< UDutheronomi 15 >

1 Ekupheleni kweminyaka yonke eyisikhombisa uzakwenza inkululeko.
Kumapeto kwa zaka zisanu ndi ziwiri zilizonse, muzikhululukirana ngongole.
2 Njalo le yindlela yenkululeko: Wonke umkweledisi oweboleka umakhelwane wakhe uzakhulula isikwelede; kayikusibamba ngamandla kumakhelwane wakhe kumbe kumfowabo, ngoba kumenyezelwe inkululeko eNkosini.
Zimenezi muzichita motere: wobwereketsa aliyense adzakhululukira ngongole imene anabwereketsa kwa Mwisraeli mnzake. Iye asadzafunenso kuti Mwisraeli mnzakeyo kapena mʼbale wake amubwezere chifukwa nthawi ya Ambuye yokhululukirana ngongole yalengezedwa.
3 Kowezizweni uzasibamba ngamandla; kodwa lokho okwakho okukumfowenu isandla sakho sizakukhulula;
Mukhoza kulonjerera ngongole kwa mlendo, koma mukhululukire ngongole ina iliyonse imene mʼbale wanu ali nayo.
4 ukuze kungabi lomyanga phakathi kwakho; ngoba iNkosi izakubusisa lokukubusisa elizweni iNkosi uNkulunkulu wakho ekunika lona ukuthi libe yilifa ukudla ilifa lalo,
Komabe pasadzakhale wosauka pakati panu chifukwa Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani kwambiri mʼdziko limene adzakupatsani kuti likhale lanu ngati cholowa chanu.
5 kuphela uba ulalela lokulalela ilizwi leNkosi uNkulunkulu wakho, ugcine ukuyenza limithetho yonke engikulaya yona lamuhla.
Adzakudalitsani pokhapokha ngati mudzamveradi Yehova Mulungu wanu posunga ndi kutsatira malamulo onse amene ndikukupatsani lero.
6 Ngoba iNkosi uNkulunkulu wakho izakubusisa njengokuthembisa kwayo kuwe. Njalo uzakweboleka izizwe ezinengi, kodwa wena kawuyikweboleka kuzo; uzabusa izizwe ezinengi, kodwa wena kaziyikukubusa.
Pakuti Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani monga analonjeza, ndipo inu mudzabwereketsa chuma kwa mitundu yambiri ya anthu koma inu simudzabwereka kwa aliyense. Mudzalamulira mitundu yambiri ya anthu koma inuyo palibe amene adzakulamulireni.
7 Uba kukhona phakathi kwakho umyanga ongomunye wabafowenu, kwelinye lamasango akho, elizweni lakho, iNkosi uNkulunkulu wakho ekunika lona, ungenzi lukhuni inhliziyo yakho, ungamvaleli umfowenu ongumyanga isandla sakho,
Ngati pali mʼbale wanu wina wosauka mu mzinda wanu wina uliwonse mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, musawumitse mitima yanu kapena kuchita kaligwiritsa kwa mʼbale wanu wosaukayo.
8 kodwa uzamvulela lokumvulela isandla sakho, umeboleke lokumeboleka okwanela ukuswela kwakhe, lokho akuswelayo.
Koma mukhale ofewa manja ndipo mumukongoze mʼbale wanu momasuka pa chilichonse chimene akufuna.
9 Ziqaphele hlezi kube khona ilizwi enhliziyweni yakho embi lisithi: Umnyaka wesikhombisa, umnyaka wenkululeko useduze; lelihlo lakho libe libi limelane lomfowenu ongumyanga, ukuze ungamniki, abesekhala ngawe eNkosini, njalo kube yisono kuwe.
Musayesere ndi pangʼono pomwe kusunga maganizo oyipa awa mu mtima mwanu: “Chaka chachisanu ndi chiwiri, chaka chokhululukirana ngongole, chayandikira,” kuti musaonetse mtima woyipa kwa mʼbale wanu wosauka nʼkusamupatsa chilichonse. Iye angadzakunenereni inu mlandu kwa Ambuye, ndipo mudzapezeka wochimwa.
10 Umnike lokumnika, lenhliziyo yakho ingadani nxa umnika; ngoba ngenxa yalinto iNkosi uNkulunkulu wakho izakubusisa emsebenzini wonke wakho lakukho konke obeka kukho isandla sakho.
Mumupatse iye mowolowamanja ndipo muchite zimenezi mosasungira kanthu kumtima. Tsono chifukwa cha zimenezi, Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani pa ntchito zanu zonse ndi pa chilichonse chimene mukhudza.
11 Ngoba umyanga kayikuphela phakathi kwelizwe. Ngakho ngiyakulaya ngithi: Uzamvulela kakhulu isandla sakho umfowenu, umyanga wakho, loswelayo wakho, elizweni lakho.
Anthu osauka sadzatha mʼdziko lanu. Chomwecho ndikukulamulani kuti mukhale ofewa manja kwa abale anu ndi kwa osauka, osowa mʼdziko mwanu.
