< Sie Tokosra 1 >

1 In pulan pacl se inge Tokosra David el arulana matuoh. Mwet kulansap lal finne katelya ke kaot fusrfusr, a el tiana fusrfusr.
Mfumu Davide atakalamba sankamva kufunda ngakhale akamufunditsa mabulangeti.
2 Ouinge mwet kulansap lal elos fahk nu sel, “Leum lasr, lela kut in sokak sie mutan fusr in muta yurum in karingin kom. El ac fah oan apkuran nu yurum, in akfusrfusrye kom.”
Choncho nduna zake zinamuwuza kuti, “Tiloleni tifune namwali woti azikhala nanu ndi kumakusamalirani. Namwaliyo azigona pafupi nanu kuti mbuye wathu mfumu muzimva kufundira.”
3 Sukok se inge orek in acn Israel nufon, nwe ke elos konauk sie mutan na oasku in acn Shunem, su pangpang Abishag, ac elos usalu nu yorol tokosra.
Kotero anafunafuna mʼdziko lonse la Israeli mtsikana wokongola ndipo anapeza Abisagi wa ku Sunemu, nabwera naye kwa mfumu.
4 Mutan se inge el arulana oasku. El muta yurin tokosra ac kulansupwal, tusruktu tokosra el tiana oru kutu ma nu sel.
Mtsikanayo anali wokongola kwambiri ndipo ankasamalira mfumu ndi kumayitumikira, koma mfumuyo sinakhale naye malo amodzi.
5 Inge, Adonijah wen natul David sel Haggith, el sifacna akfulatyalak ac fahk, “Nga pa ac tokosra.” El akoela chariot ac mwet kasrusr fin horse, ac sulela mwet lumngaul in atlol.
Nthawi imeneyi Adoniya, mwana wa Hagiti, anayamba kudzitukumula ndipo anati, “Ndidzakhala mfumu ndine.” Choncho anadzikonzera galeta ndi akavalo, pamodzi ndi anthu 50 woti azithamanga patsogolo pake.
6 El mukul na oasku se, ac el pa matu sin mukul natul David ma srakna moul. Wanginna pacl David el multikin nu sel ke ma el oru.
(Abambo ake sanalowererepo nʼkamodzi komwe ndipo sanafunsepo kuti, “Nʼchifukwa chiyani ukuchita zimenezi?” Adoniyayo anali wokongola kwambiri ndipo anali wopondana ndi Abisalomu).
7 Adonijah el pwapa nu sel Joab (su nina kial pa Zeruiah) ac nu sel Abiathar mwet tol, ac eltal insese in kasrel ke pwapa lal.
Adoniya anagwirizana ndi Yowabu mwana wa Zeruya ndiponso Abiatara wansembe, ndipo iwowa anamuthandiza.
8 Tusruktu Zadok mwet tol, ac Benaiah wen natul Jehoiada, ac Nathan mwet palu, Shimei, Rei, ac mwet mweun karinginyal David, elos nukewa tia insese nu sel Adonijah.
Koma Zadoki wansembe, Benaya mwana wa Yehoyada, mneneri Natani, Simei ndi Rei ndiponso asilikali amphamvu a Davide sanamutsate Adoniya uja.
9 Sie len ah Adonijah el orek kisa ke sheep, cow mukul, ac cow fusr na fact, in acn se pangpang Eot in Serpent, ma apkuran nu ke unon in kof Enrogel. El suli kutu sin tamulel lal su wen pac natul David, wi pac mwet kacto lun tokosra su mwet Judah, elos in tuku nu ke kufwa in kisa se inge.
Kenaka Adoniya anapereka nsembe za nkhosa ndi ngʼombe ndiponso ana angʼombe onenepa ku Mwala wa Zohereti kufupi ndi Eni Rogeli. Iye anayitana abale ake onse, ana aamuna a mfumu ndiponso akuluakulu onse a ku Yuda,
10 Tusruktu el tia solal Solomon, sie pac tamulel lal, ku Nathan mwet palu, ku Benaiah, ku mwet mweun karinginyal tokosra.
koma sanayitane mneneri Natani kapena Benaya kapenanso asilikali amphamvu a Davide ngakhalenso mʼbale wake Solomoni.
