< U-Esta 8 >
1 Ngalolosuku inkosi uAhasuwerusi yanika uEsta indlovukazi indlu kaHamani isitha samaJuda. UModekhayi wasesiza phambi kwenkosi ngoba uEsta wayeselandisile ukuthi wayeyini kuye.
Tsiku lomwelo mfumu Ahasiwero anamupatsa mfumukazi Estere nyumba ya Hamani, mdani wa Ayuda. Ndipo Mordekai anafika pamaso pa mfumu, popeza Estere anamuwuza ubale wawo.
2 Inkosi yasikhupha indandatho yophawu lwayo eyayiyithathele uHamani, yayinika uModekhayi. UEsta wasebeka uModekhayi phezu kwendlu kaHamani.
Mfumu inavula mphete yake yodindira imene analanda kwa Hamani ndipo Estere anamusankha Mordekai kukhala woyangʼanira nyumba ya Hamani.
3 UEsta wasebuya ekhuluma phambi kwenkosi, wawa phambi kwenyawo zayo wakhala inyembezi wayincenga ukuthi isuse ububi bukaHamani umAgagi, logobe lwakhe ayelucebe ngamaJuda.
Estere anayankhulanso ndi mfumu ndipo anadzigwetsa pa mapazi ake. Uku akulira iye anapempha mfumu kuti iletse choyipa, makamaka chiwembu chimene Hamani Mwagagi anakonza kuti awononge a Yuda.
4 Inkosi yasiselulela intonga yobukhosi yegolide kuEsta. UEsta wasesukuma wema phambi kwenkosi,
Ndipo mfumu inamuloza Estere ndi ndodo yake yagolide ndipo Estere anadzuka ndi kuyima pamaso pake.
5 wasesithi: Uba kukuhle enkosini, uba-ke ngithole umusa phambi kwayo, lodaba lulungile phambi kwenkosi, lami ngilungile emehlweni ayo, kakubhalwe ukubuyisela emuva izincwadi, ugobe lukaHamani indodana kaHamedatha umAgagi, ayelubhalele ukubhubhisa amaJuda asezabelweni zonke zenkosi.
Iye anati, “Ngati chikomera mfumu ndi kukukondweretsani, ngati pempho langa muliona kuti ndi loyenera ndi kuti mukondwera nane tsono mfumu ilole kuti lamulo lilembedwe kusintha mawu a mʼmakalata amene Hamani mwana wa Hamedata, Mwagagi, anatumiza ku zigawo zonse za mfumu. Paja Hamani analemba kuti Ayuda onse awonongedwe.
6 Ngoba ngingaba lakho njani ukubona ububi obuzathola isizwe sakithi? Kumbe ngingaba lakho njani ukubona ukubhujiswa kwezihlobo zami?
Kodi ndingapirire bwanji pamene ndi kuona tsoka likugwera anthu a mtundu wanga? Ndingapirire bwanji pamene abale anga akuwonongedwa?”
7 Inkosi uAhasuwerusi yasisithi kuEsta indlovukazi lakuModekhayi umJuda: Khangelani, indlu kaHamani ngiyinike uEsta, yena-ke bamlengise egodweni, ngenxa yokuthi welulela isandla sakhe kumaJuda.
Mfumu Ahasiwero anamuyankha mfumukazi Estere ndi Mordekai Myuda kuti, “Ndapereka nyumba ya Hamani kwa Estere ndipo Hamaniyo amupachika kale pa mtanda chifukwa anafuna kuwononga Ayuda.
8 Ngakho lina bhalelani amaJuda ebizweni lenkosi, njengokuhle emehlweni enu, likunameke ngophawu lwendandatho yenkosi, ngoba umbhalo obhalwe ngebizo lenkosi wananyekwa ngophawu lwendandatho yenkosi, kakho ongawubuyisela emuva.
Tsono inu awiri, lembani za Ayudawo monga mufunira. Mulembe mʼdzina la mfumu ndipo musindikize chizindikiro cha mphete ya mfumu popeza kuti cholembedwa mʼdzina la mfumu ndi kusindikizidwa ndi chizindikiro cha mphete ya mfumu sichingasinthidwe.”
9 Kwasekubizwa ababhali benkosi ngalesosikhathi ngenyanga yesithathu, eyinyanga uSivani, ngolwamatshumi amabili lantathu lwayo; kwasekubhalwa njengakho konke uModekhayi akulaya kumaJuda, lezikhulwini lakubabusi lakuziphathamandla zezabelo ezisukela eIndiya kuze kufike eEthiyophiya, izabelo ezilikhulu lamatshumi amabili lesikhombisa, isabelo lesabelo njengokombhalo waso, lesizwe ngesizwe njengokolimi lwaso, lakumaJuda njengokombhalo wawo lanjengokolimi lwawo.
