< UJoshuwa 10 >
1 Kwasekusithi lapho uAdonizedeki inkosi yeJerusalema esezwile ukuthi uJoshuwa uyithumbile iAyi, wayitshabalalisa, njengalokho akwenza eJeriko lenkosini yayo, wenze njalo eAyi lenkosini yayo, lokuthi abahlali beGibeyoni benza ukuthula loIsrayeli, babephakathi kwabo,
Adoni-Zedeki mfumu ya ku Yerusalemu inamva kuti Yoswa wagonjetsa ndi kuwononga kotheratu mzinda wa Ai pamodzi ndi mfumu yake, monga anachitira ndi Yeriko ndi mfumu yake. Inamvanso kuti anthu a ku Gibiyoni anachita pangano la mtendere ndi Israeli ndipo amakhala pakati pawo.
2 besaba kakhulu, ngoba iGibeyoni yayingumuzi omkhulu njengomunye wemizi yenkosi, langoba yayinkulu kuleAyi, lamadoda ayo wonke engamaqhawe.
Choncho iye ndi anthu ake anachita mantha aakulu, chifukwa Gibiyoni unali mzinda waukulu kwambiri, monga mzinda uliwonse wokhala ndi mfumu. Unali waukulu ndipo ankhondo ake anali olimba mtima.
3 Ngakho uAdonizedeki inkosi yeJerusalema yathumela kuHohamu inkosi yeHebroni, lakuPiramu inkosi yeJarimuthi, lakuJafiya inkosi yeLakishi, lakuDebiri inkosi yeEgiloni, esithi:
Chotsatira chake Adoni-Zedeki mfumu ya Yerusalemu inatuma uthenga kwa Hohamu mfumu ya Hebroni, Piramu mfumu ya Yarimuti, Yafiya mfumu ya Lakisi ndi Debri mfumu ya Egiloni.
4 Yenyukelani kimi lingisize, ukuze siyitshaye iGibeyoni; ngoba yenzile ukuthula loJoshuwa labantwana bakoIsrayeli.
Iye anatumiza mawu kuti, “Bwerani mudzandithandize kumenyana ndi Gibiyoni, chifukwa anthu ake achita pangano la mtendere ndi Yoswa ndi Aisraeli.”
5 Ngakho amakhosi amahlanu amaAmori, inkosi yeJerusalema, inkosi yeHebroni, inkosi yeJarimuthi, inkosi yeLakishi, inkosi yeEgiloni, ahlangana enyuka, wona lamabutho awo wonke, amisa inkamba maqondana leGibeyoni, alwa layo.
Mafumu asanu a Aamori aja, mfumu ya Yerusalemu, mfumu ya Hebroni, mfumu ya Yarimuti, mfumu ya Lakisi ndi mfumu ya Egiloni, anagwirizana. Iwo anasonkhanitsa ankhondo awo nazungulira mzinda wa Gibiyoni ndi kuwuthira nkhondo.
6 Amadoda eGibeyoni asethumela kuJoshuwa enkambeni yeGiligali esithi: Isandla sakho singatshiyi izinceku zakho; yenyukela kithi masinyane usisindise usisize, ngoba amakhosi wonke amaAmori ahlala ezintabeni asesihlanganyele.
Koma anthu a ku Gibiyoni anatumiza uthenga kwa Yoswa ku misasa ya ku Giligala nati, “Musawataye anthu anu! Bwerani msanga mudzatipulumutse! Dzatithandizeni chifukwa mafumu a Aamori ochokera ku dziko la ku mapiri agwirizana kuti adzatithire nkhondo.”
7 Ngakho uJoshuwa wenyuka esuka eGiligali, yena labo bonke abantu bempi kanye laye, lawo wonke amaqhawe alamandla.
Choncho Yoswa ananyamuka kuchoka ku Giligala ndi gulu lake la ankhondo pamodzi ndi anthu ake olimba mtima.