11 Na Nathan el som nu yorol Bathsheba, nina kial Solomon, ac siyuk sel, “Ku kom soenna lohng lah Adonijah, wen natul Haggith, el sifacna akwalyalak nu ke tokosra? Ac Tokosra David el tiana etu.
Pamenepo Natani anafunsa Batiseba, amayi ake a Solomoni, kuti, “Kodi simunamve kuti Adoniya, mwana wa Hagiti, walowa ufumu popanda Davide mbuye wathu kudziwa?
12 Kom fin lungse loangela moul lal Solomon, wen nutum, oayapa moul lom sifacna, kasru luk nu sum pa inge:
Tsopano ine ndikulangizeni inu mmene mungapulumutsire moyo wanu ndi moyo wa mwana wanu Solomoni.
13 kom in aksaye som nu yorol Tokosra David ac siyuk sel, ‘Leum Fulat, ya kom tuh tia wulela nu sik Inen LEUM GOD mu Solomon, wen nutik, pa ac tokosra in aol kom? Fuka tuh Adonijah el tokosrala?’”
Pitani msanga kwa Mfumu Davide ndipo mukanene kuti, ‘Mbuye wanga mfumu, kodi simunalumbire kwa ine mdzakazi wanu kuti, ‘Ndithu mwana wako Solomoni ndiye adzakhale mfumu mʼmalo mwanga, ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu?’ Nanga nʼchifukwa chiyani Adoniya walowa ufumu?’
14 Ac Nathan el sifilpa fahk, “Kom ac srakna sramsram nu sel Tokosra David, na nga ac utyak ac akkeye ma kom srumun an.”
Pamene inu muzikayankhula ndi mfumu, ine ndidzalowa ndi kuchitira umboni mawu anuwo.”
15 Ouinge Bathsheba el som in osun nu sin tokosra infukil in motul sel. Tokosra el arulana matuoh, ac Abishag, mutan fusr Shunem sac, el muta infarol karinganul.
Choncho Batiseba anapita nakalowa ku chipinda kukaonana ndi mfumu imene inali itakalamba kwambiri, kumene Abisagi wa ku Sunemu uja ankayisamalira.
16 Bathsheba el pasrla nu ye mutun tokosra, ac tokosra el siyuk sel, “Mea kom lungse?”
Batiseba anagwada nalambira mfumu. Mfumu inamufunsa kuti, “Kodi nʼchiyani chimene ukufuna?”
17 Bathsheba el topuk, “Leum Fulat, kom tuh wulela na ku nu sik Inen LEUM GOD lom mu Solomon, wen nutik, pa ac aol kom in tokosra.
Iye anayankha kuti, “Mbuye wanga, inu mwini munalumbira kwa ine mdzakazi wanu mʼdzina la Yehova Mulungu wanu kuti, ‘Solomoni mwana wako ndiye adzakhale mfumu mʼmalo mwa ine, ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu.’
18 Tuh pa Adonijah el tokosrala tari, ac kom tiana etu.
Koma tsopano Adoniya ndiye walowa ufumu, ndipo inu mbuye wanga mfumu, simukuzidziwa zimenezi.
19 El kisakin mwe kisa na pus ke cow mukul, sheep, ac cow fusr na fact, ac suli wen nutum an, ac Abiathar mwet tol, ac Joab captain lun un mwet mweun lom nu ke kufwa uh, a el tia solal Solomon, wen nutum.
Ndipo wapereka nsembe ngʼombe zambiri, ana angʼombe onenepa ndi nkhosa ndi mbuzi ndipo wayitana ana anu onse, wansembe Abiatara ndiponso Yowabu mkulu wa ankhondo, koma sanayitane kapolo wanu Solomoni.
20 Leum fulat, mwet Israel nukewa tawi kom in fahk nu selos lah su ac aol kom in tokosra.
Mbuye wanga mfumu, maso a Aisraeli onse ali pa inu, kuti adziwe kuchokera kwa inu amene adzakhala pa mpando waufumu wa mbuye wanga mʼmalo mwanu.
21 Kom fin tia akkalemye inge, na pacl se na kom ac misa, nga ac Solomon, wen nutik, ac fah oaoala mwet lokoalok lain tokosra.”
Mukapanda kutero, mbuye wanga, mukadzangotisiya nʼkulondola kumene kunapita makolo anu, ine pamodzi ndi mwana wangayu Solomoni adzatiyesa owukira.”
