< U-Eksodusi 1 >

1 La-ke ngamabizo amadodana kaIsrayeli afika eGibhithe loJakobe; afika, ileyo laleyo lomuzi wayo,
Awa ndi mayina a ana a Israeli amene anapita ku Igupto pamodzi ndi Yakobo abambo awo, aliyense ndi banja lake:
2 uRubeni, uSimeyoni, uLevi, loJuda,
Rubeni, Simeoni, Levi, Yuda;
3 uIsakari, uZebuluni, loBhenjamini,
Isakara, Zebuloni, Benjamini;
4 uDani, loNafithali, uGadi, loAsheri.
Dani, Nafutali; Gadi ndi Aseri.
5 Njalo yonke imiphefumulo eyaphuma ekhalweni lukaJakobe yayiyimiphefumulo engamatshumi ayisikhombisa. Kodwa uJosefa wayeseGibhithe.
Anthu onse obadwa mwa Yakobo analipo 70. Yosefe nʼkuti ali kale ku Igupto.
6 UJosefa wasesifa labo bonke abafowabo, lalesosizukulwana sonke.
Tsono Yosefe ndi abale ake onse ndiponso mʼbado wawo wonse anamwalira.
7 Njalo abantwana bakoIsrayeli bazalana, baba banengi, banda, baba lamandla kakhulukazi, ilizwe laze lagcwaliswa yibo.
Koma Aisraeli anaberekana ndi kuchuluka kwambiri nakhala amphamvu kwambiri, kotero kuti anadzaza dzikolo.
8 Kwasekuvela inkosi entsha phezu kweGibhithe eyayingamazi uJosefa.
Pambuyo pake mfumu yatsopano imene sinkamudziwa Yosefe, inayamba kulamulira dziko la Igupto.
9 Yasisithi esizweni sayo: Khangela, isizwe sabantwana bakoIsrayeli sinengi, futhi silamandla kulathi.
Iyo inati kwa anthu ake, “Taonani, Aisraeli achuluka ndipo ndi amphamvu kwambiri kuposa ife.
10 Wozani, asisihlakanipheleni, hlezi sande, njalo kuzakuthi lapho kusehla impi, laso sihlangane lezitha zethu, silwe simelene lathi, senyuke sisuke elizweni.
Tiyeni tiwachenjerere. Tikapanda kutero adzachuluka kuposa ife, ndipo ngati kutakhala nkhondo, adzadziphatika kwa adani athu nadzamenyana nafe, kenaka nʼkudzachoka mʼdziko muno.”
11 Ngakho bamisa phezu kwaso izinduna zesibhalo ukusihlupha ngemithwalo yabo. Njalo samakhela uFaro imizi eyiziphala, iPithoma leRamesesi.
Kotero anayika akapitawo kuti aziwazunza ndi kuwagwiritsa ntchito yolemetsa mokakamiza. Iwo anamangira Farao mizinda ya Pitomu ndi Ramesesi kumene ankasungirako chakudya.
12 Kodwa kwathi ekusihlupheni kwaso kwang'khona sisanda, kwang'khona sisabalala. Ngakho banengwa ngabantwana bakoIsrayeli.
Koma pamene ankawazunza kwambiri, Aisraeli ndiye ankachulukirachulukira mpaka kubalalikira mʼdziko lonse. Kotero Aigupto anayamba kuopa Aisraeliwo
13 Njalo amaGibhithe abasebenzisa abantwana bakoIsrayeli ngochuku,
ndipo anawagwiritsa ntchito mwankhanza kwambiri.
14 aze enza impilo zabo zababa ngomsebenzi onzima, ngodaka langezitina, langawo wonke umsebenzi emasimini; ngomsebenzi wabo wonke, ababenza bawenza ngodlakela.
Aigupto anachititsa moyo wa Aisraeli kukhala owawa kwambiri powagwiritsa ntchito yakalavulagaga yowumba njerwa ndi kuponda dothi lomangira, pamodzi ndi ntchito zina zosiyanasiyana zamʼminda. Iwo anakakamiza Aisraeli mwankhanza kuti agwire ntchito yowawayi.
15 Inkosi yeGibhithe yasikhuluma lababelethisi amaHebherukazi, obizo lowokuqala lalinguShifira, lebizo lowesibili lalinguPhuwa,
Mfumu ya Igupto inati kwa azamba a Chihebri omwe mayina awo anali Sifira ndi Puwa,
16 yasisithi: Nxa libelethisa amaHebherukazi, lapho libabona ezihlalweni zokubeletha, uba kuyindodana, liyibulale; kodwa uba kuyindodakazi, iyekeleni iphila.
“Mukamathandiza amayi a Chihebri pa mwala wochirira, muzionetsetsa kuti akabadwa mwana wamwamuna muzipha, koma akakhala wamkazi muzimuleka akhale ndi moyo.”
17 Kodwa ababelethisi babemesaba uNkulunkulu, kabenzanga njengalokho yakhuluma kubo inkosi yeGibhithe, kodwa babayekela abafana baphila.
Koma azambawo ankaopa Mulungu ndipo sanachite zimene mfumu ya Igupto inawawuza kuti achite. Iwo analeka ana aamuna kuti akhale ndi moyo.
18 Inkosi yeGibhithe yasibiza ababelethisi, yathi kubo: Liyenzeleni linto ukuthi liyekele abafana baphile?
Kenaka mfumu ya Igupto inayitanitsa azamba aja ndi kuwafunsa kuti, “Chifukwa chiyani mwachita zimenezi? Bwanji mwasiya ana aamuna kuti akhale ndi moyo?”
19 Ababelethisi basebesithi kuFaro: Ngoba amaHebherukazi kawanjengabafazi bamaGibhithe; ngoba alamandla, umbelethisi engakafiki kuwo, asebelethile.
Azambawo anamuyankha Farao kuti, “Amayi a Chihebri sali ngati amayi a Chiigupto; Iwo ndi amphamvu ndipo amachira azamba asanafike.”
20 Ngalokhu uNkulunkulu wabenzela ababelethisi okuhle, labantu banda, baba lamandla kakhulu.
Kotero Mulungu anawakomera mtima azambawo, ndipo Aisraeli anapitirirabe kuchulukana nakhala amphamvu kwambiri.
21 Kwasekusithi, ngoba ababelethisi bamesaba uNkulunkulu, wabakhela imizi.
Pakuti azambawo ankaopa Mulungu, Iye anawapatsa mabanja awoawo.
22 UFaro waselaya isizwe sakhe sonke esithi: Yonke indodana ezalwayo liyiphosele emfuleni, kodwa yonke indodakazi liyiyekele iphile.
Pamenepo Farao analamulira anthu ake onse kuti, “Mwana wamwamuna aliyense akabadwa, mukamuponye mu mtsinje wa Nailo, koma wamkazi mulekeni akhale ndi moyo.”

< U-Eksodusi 1 >