< UDutheronomi 28 >

1 Kuzakuthi-ke, uba ulalela lokulalela ilizwi leNkosi uNkulunkulu wakho, ukugcina ukwenza yonke imilayo yayo engikulaya yona lamuhla, iNkosi uNkulunkulu wakho izakumisa phezulu phezu kwazo zonke izizwe zomhlaba.
Ngati mumvera Yehova Mulungu wanu ndi kutsatira mosamalitsa malamulo ake onse amene ndikukupatsani lero lino, Yehova Mulungu wanu adzakukwezani pamwamba pa mitundu yonse ya pa dziko lapansi.
2 Lalezizibusiso zonke zizakuza phezu kwakho, zikufice, nxa ulalela ilizwi leNkosi uNkulunkulu wakho.
Madalitso awa adzabwera kwa inu ndi kuyenda nanu ngati mumvera Yehova Mulungu wanu:
3 Uzabusiswa emzini, ubusiswe futhi ensimini.
Mudzadalitsika mʼmizinda yanu ndi kudalitsika mʼdzikolo.
4 Sizabusiswa isithelo sesizalo sakho, lesithelo somhlaba wakho, lenzalo yezifuyo zakho, umqegu wenkomo zakho, lamazinyane ezimvu zakho.
Yehova adzadalitsa ana anu, zokolola za mʼdziko lanu, ngʼombe zanu pamodzi ndi ziweto zanu zonse.
5 Kuzabusiswa isitsha sakho, lomganu wakho wokuxovela izinkwa.
Dengu lanu ndi chiwaya chanu cha buledi zidzadalitsika.
6 Uzabusiswa ekungeneni kwakho, ubusiswe ekuphumeni kwakho.
Mudzadalitsika pa kulowa kwanu ndi pa kutuluka kwanu.
7 INkosi izakwenza izitha zakho ezikuvukelayo zitshaywe phambi kwakho; zizaphuma ukumelana lawe ngandlelanye, zibaleke phambi kwakho ngezindlela eziyisikhombisa.
Yehova adzaonetsetsa kuti adani anu amene adzakuwukirani agonjetsedwe pamaso panu. Iwo adzabwera kwa inu kuchokera mbali imodzi koma adzakuthawani ku mbali zisanu ndi ziwiri.
8 INkosi izalaya isibusiso phezu kwakho, eziphaleni zakho lakukho konke obeka kukho isandla sakho, ikubusise elizweni iNkosi uNkulunkulu wakho ekunika lona.
Yehova adzatumiza madalitso pa nkhokwe zanu ndi pa chilichonse chimene muchikhudza. Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani mʼdziko limene akukupatsani.
9 INkosi izazimisela wena ube yisizwe esingcwele, njengokufunga kwayo kuwe, uba ugcina imilayo yeNkosi uNkulunkulu wakho, uhambe endleleni zayo.
Yehova Mulungu wanu adzachititsa kuti mukhale anthu ake opatulika, monga momwe analonjezera pa malumbiro ake, ngati musunga malamulo ake ndi kuyenda mʼnjira zake.
10 Labo bonke abantu basemhlabeni bazabona ukuthi ibizo leNkosi libizwa phezu kwakho, bakwesabe.
Pamenepo anthu onse a dziko lapansi adzaona kuti mumadziwika ndi dzina la Yehova ndipo adzakuopani.
11 LeNkosi izakwandisela okuhle, esithelweni sesizalo sakho, lenzalweni yezifuyo zakho, lesithelweni somhlaba wakho, elizweni iNkosi eyafungela oyihlo ukukunika lona.
Yehova adzakupambanitsani kwambiri ndipo adzakupatsani ana ambiri, ziweto zambiri, ndi zokolola zochuluka, mʼdziko limene Yehova analumbira kwa makolo anu kuti adzakupatsani.
