< Oekyuk 29 >

1 Ke len se emeet in malem se akitkosr, kowos fah tukeni in alu, ac tia oru kutena orekma. Ke len sac kowos in uk mwe ukuk uh.
“‘Pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Ili ndi tsiku limene muziliza malipenga.
2 Kisakin sie mwe kisa firir nu sin LEUM GOD, su fohlo uh mwe akinsewowoyal: soko cow fusr mukul, soko sheep mukul, ac itkosr sheep fusr mukul yac se matwa — kewana in wangin kutena ma koluk ke mano.
Muzipereka mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi wopanda chilema monga nsembe zopsereza, fungo lokoma kwa Yehova.
3 Akfalye srikasrak ke mwe kisa wheat, ma orek ke flao karyak ke oil in olive: paun onkosr in wi cow mukul soko, paun akosr in wi sheep mukul soko ah,
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzipereka chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa yayimuna iliyonse muzipereka makilogalamu awiri.
4 ac paun luo in wi kais soko sheep fusr.
Pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja muzipereka kilogalamu imodzi.
5 Kisakin pac soko nani mukul in mwe kisa ke ma koluk, ac in ouiya se inge kom fah oru alu in aknasnas ke mwet uh.
Muziperekanso mbuzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu.
6 Kisakin ma inge in weang mwe kisa firir lun len se oemeet lun malem, wi mwe kisa wheat nu kac, oayapa mwe kisa firir ke len nukewa wi mwe kisa wheat ac wain nu kac. Foulin mwe kisa mongo inge ma orek ke e uh akinsewowoye LEUM GOD.
Izi ndi zowonjezera pa nsembe zopsereza za mwezi ndi mwezi komanso za tsiku ndi tsiku pamodzi ndi zopereka za chakudya ndi zopereka za chakumwa potsata malamulo ake. Izi ndi zopereka zotentha pa moto, zoperekedwa kwa Yehova, fungo lokoma.
7 Ke len se aksingoul in malem akitkosr uh, kowos in tukeni ac alu. Kowos in tia kang kutena mwe mongo, ku oru kutena orekma.
“‘Pa tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiwiriwu, muzichita msonkhano wopatulika. Muzisala zakudya ndipo musamagwire ntchito.
8 Kisakin sie mwe kisa firir nu sin LEUM GOD, su fohlo uh mwe akinsewowoyal: soko cow fusr mukul, soko sheep mukul, ac itkosr sheep fusr mukul yac se matwa — kewana in wangin kutena ma koluk ke mano.
Muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza, yotulutsa fungo lokoma lokondweretsa Yehovayo; ngʼombe yayimuna imodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi. Zimenezi zizikhala zopanda chilema.
9 Akfalye srikasrak ke mwe kisa wheat, ma orek ke flao karyak ke oil in olive: paun onkosr in wi cow mukul soko, paun akosr in wi sheep mukul soko ah,
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri;
10 ac paun luo in wi kais soko sheep fusr.
kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiriwo.
11 Kisakin pac soko nani mukul in mwe kisa ke ma koluk, in weang pacna nani soko ma kisakinyuk ke alu in aknasnas ke mwet uh, oayapa mwe kisa firir ke len nukewa wi mwe kisa wheat ac wain nu kac.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe yopepesera machimo ya pa tsiku la mwambo ija, kuwonjezanso pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija, pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi cha chakumwa.
12 Ke len se aksingoul limekosr in malem akitkosr uh, kowos in tukeni ac alu. Oru sie kufwa in akfulatye LEUM GOD ke lusen len itkosr, ac tia oru kutena orekma.
“‘Pa tsiku la mwezi wachisanu ndi chiwiri, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Muzichita madyerero a Yehova masiku asanu ndi awiri.
13 Ke len se emeet, oru sie mwe kisa mongo ma orek ke e nu sin LEUM GOD, su fohlo uh mwe akinsewowoyal: cow mukul fusr singoul tolkwe, sheep mukul lukwa, ac sheep fusr mukul singoul akosr yac se matwa — kewana ma inge in wangin kutena ma koluk ke mano.
Muzipereka nsembe yotentha pa moto, kuti izikhala fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu, nkhosa zazimuna ziwiri, ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
14 Akfalye srikasrak ke mwe kisa wheat, ma orek ke flao karyak ke oil in olive: paun onkosr in wi kais soko cow mukul, paun akosr in wi kais soko sheep mukul,
Pa mwana wangʼombe aliyense mwa ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu aja, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa iliyonse mwa nkhosa ziwiri zija, mukonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri.
15 ac paun luo in wi kais soko sheep fusr, wi mwe kisa wain ma oakwuk nu kac.
Pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa aamuna khumi ndi anayiwo, muzipereka chakudya cha kilogalamu imodzi.
16 Kisakin pac soko nani mukul in mwe kisa ke ma koluk. Oru ma inge in weang mwe kisa firir ke len nukewa wi mwe kisa wheat ac mwe kisa wain nu kac.
Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhale nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
17 Ke len se akluo, kisakin cow fusr mukul singoul lukwa, sheep mukul lukwa, ac sheep fusr mukul singoul akosr, yac se matwa. Ma inge nukewa in wangin kutena ma koluk ke mano.
“‘Pa tsiku lachiwiri muzipereka ana angʼombe aamuna khumi ndi awiri aja, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi aja, zonse zopanda chilema.