22 El srakna sramsram, na Nathan el sun lohm sin tokosra.
Pamene Batiseba amayankhula ndi mfumu, mneneri Natani analowa.
23 Fwackyang nu sin tokosra lah mwet palu el a inge, na Nathan el utyak ac pasrla yetun tokosra.
Ndipo anthu anawuza mfumu kuti, “Kwabwera mneneri Natani.” Kotero iye anafika pamaso pa mfumu ndipo anawerama nagunditsa nkhope yake pansi.
24 Na el fahk, “Ya kom fahkla tari lah Adonijah pa ac aol kom in tokosra uh?
Natani anafunsa kuti, “Mbuye wanga mfumu, kodi mwalengeza kuti Adoniya adzakhala mfumu mʼmalo mwanu, ndi kuti adzakhala pa mpando wanu waufumu?
25 Misenge na el som ac kisakin mwe kisa pukanten ke cow mukul, sheep, ac cow fusr na fact. El suli wen nutum nukewa, ac Joab captain lun un mwet mweun lom, ac Abiathar mwet tol, ac ingena elos tukeni mongo, sasa, ac fahk, ‘In paht moul lal Tokosra Adonijah!’
Lero lomwe lino wakapereka nsembe ngʼombe zambiri, ana angʼombe onenepa ndiponso nkhosa ndi mbuzi. Iye wayitana ana anu onse, atsogoleri a nkhondo, ndiponso wansembe Abiatara. Panopa onsewa akudya ndi kumwa naye ndipo akunena kuti, ‘Akhale ndi moyo wautali mfumu Adoniya!’
26 Tusruktu el tiana suliyu, ku Zadok mwet tol, ku Benaiah, ku Solomon.
Koma ine kapolo wanu, wansembe Zadoki ndi Benaya mwana wa Yehoyada, ndiponso kapolo wanu Solomoni sanatiyitane.
27 Ya kom insese nu kac, ac tiana fahk nu sin mwet pwapa lom lah su ac aol kom in tokosra?”
Kodi zimenezi mbuye wanga mfumu mwazichita ndinu, osawawuza atumiki anu kuti adziwe amene adzakhale pa mpando waufumu mʼmalo mwanu?”
28 Ac Tokosra David el fahk, “Sap Bathsheba elan foloko.” Ac el foloko ac tu ye mutal.
Pamenepo mfumu Davide anati, “Muyitaneni Batiseba.” Kotero Batiseba analowa ndipo anayimirira pamaso pa mfumu.
29 Na tokosra el fahk nu sel, “Nga wuleot nu sum Inen LEUM GOD moul, su tuh moliyula liki ongoiya luk nukewa,
Tsono mfumu inalumbira kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene anandipulumutsa ine ku mavuto onse,
30 lah misenge nga srakna sruokya wulela se ma nga tuh orala nu sum Inen LEUM GOD lun Israel: lah Solomon, wen nutum, pa ac aolyu in tokosra.”
ndithu ine lero ndichita zonse zimene ndinalumbira kwa Yehova Mulungu wa Israeli kuti, mwana wako Solomoni adzakhala mfumu mʼmalo mwanga ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu.”
31 Bathsheba el pasrla nwe ten ac fahk, “Lela tokosra, leum luk, in moul ma pahtpat!”
Pamenepo Batiseba anawerama, nagunditsa mutu wake pansi nalambira mfumu, ndipo anati, “Mbuye wanga Mfumu Davide mukhale ndi moyo wautali!”
32 Na Tokosra David el sapla nu sel Zadok, Nathan, ac Benaiah. Ke elos tuku,
Mfumu Davide anati, “Ndiyitanireni wansembe Zadoki, mneneri Natani ndi Benaya mwana wa Yehoyada.” Atafika pamaso pa mfumu,
33 el fahk nu selos, “Us mwet kacto luk in wi kowos, ac sang Solomon, wen nutik, elan kasrusr fin kosro miul nutik sifacna, ac pwanul nwe ke Unon in kof Gihon,
mfumuyo inati kwa iwo, “Tengani atumiki anga ndipo mukweze mwana wanga Solomoni pa bulu wanga ndipo mupite naye ku Gihoni. Mukalize lipenga ndi kufuwula kuti, ‘Akhale ndi moyo wautali mfumu Solomoni!’