12 INkosi izakuvulela okuligugu kwayo okulungileyo, amazulu, ukunika izulu elizweni lakho ngesikhathi salo, lokubusisa umsebenzi wonke wesandla sakho; njalo uzakweboleka izizwe ezinengi, kodwa wena ungeboleki kuzo.
Yehova adzatsekula kumwamba kumene amasungirako chuma chake, kutumiza mvula mʼdziko lanu pa nthawi yake ndi kudalitsa ntchito yonse ya manja anu. Mudzakongoza mitundu yambiri koma inu simudzakongola kwa aliyense.
13 INkosi izakwenza ube yinhloko, ungabi ngumsila; uzakuba ngaphezulu kuphela, ungabi ngaphansi, uba ulalela imilayo yeNkosi uNkulunkulu wakho engikulaya yona lamuhla ukuyigcina lokuyenza.
Yehova adzakuthandizani kukhala mutu osati mchira. Mukakhala ndi chidwi ndi malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani lero lino ndi kuwatsata mosamalitsa, inu mudzakhala apamwamba nthawi zonse osati apansi.
14 Ungaphambuki lakwelilodwa lamazwi engililaya wona lamuhla, ukuya ngakwesokunene langakwesokhohlo, ukulandela abanye onkulunkulu ukubakhonza.
Musapatukire ku dzanja lamanja kapena lamanzere pa lamulo lina lililonse limene ndikukupatsani lero lino ndi kumatsatira kapena kuyitumikira milungu ina.
15 Kodwa kuzakuthi, uba ungalaleli ilizwi leNkosi uNkulunkulu wakho, ukugcina ukwenza yonke imilayo yayo lezimiso zayo engikulaya zona lamuhla, leziziqalekiso zonke zize phezu kwakho zikufice.
Koma ngati simumvera Yehova Mulungu wanu ndi kusatsata mosamalitsa malamulo ake ndi malangizo ake onse amene ndikukupatsani lero lino, matemberero awa adzabwera pa inu ndikukugonjetsani:
16 Uzaqalekiswa emzini, uqalekiswe futhi ensimini.
Mudzatembereredwa mu mzinda ndi kutembereredwa mʼmudzi.
17 Kuzaqalekiswa isitsha sakho lomganu wakho wokuxovela izinkwa.
Dengu lanu ndi chiwaya chanu cha buledi zidzatembereredwa.
18 Kuzaqalekiswa isithelo sesizalo sakho, lesithelo somhlaba wakho, umqegu wenkomo zakho, lamazinyane ezimvu zakho.
Zipatso za mʼmimba mwanu zidzatembereredwa, ndiponso zomera za mʼdziko lanu, ana angʼombe zanu ndi ana ankhosa zanu zidzatembereredwa.
19 Uzaqalekiswa ekungeneni kwakho, uqalekiswe ekuphumeni kwakho.
Mudzatembereredwa pa kulowa kwanu ndi pa kutuluka kwanu.
20 INkosi izathumela phakathi kwakho isiqalekiso, inhlupheko, lokukhuza, kukho konke obeka isandla sakho kukho ukukwenza, uze uchithwe, njalo uze ubhubhe masinyane, ngenxa yobubi bezenzo zakho, ongidele ngazo.
Yehova adzakutumizirani matemberero, chisokonezo ndi minyozo pa chilichonse chimene mudzachichita mpaka mudzawonongedwa ndi kukhala bwinja mofulumira chifukwa cha zoyipa zimene mwazichita pa kumutaya Yehova.
21 INkosi izanamathelisa kuwe umatshayabhuqe wesifo, aze akuqede usuke elizweni oya kulo ukudla ilifa lalo.
Yehova adzakugwetserani mliri wa matenda mpaka atakuwonongani mʼdziko limene mukulowa kukalitengali.
22 INkosi izakutshaya ngesifo esicakisayo, langoqhuqho, langokuvuvuka komzimba, langokutshisa okukhulukazi, langenkemba, langokuhanguka, langengumane; njalo kuzakuxotsha uze ubhubhe.