8 INkosi yasisithi kuJoshuwa: Ungabesabi, ngoba ngibanikele esandleni sakho; kakulamuntu wabo ozakuma phambi kwakho.
Yehova anati kwa Yoswa, “Usawaope, Ine ndawapereka mʼdzanja lako. Palibe ndi mmodzi mwa amenewa amene adzalimbe.”
9 UJoshuwa wasebajuma, enyuke ubusuku bonke esuka eGiligali.
Atayenda usiku wonse kuchokera ku Giligala, Yoswa anawathira nkhondo mwadzidzidzi.
10 INkosi yabasanganisa phambi kukaIsrayeli, yabatshaya ngokutshaya okukhulu eGibeyoni, yaxotshana labo endleleni enyukela eBhethi-Horoni, yabatshaya kwaze kwaba seAseka kwaze kwaba seMakeda.
Yehova anachititsa mantha adani aja atangoona gulu lankhondo la Israeli. Choncho Aisraeli anagonjetsa Aamori ku Gibiyoni ndipo anawathamangitsa mu msewu wopita ku Beti-Horoni ndi kuwapha njira yonse yopita ku Azeka ndi Makeda.
11 Kwasekusithi besabaleka phambi kukaIsrayeli ekwehleni kweBhethi-Horoni, iNkosi yaphosela phezu kwabo amatshe amakhulu evela emazulwini, kwaze kwaba seAzeka, njalo bafa. Babebanengi abafa ngesiqhotho okwedlula labo abantwana bakoIsrayeli abababulala ngenkemba.
Pamene ankathawa pamaso pa Israeli pa njira yochokera ku Beti-Horoni mpaka ku Azeka, Yehova anawagwetsera matalala akuluakulu kuchokera kumwamba ndipo ambiri mwa iwo anafa ndi matalala kuposa amene anaphedwa ndi lupanga la Israeli.
12 Ngalesosikhathi uJoshuwa wakhuluma eNkosini mhla iNkosi inikela amaAmori phambi kwabantwana bakoIsrayeli, wathi phambi kwamehlo kaIsrayeli: Langa, mana eGibeyoni, lawe nyanga, esihotsheni seAjaloni.
Pa tsiku limene Yehova anapereka Aamori mʼmanja mwa Israeli, Yoswa ananena kwa Yehova pamaso pa Israeli kuti, “Iwe dzuwa, ima pamwamba pa Gibiyoni, mwezi ima pamwamba pa chigwa cha Ayaloni.”
13 Lelanga lathi mpo lenyanga yema, abantu baze baziphindisela ezitheni zabo. Lokhu kakubhaliwe yini egwalweni lukaJashari? Ngakho ilanga lema phakathi komkhathi, kalaze laphangisa ukutshona phose okosuku olupheleleyo.
Choncho dzuwa linayima, mwezinso unayima, mpaka dziko la Israeli litagonjetsa adani ake. Zimenezi zalembedwa mʼbuku la Yasari. Dzuwa linayima pamodzimodzi pakati pa thambo mlengalenga, osayendanso kwa tsiku lathunthu.
14 Kaluzanga lube khona usuku olunjalo ngaphambi kwalo loba emva kwalo lapho iNkosi eyalizwa khona ilizwi lomuntu, ngoba iNkosi yamlwela uIsrayeli.
Sipanakhaleponso tsiku ngati limeneli kuyambira kale, tsiku limene Yehova anamvera munthu. Izi zinatero chifukwa Yehova ankamenyera nkhondo Aisraeli.
15 UJoshuwa wasebuyela enkambeni eGiligali loIsrayeli wonke kanye laye.
Kenaka Yoswa anabwerera pamodzi ndi Aisraeli onse ku misasa ku Giligala.
16 Kodwa lawomakhosi amahlanu abaleka, acatsha ebhalwini eMakeda.
Mafumu asanu aja anathawa ndi kukabisala ku phanga la Makeda.
