< Psalmorum 119 >

1 Alleluia. ALEPH. Beati immaculati in via: qui ambulant in lege Domini.
Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
2 Beati, qui scrutantur testimonia eius: in toto corde exquirunt eum.
Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
3 Non enim qui operantur iniquitatem, in viis eius ambulaverunt.
Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
4 Tu mandasti mandata tua custodiri nimis.
Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
5 Utinam dirigantur viae meae, ad custodiendas iustificationes tuas.
Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
6 Tunc non confundar, cum perspexero in omnibus mandatis tuis.
Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
7 Confitebor tibi in directione cordis: in eo quod didici iudicia iustitiae tuae.
Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
8 Iustificationes tuas custodiam: non me derelinquas usquequaque.
Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
9 BETH. In quo corrigit adolescentior viam suam? in custodiendo sermones tuos.
Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
10 In toto corde meo exquisivi te: ne repellas me a mandatis tuis.
Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
11 In corde meo abscondi eloquia tua: ut non peccem tibi.
Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
12 Benedictus es Domine: doce me iustificationes tuas.
Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
13 In labiis meis, pronunciavi omnia iudicia oris tui.
Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
14 In via testimoniorum tuorum delectatus sum, sicut in omnibus divitiis.
Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
15 In mandatis tuis exercebor: et considerabo vias tuas.
Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
16 In iustificationibus tuis meditabor: non obliviscar sermones tuos.
Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
17 GHIMEL. Retribue servo tuo, vivifica me: et custodiam sermones tuos.
Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
18 Revela oculos meos: et considerabo mirabilia de lege tua.
Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
19 Incola ego sum in terra: non abscondas a me mandata tua.
Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
20 Concupivit anima mea desiderare iustificationes tuas, in omni tempore.
Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
21 Increpasti superbos: maledicti qui declinant a mandatis tuis.
Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
22 Aufer a me opprobrium, et contemptum: quia testimonia tua exquisivi.
Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
23 Etenim sederunt principes, et adversum me loquebantur: servus autem tuus exercebatur in iustificationibus tuis.
Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
24 Nam et testimonia tua meditatio mea est: et consilium meum iustificationes tuae.
Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
25 DALETH. Adhaesit pavimento anima mea: vivifica me secundum verbum tuum.
Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
26 Vias meas enunciavi, et exaudisti me: doce me iustificationes tuas.
Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
27 Viam iustificationum tuarum instrue me: et exercebor in mirabilibus tuis.
Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
28 Dormitavit anima mea prae taedio: confirma me in verbis tuis.
Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
29 Viam iniquitatis amove a me: et de lege tua miserere mei.
Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
30 Viam veritatis elegi: iudicia tua non sum oblitus.
Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
31 Adhaesi testimoniis tuis Domine: noli me confundere.
Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
32 Viam mandatorum tuorum cucurri, cum dilatasti cor meum.
Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
33 HE. Legem pone mihi Domine viam iustificationum tuarum: et exquiram eam semper.
Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
34 Da mihi intellectum, et scrutabor legem tuam: et custodiam illam in toto corde meo.
Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
35 Deduc me in semitam mandatorum tuorum: quia ipsam volui.
Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
36 Inclina cor meum in testimonia tua: et non in avaritiam.
Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
37 Averte oculos meos ne videant vanitatem: in via tua vivifica me.
Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
38 Statue servo tuo eloquium tuum, in timore tuo.
Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
39 Amputa opprobrium meum, quod suspicatus sum: quia iudicia tua iucunda.
Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
40 Ecce concupivi mandata tua: in aequitate tua vivifica me.
Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
41 VAU. Et veniat super me misericordia tua Domine: salutare tuum secundum eloquium tuum.
Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
42 Et respondebo exprobrantibus mihi verbum: quia speravi in sermonibus tuis.
ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
43 Et ne auferas de ore meo verbum veritatis usquequaque: quia in iudiciis tuis supersperavi.
Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
44 Et custodiam legem tuam semper: in saeculum et in saeculum saeculi.
Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
45 Et ambulabam in latitudine: quia mandata tua exquisivi.
Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