Yehova adzakukanthani ndi nthenda yowondetsa, ya malungo ndi ya zotupatupa, ndi kutentha kwakukulu ndi chilala, ndi chinsikwi ndi chiwawu zimene zidzakusautsani mpaka mutawonongeka.
23 Lesibhakabhaka sakho esiphezu kwekhanda lakho sizakuba lithusi, lomhlaba ongaphansi kwakho ube yinsimbi.
Mitambo ya pamutu panu idzawuma ngati mkuwa ndipo sidzagwetsa mvula mpaka nthaka yanu idzawuma gwaa ngati chitsulo.
24 INkosi izakwenza izulu lelizwe lakho libe lubhuqu lothuli, kwehlele phezu kwakho kuvela emazulwini, uze ubhujiswe.
Mʼmalo mwa mvula Yehova adzakupatsani fumbi ndi dothi ndipo lidzakugwerani kuchokera kumwamba mpaka mutawonongeka.
25 INkosi izakwenza utshaywe phambi kwezitha zakho; uzaphuma umelane lazo ngandlelanye, njalo uzabaleka phambi kwazo ngezindlela eziyisikhombisa; uzakuba yinto eyesabekayo kuyo yonke imibuso yomhlaba.
Yehova adzalola kuti adani anu akugonjetseni. Mudzadzera njira imodzi pokalimbana ndi adani anu koma pothawa mudzabalalika mbali zisanu ndi ziwiri. Mudzakhala chinthu chochititsa mantha pakati pa maufumu onse a dziko lapansi.
26 Lesidumbu sakho sizakuba yikudla kwenyoni zonke zamazulu lokwezinyamazana zomhlaba, njalo kungabi khona ozethusayo.
Mitembo yanu idzadyedwa ndi mbalame zamumlengalenga ndi nyama zakutchire, ndipo palibe amene adzaziyingitse.
27 INkosi izakutshaya ngamathumba eGibhithe, lamaqhubu, loqweqwe, lenkomo, ongelakwelatshwa kukho.
Yehova adzakusautsani ndi zithupsa za ku Igupto ndi zotupatupa, zipere, ndi mphere zimene simudzachiritsika nazo.
28 INkosi izakutshaya ngobuhlanya langobuphofu langokudideka kwenhliziyo.
Yehova adzakusautsani inu ndi misala, khungu ndi chisokonekero cha maganizo.
29 Njalo uzaphumputha emini njengesiphofu siphumputha emnyameni, ungenzi indlela zakho ziphumelele; ucindezelwe kuphela, uphangwe insuku zonke, kungabi khona osindisayo.
Masanasana mudzayenda ngati muli mu mdima, kumafufuzira njira ngati wosaona. Mudzakhala olephera pa chilichonse mungachite. Tsiku ndi tsiku mudzaponderezedwa ndi kuberedwa wopanda wokupulumutsani.
30 Uzagana umfazi, kodwa enye indoda ilale laye; uzakwakha indlu, kodwa ungahlali kuyo; uhlanyele isivini, kodwa ungakhi izithelo zaso.
Mudzachita chinkhoswe ndi mkazi, koma wina adzakulandani ndi kumukwatira. Mudzamanga nyumba koma simudzagonamo. Mudzalima munda wamphesa koma simudzadyako zipatso zake.
31 Inkabi yakho izahlatshwa phambi kwamehlo akho, ungadli okwayo; ubabhemi wakho athathwe ngodlakela phambi kobuso bakho, angabuyiselwa kuwe; izimvu zakho zizanikwa izitha zakho, kungabi khona okusindiselayo.
Ngʼombe yanu yamtheno idzaphedwa inu muli pomwepo koma simudzadyako. Bulu wanu adzalandidwa kwa inu mwamakani osabwera nayenso. Nkhosa zanu zidzapatsidwa kwa adani anu, ndipo palibe amene adzazipulumutsa.
