< Nahoma 1 >
1 Ty talily i Ninevè. Ty boken’ aroñaro’ i Nakòme nte-Elkose.
Uthenga wonena za Ninive. Buku la masomphenya a Nahumu wa ku Elikosi.
2 Mpamarahy t’i Andrianañahare, Mpamale fate t’Iehovà; Mpañondroke miforoforo t’Iehovà; Mpañava-kabò amo rafelahi’eo t’Iehovà, ie mañaja haviñerañe amo malaiñe azeo.
Yehova ndi Mulungu wansanje ndiponso wobwezera; Yehova amabwezera ndipo ndi waukali. Yehova amabwezera adani ake ndipo ukali wake umakhala nthawi zonse pa adani akewo.
3 Malaon-kaviñerañe t’Iehovà, ra’elahy ty haozara’e, fe tsy hapò’e tsy ho lafaeñe o aman-kakeoo; Iehovà: amo tangololahio o lala’eo, naho ami’ty tio-bey ao; o rahoñeo ro debom-pandia’e.
Yehova sakwiya msanga koma ndi wa mphamvu yayikulu; ndipo sadzalola kuti munthu wolakwa asalangidwe. Iye amayenda mʼkamvuluvulu ndi mʼnamondwe, ndipo mitambo ndi fumbi la ku mapazi ake.
4 Endaha’e i riakey le ampimaihe’e, ampikarakankaiñe’e o sakao; rinotsake t’i Basane naho i Karmele; miheatse ty voñen-katae’ i Libanone.
Amalamulira nyanja ndipo imawuma; amawumitsa mitsinje yonse. Zomera za ku Basani ndi Karimeli zimawuma ndipo maluwa a ku Lebanoni amafota.
5 Miezeñezeñe aolo’e eo o vohitseo, mitranake iaby o haboañeo, forototo ty tane toy ami’ty fiatrefa’e, ty voatse toy naho ze mpimoneñe ama’e ao.
Mapiri amagwedera pamaso pake ndipo zitunda zimasungunuka. Dziko lapansi limanjenjemera pamaso pake, dziko lonse ndi zonse zokhala mʼmenemo.
6 Ia ty mahafijohañe añatrefa’ o fifombo’eo? Ia ty mahatambeloñe amy fiforoforoan-kaviñera’ey? Ailiñe hoe afo ty filevelevea’e, avokovoko’e ambane iaby ze vato.
Ndani angathe kuyima pamaso pake Iye akalusa? Ndani angapirire mkwiyo wake woopsa? Ukali wake ukuyaka ngati moto; matanthwe akunyeka pamaso pake.
7 Soa t’Iehovà, fipalirañe añ’andron-kankàñe; arofoana’e iaby o miato ama’eo.
Yehova ndi wabwino, ndiye kothawirako nthawi ya masautso. Amasamalira amene amamudalira,
8 F’ie an-tsorotombahañe mivovò, ty hamongora’e i toe’ey, vaho ho roahe’e mb’ an-kamoromoroñañe ao o rafelahi’eo.
koma ndi madzi achigumula choopsa Iye adzawononga adani ake (Ninive); adzapirikitsira adani ake ku malo a mdima.
9 Ino ze o fikililia’ areo am’ Iehovà zao? Fa harotsa’e, tsy hiongake fañindroe’e ty hekoheko.
Chiwembu chilichonse chimene akukonzekera kumuchitira Yehova adzachiwononga kotheratu; msautso sudzabweranso kachiwiri.
10 Fa manahake ty fivandiram-patike naho ty hamamoa’ o jikeo, ty hampangotomomoheñe iereo hoe ahe-maike.
Iwo adzakodwa mu ziyangoyango za minga ndipo adzaledzera ndi vinyo wawo; adzatenthedwa ngati ziputu zowuma.
11 Boak’ ama’o ty niavia’ i nikitro-draha am’ Iehovày, ie mañeretse hatsivokarañe.
Kwa iwe, Ninive, kunachokera munthu wa cholinga choyipa, wofuna kuchitira Yehova chiwembu, amene amapereka uphungu woyipa.
12 Hoe t’Iehovà: ndra t’ie lifo-kaozarañe, naho mitozantozañe, mbe hampikorovoheñe, vaho hihelañe añe; fa ndra te nanilofeko irehe, tsy ho silofeko ka.
Yehova akuti, “Ngakhale Asiriyawo ali ndi abwenzi, kaya iwowo ndi ambiri, koma adzawonongedwa ndi kutheratu. Ngakhale ndinakuzunza iwe Yuda, sindidzakuzunzanso.
13 Hapozako ama’o henaneo ty joka’e, vaho ho rafadrafateko o tali-randra’oo.
Tsopano ndidzathyola goli lake pa khosi lako ndipo ndidzadula maunyolo ako.”
14 Fa nandily ty ama’o t’Iehovà, te tsy ho tongisañe ka ty tahina’o; le haitoako amy akiban-drahare’oy ty sare sokin-katae naho ty sare natranake; f’ie hanoako kibory, amy t’ie tsy manjofake.
Yehova walamulira za iwe, Ninive kuti, “Sudzakhala ndi zidzukulu zimene zidzadziwike ndi dzina lako. Ndidzawononga zifanizo zosema ndi mafano owumba amene ali mʼnyumba ya milungu yako. Ine ndidzakukumbira manda chifukwa ndiwe woyipitsitsa.”
15 Hehek’ an-kaboañe ey o fandia’ i mpinday talily soaio, i mampiboele fifampilongoañey! O ry Iehodà, anò o sabadidake miavakeo, henefo o nifantà’oo; amy te tsy hiranga ama’o ka ty Beliale, fa naitoañe.
Taonani, pa phiripo, mapazi a munthu amene akubweretsa nkhani yabwino, amene akulengeza za mtendere! Inu anthu a ku Yuda, chitani madyerero anu ndipo kwaniritsani malumbiro anu. Anthu oyipa sadzakuthiraninso nkhondo; iwo adzawonongedwa kotheratu.