< Proverbiorum 11 >

1 Statera dolosa, abominatio est apud Deum: et pondus aequum, voluntas eius.
Muyeso wachinyengo Yehova umamunyansa, koma amakondwera ndi muyeso woyenera.
2 Ubi fuerit superbia, ibi erit et contumelia: ubi autem est humilitas, ibi et sapientia.
Kunyada kukalowa, pamafikanso manyazi, koma pamene pali kudzichepetsa pameneponso pali nzeru.
3 Simplicitas iustorum diriget eos: et supplantatio perversorum vastabit illos.
Ungwiro wa anthu olungama umawatsogolera, koma anthu osakhulupirika amawonongeka ndi chinyengo chawo.
4 Non proderunt divitiae in die ultionis: iustitia autem liberabit a morte.
Chuma sichithandiza pa tsiku lawukali wa Mulungu, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
5 Iustitia simplicis diriget viam eius: et in impietate sua corruet impius.
Chilungamo cha anthu angwiro chimawongolera moyo wawo, koma ntchito zoyipa zimagwetsa mwini wake yemweyo.
6 Iustitia rectorum liberabit eos: et in insidiis suis capientur iniqui.
Chilungamo cha anthu oyera mtima chimawapulumutsa, koma anthu onyenga adzagwidwa ndi zilakolako zawo zomwe.
7 Mortuo homine impio, nulla erit ultra spes: et expectatio solicitorum peribit.
Pamene munthu woyipa wafa, chiyembekezo chake chimathanso. Chiyembekezo cha munthu wosalungama chimawonongeka.
8 Iustus de angustia liberatus est: et tradetur impius pro eo.
Munthu wolungama amapulumutsidwa ku mavuto, koma mʼmalo mwake amagwa mʼmavutomo ndi anthu oyipa.
9 Simulator ore decipit amicum suum: iusti autem liberabuntur scientia.
Munthu wosapembedza amawononga mnansi wake ndi pakamwa pake, koma munthu wolungama amapulumuka chifukwa cha kudziwa zinthu.
10 In bonis iustorum exultabit civitas: et in perditione impiorum erit laudatio.
Anthu olungama zinthu zikamawayendera bwino, mzinda wonse umakondwera, ndipo oyipa akamawonongeka anthu amafuwula mwachimwemwe.
11 Benedictione iustorum exaltabitur civitas: et ore impiorum subvertetur.
Mzinda umakwezeka chifukwa cha madalitso a anthu oyera mtima, koma umawonongedwa chifukwa cha pakamwa pa anthu oyipa.
12 Qui despicit amicum suum, indigens corde est: vir autem prudens tacebit.
Munthu wonyoza mnzake ndi wopanda nzeru, koma munthu wanzeru zomvetsa zinthu amakhala chete.
13 Qui ambulat fraudulenter, revelat arcana: qui autem fidelis est, celat amici commissum.
Amene amanka nachita ukazitape amawulula zinsinsi; koma munthu wokhulupirika amasunga pakamwa pake.
14 Ubi non est gubernator, populus corruet: salus autem, ubi multa consilia.
Pakasoweka uphungu mtundu wa anthu umagwa; koma pakakhala aphungu ambiri pamakhalanso chipulumutso.
15 Affligetur malo, qui fidem facit pro extraneo: qui autem cavet laqueos, securus erit.
Woperekera mlendo chikole adzapeza mavuto, koma wodana ndi za chikole amakhala pa mtendere.
16 Mulier gratiosa inveniet gloriam: et robusti habebunt divitias.
Mkazi wodekha amalandira ulemu, koma amuna ankhanza amangopata chuma.
17 Benefacit animae suae vir misericors: qui autem crudelis est, etiam propinquos abiicit.
Munthu wachifundo amadzipindulira zabwino koma munthu wankhanza amadzibweretsera mavuto.
18 Impius facit opus instabile: seminanti autem iustitiam merces fidelis.
Munthu woyipa amalandira malipiro wopanda phindu, koma wochita chilungamo amakolola mphotho yeniyeni.
19 Clementia praeparat vitam: et sectatio malorum mortem.
Munthu wochita za chilungamo amapeza moyo, koma wothamangira zoyipa adzafa.
20 Abominabile Domino cor pravum: et voluntas eius in iis, qui simpliciter ambulant.
Yehova amanyansidwa ndi anthu a mtima wokhotakhota koma amakondwera ndi anthu a makhalidwe angwiro.
21 Manus in manu non erit innocens malus: semen autem iustorum salvabitur.
Zoonadi, anthu oyipa adzalangidwa, koma anthu olungama adzapulumuka.
22 Circulus aureus in naribus suis, mulier pulchra et fatua.
Monga imaonekera mphete yagolide ikakhala pa mphuno ya nkhumba, ndi momwenso amaonekera mkazi wokongola wamʼkamwa.
23 Desiderium iustorum omne bonum est: praestolatio impiorum furor.
Zokhumba za anthu olungama zimathera pa zabwino zokhazokha, koma chiyembekezo cha anthu oyipa chimathera mu ukali wa Mulungu.
24 Alii dividunt propria, et ditiores fiunt: alii rapiunt non sua, et semper in egestate sunt.
Munthu wina amapatsako anzake zinthu mwaufulu nʼkumangolemererabe; wina amamana chomwe akanatha kupereka, koma kumanka nasawukabe.
25 Anima, quae benedicit, impinguabitur: et qui inebriat, ipse quoque inebriabitur.
Munthu wopereka mowolowamanja adzalemera; iye amene amathandiza ena iyenso adzathandizidwa.
26 Qui abscondit frumenta, maledicetur in populis: benedictio autem super caput vendentium.
Anthu amatemberera womana anzake chakudya, koma madalitso amakhala pamutu pa munthu amene amagulitsa chakudyacho.
27 Bene consurgit diluculo qui quaerit bona: qui autem investigator malorum est, opprimetur ab eis.
Iye amene amafunafuna zabwino mwakhama amapeza zabwinozo, koma wofunafuna zoyipa zidzamupeza.
28 Qui confidit in divitiis suis, corruet: iusti autem quasi virens folium germinabunt.
Aliyense amene amadalira chuma chake adzafota, koma wolungama adzaphukira ngati tsamba lobiriwira.
29 Qui conturbat domum suam, possidebit ventos: et qui stultus est, serviet sapienti.
Wovutitsa a mʼnyumba mwake adzalowa mʼmavuto, ndipo chitsiru chidzakhala kapolo wa munthu wa nzeru.
30 Fructus iusti lignum vitae: et qui suscipit animas, sapiens est.
Chipatso cha ntchito zabwino ndi moyo, ndipo kusatsata malamulo kumawonongetsa moyo.
31 Si iustus in terra recipit, quanto magis impius et peccator?
Ngati anthu olungama amalandira mphotho zawo pa dziko lapansi, kuli bwanji anthu osapembedza ndi ochimwa!

< Proverbiorum 11 >