12 Uba umfowenu, umHebheru loba umHebherukazi, ethengiswa kuwe, akusebenzele iminyaka eyisithupha, ngakho ngomnyaka wesikhombisa uzamyekela ukuthi ahambe ekhululekile asuke kuwe.
Ngati mʼbale wanu wamwamuna kapena wamkazi adzigulitsa yekha kwa inu, nakugwirirani ntchito zaka zisanu ndi chimodzi, muzimumasula mʼchaka cha chisanu ndi chiwiri.
13 Lalapho umyekela ukuthi ahambe ekhululekile esuka kuwe, ungamyekeli ukuthi ahambe engaphathanga lutho;
Ndipo pamene mumumasula, musangomulola apite chimanjamanja.
14 uzamnakekela lokumnakekela ezimvini zakho, lokwebala lokubhulela lakho, lokwesikhamelo sakho sewayini; kulokho iNkosi uNkulunkulu wakho ekubusise ngakho uzamupha.
Mumupatse mowolowamanja zochokera pa ziweto zanu, kopunthira tirigu ndi kopsinyira vinyo. Inu mumupatse iye monga Yehova Mulungu wanu wakudalitsirani.
15 Njalo uzakhumbula ukuthi wawuyisigqili elizweni leGibhithe, lokuthi iNkosi uNkulunkulu wakho yakuhlenga. Ngalokho ngiyakulaya linto lamuhla.
Kumbukirani kuti munali akapolo mʼdziko la Igupto ndipo Yehova Mulungu wanu anakupulumutsani. Nʼchifukwa chake ndikukupatsani lamulo ili lero lino.
16 Kodwa kuzakuthi, uba esithi kuwe: Kangiyikusuka kuwe, ngoba ethanda wena lendlu yakho, ngoba kulungile kuye elawe,
Koma ngati kapoloyo akuwuzani kuti, “Ine sindikufuna kumasulidwa,” chifukwa choti wakukondani inuyo pamodzi ndi banja lanu ndiponso kuti kwamukomera iyeyo kuti azikhalabe nanu,
17 uzathatha usungulo, ubhobozele indlebe yakhe ngalo esivalweni, ukuze abe yisigqili sakho laphakade. Lakuso isigqilikazi sakho wenze njalo.
pamenepo muzitenga chobowolera chachitsulo ndi kubowola khutu lake pa chitseko, ndipo mukatero adzakhala kapolo wanu moyo wake wonse. Mdzakazi wanu muzimuchitanso chimodzimodzi.
18 Kakungabi lukhuni emehlweni akho nxa umyekela ehamba ekhululekile kuwe; ngoba ngokuphindwe kabili kweholo lesiqatshwa ukusebenzele iminyaka eyisithupha. Ngakho iNkosi uNkulunkulu wakho izakubusisa kukho konke okwenzayo.
Musaone ngati chopweteka kumasula wantchito wanu, chifukwa ntchito imene wayigwira pa zaka zisanu ndi chimodzi zimenezi ndi yopindula kawiri pa ntchito imene akanagwira waganyu chabe. Ndipo Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani pa chilichonse chimene mukuchita.
19 Wonke amazibulo azazalwa enkomeni zakho lezimvini zakho, amaduna, uzawangcwelisela iNkosi uNkulunkulu wakho; kawuyikusebenza ngezibulo lejongosi lakho, futhi kawuyikugunda izibulo lezimvu zakho.
Mumupatulire Yehova Mulungu wanu choyamba kubadwa chachimuna chilichonse pa ngʼombe ndi nkhosa zanu. Musamazigwiritse ntchito ngʼombe zoyamba kubadwa kapena kumeta nkhosa zoyamba kubadwa.
20 Phambi kweNkosi uNkulunkulu wakho uzalidla, umnyaka ngomnyaka, endaweni iNkosi ezayikhetha, wena lendlu yakho.
Inuyo ndi banja lanu, chaka chilichonse muzizidya zimenezi pamaso pa Yehova Mulungu wanu pa malo amene Iye adzasankhe.
21 Kodwa uba kulesici kulo, liqhula, loba liyisiphofu, loba lilasiphi isici esibi, ungalihlabeli iNkosi uNkulunkulu wakho.
Ngati chiweto chili ndi chilema monga kulumala kapena chosaona, kapena ngati chili ndi cholakwika chachikulu chilichonse, musachipereke nsembe kwa Yehova Mulungu wanu.
22 Uzalidla phakathi kwamasango akho, ongahlambulukanga lohlambulukileyo bazalidla bendawonye, njengomziki lanjengendluzele.
Muzichidya mʼmizinda yanuyanu. Onse odetsedwa monga mwa mwambo ndi oyeretsedwa omwe akhoza kuchidya monga akudya gwape kapena mbawala.
23 Kuphela igazi lalo ungalidli; ulichithele emhlabathini njengamanzi.
Koma musadye magazi ake. Muwathire pansi ngati madzi.

< UDutheronomi 15 >