32 Amadodana akho lamadodakazi akho azanikelwa kwesinye isizwe, lamehlo akho azakhangela abalangathe usuku lonke; kodwa kungabi lamandla esandleni sakho.
Ana anu aamuna ndi aakazi adzaperekedwa kwa anthu a mitundu ina ndipo inu mudzafika potopa ndi kulefuka nʼkudikirira tsiku ndi tsiku kuti mwina anawo abwerako.
33 Isithelo somhlaba wakho, lomsebenzi wakho wonke, isizwe ongasaziyo sizakudla. Uzacindezelwa kuphela, uchotshozwe insuku zonke,
Anthu amene simukuwadziwa adzakudyerani zokolola zanu, ndipo mudzakhala mukuponderezedwa mwankhanza masiku onse.
34 uze uhlanye ngenxa yokubona kwamehlo akho ozakubona.
Zimene muzidzaziona zidzakusokonezani mitu.
35 INkosi izakutshaya emadolweni lemilenzeni ngamathumba amabi angelakwelatshwa, kusukela kungaphansi yonyawo lwakho kuze kube senkanda yakho.
Yehova adzakusautsani ndi zithupsa zaululu ndi zosachiritsika za mʼmawondo ndi mʼmiyendo ndipo zidzafalikira kuchoka kuphazi mpaka kumutu.
36 INkosi izakusa wena lenkosi yakho owayibeka phezu kwakho esizweni ongasaziyo wena laboyihlo, ukhonze lapho abanye onkulunkulu, isigodo lelitshe.
Yehova adzakuthamangitsirani, inu ndi mafumu anu amene muwayika, ku dziko losadziwika kwa inu ndi kwa makolo anu. Kumeneko mudzakapembedza milungu ina, milungu ya mitengo ndi miyala.
37 Uzakuba yinto eyesabekayo, isaga, lenhlekisa phakathi kwazo zonke izizwe, lapho iNkosi ezakusa khona.
Inu mudzakhala chinthu chochititsa mantha kuchisunga ndiponso chinthu chotukwanidwa ndi chonyozeka kwa anthu a mitundu yonse kumene Yehova adzakuthamangitsirani.
38 Uzaphuma lenhlanyelo enengi uye ensimini, kodwa ubuthelele okulutshwana, ngoba isikhonyane sizakudla.
Mudzadzala mbewu zambiri ku munda koma mudzakolola pangʼono, chifukwa dzombe lidzaziwononga.
39 Uzahlanyela izivini, uzisebenze, kodwa kawuyikunatha iwayini, kawuyikubutha lutho, ngoba imihogoyi izazidla.
Mudzadzala mpesa ndi kulimirira koma vinyo wake simudzamumwa kapena kukolola mphesazo, chifukwa mphutsi zidzadya mphesazo.
40 Uzakuba lezihlahla zemihlwathi phakathi kwemingcele yakho yonke, kodwa kawuyikugcoba ngamafutha, ngoba imihlwathi izawohloka.
Mudzakhala ndi mitengo ya olivi mʼdziko lanu lonse koma simudzagwiritsa ntchito mafuta ake, chifukwa zipatso zake zidzayoyoka.
41 Uzazala amadodana lamadodakazi, kodwa kawayikuba ngawakho, ngoba azakuya ekuthunjweni.
Mudzabereka ana aamuna ndi aakazi koma sadzakhala anu, chifukwa adzapita ku ukapolo.
42 Zonke izihlahla zakho lezithelo zomhlaba wakho zizakuba ngezesikhonyane.
Magulumagulu a dzombe adzawononga mitengo yanu ndi mbewu za mʼdziko lanu.
