< UGenesisi 6 >
1 Kwasekusithi abantu sebeqala ukwanda ebusweni bomhlaba, basebezalelwa amadodakazi,
Anthu atayamba kuchuluka pa dziko lapansi ndi kubereka ana aakazi,
2 amadodana kaNkulunkulu ebona amadodakazi abantu ukuthi wona ayemahle; asezithathela abafazi kuwo wonke awakhethayo.
ana aamuna a Mulungu anaona kuti ana aakazi a anthuwo anali okongola. Ndipo anakwatira aliyense amene anamusankha.
3 INkosi yasisithi: UMoya wami kawuyikulwisana lomuntu njalonjalo, ngoba laye eyinyama; kodwa izinsuku zakhe zizakuba yiminyaka elikhulu lamatshumi amabili.
Tsono Yehova anati, “Sindilola kuti chipwirikiti chikuchitikachi chipitirire mpaka muyaya, pakuti iye ndi munthu; masiku a moyo wake adzakhala zaka 120.”
4 Iziqhwaga zazisemhlabeni ngalezonsuku; lemva kwalokho-ke, lapho amadodana kaNkulunkulu esengenile emadodakazini abantu, asewazalela abantwana. Wona ayengamaqhawe asendulo, engamadoda alebizo.
Masiku amenewo komanso pambuyo pake, pa dziko lapansi panali Anefili, anthu amphamvu ndiponso otchuka. Anthuwa ndi amene ankabadwa ana a Mulungu aja atakwatira ana aakazi a anthu.
5 INkosi yasibona ukuthi ububi bomuntu bukhulu emhlabeni, lokuthi konke ukuceba kwemicabango yenhliziyo yakhe kwakukubi kuphela usuku lonke.
Pamene Yehova anaona kuti kuyipa kwa munthu pa dziko lapansi kunali kwakukulu ndi kuti nthawi zonse amalingalira ndi kukhumbira kuchita zoyipa zokhazokha,
6 INkosi yasizisola ngokuthi yayimenzile umuntu emhlabeni, yasidabuka enhliziyweni yayo.
Yehova anamva chisoni kuti analenga munthu ndi kumuyika pa dziko lapansi, ndipo anawawidwa mtima.
7 INkosi yasisithi: Ngizamchitha umuntu engamdalayo ngimsuse ebusweni bomhlaba, kusukela emuntwini kusiya enyamazaneni, kuze kube kokuhuquzelayo, lenyonini zamazulu; ngoba ngiyazisola ukuthi ngikwenzile.
Choncho Yehova anati, “Ndidzafafaniza munthu, nyama, zonse zokwawa, ndi mbalame za mu mlengalenga pa dziko lapansi, pakuti ndikumva chisoni kuti ndinazilenga zimenezi.”
8 Kodwa uNowa wazuza umusa emehlweni eNkosi.
Koma Yehova anamukomera mtima Nowa.
9 Lezi yizizukulwana zikaNowa. UNowa wayeyindoda elungileyo epheleleyo esizukulwaneni sakhe; uNowa wahamba loNkulunkulu.
Mbiri ya Nowa inali yotere: Nowa anali munthu wolungama ndi wopanda tchimo pakati pa anthu a mʼbado wake. Ndipo anayenda ndi Mulungu.
10 UNowa wasezala amadodana amathathu, uShemu, uHamu loJafethi.
Nowa anabereka ana aamuna atatu: Semu, Hamu ndi Yafeti.
11 Umhlaba wonakaliswa-ke phambi kukaNkulunkulu, lomhlaba wagcwaliswa ngobudlwangudlwangu.
Chiwawa chinadzaza pa dziko lapansi kotero kuti dziko linakhala lowonongeka pamaso pa Mulungu.
12 UNkulunkulu wasebona umhlaba, khangela-ke wonakalisiwe, ngoba yonke inyama yonakalise indlela yayo emhlabeni.
Mulungu atayangʼana, anaona kuti dziko layipadi chifukwa cha makhalidwe oyipa a anthu onse pa dziko lapansi.