17 Kwasekubikwa kuJoshuwa ukuthi: Amakhosi amahlanu atholwe ecatshile ebhalwini eMakeda.
Koma Yoswa anamva kuti mafumu asanu awapeza akubisala ku phanga la Makeda.
18 UJoshuwa wasesithi: Giqelani amatshe amakhulu emlonyeni wobhalu, limise amadoda kulo ukuwalinda.
Tsono Yoswa analamula kuti, “Mugubuduzire miyala ikuluikulu pa khomo la phangalo, ndipo muyike anthu ena kuti azilondera.
19 Kodwa lina lingami; xotshanani lezitha zenu, lizitshaye ngemuva kwazo, lingaziyekeli zingene emizini yazo, ngoba iNkosi uNkulunkulu wenu izinikele esandleni senu.
Koma inu musakhaleko! Thamangitsani adani anu, muwathire nkhondo kuchokera kumbuyo ndipo musawalole kuti akafike ku mizinda yawo, pakuti Yehova Mulungu wanu wawapereka mʼmanja mwanu.”
20 Kwasekusithi lapho uJoshuwa labantwana bakoIsrayeli sebeqedile ukuzitshaya ngokutshaya okukhulukazi zaze zaqedwa, insali eyasalayo yazo yangena emizini evikelweyo.
Kotero Yoswa ndi Aisraeli anapha anthu aja, kupatulapo ochepa amene anathawa nakabisala ku mizinda yawo.
21 Labantu bonke babuyela enkambeni kuJoshuwa eMakeda ngokuthula; kakho owanyikinya ulimi lwakhe emelana labantwana bakoIsrayeli.
Kenaka gulu lonse la ankhondo linabwerera bwinobwino kwa Yoswa ku misasa ya ku Makeda, palibe aliyense mu mzindamo amene anaputanso Aisraeli.
22 UJoshuwa wasesithi: Vulani umlomo wobhalu, likhuphele kimi lawomakhosi amahlanu evela ebhalwini.
Yoswa anati, “Tsekulani khomo la phangalo ndipo muwabweretse kwa ine mafumu asanuwo.”
23 Basebesenza njalo, bawakhuphela kuye lawomakhosi amahlanu evela ebhalwini: Inkosi yeJerusalema, inkosi yeHebroni, inkosi yeJarimuthi, inkosi yeLakishi, inkosi yeEgiloni.
Pamenepo mafumu asanu aja anatulutsidwa, mfumu ya ku Yerusalemu, mfumu ya ku Hebroni, mfumu ya ku Yarimuti, mfumu ya ku Lakisi, ndi mfumu ya ku Egiloni.
24 Kwasekusithi sebewakhuphele kuJoshuwa lawomakhosi, uJoshuwa wabiza wonke amadoda akoIsrayeli, wathi ezinduneni zamadoda empi ezazihambe laye: Sondelani, libeke inyawo zenu entanyeni zalamakhosi. Zasezisondela, zabeka inyawo zazo entanyeni zawo.
Atabwera nawo kwa Yoswa, iye anayitana Aisraeli onse. Ndipo analamula akuluakulu ake amene anapita naye limodzi kuti, “Bwerani kuno ndipo apondeni pakhosi mafumuwa.”
25 UJoshuwa wasesithi kuzo: Lingesabi lingatshaywa luvalo; qinani lime isibindi, ngoba iNkosi izakwenza njalo kuzo zonke izitha zenu elilwa limelene lazo.
Yoswa anawawuza kuti, “Musaope kapena kutaya mtima. Khalani amphamvu ndi olimba mtima popeza umo ndi mmene Yehova adzachitire ndi adani anu onse amene mudzamenyana nawo.”
26 Emva kwalokho uJoshuwa wasewatshaya wawabulala, wawalengisa ezihlahleni ezinhlanu; njalo ayelenga ezihlahleni kwaze kwahlwa.