43 Owemzini ophakathi kwakho uzaphakama phezu kwakho aqonge phezulu, wena-ke uzakwehlela phansi phansi.
Mlendo wokhala pakati panu adzatukuka kuposa inu, koma inuyo mudzaloweralowera pansi.
44 Yena uzakweboleka, kodwa wena ungameboleki; yena uzakuba yinhloko, kodwa wena ube ngumsila.
Iye adzakubwereketsani, koma inu simudzatha kubwereketsa. Iye adzakhala mutu ndipo inu mudzakhala mchira.
45 Lazo zonke leziziqalekiso zizakwehlela, zixotshane lawe, zikufice, uze ubhujiswe, ngoba ungalilalelanga ilizwi leNkosi uNkulunkulu wakho, ukugcina imilayo yayo lezimiso zayo eyakulaya zona.
Matemberero onsewa adzabwera pa inu. Adzakulondolani ndi kukugonjetsani mpaka mutawonongeka, chifukwa simunamvere Yehova Mulungu wanu ndi kusunga malamulo ndi malangizo amene anakupatsani.
46 Njalo zizakuba phezu kwakho ukuba yisibonakaliso lokuba yisimangaliso, laphezu kwenzalo yakho kuze kube nininini.
Matemberero amenewa adzakhala chizindikiro ndi chozizwitsa kwa inu ndi zidzukulu zanu mpaka kalekale.
47 Njengoba ungayikhonzanga iNkosi uNkulunkulu wakho ngentokozo langokuhle kwenhliziyo, ngenxa yobunengi bakho konke,
Pakuti inu simunatumikire Yehova Mulungu wanu pa nthawi imene zinthu zinkakuyenderani bwino,
48 ngakho uzakhonza izitha zakho iNkosi ezazithuma ukumelana lawe, endlaleni, lekomeni, lekuhambenize, lekusweleni konke. Njalo izabeka ijogwe lensimbi entanyeni yakho, ize ikubhubhise.
chomwecho pa nthawi ya njala ndi ludzu, ya maliseche ndi umphawi woopsa, mudzatumikira adani amene Yehova adzakutumizirani. Iye adzayika goli lachitsulo mʼkhosi mwanu kufikira atakuwonongani.
49 INkosi izakuvusela isizwe esivela khatshana, emkhawulweni womhlaba, njengokuphapha kokhozi, isizwe olimi lwaso ongayikuluzwa,
Yehova adzakutumizirani mtundu wa anthu kuchokera kutali kumapeto kwa dziko lapansi nudzachita ngati mphungu yowulukira pansi, mtundu wa anthu umene chiyankhulo chawo simudzachimva,
50 isizwe esilobuso obesabekayo, esingemukeli ubuso bomdala, esingelamusa komutsha.
mtundu wooneka wochititsa mantha, wopanda ulemu kwa okalamba kapena chisoni kwa ana.
51 Sizakudla isithelo sezifuyo zakho lesithelo somhlaba wakho, uze ubhujiswe; okungayikukutshiyela amabele, iwayini elitsha, lamafutha, umqegu wenkomo zakho, lamazinyane ezimvu zakho, size sikuchithe.
Iwo adzagwira ana a ziweto zanu, natenga zokolola za mʼdziko lanu kufikira mutawonongeka. Iwo sadzakusiyirani tirigu, vinyo watsopano kapena mafuta a olivi, kapena mwana wangʼombe aliyense kapena mwana wankhosa mpaka mutasanduka bwinja.
52 Sizakuvimbezela emasangweni akho wonke, ize idilike imiduli yakho ephakemeyo lebiyelwe ngemithangala obuthembela kuyo, elizweni lonke lakho; njalo sizakuvimbezela emasangweni akho wonke elizweni lonke lakho iNkosi uNkulunkulu wakho ekunike lona.
Iwo adzathira nkhondo mizinda yonse mʼdziko lanu lonse mpaka malinga anu ataliatali omwe mumadalira aja atagwa. Adzathira nkhondo mizinda yonse ya mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.
