anayangʼana kumwamba ndipo ndi mawu otsitsa moyo, anati kwa iye, “Efataa!” (Kutanthauza kuti, “Tsekuka!”)
35 Lukumbi lulalula akatumbula kuyuwana bwina, mewawa lulimi lwaki lukajova bwina.
Atachita izi, makutu a munthuyo anatsekuka komanso lilime lake linamasuka ndipo anayamba kuyankhula momveka bwino.
36 Yesu akavalagiza vakotoka kumjovela mundu lijambu lila. Nambu cheayonjokisi kuvabesa, ndi chevadandisi malovi gala.
Yesu anawalamula kuti asawuze wina aliyense. Koma pamene anapitiriza kuwaletsa, iwo anapitiriza kuyankhula za izi.
37 Vandu vakangisi neju, vakajova, “Avakitili goha gabwina hati vangayuwa kuyuwana, na vangajova kujova!”
Anthu anadabwa kwambiri. Iwo anati, “Wachita zonse bwino, ngakhale Iyenso atsekula makutu a osamva ndi osayankhula kuti ayankhule.”

< Maluko 7 >