Kenaka Yoswa anawabaya ndi kuwapha mafumuwo ndipo anawapachika pa mitengo isanu ndipo anakhala pamenepo mpaka madzulo.
27 Kwasekusithi ngesikhathi sokutshona kwelanga uJoshuwa walaya ukuthi bawethule ezihlahleni, bawaphosele ebhalwini ayecatshe khona; basebefaka amatshe amakhulu emlonyeni wobhalu, akhona kuze kube yilona lolusuku.
Dzuwa litalowa, Yoswa analamula kuti awachotse pa mitengo ija ndi kuwaponya mʼphanga limene ankabisalamo. Pa khomo pa phangalo anayikapo miyala ikuluikulu imene ilipo mpaka lero.
28 UJoshuwa wathumba layo iMakeda ngalolosuku, wayitshaya ngobukhali benkemba, watshabalalisa lenkosi yayo, bona, layo yonke imiphefumulo eyayikiyo, katshiyanga insali. Wasesenza enkosini yeMakeda njengalokho akwenza enkosini yeJeriko.
Tsiku lomwelo Yoswa analanda mzinda wa Makeda. Iye anapha anthu a mu mzindamo ndi mfumu yake ndipo sanasiye aliyense wamoyo. Yoswa anachita ndi mfumu ya ku Makeda monga anachitira ndi mfumu ya Yeriko.
29 UJoshuwa, loIsrayeli wonke laye, wasedlula esuka eMakeda waya eLibhina, walwa emelene leLibhina.
Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anapitirira kuchokera ku Makeda nakafika ku Libina ndi kuthira nkhondo mzindawo.
30 INkosi yasiyinikela layo lenkosi yayo esandleni sikaIsrayeli; waseyitshaya ngobukhali benkemba lemiphefumulo yonke eyayikiyo; katshiyanga insali kiyo; wenza enkosini yayo njengalokho akwenza enkosini yeJeriko.
Yehova anaperekanso mzindawo ndi mfumu yake mʼmanja mwa Aisraeli. Ndipo Yoswa anapha onse amene anali mu mzindamo. Palibe amene anatsala wamoyo. Ndipo Yoswa anachita ndi mfumu ya Libina monga anachitira ndi mfumu ya Yeriko.
31 UJoshuwa wasesedlula esuka eLibhina, loIsrayeli wonke kanye laye, waya eLakishi, wamisa inkamba maqondana layo, walwa emelene layo.
Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anapitirira kuchokera ku Libina kupita ku Lakisi. Iye anazungulira mzindawo ndi kuwuthira nkhondo.
32 INkosi yasiyinikela iLakishi esandleni sikaIsrayeli; waseyithumba ngosuku lwesibili, wayitshaya ngobukhali benkemba layo yonke imiphefumulo eyayikiyo, njengakho konke akwenza eLibhina.
Yehova anapereka Lakisi kwa Israeli; ndipo Yoswa anawulanda pa tsiku lachiwiri. Monga anachita ndi mzinda wa Libina, Yoswa anapha anthu onse okhala mu mzinda wa Lakisi, ndipo palibe amene anatsala ndi moyo.
33 Ngalesosikhathi uHoramu inkosi yeGezeri wenyuka ukusiza iLakishi; kodwa uJoshuwa wamtshaya labantu bakhe, kwaze kwathi kamtshiyelanga insali.
Nthawi imeneyi nʼkuti Horamu mfumu ya Gezeri itabwera kudzathandiza Lakisi koma Yoswa anamugonjetsa pamodzi ndi asilikali ake ndipo palibe anatsala wamoyo.
34 UJoshuwa wasesedlula esuka eLakishi, loIsrayeli wonke kanye laye, baya eEgiloni, bamisa inkamba maqondana layo, balwa bemelene layo.
Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anapitirira kuchokera ku Lakisi nakafika ku Egiloni. Iwo anazungulira mzindawo ndi kuwuthira nkhondo.