46 Et loquebar in testimoniis tuis in conspectu regum: et non confundebar.
Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
47 Et meditabar in mandatis tuis, quae dilexi.
popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
48 Et levavi manus meas ad mandata tua, quae dilexi: et exercebor in iustificationibus tuis.
Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
49 ZAIN. Memor esto verbi tui servo tuo, in quo mihi spem dedisti.
Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
50 Haec me consolata est in humilitate mea: quia eloquium tuum vivificavit me.
Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
51 Superbi inique agebant usquequaque: a lege autem tua non declinavi.
Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
52 Memor fui iudiciorum tuorum a saeculo Domine: et consolatus sum.
Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
53 Defectio tenuit me, pro peccatoribus derelinquentibus legem tuam.
Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
54 Cantabiles mihi erant iustificationes tuae, in loco peregrinationis meae.
Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
55 Memor fui nocte nominis tui Domine: et custodivi legem tuam.
Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
56 Haec facta est mihi: quia iustificationes tuas exquisivi.
Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
57 HETH. Portio mea Domine, dixi custodire legem tuam.
Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
58 Deprecatus sum faciem tuam in toto corde meo: miserere mei secundum eloquium tuum.
Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
59 Cogitavi vias meas: et converti pedes meos in testimonia tua.
Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
60 Paratus sum, et non sum turbatus: ut custodiam mandata tua.
Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
61 Funes peccatorum circumplexi sunt me: et legem tuam non sum oblitus.
Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
62 Media nocte surgebam ad confitendum tibi, super iudicia iustificationis tuae.
Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
63 Particeps ego sum omnium timentium te: et custodientium mandata tua.
Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
64 Misericordia tua Domine plena est terra: iustificationes tuas doce me.
Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
65 TETH. Bonitatem fecisti cum servo tuo Domine, secundum verbum tuum.
Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
66 Bonitatem, et disciplinam, et scientiam doce me: quia mandatis tuis credidi.
Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
67 Priusquam humiliarer ego deliqui: propterea eloquium tuum custodivi.
Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
68 Bonus es tu: et in bonitate tua doce me iustificationes tuas.
Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
69 Multiplicata est super me iniquitas superborum: ego autem in toto corde scrutabor mandata tua.
Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
70 Coagulatum est sicut lac cor eorum: ego vero legem tuam meditatus sum.
Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
71 Bonum mihi quia humiliasti me: ut discam iustificationes tuas.
Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
72 Bonum mihi lex oris tui, super millia auri, et argenti.
Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
73 IOD. Manus tuae fecerunt me, et plasmaverunt me: da mihi intellectum, ut discam mandata tua.
Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
74 Qui timent te videbunt me, et laetabuntur: quia in verba tua supersperavi.
Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
75 Cognovi Domine quia aequitas iudicia tua: et in veritate tua humiliasti me.
Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
76 Fiat misericordia tua ut consoletur me, secundum eloquium tuum servo tuo.
Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
77 Veniant mihi miserationes tuae, et vivam: quia lex tua meditatio mea est.
Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
78 Confundantur superbi, quia iniuste iniquitatem fecerunt in me: ego autem exercebor in mandatis tuis.
Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
79 Convertantur mihi timentes te: et qui noverunt testimonia tua.
Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
80 Fiat cor meum immaculatum in iustificationibus tuis, ut non confundar.
Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
81 CAPH. Defecit in salutare tuum anima mea: et in verbum tuum supersperavi.
Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
82 Defecerunt oculi mei in eloquium tuum, dicentes: Quando consolaberis me?
Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
83 Quia factus sum sicut uter in pruina: iustificationes tuas non sum oblitus.
Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
84 Quot sunt dies servi tui: quando facies de persequentibus me iudicium?
Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
85 Narraverunt mihi iniqui fabulationes: sed non ut lex tua.
Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
86 Omnia mandata tua veritas: iniqui persecuti sunt me, adiuva me.
Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
87 Paulominus consummaverunt me in terra: ego autem non dereliqui mandata tua.
Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
88 Secundum misericordiam tuam vivifica me: et custodiam testimonia oris tui.
Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
89 LAMED. In aeternum Domine, verbum tuum permanet in caelo.
Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
90 In generatione et generationem veritas tua: fundasti terram, et permanet.
Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
91 Ordinatione tua perseverat dies: quoniam omnia serviunt tibi.
Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
92 Nisi quod lex tua meditatio mea est: tunc forte periissem in humilitate mea.
Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
93 In aeternum non obliviscar iustificationes tuas: quia in ipsis vivificasti me.
Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
94 Tuus sum ego, salvum me fac: quoniam iustificationes tuas exquisivi.
Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
95 Me expectaverunt peccatores ut perderent me: testimonia tua intellexi.
Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
96 Omnis consummationis vidi finem: latum mandatum tuum nimis.
Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
97 MEM. Quomodo dilexi legem tuam Domine? tota die meditatio mea est.
Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
98 Super inimicos meos prudentem me fecisti mandato tuo: quia in aeternum mihi est.
Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
99 Super omnes docentes me intellexi: quia testimonia tua meditatio mea est.
Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
100 Super senes intellexi: quia mandata tua quaesivi.
Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
101 Ab omni via mala prohibui pedes meos: ut custodiam verba tua.
Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
102 A iudiciis tuis non declinavi: quia tu legem posuisti mihi.
Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
103 Quam dulcia faucibus meis eloquia tua, super mel ori meo!
Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
104 A mandatis tuis intellexi: propterea odivi omnem viam iniquitatis.
Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
105 NUN. Lucerna pedibus meis verbum tuum, et lumen semitis meis.
Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
106 Iuravi, et statui custodire iudicia iustitiae tuae.
Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
107 Humiliatus sum usquequaque Domine: vivifica me secundum verbum tuum.
Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
108 Voluntaria oris mei beneplacita fac Domine: et iudicia tua doce me.
Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
109 Anima mea in manibus meis semper: et legem tuam non sum oblitus.
Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
110 Posuerunt peccatores laqueum mihi: et de mandatis tuis non erravi.
Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
111 Hereditate acquisivi testimonia tua in aeternum: quia exultatio cordis mei sunt.
Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
112 Inclinavi cor meum ad faciendas iustificationes tuas in aeternum, propter retributionem.
Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
113 SAMECH. Iniquos odio habui: et legem tuam dilexi.
Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
114 Adiutor, et susceptor meus es tu: et in verbum tuum supersperavi.
Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
115 Declinate a me maligni: et scrutabor mandata Dei mei.
Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
116 Suscipe me secundum eloquium tuum, et vivam: et non confundas me ab expectatione mea.
Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
117 Adiuva me, et salvus ero: et meditabor in iustificationibus tuis semper.
Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
118 Sprevisti omnes discedentes a iudiciis tuis: quia iniusta cogitatio eorum.
Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
119 Praevaricantes reputavi omnes peccatores terrae: ideo dilexi testimonia tua.
Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
120 Confige timore tuo carnes meas: a iudiciis enim tuis timui.
Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
121 AIN. Feci iudicium et iustitiam: non tradas me calumniantibus me.
Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
122 Suscipe servum tuum in bonum: non calumnientur me superbi.
Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
123 Oculi mei defecerunt in salutare tuum: et in eloquium iustitiae tuae.
Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
124 Fac cum servo tuo secundum misericordiam tuam: et iustificationes tuas doce me.
Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
125 Servus tuus sum ego: da mihi intellectum, ut sciam testimonia tua.
Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
126 Tempus faciendi Domine: dissipaverunt legem tuam.
Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
127 Ideo dilexi mandata tua, super aurum et topazion.
Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
128 Propterea ad omnia mandata tua dirigebar: omnem viam iniquam odio habui.
ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
129 PHE. Mirabilia testimonia tua: ideo scrutata est ea anima mea.
Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
130 Declaratio sermonum tuorum illuminat: et intellectum dat parvulis.
Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
131 Os meum aperui, et attraxi spiritum: quia mandata tua desiderabam.
Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
132 Aspice in me, et miserere mei, secundum iudicium diligentium nomen tuum.
Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
133 Gressus meos dirige secundum eloquium tuum: et non dominetur mei omnis iniustitia.
Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
134 Redime me a calumniis hominum: ut custodiam mandata tua.
Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
135 Faciem tuam illumina super servum tuum: et doce me iustificationes tuas.
Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
136 Exitus aquarum deduxerunt oculi mei: quia non custodierunt legem tuam.
Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
137 SADE. Iustus es Domine: et rectum iudicium tuum.
Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
138 Mandasti iustitiam testimonia tua: et veritatem tuam nimis.
Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
139 Tabescere me fecit zelus meus: quia obliti sunt verba tua inimici mei.
Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
140 Ignitum eloquium tuum vehementer: et servus tuus dilexit illud.
Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
141 Adolescentulus sum ego, et contemptus: iustificationes tuas non sum oblitus.
Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
142 Iustitia tua, iustitia in aeternum: et lex tua veritas.
Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
143 Tribulatio, et angustia invenerunt me: mandata tua meditatio mea est.
Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
144 Aequitas testimonia tua in aeternum: intellectum da mihi, et vivam.
Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
145 COPH. Clamavi in toto corde meo, exaudi me Domine: iustificationes tuas requiram.
Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
146 Clamavi ad te, salvum me fac: ut custodiam mandata tua.
Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
147 Praeveni in maturitate, et clamavi: quia in verba tua supersperavi.
Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
148 Praevenerunt oculi mei ad te diluculo: ut meditarer eloquia tua.
Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
149 Vocem meam audi secundum misericordiam tuam Domine: et secundum iudicium tuum vivifica me.
Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
150 Appropinquaverunt persequentes me iniquitati: a lege autem tua longe facti sunt.
Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
151 Prope es tu Domine: et omnes viae tuae veritas.
Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
152 Initio cognovi de testimoniis tuis: quia in aeternum fundasti ea.
Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
153 RES. Vide humilitatem meam, et eripe me: quia legem tuam non sum oblitus.
Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
154 Iudica iudicium meum, et redime me: propter eloquium tuum vivifica me.
Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
155 Longe a peccatoribus salus: quia iustificationes tuas non exquisierunt.
Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
156 Misericordiae tuae multae Domine: secundum iudicium tuum vivifica me.
Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
157 Multi qui persequuntur me, et tribulant me: a testimoniis tuis non declinavi.
Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
158 Vidi praevaricantes, et tabescebam: quia eloquia tua non custodierunt.
Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
159 Vide quoniam mandata tua dilexi Domine: in misericordia tua vivifica me.
Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
160 Principium verborum tuorum, veritas: in aeternum omnia iudicia iustitiae tuae.
Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
161 SIN. Principes persecuti sunt me gratis: et a verbis tuis formidavit cor meum.
Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
162 Laetabor ego super eloquia tua: sicut qui invenit spolia multa.
Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
163 Iniquitatem odio habui, et abominatus sum: legem autem tuam dilexi.
Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
164 Septies in die laudem dixi tibi, super iudicia iustitiae tuae.
Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
165 Pax multa diligentibus legem tuam: et non est illis scandalum.
Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
166 Expectabam salutare tuum Domine: et mandata tua dilexi.
Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
167 Custodivit anima mea testimonia tua: et dilexit ea vehementer.
Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
168 Servavi mandata tua, et testimonia tua: quia omnes viae meae in conspectu tuo.
Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
169 TAU. Appropinquet deprecatio mea in conspectu tuo Domine: iuxta eloquium tuum da mihi intellectum.
Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
170 Intret postulatio mea in conspectu tuo: secundum eloquium tuum eripe me.
Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
171 Eructabunt labia mea hymnum, cum docueris me iustificationes tuas.
Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
172 Pronunciabit lingua mea eloquium tuum: quia omnia mandata tua aequitas.
Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
173 Fiat manus tua ut salvet me: quoniam mandata tua elegi.
Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
174 Concupivi salutare tuum Domine: et lex tua meditatio mea est.
Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
175 Vivet anima mea, et laudabit te: et iudicia tua adiuvabunt me.
Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
176 Erravi, sicut ovis, quae periit: quaere servum tuum, quia mandata tua non sum oblitus.
Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.

< Psalmorum 119 >