< Oekyuk 28 >

1 LEUM GOD El fahk nu sel Moses,
Yehova anawuza Mose kuti,
2 elan sapkin nu sin mwet Israel in sang mwe mongo ma fal in kisakinyuk nu sin God ke pacl pakiyuki nu kac, su fohlo uh akinsewowoyal.
“Lamula Aisraeli kuti, ‘Onetsetsani kuti mukupereka kwa Ine pa nthawi yoyikika, chopereka cha chakudya chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Ine.’
3 Pa inge mwe mongo ma fal in kisakinyuk nu sin LEUM GOD: kais sie len, kisakin sheep fusr mukul lukwa yac se matwa su wangin kutena ma koluk ke mano.
Awuze kuti, ‘Nsembe ya chakudya imene muzipereka pa moto kwa Yehova tsiku ndi tsiku ndi iyi: Ana ankhosa a chaka chimodzi awiri, wopanda chilema.
4 Kisakin soko sheep fusr inge ke lotutang, ac ma soko ngia ke ekela.
Mmawa muzipereka mwana wankhosa mmodzi ndipo winayo madzulo.
5 Ke kais soko sheep inge, sang pac paun in flao luo ma karkarak ke cup akosr ke oil in olive wowo tuh in mwe kisa wheat.
Muziperekanso kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi lita imodzi ya mafuta a olivi.
6 Pa inge mwe kisa firir ma eneneyuk in orek ke len nukewa, su tuh mutawauk orek Fineol Sinai — sie mwe kisa mongo ma orek ke e, su fohlo uh akinsewowoye LEUM GOD.
Iyi ndi nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku imene analamula pa phiri la Sinai kuti ikhale fungo lokoma, nsembe yopsereza pa moto yopereka kwa Yehova.
7 Okoala cup akosr ke wain sisken loang uh tuh in weang sheep fusr soko meet ah.
Chopereka chachakumwa chikhale lita imodzi yachakumwa chaukali pa nkhosa iliyonse. Muzithira pamalo opatulika, kupereka kwa Yehova.
8 Ke ekela, kisakin sheep fusr soko aklukwa in lumah se na ma orek ke mwe kisa ke lotutang, wi kisa wheat ac kisa wain nu kac. Kisakin ma inge oana sie mwe kisa mongo orek ke e, su fohlo uh akinsewowoye LEUM GOD.
Muzipereka mwana wankhosa winayo madzulo, pamodzi ndi chopereka chachakudya monga poyamba paja ndi chopereka chachakumwa monga mmawa. Ichi ndi chopereka chachakudya, fungo lokoma kwa Yehova.’”
9 Ke len Sabbath, kisakin lukwa sheep fusr mukul yac se matwa su wangin kutena ma koluk ke mano, wi paun in flao akosr karak ke oil in olive tuh in mwe kisa wheat, oayapa mwe kisa ke wain.
“‘Pa tsiku la Sabata, muzipereka nsembe ana ankhosa awiri a chaka chimodzi wopanda chilema, pamodzi ndi chopereka chachakumwa ndi chopereka chachakudya chokwana makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta.
10 Mwe kisa firir se inge ac orek ke len Sabbath nukewa, in weang pacna mwe kisa lun len nukewa wi mwe kisa wain uh.
Iyi ndi nsembe yopsereza ya pa Sabata iliyonse, kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake chachakumwa.’”
11 Ke len se emeet ke malem nukewa, kisakin sie mwe kisa firir nu sin LEUM GOD ke cow mukul fusr lukwa, sheep mukul soko, itkosr sheep fusr mukul yac sie matwa, ac kewana in wangin kutena ma koluk ke mano.
“Pa tsiku loyamba la mwezi uliwonse muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi, ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, onse wopanda chilema.
12 In akfalye mwe kisa wheat, sang onkosr paun in flao karyak ke oil in olive in wi kais soko cow mukul, ac paun akosr ke flao in wi sheep mukul soko;
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; ndi nkhosa yayimuna, chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta;
13 ac paun luo ke flao in wi kais soko sheep fusr. Mwe kisa firir inge pa sie mwe kisa mongo ma orek ke e, su fohlo uh akinsewowoye LEUM GOD.
ndipo pa mwana wankhosa aliyense, chopereka cha ufa wa kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, izi ndi za nsembe yopsereza, fungo lokoma, nsembe yotentha pa moto ya kwa Yehova.
14 Srikasrak nu ke mwe kisa wain uh pa quart luo in wi kais soko cow mukul, quart se tafu in wi sheep mukul soko, ac quart se in wi kais soko sheep fusr. Pa inge oakwuk nu ke mwe kisa firir ke len se emeet ke malem nukewa in yac se.