34 yen ma Zadok ac Nathan ac fah akmusraella we tuh elan tokosrala lun Israel. Na kowos ukya mwe ukuk ac sasa ac fahk, ‘In paht moul lal Tokosra Solomon!’
Kumeneko Zadoki wansembe ndi mneneri Natani akamudzoze kuti akhale mfumu ya Israeli. Kenaka mukalize lipenga ndi kumanena kuti ‘Akhale ndi moyo wautali Mfumu Solomoni.’
35 Kowos welul na foloko nwe ke na el muta fin tron luk uh. El fah aolyu in tokosra, mweyen el pa nga sulela in leumi Israel ac Judah.”
Ndipo pobwera muzikamutsata pambuyo. Iyeyo akabwere kuno ndi kudzakhala pa mpando wanga waufumu ndi kudzalamulira mʼmalo mwanga. Ndamusankha kukhala wolamulira Israeli ndi Yuda.”
36 Benaiah el topuk, “Ac fah ou lungse lom, ac lela LEUM GOD lom Elan akkeye!
Benaya mwana wa Yehoyada anayankha mfumu kuti, “Ameni! Yehova Mulungu wa mbuye wanga mfumu akhazikitse kuti zichitike motero.
37 Leum Fulat, oana ke LEUM GOD El wi kom, lela Elan welul pac Solomon, ac oru tuh tokosrai lal in akinsewowoyeyuk yohk liki tokosrai lom.”
Monga momwe Yehova wakhalira ndi inu mbuye wanga mfumu, momwemonso akhale ndi Solomoni ndi kukhazikitsa ufumu wake kuti ukhale waukulu kuposa ufumu wa mbuye wanga Mfumu Davide!”
38 Ouinge Zadok, Nathan, ac Benaiah, ac mwet mweun karinginyal tokosra, elos eisalang Solomon nu fin miul natul Tokosra David, ac pwanul nwe ke Unon in kof Gihon.
Kotero Zadoki wansembe, mneneri Natani, Benaya mwana wa Yehoyada, Akereti ndiponso Apeleti, anthu oteteza mfumu, anapita kukamukweza Solomoni pa bulu wa Mfumu Davide ndi kupita naye ku Gihoni.
39 Zadok el srukak oil in olive se ma el use liki Lohm Nuknuk sin LEUM GOD ac mosrwella Solomon. Elos ukya mwe ukuk ac mwet nukewa sala ac fahk, “In paht moul lal Tokosra Solomon!”
Wansembe Zadoki anatenga nyanga ya mafuta yochokera ku malo opatulika ndi kumudzoza Solomoni. Kenaka analiza lipenga ndipo anthu onse anafuwula kuti, “Akhale ndi moyo wautali Mfumu Solomoni!”
40 Ouinge Solomon el folokla, ac mwet nukewa fahsr tokol, ac sasa ke engan. Pusren mwe ukuk natulos arulana yohk, pwanang infohk uh kusrusryak.
Ndipo anthu onsewo anapita namutsatira pambuyo akuyimba zitoliro ndi kukondwerera kwambiri, kotero nthaka inagwedezeka chifukwa cha phokoso lawo.
41 Ke Adonijah ac mwet welul elos aksafye mongo lalos, elos lohngak pusra sac. Ac ke Joab el lohng pusren mwe ukuk el siyuk, “Efu ku siti uh arulana ngisyak?”
Adoniya pamodzi ndi anthu onse oyitanidwa amene anali naye anamva zimenezi pamene ankamaliza madyerero awo. Atamva kulira kwa malipenga, Yowabu anafunsa kuti, “Kodi phokoso lonselo mu mzindamo likutanthauza chiyani?”
42 El srakna kaskas a Jonathan wen natul mwet tol Abiathar, el tuku. Adonijah el fahk, “Utyak. Ke kom mwet wo se, kalem lah oasr pweng wo kom us.”
Iye akuyankhula, Yonatani mwana wa wansembe Abiatara anafika. Adoniya anati, “Lowa. Munthu wabwino ngati iwe ayenera kubweretsa nkhani yabwino.”
43 Jonathan el topuk ac fahk, “Tia wo ma! Tokosra David, leum lasr, el sraklalak Solomon elan tokosra.
Yonatani anayankha Adoniya kuti, “Ayi ndithu, zinthu sizili bwino! Mbuye wathu Mfumu Davide walonga Solomoni ufumu.
