< Psalmi 45 >
1 Koraha bērnu mīlestības dziesma un pamācība. Dziedātāju vadonim, pēc, „lilijas.“Mana sirds izverd košu vārdu; es dziedāšu Ķēniņam; mana mēle ir veikla rakstītāja rakstāmais.
Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a “Maluwa a Kakombo.” Salimo la ana a Kora. Nyimbo ya pa ukwati. Mtima wanga watakasika ndi nkhani yokoma pamene ndikulakatula mawu anga kwa mfumu; lilime langa ndi cholembera cha wolemba waluso.
2 Tu esi tas skaistākais starp cilvēku bērniem, Tavas lūpas ir laipnības pilnas, tādēļ Dievs Tevi svētī mūžīgi.
Inu ndinu abwino kwambiri kuposa anthu onse ndipo milomo yanu inadzozedwa ndi chikondi cha Mulungu chosasinthika, popeza Mulungu wakudalitsani kwamuyaya.
3 Apjozi Savu zobenu pie Saviem gurniem, Tu varenais, Savu godību un jaukumu.
Mangirirani lupanga lanu mʼchiwuno mwanu, inu munthu wamphamvu; mudziveke nokha ndi ulemerero ndi ukulu wanu.
4 Lai Tev labi izdodas Tavā godībā, celies patiesībai, lēnībai un taisnībai par labu, tad Tava labā roka Tev mācīs brīnuma darbus.
Mu ukulu wanu mupite mutakwera mwachigonjetso mʼmalo mwa choonadi, kudzichepetsa ndi chilungamo; dzanja lanu lamanja lionetsere ntchito zanu zoopsa.
5 Tavas bultas ir asas ķēniņa ienaidnieku sirdī; tautas apakš Tevis kritīs.
Mivi yanu yakuthwa ilase mitima ya adani a mfumu, mitundu ya anthu igwe pansi pa mapazi anu.
6 Tavs godības krēsls, ak Dievs, paliek mūžīgi mūžam, Tavas valstības scepteris ir taisns scepteris.
Mpando wanu waufumu, Inu Mulungu, udzakhala ku nthawi za nthawi; ndodo yaufumu yachilungamo idzakhala ndodo yaufumu ya ufumu wanu.
7 Tu mīļo taisnību un ienīsti bezdievību, tādēļ Dievs, Tavs Dievs, Tevi svaidījis ar prieka eļļu pāri pār Taviem biedriem.
Inu mumakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa; choncho Mulungu, Mulungu wanu, wakukhazikani pamwamba pa anzanu pokudzozani ndi mafuta a chimwemwe.
8 Visas Tavas drēbes ir(smaržu pilnas ar) mirres, alvejas un kasija(kanēlis), ziloņkaulu namos stīgu spēles Tevi iepriecina.
Mikanjo yanu yonse ndi yonunkhira ndi mure ndi aloe ndi kasiya; kuchokera ku nyumba zaufumu zokongoletsedwa ndi mnyanga wanjovu nyimbo za zoyimbira zazingwe zimakusangalatsani.
9 Tavā glītumā staigā ķēniņu meitas, brūte stāv Tev pa labo roku šķīstā Ofira zeltā.
Ana aakazi a mafumu ali pakati pa akazi anu olemekezeka; ku dzanja lanu lamanja kuli mkwatibwi waufumu ali mu golide wa ku Ofiri.
10 Klausies, meita, un redzi un griez šurp savas ausis, un aizmirsti savus ļaudis un sava tēva namu.
Tamvera, iwe mwana wa mkazi ganizira ndipo tchera khutu; iwala anthu ako ndi nyumba ya abambo ako.
11 Tad Ķēniņam patiks tavs skaistums, jo Viņš ir tavs Kungs, un tev būs Viņu pielūgt.
Mfumu yathedwa nzeru chifukwa cha kukongola kwako; mulemekeze pakuti iyeyo ndiye mbuye wako.
12 Cora meita būs klāt ar dāvanām, bagāti ļaudis tavā priekšā pielūgs.
Mwana wa mkazi wa ku Turo adzabwera ndi mphatso, amuna a chuma adzafunafuna kukoma mtima kwako.
13 Viscaur skaistums ir ķēniņa meitas pilī, viņas apģērbs ir no rakstīta zelta darba!
Wokongola kwambiri ndi mwana wa mfumu ali mʼchipinda mwake, chovala chake ndi cholukidwa ndi thonje ndi golide.
14 Izrakstītās drēbēs viņa top vadīta pie Ķēniņa, viņas draudzenes, tās jaunavas, kas iet viņai pakaļ, top vestas pie Tevis!
Atavala zovala zamaluwamaluwa akupita naye kwa mfumu; anamwali okhala naye akumutsatira ndipo abweretsedwa kwa inu.
15 Ar prieku un līksmību tās top vadītas, un ieiet Ķēniņa pilī.
Iwo akuwaperekeza ndi chimwemwe ndi chisangalalo; akulowa mʼnyumba yaufumu.
16 Tavu tēvu vietā Tev būs dēli, tos Tu celsi par lieliem kungiem pār visu zemi.
Ana ako aamuna adzatenga malo a makolo ako; udzachititsa kuti akhale ana a mfumu mʼdziko lonse.
17 Es pieminēšu Tavu vārdu uz visiem radu radiem, tādēļ tautas Tevi teiks mūžīgi mūžam.
Ndidzabukitsa mbiri yako mʼmibado yonse; choncho mitundu yonse idzakutamanda ku nthawi za nthawi.