35 Bayithumba ngalolosuku, bayitshaya ngobukhali benkemba, lemiphefumulo yonke eyayikiyo bayitshabalalisa ngalolosuku, njengakho konke akwenza eLakishi.
Anawulanda tsiku lomwelo ndipo anapha aliyense amene anali mu mzindawo monga momwe anachitira ku Lakisi.
36 UJoshuwa wasesenyuka esuka eEgiloni loIsrayeli wonke kanye laye, baya eHebroni, balwa bemelene layo,
Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anachoka ku Egiloni nakafika ku Hebroni ndi kukawuthira nkhondo.
37 bayithumba, bayitshaya ngobukhali benkemba, lenkosi yayo lemizi yayo yonke lawo wonke umphefumulo owawukiyo; katshiyanga insali, njengakho konke akwenza eEgiloni, wawutshabalalisa lawo wonke umphefumulo owawukiyo.
Iwo analanda mzindawo napha ndi lupanga mfumu yake pamodzi ndi onse amene ankakhala mʼmenemo. Monga anachita ndi mzinda wa Egiloni, kuti sanasiye aliyense ndi moyo, anachitanso chimodzimodzi ndi mzinda wa Hebroni.
38 UJoshuwa wasebuyela eDebiri loIsrayeli wonke kanye laye, balwa bemelene layo,
Pambuyo pake Yoswa ndi Aisraeli onse anatembenukira mzinda wa Debri ndi kukawuthira nkhondo.
39 bayithumba lenkosi yayo layo yonke imizi yayo, bayitshaya ngobukhali benkemba, batshabalalisa wonke umphefumulo owawukiyo; katshiyanga insali. Njengokwenza kwakhe eHebroni wenza njalo eDebiri lenkosini yayo, lanjengokwenza kwakhe eLibhina lenkosini yayo.
Iwo analanda mzindawo ndi midzi ndi kupha mfumu yake pamodzi ndi onse okhala mʼmenemo. Anachita ndi mzinda wa Debri pamodzi ndi mfumu yake zofanana ndi zimene anachita ndi mzinda wa Libina ndi wa Hebroni.
40 Ngakho uJoshuwa walitshaya ilizwe lonke lezintaba leleningizimu lelesihotsha lelamawatha lawo wonke amakhosi abo; katshiyanga insali, kodwa watshabalalisa konke okuphefumulayo, njengokulaya kweNkosi uNkulunkulu kaIsrayeli.
Motero Yoswa anagonjetsa dziko lonselo. Anapha mafumu onse a dera la kumapiri, dera la kummawa, dera la kumadzulo mʼmphepete mwa phiri, ndiponso dera la ku magomo, kummwera. Iye sanasiye wina aliyense wamoyo. Anapha onse amene anali moyo monga momwe Yehova Mulungu wa Israeli analamulira.
41 UJoshuwa wasebatshaya kusukela eKadeshi-Bhaneya kwaze kwaba seGaza, lelizwe lonke leGosheni, kwaze kwaba seGibeyoni.
Yoswa anawagonjetsa iwo kuyambira ku Kadesi Barinea mpaka ku Gaza, ndiponso kuchokera ku chigawo chonse cha Goseni mpaka ku Gibiyoni.
42 UJoshuwa wasethumba wonke lamakhosi lelizwe lawo ngasikhathi sinye, ngoba iNkosi uNkulunkulu kaIsrayeli yamlwela uIsrayeli.
Yoswa anagonjetsa mafumu onsewa ndi kulanda dziko lawo kamodzinʼkamodzi chifukwa Yehova Mulungu wa Israeli anawamenyera nkhondo.
43 UJoshuwa wasebuyela, loIsrayeli wonke kanye laye, enkambeni eGiligali.
Pambuyo pake Yoswa ndi Aisraeli onse anabwerera ku misasa yawo ku Giligala.