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakumwa cha malita awiri a vinyo; ndipo pa nkhosa yayimuna, lita limodzi ndi theka, ndipo pa mwana wankhosa, lita limodzi. Iyi ndi nsembe yopsereza ya mwezi ndi mwezi yoperekedwa pa mwezi watsopano mʼkati mwa chaka.
15 In weang mwe kisa firir lun kais sie len wi mwe kisa wain uh, kisakin soko nani mukul tuh in sie mwe kisa ke ma koluk.
Powonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake cha chakumwa, mbuzi yayimuna imodzi iperekedwe kwa Yehova ngati nsembe yopepesera machimo.
16 Kufwen Alukela uh ma orek in akfulatye LEUM GOD ac fah orek ke len aksingoul akosr ke malem se meet.
“‘Pa tsiku la 14 la mwezi woyamba muzichita Paska wa Yehova.
17 Na ke len aksingoul limekosr in malem sac, sie pac kufwa ac fah orek ke lusen len itkosr. In len inge kewa, ma ac mongo uh pa bread wangin mwe pulol kac.
Pa tsiku la 15 la mwezi womwewo pazikhala chikondwerero. Muzidya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri.
18 Ke len se emeet lun kufwa se inge kowos fah tukeni in alu, ac tia oru kutena orekma.
Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
19 Oru sie mwe kisa firir nu sin LEUM GOD, su sie mwe kisa mongo ma orek ke e. Kisakin cow mukul fusr lukwa, sheep mukul soko, ac sheep fusr mukul itkosr, yac sie matwa — nufonna in wangin kutena ma koluk ke mano.
Koma muzipereka kwa Yehova nsembe yotentha pa moto, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri aamuna a chaka chimodzi, onsewo wopanda chilema.
20 Mwe kisa wheat in orek ke flao karkar ke oil in olive: paun onkosr in wi kais soko cow mukul, paun akosr in wi sheep mukul soko,
Pamodzi ndi ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; makilogalamu awiri pa nkhosa yayimuna iliyonse.
21 ac paun luo in wi kais soko sheep fusr.
Kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa asanu ndi awiri aja.
22 Kisakin pac soko nani mukul in mwe kisa ke ma koluk, ac in ouiya se inge kom fah oru alu in aknasnas ke mwet uh.
Muziphatikizapo mbuzi yayimuna monga nsembe yopepesera machimo anu.
23 Oru ma inge in weang mwe kisa firir ma orek ke lotutang nukewa.
Muzikonza zimenezi nthawi zonse, powonjezera pa nsembe yopsereza ya mmawa.
24 In lumah sacna, ke len itkosr kowos in kisakin mwe kisa mongo ma orek ke e, su fohlo uh akinsewowoye LEUM GOD. Oru ma inge in weang mwe kisa firir ke len nukewa, ac mwe kisa wain.
Motere muzikonza chakudya cha nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pa masiku asanu ndi awiri ngati fungo lokomera Yehova. Zimenezi ziziperekedwa kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse pamodzi ndi nsembe yachakumwa.
25 Ke len se akitkosr kowos in tukeni alu, ac tia oru kutena orekma.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
26 Ke len in kisakin fahko se meet lun kosrani, ke kowos sang mwe kisa ke wheat sasu nu sin LEUM GOD, kowos in tukeni in alu, ac tia oru kutena orekma.
“‘Pa tsiku la zipatso zoyambirira kucha, pamene mukupereka chopereka cha chakudya chatsopano kwa Yehova, pa nthawi ya chikondwerero cha Masabata, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musagwire ntchito zolemetsa.
27 Oru sie mwe kisa firir, su fohlo uh mwe akinsewowoye LEUM GOD: lukwa cow fusr mukul, soko sheep mukul, ac itkosr sheep fusr mukul yac se matwa — kewana in wangin kutena ma koluk ke mano.
Muzipereka nsembe zopsereza za ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa imodzi yayimuna ndi ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi monga fungo lokomera Yehova.
28 Akfalye srikasrak ke mwe kisa wheat, ma orek ke flao karyak ke oil in olive: paun onkosr in wi kais soko cow mukul, paun akosr in wi sheep mukul soko ah,
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pazikhala chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri.
29 ac paun luo in wi kais soko sheep fusr.
Ndipo pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja, kilogalamu imodzi.
30 Kisakin pac soko nani mukul in mwe kisa ke ma koluk, ac in ouiya se inge kom fah oru alu in aknasnas ke mwet uh.
Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu.
31 Kisakin ma inge oayapa mwe kisa wain, in weang mwe kisa firir lun len nukewa ac mwe kisa wheat.
Muzipereka zimenezi pamodzi ndi zopereka za zakumwa ndi nsembe yake ya chakudya. Onetsetsani kuti nyamazo zilibe chilema.

< Oekyuk 28 >