53 Njalo uzakudla isithelo sesizalo sakho, inyama yamadodana leyamadodakazi akho, iNkosi uNkulunkulu wakho ekunike wona, ekuvinjezelweni lekucindezelweni, izitha zakho ezizakucindezela ngakho.
Chifukwa cha zosautsa zimene mdani wanu adzabweretsa pa nthawi yokuthirani nkhondo, inu mudzadya ana anu, mnofu wa ana anu aamuna ndi aakazi amene Yehova Mulungu wanu wakupatsani.
54 Indoda ebuthakathaka phakathi kwakho letotoziweyo kakhulu, ilihlo layo lizakuba libi kumfowabo, lakumkayo wesifuba sayo, lakunsali yabantwana bayo ezabatshiya;
Ngakhale munthu woleza mtima ndi wachifundo kwambiri pakati panu sadzakhala ndi chifundo pa mʼbale wake weniweni kapena mkazi wake amene iye amamukonda kapena ana ake otsalawo,
55 ukuze inganiki lamunye wabo okwenyama yabantwana bayo ebadlayo, ngoba ingasalelwanga lutho ekuvinjezelweni lekucindezelweni, izitha zakho ezizakucindezela ngakho emasangweni akho wonke.
ndipo sadzagawirako aliyense wa iwo mnofu wa ana ake amene akudyawo. Kadzakhala kali komweko basi kamene kamutsalira chifukwa cha msautso umene mdani wanu adzagwetsa pa nthawi yothira nkhondo mizinda yanu yonse.
56 Owesifazana obuthakathaka lototoziweyo phakathi kwakho ongazamanga ukubeka ingaphansi yonyawo lwakhe emhlabathini ngenxa yokutotozwa lobuthakathaka, ilihlo lakhe lizakuba libi endodeni yesifuba sakhe, lasendodaneni yakhe, lasendodakazini yakhe,
Mayi woleza mtima ndi wachifundo kwambiri pakati panu, uja woti sangayerekeze kuponda pansi, adzabisira mwamuna wake amene amamukonda ndi ana ake omwe aamuna ndi aakazi
57 lakumnakwabo ophuma phakathi kwenyawo zakhe, lebantwaneni azabazala; ngoba uzabadla ensitha ngenxa yokuswela konke, ekuvinjezelweni lekucindezelweni, isitha sakho esizakucindezela ngakho emasangweni akho.
zotsalira za uchembere zochoka mʼmimba mwake ndi ana amene wabereka. Pakuti adzafuna kuti adye zimenezi yekha mobisa pa nthawi yothiridwa nkhondo chifukwa cha masautso amene mdani wanu adzagwetsa pa inu mʼmizinda yanu.
58 Uba ungayikugcina ukwenza wonke amazwi alumlayo abhaliweyo egwalweni lolu, ukwesaba lelibizo elilodumo lelesabekayo, iNkosi uNkulunkulu wakho,
Ngati simutsata mosamalitsa mawu onse a malamulo awa amene alembedwa mʼbuku lino, komanso ngati simuopa dzina la ulemerero ndi loopsa, dzina la Yehova Mulungu wanu,
59 iNkosi izakwenza-ke inhlupheko zakho zimangalise, lenhlupheko zenzalo yakho, inhlupheko ezinkulu leziqhubekayo, lemikhuhlane emibi leqhubekayo.
Yehova adzatumiza pa inu ndi zidzukulu zanu miliri yoopsa, zosautsa zowawa ndi zokhalitsa, ndi matenda aakulu ndi ovuta kuchiritsika.
60 Njalo izabuyisela kuwe zonke izifo zeGibhithe owawuzesaba, zizanamathela kuwe,
Adzakubweretserani matenda onse a ku Igupto aja mumawaopawa ndipo adzakukanirirani.
