< Psalmorum 120 >

1 Canticum graduum. Ad Dominum cum tribularer clamavi: et exaudivit me.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndimafuwulira kwa Yehova mʼmasautso anga, ndipo Iye amandiyankha.
2 Domine libera animam meam a labiis iniquis, et a lingua dolosa.
Pulumutseni Yehova ku milomo yabodza, ndi kwa anthu achinyengo.
3 Quid detur tibi, aut quid apponatur tibi ad linguam dolosam?
Kodi adzakuchitani chiyani, ndipo adzawonjezerapo zotani, inu anthu achinyengo?
4 Sagittae potentis acutae, cum carbonibus desolatoriis.
Adzakulangani ndi mivi yakuthwa ya munthu wankhondo, ndi makala oyaka a mtengo wa tsanya.
5 Heu mihi, quia incolatus meus prolongatus est: habitavi cum habitantibus Cedar:
Tsoka ine kuti ndimakhala ku Mesaki, kuti ndimakhala pakati pa matenti a ku Kedara!
6 multum incola fuit anima mea.
Kwa nthawi yayitali ndakhala pakati pa iwo amene amadana ndi mtendere.
7 Cum his, qui oderunt pacem, eram pacificus: cum loquebar illis, impugnabant me gratis.
Ine ndine munthu wamtendere; koma ndikamayankhula, iwo amafuna nkhondo.

< Psalmorum 120 >