< Proverbiorum 16 >

1 Hominis est animam praeparare: et Domini gubernare linguam.
Zolinga za mu mtima ndi za munthu, koma kwa Yehova ndiye kumachokera yankho.
2 Omnes viae hominis patent oculis eius: spirituum ponderator est Dominus.
Zochita zonse za munthu zimaoneka zabwino pamaso pake, koma Yehova ndiye amasanthula zolinga zako.
3 Revela Domino opera tua, et dirigentur cogitationes tuae.
Pereka ntchito zako zonse mʼmanja mwa Yehova, ndipo zolinga zako zidzachitikadi.
4 Universa propter semetipsum operatus est Dominus: impium quoque ad diem malum.
Yehova amachita zonse ndi cholinga chake, ngakhale anthu oyipa kuti aone tsiku latsoka.
5 Abominatio Domini est omnis arrogans: etiamsi manus ad manum fuerit, non est innocens. Initium viae bonae, facere iustitiam: accepta est autem apud Deum magis, quam immolare hostias.
Munthu aliyense wodzikuza amamunyansa Yehova. Koma dziwani izi: Iwo sadzakhala osalangidwa.
6 Misericordia et veritate redimitur iniquitas: et in timore Domini declinatur a malo.
Chifukwa cha chikondi chosasinthika ndi kukhulupirika, munthu amakhululukidwa machimo ake; chifukwa cha kuopa Yehova munthu amapewa zoyipa.
7 Cum placuerint Domino viae hominis, inimicos quoque eius convertet ad pacem.
Pamene makhalidwe a munthu akondweretsa Yehova, ngakhale adani ake amakhala naye mwa mtendere.
8 Melius est parum cum iustitia, quam multi fructus cum iniquitate.
Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono zozipeza mwachilungamo, kusiyana ndi kukhala ndi zinthu zambiri zozipeza popanda chilungamo.
9 Cor hominis disponit viam suam: sed Domini est dirigere gressus eius.
Mtima wa munthu umalingalira zochita, koma Yehova ndiye amakhazikitsa njira zake.
10 Divinatio in labiis regis, in iudicio non errabit os eius.
Mawu a mfumu ali ngati mawu ochokera kwa Mulungu; ndipo pakamwa pake sipalakwa poweruza mlandu.
11 Pondus et statera iudicia Domini sunt: et opera eius omnes lapides sacculi.
Miyeso ndi masikelo achilungamo zimachokera kwa Yehova; miyala yonse yoyesera ya mʼthumba anayipanga ndi Yehova.
12 Abominabiles regi qui agunt impie: quoniam iustitia firmatur solium.
Kuchita zoyipa kumanyansa mafumu, pakuti chilungamo ndiye maziko a ufumu wake.
13 Voluntas regum labia iusta: qui recta loquitur, diligetur:
Mawu owona amakondweretsa mfumu. Iyo imakonda munthu woyankhula choonadi.
14 Indignatio regis, nuncii mortis: et vir sapiens placabit eam.
Ukali wa mfumu ndi mthenga wa imfa, koma munthu wanzeru amawupepesa ukaliwo.
15 In hilaritate vultus regis, vita: et clementia eius quasi imber serotinus.
Kuwala kwa nkhope ya mfumu kumapatsa moyo; ndipo kukoma mtima kwake kuli ngati mitambo ya mvula nthawi ya chilimwe.
16 Posside sapientiam, quia auro melior est: et acquire prudentiam, quia pretiosior est argento.
Nʼkwabwino kwambiri kupeza nzeru kupambana golide. Kukhala womvetsa bwino zinthu nʼkwabwino kupambana ndi kukhala ndi siliva.
17 Semita iustorum declinat mala: custos animae suae servat viam suam.
Msewu wa munthu wowongoka mtima umapewa zoyipa; wopenyetsetsa kumene akupita amasunga moyo wake.
18 Contritionem praecedit superbia: et ante ruinam exaltatur spiritus.
Kunyada kumafikitsa ku chiwonongeko, ndipo munthu wodzikuza adzagwa.
19 Melius est humiliari cum mitibus, quam dividere spolia cum superbis.
Nʼkwabwino kukhala ndi mtima wodzichepetsa pakati pa anthu oponderezedwa, kusiyana ndi kugawana zolanda ndi anthu onyada.
20 Eruditus in verbo reperiet bona: et qui sperat in Domino, beatus est.
Munthu womvera malangizo zinthu zimamuyendera bwino, ndipo wodala ndi amene amadalira Yehova.
21 Qui sapiens est corde, appellabitur prudens: et qui dulcis eloquio, maiora reperiet.
A mtima wanzeru amatchedwa ozindikira zinthu, ndipo mawu ake okoma amawonjezera nzeru.
22 Fons vitae eruditio possidentis: doctrina stultorum fatuitas.
Kumvetsa zinthu ndi kasupe wa moyo kwa iwo amene ali nako, koma uchitsiru umabweretsa chilango kwa zitsiru.
23 Cor sapientis erudiet os eius: et labiis eius addet gratiam.
Mtima wanzeru umathandiza munthu kuyankhula mwa nzeru, ndipo mawu ake amawonjezera nzeru.
24 Favus mellis, composita verba: dulcedo animae, sanitas ossium.
Mawu okometsera ali ngati chisa cha njuchi, amakoma mu mtima ndipo amalimbitsa thupi.
25 Est via quae videtur homini recta: et novissima eius ducunt ad mortem.
Pali njira ina yooneka ngati yowongoka kwa munthu koma kumatsiriziro kwake ndi imfa.
26 Anima laborantis laborat sibi, quia compulit eum os suum:
Njala ya munthu wantchito imamuthandiza kulimbikira; njalayo imamukakamiza kuchitapo kanthu.
27 Vir impius fodit malum, et in labiis eius ignis ardescit.
Munthu wopanda pake amakonzekera kuchita zoyipa ndipo mawu ake ali ngati moto wopsereza.
28 Homo perversus suscitat lites: et verbosus separat principes.
Munthu woyipa mtima amayambitsa mikangano, ndipo miseche imalekanitsa anthu okondana kwambiri.
29 Vir iniquus lactat amicum suum: et ducit eum per viam non bonam.
Munthu wandewu amakopa mnansi wake, ndipo amamuyendetsa njira imene si yabwino.
30 Qui attonitis oculis cogitat prava, mordens labia sua perficit malum.
Amene amatsinzinira maso ake amalingalira zinthu zokhota; amene amachita msunamo amakonzeka kuchita zoyipa.
31 Corona dignitatis senectus, quae in viis iustitiae reperietur.
Imvi zili ngati chipewa chaufumu chaulemerero; munthu amazipeza akakhala moyo wolungama.
32 Melior est patiens viro forti: et qui dominatur animo suo, expugnatore urbium.
Munthu wosapsa mtima msanga amaposa munthu wankhondo, munthu wowugwira mtima wake amaposa amene amalanda mzinda.
33 Sortes mittuntur in sinum, sed a Domino temperantur.
Maere amaponyedwa pa mfunga, koma ndiye Yehova amene amalongosola zonse.

< Proverbiorum 16 >