< Luo Tokosra 8 >

1 Na Elisha el tuh fahk nu sin mutan se ma muta Shunem, su el tuh akmoulyauk wen se natu ah, lah LEUM GOD El ac supwama sracl se nu fin acn uh ke lusen yac itkosr, ac mutan sac in som liki acn uh wi sou lal, ac muta in siena acn saya.
Ndipo Elisa anawuza mayi amene anamuukitsira mwana wake kuti, “Choka kuno pamodzi ndi banja lako ndipo ukakhale kulikonse ukufuna, chifukwa Yehova akubweretsa njala ya zaka zisanu ndi ziwiri mʼdziko muno.”
2 Mutan sac tuh wi na ma fwackyang nu sel ah, na el ac sou lal ah som muta Philistia ke yac itkosr.
Mayiyo ananyamuka nachita zimene munthu wa Mulungu ananena. Iye pamodzi ndi banja lake anachoka nakakhala ku dziko la Afilisti zaka zisanu ndi ziwiri.
3 Ke safla yac itkosr ah, el foloko nu Israel, ac el som nu yorol tokosra ac siyuk tuh lohm sel ac acn sel in folokyang nu sel.
Zitatha zaka zisanu ndi ziwirizo anabwera kuchokera ku dziko la Afilisti ndipo anapita kwa mfumu kukafunsa za nyumba yake ndi munda wake.
4 Ke el utyak, tokosra el sramsram nu sel Gehazi, mwet kulansap lal Elisha. Tokosra el lungse etu ke mwenmen lal Elisha.
Ndipo mfumu inkayankhula ndi Gehazi, mtumiki wa munthu wa Mulungu kuti, “Tandiwuza zinthu zikuluzikulu zimene Elisa wachita.”
5 Ke pacl se Gehazi el srumun nu sel tokosra ke luman ma Elisha el oru ke el akmoulyauk sie mwet misa, na mutan sac sang pac siyuk lal nu sel tokosra. Gehazi el fahk nu sel, “Leum fulat, pa ingan mutan sac, ac pa ingan wen se natul ma Elisha el akmoulyauk ah!”
Pamene Gehazi ankayiwuza mfumuyo momwe Elisa anaukitsira anthu akufa, mayi amene mwana wake Elisa anamuukitsa kwa akufayo analowa kudzafunsa mfumu za nyumba yake ndi munda wake. Gehazi anati, “Mbuye wanga mfumu, mayi wake ndi uyu ndipo mwana wakeyo ndi uyu amene Elisa anamuukitsa kwa akufa.”
6 Ke tokosra el kusen siyuk kac, mutan sac el akkeyala ma Gehazi el fahk. Na tokosra el pangonma sie mwet pwapa lal ac fahkang elan folokonang ma nukewa lun mutan sac nu sel, weang pac molin fokin ima ke acn sel ke lusen yac itkosr ma el muta ke siena facl.
Mfumu inafunsa mayiyo za nkhaniyi ndipo iye anayifotokozera mfumuyo. Ndipo mfumu inasankha munthu woti ayendetse nkhani yake ndipo inati, “Mubwezereni zonse zimene zinali zake, kuphatikizapo phindu lonse lochokera mʼmunda wake, kuyambira tsiku limene anachoka mpaka tsopano lino.”
7 Elisha el som nu Damascus ke pacl se ma Tokosra Benhadad lun Syria el mas. Ke fwackyang nu sel tokosra lah Elisha el oasr we,
Elisa anapita ku Damasiko, ndipo Beni-Hadadi mfumu ya ku Aramu ankadwala. Mfumuyo itawuzidwa kuti, “Munthu wa Mulungu wabwera kuno kuchokera kutali,”
8 tokosra el fahk nu sel Hazael, sie sin mwet pwapa lal ah, “Us sie mwe lung an sang nu sin mwet palu sac, ac sap elan lolngok nu sin LEUM GOD lah nga ac kwela ku tia.”
inawuza Hazaeli kuti, “Tenga mphatso ndipo pita ukakumane ndi munthu wa Mulungu. Ukandifunsire kwa Yehova kudzera mwa iye kuti, ‘Kodi ndidzachira matenda angawa?’”
9 Na Hazael el nwakla kain in ma wo nukewa in acn Damascus nu fin camel angngaul, ac som nu yorol Elisha. Ke Hazael el sonol el fahk, “Tokosra Benhadad, mwet kulansap lom, el supweyume ngan tuh siyuk sum lah el ac ku in kwela liki mas lal ah ku tia.”