61 lawo wonke umkhuhlane layo yonke inhlupheko engabhalwanga egwalweni lwalumlayo, iNkosi izakwehlisela zona uze ubhujiswe.
Yehova adzakubweretseraninso mtundu uliwonse wa matenda ndi zosautsa zimene sizinalembedwe mʼbuku la malamulo lino, mpaka mutawonongeka.
62 Njalo lizasala lilabantu abalutshwana, endaweni yokuthi lalinjengenkanyezi zamazulu ngobunengi, ngoba kawulalelanga ilizwi leNkosi uNkulunkulu wakho.
Inu aja munali ochuluka ngati nyenyezi zakumwamba mudzatsala ochepa chabe chifukwa simunamvere Yehova Mulungu wanu.
63 Kuzakuthi-ke, njengalokhu iNkosi yathokoza ngani ukulenzela okuhle lokulandisa, ngokunjalo iNkosi izajabula ngani ukulichitha lokuliqeda, lihluthunwe elizweni ongena kulo ukudla ilifa lalo.
Monga kunamukomera Yehova kukulemeretsani ndi kukuchulukitsani, momwemonso kudzamukondweretsa kukunthani ndi kukuwonongani. Inu mudzazulidwa kukuchotsani mʼdziko limene mukulowa kukalitengali.
64 INkosi izakuhlakazela-ke phakathi kwezizwe zonke, kusukela komunye umkhawulo womhlaba kuze kube komunye umkhawulo womhlaba, ukhonze lapho abanye onkulunkulu, wena laboyihlo elingabazanga, isigodo lelitshe.
Kenaka Yehova adzakubalalitsani pakati pa anthu a mitundu yonse, kuchokera ku mapeto a dziko kufika ku mapeto ena. Kumeneko mudzapembedza milungu ina, milungu ya mitengo ndi ya miyala, imene inu eni kapena makolo anu sanayidziwepo.
65 Laphakathi kwalezozizwe kawuyikuphumula, lengaphansi yonyawo lwakho kayiyikuba lendawo yokuphumula; kodwa lapho iNkosi izakupha inhliziyo ethuthumelayo, lokufiphala kwamehlo, lokudangala komphefumulo.
Pakati pa mitundu ya anthu imeneyi simudzapeza mpata, popanda malo woti nʼkuyikapo phazi. Kumeneko Yehova adzakupatsani moyo wa nkhawa, maso otopa ndi chiyembekezo, ndi mtima wosakhazikika.
66 Lempilo yakho izahlala isevalweni phambi kwakho; uzatshaywa luvalo ebusuku lemini, ungabi lethemba lempilo yakho.
Inu mudzakhala osakhazikika mopitirira, odzazidwa ndi mantha usiku ndi usana womwe, osowa chitsimikizo cha pa moyo wanu.
67 Ekuseni uzakuthi: Kungathi kungahlwa! Lakusihlwa uzakuthi: Kungathi kungasa! ngenxa yokwesaba kwenhliziyo ozakwesaba ngakho, langenxa yokubona kwamehlo akho ozakubona.
Mmawa muzidzati, “Chikhala anali madzulo!” ndipo madzulo mudzati, “Chikhala unali mmawa!” Mudzanena zimenezi chifukwa cha mantha amene adzakhale mu mtima mwanu ndi chifukwa cha zomwe muzidzaziona.
68 LeNkosi izakubuyisela eGibhithe ngemikhumbi, ngendlela engatsho ngayo kuwe ukuthi: Kawusayikuyibona futhi. Lapho lizazithengisa ezitheni zakho libe yizigqili lezigqilikazi, kodwa kakuyikuba lomthengi.
Yehova adzakubwezani ku Igupto pa sitima zapamadzi paulendo umene Ine ndinati musawuyendenso. Kumeneko mudzadzitsatsa nokha kwa adani anu monga akapolo aamuna ndi aakazi, koma palibe amene adzakuguleni.

< UDutheronomi 28 >