Nthawi yomweyo, pa tsiku la 23 la mwezi wachitatu wa Sivani, mfumu inayitana alembi ake. Analemba zonse zokhudza Ayuda monga ananenera Mordekai. Analembera akazembe, abwanamkubwa ndi nduna za zigawo 127 kuyambira ku India mpaka ku Kusi. Zimene analamula Mordekai zinalembedwa mʼzilembo za chigawo chilichonse ndi chiyankhulo cha mtundu uliwonse wa anthu. Ayudanso anawalembera mʼmalemba awo ndi chiyankhulo chawo.
10 Wasebhala ebizweni lenkosi uAhasuwerusi, wanameka ngophawu lwendandatho yenkosi, wathumela izincwadi ngesandla sezigijimi ezigade amabhiza, ezigade amabhiza alejubane awesikhosini, amabhizakazi amatsha.
Mordekai analemba makalatawo mʼdzina la mfumu Ahasiwero, nawadinda ndi chizindikiro cha mphete ya mfumu. Ndipo anawatumiza ndi anthu amithenga amene anakwera pa akavalo a ufumu othamanga kwambiri obadwa mu khola la ufumu.
11 Ukuthi inkosi yavumela amaJuda ayesemzini ngomuzi wonke ukuthi ahlangane amele impilo yawo ukubhubhisa abulale aqede wonke amandla abantu lesabelo abawahlaseleyo, abantwanyana labesifazana, lokuphanga impango yabo,
Mʼmakalata amenewa mfumu inalola kuti Ayuda okhala mu mzinda uliwonse akhale ndi ufulu wokumana ndi kudzitchinjiriza komanso kuwononga, kupha ndi kufafaniziratu gulu lililonse la nkhondo la anthu a mtundu uliwonse kapena chigawo chimene chingawathire nkhondo. Ayudawo analoledwa kuwononga gulu lankhondo lija, ana awo ndi akazi awo komanso kuti afunkhe katundu wawo.
12 ngasuku lunye kuzo zonke izabelo zenkosi uAhasuwerusi, ngolwetshumi lantathu lwenyanga yetshumi lambili, eyinyanga uAdari.
Ayuda analoledwa kuchita zimenezi mʼzigawo zonse za Mfumu Ahasiwero pa tsiku limodzi lokha la 13 la mwezi wa 12, mwezi wa Adara.
13 Ikhophi yombhalo yomthetho ozamiswa kuso sonke isabelo ngesabelo yayisobala kubo bonke abantu, ukuthi amaJuda azilungisele lolusuku ukuziphindiselela ezitheni zawo.
Mawu a mʼmakalatawo anayenera kudziwitsidwa kwa anthu a mtundu uliwonse mu chigawo chilichonse kuti ndi lamulo ndithu kwa anthu a mtundu uliwonse ndi kuti Ayuda adzakhale okonzeka pa tsikulo kulipsira kwa adani awo.
14 Izigijimi zigade amabhiza esikhosini alejubane zaphuma, ziphangisiswa zicindezelwa yilizwi lenkosi, lomthetho wanikwa eShushani isigodlo.
Atawalamulira a mfumu, amithenga aja anapita nawo makalata mwachangu, atakwera pa akavalo a mfumu. Ndipo lamulolo analiperekanso ku likulu la mzinda wa Susa.
15 UModekhayi wasephuma phambi kwenkosi ekusembatho sobukhosi sobuluhlaza okwesibhakabhaka lesimhlophe, lomqhele omkhulu wegolide, lesembatho selembu elicolekileyo kakhulu leliyibubende. Umuzi weShushani wasuthokoza wathaba.
Mordekai anachoka pamaso pa mfumu atavala zovala zaufumu zooneka ngati mtambo ndi zofewa zoyera, chipewa chachikulu cha golide ndi mkanjo wapepo. Ndipo mzinda wa Susa unafuwula mokondwa.
16 AmaJuda ayelokukhanya lentokozo lenjabulo lodumo.
Kwa Ayuda inali nthawi ya nkhope zowala ndi za chimwemwe, chikondwerero ndi ulemu.
17 Lakuso sonke isabelo ngesabelo lakuwo wonke umuzi ngomuzi endaweni lapho ilizwi lenkosi lomthetho wayo okwafika khona amaJuda aba lentokozo, lenjabulo, idili, losuku oluhle. Labanengi babantu belizwe baba ngamaJuda, ngoba ukwesaba amaJuda kwabehlela.
Mʼchigawo chilichonse ndi mu mzinda uliwonse, kumene mawu a mfumu onena za lamulo lake anafika, kunali chimwemwe ndi chikondwerero pakati pa Ayuda. Linali tsiku la phwando ndi chikondwerero. Ndipo anthu ambiri a mitundu ina anazitcha Ayuda chifukwa anachita mantha ndi Ayudawo.