44 El supwalla Zadok, Nathan, Benaiah, ac mwet mweun karinginyen tokosra in pwanul. Elos sang el kasrusr fin miul natul tokosra,
Mfumu yatuma Zadoki wansembe, mneneri Natani, Benaya mwana wa Yehoyada, Akereti ndi Apeleti ku Gihoni ndipo iwo amukweza pa bulu wa mfumu,
45 na Zadok ac Nathan akmusraella ke Unon in kof Gihon. Na elos ilyak nu in siti uh ac sasa, ac mwet nukewa tukeni wonak ke engan. Pa ingan pusra se kowos lohng ah.
ndipo Zadoki wansembe ndi mneneri Natani adzoza Solomoni ku Gihoni kuti akhale mfumu. Ndipo kuchokera kumeneko akhala akululutira, kotero kuti mu mzinda monse muli phokoso lokhalokha. Ndiyetu phokoso limene mukulimvalo.
46 Inge Solomon el tokosra.
Ndipo Solomoni wakhala kale pa mpando wake waufumu.
47 Oayapa mwet kacto lun tokosra elos utyak nu yorol Tokosra David ac fahk, ‘Lela God lom Elan oru tuh Solomon elan pwengpeng yohk liki kom, ac tokosrai lal in akinsewowoyeyuk yohk liki tokosrai lom.’ Na Tokosra David el pasrla fin mwe oan kial
Kuwonjezera pamenepo, nduna za mfumu zabwera kale kudzayamika mbuye wathu Mfumu Davide, pomanena kuti, ‘Mulungu wanu atchukitse dzina la Solomoni kuposa dzina lanu ndipo ufumu wake ukule kupambana ufumu wanu!’ Ndipo mfumu inawerama niyamba kupembedza pa bedi lake,
48 ac pre ac fahk, ‘Lela kut in kaksakin LEUM GOD lun Israel, su orala tuh sie sin wen nutik in aolyula in tokosra misenge, oayapa ke El lela nga in moul nwe ke nga liye!’”
inati, ‘Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, amene wasankha wolowa mʼmalo mwanga ine ndikanali ndi moyo lero lino.’”
49 Na mwet welul Adonijah elos sangeng, ac elos nukewa tuyak ac folokelik nu yen selos.
Anthu onse amene Adoniya anawayitana ananjenjemera ndi mantha, ndipo anayimirira, kenaka anamwazikana.
50 Adonijah el arulana sangeng sel Solomon, ac el som nu in Lohm Nuknuk sin LEUM GOD, ac sruokya koac ke loang uh.
Koma Adoniya, poopa Solomoni, anapita ku Nyumba ya Mulungu nakagwira msonga za guwa lansembe.
51 Fwackyang nu sel Tokosra Solomon lah Adonijah el sangeng sel, ac el sruokya koac ke loang sac ac fahk, “Nga kena Tokosra Solomon elan fulahk nu sik meet lah el ac tia sap in anwuki nga.”
Tsono Solomoni anawuzidwa kuti, “Adoniya akukuopani inu Mfumu Solomoni ndipo wagwira msonga za guwa lansembe. Iye akuti, ‘Mfumu Solomoni alumbire kuti sadzapha kapolo wake ndi lupanga.’”
52 Solomon el topuk, “El fin pwaye nu sik, tia sokofanna aunsifal fah pusralyukla, a el fin tia pwaye nu sik, el ac misa.”
Solomoni anayankha kuti, “Ngati iyeyo aonetse kuti ndi munthu wakhalidwe labwino, ngakhale tsitsi la mʼmutu mwake silidzathothoka ndi kugwera pansi, koma akapezeka kuti ali ndi khalidwe loyipa, adzafa ndithu.”
53 Na Tokosra Solomon el sapla in utuki Adonijah liki loang sac. Adonijah el som nu yorol tokosra, ac pasrla ye mutal, ac tokosra el fahk, “Kom ku in som nu lohm sum.”
Pamenepo Mfumu Solomoni inatuma anthu ndipo anakamutenga paguwa paja. Adoniya anabwera ndi kudzalambira Mfumu Solomoni, ndipo Solomoni anati, “Pita ku nyumba yako.”

< Sie Tokosra 1 >