< Psalmi 44 >

1 Koraha bērnu pamācība. Dziedātāju vadonim. Dievs, ar savām ausīm mēs to esam dzirdējuši, mūsu tēvi to mums ir teikuši: vienu darbu Tu esi darījis viņu laikā sendienās.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora. Ife tamva ndi makutu athu, Inu Mulungu; makolo athu atiwuza zimene munachita mʼmasiku awo, masiku akalekalewo.
2 Ar savu roku pagānus Tu esi izdzinis, bet viņus Tu esi dēstījis; tautas Tu esi mocījis, bet viņus Tu esi izplatījis.
Ndi dzanja lanu munathamangitsa mitundu ya anthu ena ndi kudzala makolo athu; Inu munakantha mitundu ya anthu, koma makolo athuwo Inu munawapatsa ufulu.
3 Jo tie to zemi caur savu zobenu nav iemantojuši, un viņu elkonis tiem nav palīdzējis, bet Tava labā roka un Tavs elkonis un Tava vaiga gaišums, jo Tev bija labs prāts pie tiem.
Sanalande dziko ndi lupanga lawo, si mkono wawo umene unawabweretsera chigonjetso, koma ndi dzanja lanu lamanja, mkono wanu ndi kuwala kwa nkhope yanu, pakuti munawakonda.
4 Tu tas esi, ak Dievs, mans ķēniņš; sūti Jēkabam pestīšanu.
Inu ndinu Mfumu yanga ndi Mulungu wanga amene mumalamulira chigonjetso cha Yakobo.
5 Ar Tevi mēs gribam sadauzīt savus ienaidniekus, Tavā vārdā gribam samīt, kas mums ceļas pretim.
Kudzera kwa inu ife timabweza adani athu; kudzera mʼdzina lanu timapondereza otiwukirawo.
6 Jo es neceru uz savu stopu, un mans zobens man nevar palīdzēt.
Sindidalira uta wanga, lupanga langa silindibweretsera chigonjetso;
7 Bet Tu mūs izglābi no mūsu pretiniekiem, un Tu mūsu ienaidniekus lieci kaunā.
koma Inu mumatigonjetsera adani athu, mumachititsa manyazi amene amadana nafe.
8 Ar Dievu mēs lielāmies cauru dienu un pateicamies Tavam vārdam mūžīgi. (Sela)
Timanyadira mwa Mulungu wathu tsiku lonse, ndipo tidzatamanda dzina lanu kwamuyaya.
9 Bet nu Tu mūs atstūmi un lieci mūs kaunā un neizej ar mūsu karaspēku.
Koma tsopano mwatikana ndi kutichepetsa; Inu simupitanso ndi ankhondo athu.
10 Tu mūs dzeni atpakaļ priekš mūsu pretiniekiem, ka mūsu ienaidnieki mūs aplaupa.
Munachititsa ife kubwerera mʼmbuyo pamaso pa mdani ndipo amene amadana nafe atilanda katundu.
11 Tu mūs nodevi kā avis par barību, un mūs izkaisi starp pagāniem.
Inu munatipereka kuti tiwonongedwe monga nkhosa ndipo mwatibalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina.
12 Tu pārdevi Savus ļaudis pa velti, un nespriedi priekš viņiem nekādas maksas.
Inu munagulitsa anthu anu pa mtengo wotsika, osapindulapo kanthu pa malondawo.
13 Tu mūs cēli par apsmieklu mūsu kaimiņiem, par nievāšanu un apmēdīšanu tiem, kas ir ap mums.
Mwachititsa kuti tikhale chochititsa manyazi kwa anthu a mitundu ina, chonyozeka ndi chothetsa nzeru kwa iwo amene atizungulira.
14 Tu mūs dari par sakāmu vārdu starp pagāniem, ka tautas par mums galvu krata.
Mwachititsa kuti tikhale onyozeka pakati pa anthu a mitundu ina; anthu amapukusa mitu yawo akationa.
15 Cauru dienu mans negods man ir klāt, un kauns apklāj manu vaigu
Manyazi anga ali pamaso panga tsiku lonse ndipo nkhope yanga yaphimbidwa ndi manyazi
16 Mēdītāju un zaimotāju valodas pēc, ienaidnieku un atriebēju dēļ.
chifukwa cha mawu otonza a iwo amene amandinyoza ndi kundichita chipongwe, chifukwa cha mdani amene watsimikiza kubwezera.
17 Viss tas mums uzgājis, taču mēs Tevi neesam aizmirsuši, nedz viltīgi darījuši pret Tavu derību.
Zonsezi zinatichitikira ngakhale kuti ifeyo sitinayiwale Inu kapena kuonetsa kusakhulupirika pa pangano lanu.
18 Mūsu sirds nav atpakaļ griezusies, nedz mūsu soļi noklīduši no Taviem ceļiem,
Mitima yathu sinabwerere mʼmbuyo; mapazi athu sanatayike pa njira yanu.
19 Ka Tu mūs tā satriec zvēru vidū, un mūs apklāj ar nāves ēnu.
Koma Inu mwatiphwanya ndi kuchititsa kuti tikhale ozunzidwa ndi ankhandwe ndipo mwatiphimba ndi mdima waukulu.
20 Ja mēs būtu aizmirsuši sava Dieva vārdu, un pacēluši savas rokas uz kādu svešu dievu,
Tikanayiwala dzina la Mulungu wathu kapena kutambasulira manja athu kwa mulungu wachilendo,
21 Vai Dievs to nevarētu samanīt? Jo Viņš zina sirds noslēpumus.
kodi Mulungu wathu sakanazidziwa zimenezi, pakuti Iye amadziwa zinsinsi zamumtima?
22 Bet Tevis pēc mēs topam nāvēti visaugošu dienu, un topam turēti līdzi kaujamām avīm.
Komabe chifukwa cha Inu timakumana ndi imfa tsiku lonse, tili ngati nkhosa zoyenera kuti ziphedwe.
23 Uzmosties, Kungs, kāpēc Tu guli? Mosties, neatstum mūžīgi.
Dzukani Ambuye! Nʼchifukwa chiyani mukugona! Dziwutseni nokha! Musatikane kwamuyaya.
24 Kāpēc Tu apslēpi Savu vaigu un aizmirsti mūsu bēdas un mokas?
Nʼchifukwa chiyani mukubisa nkhope yanu, ndi kuyiwala mavuto athu ndi kuponderezedwa kwathu?
25 Jo mūsu dvēsele ir nospiesta pīšļos, mūsu vēders līp pie zemes.
Tatsitsidwa pansi mpaka pa fumbi; matupi athu amatirira pa dothi.
26 Celies mums par palīgu, un izglāb mūs Savas žēlastības dēļ.
Imirirani ndi kutithandiza, tiwomboleni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.

< Psalmi 44 >