Choncho Hazaeli anapita kukakumana ndi Elisa, atasenzetsa ngamira 40 mphatso za zinthu zosiyanasiyana zabwino kwambiri za ku Damasiko. Iye analowa mʼnyumba ya Elisa ndi kuyima pamaso pake, ndipo anati, “Mwana wanu Beni-Hadadi wandituma kuti ndidzakufunseni kuti, ‘Kodi ndidzachira matenda angawa?’”
10 Elisha el topuk, “LEUM GOD El akkalemye nu sik mu el ac misa. Tusruktu folokot nu yorol ac fahk nu sel mu el ac kwela.”
Elisa anayankha kuti, “Pita ndipo ukamuwuze kuti, ‘Udzachira ndithu,’ koma Yehova wandionetsa kuti adzafabe.”
11 Na Elisha el ngetang na suilya ke sie ngetnget na fosrnga, nwe ke na Hazael el sensenak. Kitin pacl ah na soror sroninmutal Elisha.
Elisa anamuyangʼana kwambiri Hazaeli mpaka anachita manyazi. Pamenepo munthu wa Mulungu anayamba kulira.
12 Hazael el siyuk, “Leum luk, efu ku kom tung?” Elisha el topuk, “Mweyen nga etu ke ma na koluk kom ac oru nu sin mwet Israel uh. Kom ac esukak pot ku lalos, onela mukul fusr wowo natulos ke cutlass, sringil tulik natulos nwe ke elos misa, ac tiyala insien mutan pitutu lalos.”
Hazaeli anafunsa kuti, “Mbuye wanga mukulira chifukwa chiyani?” Elisa anayankha kuti, “Chifukwa ndikudziwa choyipa chimene udzachitira Aisraeli. Udzatentha mizinda yawo ya chitetezo, udzapha anyamata awo ndi lupanga, udzaphwanyitsa pansi makanda awo ndiponso udzatumbula mimba za akazi awo oyembekezera.”
13 Hazael el siyuk, “Ku fuka tuh ngan ku in oru ma na yohk angan? Nga tia mwet pwaye se!” Elisha el topuk, “LEUM GOD El akkalemye nu sik lah kom pa ac tokosra lun Syria.”
Ndipo Hazaeli anati, “Kodi kapolo wanune, amene ndine wonyozeka ngati galu, ndingathe bwanji kuchita chinthu chachikulu chotere?” Elisa anayankha kuti, “Yehova wandionetsa kuti iwe udzakhala mfumu ya ku Aramu.”
14 Hazael el folokla nu yorol Benhadad, su siyuk sel, “Mea Elisha el fahk?” Hazael el topuk, “El fahk nu sik mu pwayena lah kom ac kwela.”
Choncho Hazaeli anasiyana ndi Elisa ndi kubwerera kwa mbuye wake. Beni-Hadadi atafunsa kuti, “Elisa wakuwuza chiyani?” Hazaeli anayankha kuti, “Elisa wandiwuza kuti inu mudzachira ndithu.”
15 Tusruktu ke len se tok ah, Hazael el eis blanket se, isongya in kof ah, na sang nokomla mutal tokosra, nwe el malak misa. Na Hazael el aolulla Benhadad in tokosra lun acn Syria.
Koma mmawa mwake Hazaeli anatenga nsalu yokhuthala ndi kuyiviyika mʼmadzi ndipo anaphimba nayo nkhope ya mfumu, kotero mfumuyo inafa. Hazaeli analowa ufumu mʼmalo mwake.
16 In yac aklimekosr ke Joram, wen natul Ahab, el tokosra lun Israel, Jehoram wen natul Jehoshaphat el tokosrala lun Judah.
Chaka chachisanu cha ufumu wa Yoramu mwana wa Ahabu mfumu ya ku Israeli, Yehosafati ali mfumu ya ku Yuda, Yehoramu mwana wake anakhala mfumu ya Ayuda.
17 Jehoram el yac tolngoul luo in pacl sac, ac el leum in acn Jerusalem ke yac oalkosr.
Yehoramu analowa ufumu ali ndi zaka 32, ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka zisanu ndi zitatu.