13 UNkulunkulu wasesithi kuNowa: Ukuphela kwayo yonke inyama sekuze phambi kwami, ngoba umhlaba ugcwele ubudlwangudlwangu ngenxa yabo; khangela-ke, ngizabachitha kanye lomhlaba.
Ndipo Mulungu anati kwa Nowa, “Ndatsimikiza mtima kuti ndiwononge anthu onse, pakuti dziko lapansi ladzaza ndi ntchito zawo zoyipa. Ndithudi ndiwawononga pamodzi ndi zonse za pa dziko.
14 Zakhele umkhumbi ngezigodo zegofere, wenze izigaba phakathi komkhumbi, uwuhuqe ngengcino ngaphakathi langaphandle.
Tsono udzipangire chombo cha matabwa a mtengo wanjale; mʼkati mwake upange zipinda ndipo upake phula mʼkati ndi kunja.
15 Nansi indlela ozawenza ngayo; ingalo ezingamakhulu amathathu yibude bomkhumbi, ingalo ezingamatshumi amahlanu yibubanzi bawo, ingalo ezingamatshumi amathathu yikuphakama kwawo.
Uchipange motere: Chombo chikhale mamita 140 mulitali, mamita 23 mulifupi ndi mamita 13 mu msinkhu wake.
16 Iwindi uzalenza emkhunjini, uliqede libe yingalo kusukela phezulu, ufake umnyango womkhumbi ehlangothini lwawo, uwenze ube lesitezi esaphansi, esesibili, lesesithathu.
Uchipangire denga ndi kuchimaliza ndi zenera la masentimita makumi asanu. Uyike khomo mʼmbali mwa chombocho ndi kupanga zipinda zosanjikana; chapansi, chapakati ndi chapamwamba.
17 Mina-ke, khangela, ngizakwehlisela uzamcolo wamanzi phezu komhlaba, ukuchitha yonke inyama, okukuyo umoya wempilo, isuke ngaphansi kwamazulu. Konke okusemhlabeni kuzaphela.
Ndidzagwetsa mvula ya chigumula pa dziko lapansi kuti ndiwononge zamoyo zonse za pansi pa thambo ndipo chilichonse cha pa dziko lapansi chidzafa.
18 Kodwa ngizamisa isivumelwano sami lawe; njalo uzangena emkhunjini, wena lamadodana akho lomkakho labafazi bamadodana akho kanye lawe.
Koma ndidzachita pangano langa ndi iwe. Iwe, ana ako aamuna, mkazi wako ndi akazi a ana ako nonse mudzalowa mʼchombocho.
19 Lakukho konke okuphilayo, kuyo yonke inyama, okubili kwakho konke, uzakuletha emkhunjini, ukulondoloze kuphila lawe, kuzakuba ngokuduna lokusikazi;
Iwe udzalowa mʼchombocho ndi zolengedwa zamoyo zonse ziwiriziwiri, chachimuna ndi chachikazi, kuti zisungike ndi moyo pamodzi ndi iwe.
20 enyonini ngohlobo lwayo, lesifuyweni ngohlobo lwaso, lakukho konke okuhuquzelayo komhlaba ngohlobo lwakho, okubili kwakho kuzakuza kuwe, ukulondoloze kuphila.
Udzatenga ziwiriziwiri za mitundu yonse ya mbalame, mitundu yonse ya nyama, ndi mitundu yonse ya zokwawa kuti zikhale ndi moyo.
21 Lawe-ke, zithathele kukho konke ukudla okudliwayo, njalo ukubuthelele kuwe, futhi kuzakuba ngokwakho lokwazo okokudla.
Udzatengenso chakudya cha mtundu uliwonse ndi kuchisunga kuti inu ndi nyamazo muzidzadya.”
22 Wasekwenza uNowa; njengakho konke uNkulunkulu ayemlaye khona wenza njalo.
Nowa anachita zonse monga Mulungu anamulamulira.