< U-Esta 7 >
1 Bafika-ke inkosi loHamani ukuyakuba ledili loEsta indlovukazi.
Choncho mfumu ndi Hamani anabwera kudzadya phwando la mfumukazi Estere.
2 Inkosi yasisithi kuEsta langosuku lwesibili edilini lewayini: Siyini isicelo sakho, Esta ndlovukazi? njalo uzasinikwa. Siyini-ke isifiso sakho? kuzakwenziwa ngitsho kuze kube yingxenye yombuso.
Pa tsiku lachiwiri akumwa vinyo, mfumu inafunsanso kuti, “Kodi iwe mfumukazi Estere, chimene ufuna kupempha nʼchiyani? Chimene uti upemphe ndidzakupatsa. Choncho ukufuna chiyani? Ngakhale utafuna theka la ufumu ndidzakupatsa.”
3 UEsta indlovukazi wasephendula wathi: Uba ngithole umusa emehlweni akho, nkosi, njalo uba kukuhle enkosini, impilo yami kangiyinikwe ngesicelo sami labantu bakithi ngesifiso sami.
Kenaka mfumukazi Estere anayankha kuti, “Ngati mwandikomera mtima, inu mfumu, ndipo ngati chingakukomereni mfumu, pempho ndi chokhumba changa ndi ichi, mulole kuti ine ndi abale anga tisungidwe tonse ndi moyo.
4 Ngoba sithengisiwe, mina labantu bakithi, ukuthi sibhujiswe sibulawe njalo sichithwe; kodwa uba besithengiswe ukuba yizigqili lezigqilikazi ngabe ngithule; lanxa isitha besingelinganise ukoniwa kwenkosi.
Popeza ine ndi anthu a mtundu wanga tagulitsidwa kuti atiwononge, atiphe ndi kutifafaniziratu. Akanangotigulitsa kokha tikanakhala chete, chifukwa chimene mdani wathuyo akanakupatsani mfumu sibwenzi mutasowa nacho mtendere.”
5 Inkosi uAhasuwerusi yasikhuluma yathi kuEsta indlovukazi: Ngubani lo, futhi ungaphi lo ogcwalise inhliziyo yakhe ukwenza njalo?
Mfumu Ahasiwero anamufunsa mfumukazi Estere, “Kodi iyeyu ndi ndani ndipo ali kuti amene saopa kuchita chinthu chotere?”
6 UEsta wasesithi: Umuntu, umbandezeli lesitha, nguHamani lo okhohlakeleyo. UHamani waseqhaqhazela phambi kwenkosi lendlovukazi.
Estere anati, “Wotizunza ndiponso mdani wathu! Munthu woyipayo ndi Hamani.” Kenaka Hamani anagwidwa ndi mantha pamaso pa mfumu ndi mfumukazi.
7 Inkosi yasisukuma edilini lewayini olakeni lwayo, yaya esivandeni sesigodlo; uHamani wasesukuma ukuncengela impilo yakhe kuEsta indlovukazi, ngoba wabona ukuthi okubi sekuqunywe yinkosi ngaye.
Mfumu itakwiya kwambiri inanyamuka pa phwando nipita ku munda wa maluwa wa nyumba yaufumu. Koma Hamani, pozindikira kuti mfumu yaganiza kale kumuchitira choyipa, anatsalira mʼnyumba kupempha Estere kuti apulumutse moyo wake.
8 Inkosi isiphendukile ivela esivandeni sesigodlo isiya endlini yedili lewayini, uHamani wayewele phezu kombheda uEsta ayekuwo. Inkosi yasisithi: Usuzadlova indlovukazi ilami endlini yini? Ilizwi laphuma emlonyeni wenkosi; basebembomboza ubuso bukaHamani.
Mfumu itabwerera kuchokera ku munda wa maluwa wa nyumba yaufumu uja ndi kulowanso mʼchipinda chaphwando, anapeza Hamani atagona chafufumimba pa mpando wa khutagone pomwe Estere anakhalapo. Mfumu inayankhula mokweza kuti, “Kodi afunanso kuvula mfumukazi momukakamiza pamene ine ndili mʼnyumba?” Mfumu isanatsirize kuyankhula mawu awa, atumiki ake anaphimba nkhope ya Hamani.
9 UHaribona omunye wabathenwa wasesithi phambi kwenkosi: Khangela-ke, ugodo uHamani alwenzele uModekhayi, owayeyikhulumele okuhle inkosi, lumi endlini kaHamani, ubude buzingalo ezingamatshumi amahlanu. Inkosi yasisithi: Umlengiseni kulo.
Haribona, mmodzi wa adindo ofulidwa amene ankatumikira mfumu anati, “Mtanda wotalika mamita 23 uli mʼnyumba ya Hamani. Mtandawu, Hamani anapangira Mordekai, uja amene anapulumutsa mfumu ku chiwembu.” Mfumu inati, “Mpachikeni pamenepo!”
10 Basebemlengisa uHamani kulologodo ayelulungisele uModekhayi. Lwaseludeda ulaka lwenkosi.
Choncho anamupachika Hamani pa mtanda umene anakonzera Mordekai. Kenaka mkwiyo wa mfumu unatsika.