18 Mutan kial ah ma natul Ahab, ac Jehoram el oru oana sou lal Ahab — el fahsr tukun ouiya koluk lun tokosra lun Israel. El oru ma koluk lain LEUM GOD,
Iye anatsatira khalidwe la mafumu a ku Israeli, monga mmene linachitira banja la Ahabu, popeza iye anakwatira mwana wa Ahabu. Yehoramu anachita zoyipa pamaso pa Yehova.
19 tusruktu LEUM GOD El tia lungse kunausla acn Judah, mweyen El tuh wulela nu sel David, mwet kulansap lal, mu fwilin tulik natul ac fah leumi mwet lal nwe tok.
Komabe, chifukwa cha mtumiki wake Davide, Yehova sanafune kuwononga Yuda popeza Yehova analonjeza Davide kuti adzamupatsa nyale pamodzi ndi zidzukulu zake mpaka muyaya.
20 In pacl in leum lal Jehoram, acn Edom tuyak lain acn Judah, ac mutawauk in sifacnala.
Pa nthawi ya Yehoramu, Edomu anawukira ulamuliro wa Yuda ndipo anadzisankhira mfumu.
21 Ouinge Jehoram el us chariot lal nukewa ac som nu Zair, yen mwet mweun lun Edom elos raunelosla we. In fong sac, el ac mwet leum lun chariot uh mahsrikla twe kaingla, ac mwet mweun lal ah fahsrelik nu yen selos.
Choncho Yehoramu anapita ku Zairi pamodzi ndi magaleta ake onse. Ndipo iye anakantha Aedomu amene anamuzungulira pamodzi ndi oyendetsa magaleta ake usiku. Koma ankhondo ake anathawa napita ku misasa yawo.
22 In pacl sac me, acn Edom tila oan ye ku lun Judah. Ac in pacl sac pacna, siti Libnah tuyak pac ac orek alein nu sin Judah.
Mpaka lero lino Edomu ndi wowukira Yuda. Nthawi yomweyo mzinda wa Libina unawukiranso.
23 Ma nukewa saya ma Jehoram el orala simla oasr in [Sramsram Matu Ke Tokosra Lun Judah.]
Ndipo ntchito zina za Yehoramu ndi zonse zomwe anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
24 Jehoram el misa ac pukpuki inkulyuk lun tokosra in Siti sel David, ac Ahaziah, wen natul, el aolul in tokosra.
Choncho Yehoramu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Ahaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
25 In yac aksingoul luo ke pacl Joram wen natul Ahab el tokosra lun Israel, Ahaziah wen natul Jehoram el tokosrala lun Judah
Mʼchaka cha khumi ndi chiwiri cha Yoramu mwana wa Ahabu mfumu ya Israeli, Ahaziya mwana wa Yehoramu mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
26 ke el yac longoul luo, ac el leum in Jerusalem ke yac se. Nina kial pa Athaliah, acn se natul Tokosra Ahab, su ma natul Tokosra Omri lun Israel.
Ahaziya anali ndi zaka 22 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu chaka chimodzi. Amayi ake anali Ataliya, chidzukulu cha Omiri mfumu ya Israeli.
27 Ahaziah el ac sou nu sel Tokosra Ahab ke sripen nina kial, ac el oru ma koluk lain LEUM GOD oana ke sou lal Tokosra Ahab tuh oru.
Iye anatsatira makhalidwe a banja la Ahabu ndipo anachita zoyipa pamaso pa Yehova, monga linachitira banja la Ahabu, pakuti anali mkamwini wa banja la Ahabu.
28 Tokosra Ahaziah el welul Tokosra Joram lun Israel in mweun lainul Tokosra Hazael lun Syria. Mwet mweun lalos sroani mweun in acn Ramoth in Gilead, ac Joram el kineta ke mweun ah.
Ahaziya anapita pamodzi ndi Yoramu mwana wa Ahabu kukachita nkhondo ndi Hazaeli mfumu ya Aramu ku Ramoti Giliyadi. Aaramu anavulaza Yoramu.
29 El folokla nu in siti Jezreel in tuh mahla kinet kacl ah, ac Ahaziah el som nu we in osun nu sel.
Choncho mfumu Yoramu inabwerera ku Yezireeli kuti ikachire mabala ake amene Aaramu anamuvulaza ku Rama pa nkhondo yake ndi Hazaeli mfumu ya Aramu. Tsono Ahaziya mwana wa Yehoramu mfumu ya ku Yuda anapita ku Yezireeli kuti akamuone Yoramu mwana wa Ahabu, popeza nʼkuti akudwala.

< Luo Tokosra 8 >