< Job 18 >

1 Respondens autem Baldad Suhites, dixit:
Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 Usque ad quem finem verba iactabitis? intelligite prius, et sic loquamur.
“Kodi iwe Yobu utsiriza liti zoyankhula zakozi? Khala munthu wozindikira zinthu ndipo ukatero ife tidzayankhula.
3 Quare reputati sumus ut iumenta, et sorduimus coram vobis?
Chifukwa chiyani ukutiyesa ngati ngʼombe ndi kuoneka ngati opusa mʼmaso mwako?
4 Qui perdis animam tuam in furore tuo, numquid propter te derelinquetur terra, et transferentur rupes de loco suo?
Iwe amene ukudzipweteka wekha ndi mkwiyo wako, kodi dziko lapansi lisanduke bwinja chifukwa cha iweyo? Kodi kapena thanthwe lisunthidwe kuchoka pa malo ake?
5 Nonne lux impii extinguetur, nec splendebit flamma ignis eius?
“Nyale ya munthu woyipa yazimitsidwa; malawi a moto wake sakuwalanso.
6 Lux obtenebrescet in tabernaculo illius, et lucerna, quae super eum est, extinguetur.
Kuwala kwa mʼnyumba mwake kwasanduka mdima; nyale ya pambali pake yazima.
7 Arctabuntur gressus virtutis eius, et praecipitabit eum consilium suum.
Mayendedwe ake amgugu azilala; fundo zake zomwe zamugwetsa.
8 Immisit enim in rete pedes suos, et in maculis eius ambulat.
Mapazi ake amulowetsa mu ukonde ndipo akungoyendayenda mu ukondewo.
9 Tenebitur planta illius laqueo, et exardescet contra eum sitis.
Msampha wamkola mwendo; khwekhwe lamugwiritsitsa.
10 Abscondita est in terra pedica eius, et decipula illius super semitam.
Amutchera msampha pansi mobisika; atchera diwa pa njira yake.
11 Undique terrebunt eum formidines, et involvent pedes eius.
Zoopsa zikumuchititsa mantha kumbali zonse, zikutsatira mayendedwe ake onse.
12 Attenuetur fame robur eius, et inedia invadat costas illius.
Mphamvu zake zatha chifukwa cha njala, tsoka likumudikira.
13 Devoret pulchritudinem cutis eius, consumat brachia illius primogenita mors.
Wagwidwa nthenda yoopsa thupi lonse; miyendo yake, manja ake, zonse zawola.
14 Avellatur de tabernaculo suo fiducia eius, et calcet super eum, quasi rex, interitus.
Wachotsedwa mʼnyumba imene ankadalira, ndipo amukokera ku imfa, mfumu ya zoopsa zonse.
15 Habitent in tabernaculo illius socii eius, qui non est, aspergatur in tabernaculo eius sulphur.
Mʼnyumba mwake zonse zachotsedwamo; awazamo sulufule kuti aphe tizirombo ta matenda.
16 Deorsum radices eius siccentur, sursum autem atteratur messis eius.
Mizu yake ikuwuma pansi ndipo nthambi zake zikufota
17 Memoria illius pereat de terra, et non celebretur nomen eius in plateis.
Sadzakumbukiridwanso pa dziko lapansi; sadzakhalanso ndi chinthu chomutchukitsa mʼdziko.
18 Expellet eum de luce in tenebras, et de orbe transferet eum.
Amuchotsa pa malo owala ndi kumuponya ku mdima, ndipo amupirikitsa pa dziko lonse.
19 Non erit semen eius, neque progenies in populo suo, nec ullae reliquiae in regionibus eius.
Iye alibe ana kapena zidzukulu pakati pa anthu ake, kulibe wotsala kumene iye ankakhala.
20 In die eius stupebunt novissimi, et primos invadet horror.
Anthu akumadzulo adabwa kwambiri ndi tsoka lake; anthu akummawa agwidwa ndi mantha aakulu.
21 Haec sunt ergo tabernacula iniqui, et iste locus eius, qui ignorat Deum.
Ndithudi, izi ndiye zimagwera munthu woyipa; amenewa ndiye mathero a munthu amene sadziwa Mulungu.”

< Job 18 >