18 Oru pac mwe kisa ke wheat ac mwe kisa wain ke kais soko cow mukul, sheep mukul, ac sheep fusr, fal nu ke pisalos, oana ma akkalemyeyuk.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
19 Oayapa soko nani mukul in mwe kisa ke ma koluk, oapana ma orek ke len se meet ah.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
20 Ke len se aktolu, kisakin cow fusr mukul singoul soko, sheep mukul lukwa, ac sheep fusr mukul singoul akosr yac se matwa. Ma inge nukewa in wangin kutena ma koluk ke mano.
“‘Pa tsiku lachitatu muzipereka ngʼombe zazimuna khumi ndi imodzi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
21 Oru pac mwe kisa ke wheat ac mwe kisa wain ke kais soko cow mukul, sheep mukul, ac sheep fusr, fal nu ke pisalos, oana ma akkalemyeyuk.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
22 Oayapa soko nani mukul in mwe kisa ke ma koluk, oapana ma orek ke len se emeet ah.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
23 Ke len se akakosr, kisakin cow fusr mukul singoul, sheep mukul lukwa, ac sheep fusr mukul singoul akosr yac se matwa. Ma inge nukewa in wangin kutena ma koluk ke mano.
“‘Pa tsiku lachinayi muzipereka ngʼombe zazimuna khumi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
24 Oru pac mwe kisa ke wheat ac mwe kisa wain ke kais soko cow mukul, sheep mukul, ac sheep fusr, fal nu ke pisalos, oana ma akkalemyeyuk.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
25 Oayapa soko nani mukul in mwe kisa ke ma koluk, weang pacna kain kisa nukewa ma orek fahfahsru ke len se oemeet ah.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
26 Ke len se aklimekosr, kisakin cow fusr mukul eu, sheep mukul lukwa, ac sheep fusr mukul singoul akosr yac se matwa. Ma inge nukewa in wangin kutena ma koluk ke mano.
“‘Pa tsiku lachisanu muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zinayi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
27 Oru pac mwe kisa ke wheat ac mwe kisa wain ke kais soko cow mukul, sheep mukul, ac sheep fusr, fal nu ke pisalos, oana ma akkalemyeyuk.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
28 Oayapa soko nani mukul in mwe kisa ke ma koluk, weang pacna kain kisa nukewa ma orek fahfahsru ke len se oemeet ah.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
29 Ke len se akonkosr, kisakin oalkosr cow fusr mukul, sheep mukul lukwa, ac sheep fusr mukul singoul akosr yac se matwa. Ma inge nukewa in wangin kutena ma koluk ke mano.
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zitatu, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
30 Oru pac mwe kisa ke wheat ac mwe kisa wain ke kais soko cow mukul, sheep mukul, ac sheep fusr, fal nu ke pisalos, oana ma akkalemyeyuk.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
31 Oayapa soko nani mukul in mwe kisa ke ma koluk, weang pacna kain kisa nukewa ma orek fahfahsru ke len se oemeet ah.
Muziperekenso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
32 Ke len se akitkosr, kisakin itkosr cow fusr mukul, sheep mukul lukwa, sheep fusr mukul singoul akosr yac se matwa. Ma inge nukmewa in wangin kutena ma koluk ke mano.
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa amuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
33 Oru pac mwe kisa ke wheat ac mwe kisa wain ke kais soko cow mukul, sheep mukul, ac sheep fusr, fal nu ke pisalos, oana ma akkalemyeyuk.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
34 Oayapa soko nani mukul in mwe kisa ke ma koluk, weang pacna kain kisa nukewa ma orek fahfahsru ke len se oemeet ah.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
35 Ke len se akoalkosr, kowos in tukeni ac alu, ac tia oru kutena orekma.
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chitatu muzichita msonkhano ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
36 Oru sie kisa firir tuh in sie mwe kisa mongo orek ke e nu sin LEUM GOD, su fohlo uh mwe akinsewowoyal: soko cow fusr mukul, soko sheep mukul, ac sheep fusr mukul itkosr yac se matwa. Ma inge nukewa in wangin kutena ma koluk ke mano.
Muzipereka chopereka chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ngʼombe imodzi yayimuna, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa amuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
37 Oru pac mwe kisa ke wheat ac mwe kisa wain ke kais soko cow mukul, sheep mukul, ac sheep fusr, fal nu ke pisalos, oana ma akkalemyeyuk.
Pamodzi ndi ngʼombe yayimunayo, nkhosa yayimunayo ndi ana ankhosawo, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
38 Oayapa soko nani mukul in mwe kisa ke ma koluk, weang pacna kain kisa nukewa ma orek fahfahsru ke len se oemeet ah.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
39 Pa inge oakwuk nu ke mwe kisa firir, mwe kisa wheat, mwe kisa wain, ac kisa in akinsewowo ma kowos ac oru nu sin LEUM GOD ke pacl in kufwa ma oakwuki nu suwos. Ma inge in weang mwe sang kowos sang in akfalye wuleang uh, ac mwe sang ke engan na lun kais sie mwet in sang.
“‘Kuwonjezera pa zopereka zimene munalumbirira ndi pa zopereka zanu zaufulu, muzipereka zimenezi kwa Yehova pa masiku osankhika a chikondwerero chanu. Nsembe zanu zachakumwa ndi nsembe zanu zachiyanjano.’”
40 Ouinge Moses el fahk nu sin mwet Israel ma nukewa ma LEUM GOD El sapkin nu sel.
Mose anawuza Aisraeli zonse zimene Yehova anamulamulira.

< Oekyuk 29 >