< 시편 115 >

1 여호와여, 영광을 우리에게 돌리지 마옵소서 우리에게 돌리지 마옵소서 오직 주의 인자하심과 진실하심을 인하여 주의 이름에 돌리옵소서
Kwa ife ayi Yehova, kwa ife ayi koma ulemerero ukhale pa dzina lanu, chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika ndiponso chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
2 어찌하여 열방으로 저희 하나님이 이제 어디 있느냐? 말하게 하리이까
Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akunena kuti, “Mulungu wawo ali kuti?”
3 오직 우리 하나님은 하늘에 계셔서 원하시는 모든 것을 행하셨나이다
Mulungu wathu ali kumwamba; Iye amachita chilichonse chimene chimamukondweretsa.
4 저희 우상은 은과 금이요 사람의 수공물이라
Koma mafano awo ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
5 입이 있어도 말하지 못하며 눈이 있어도 보지 못하며
Pakamwa ali napo koma sayankhula, maso ali nawo koma sapenya;
6 귀가 있어도 듣지 못하며 코가 있어도 맡지 못하며
makutu ali nawo koma samva, mphuno ali nazo koma sanunkhiza;
7 손이 있어도 만지지 못하며 발이 있어도 걷지 못하며 목구멍으로 소리도 못하느니라
manja ali nawo koma akakhudza samva kanthu; mapazi ali nawo koma sayenda; kapena pakhosi pawo kutulutsa mawu.
8 우상을 만드는 자와 그것을 의지하는 자가 다 그와 같으리로다
Anthu amene amapanga mafanowo adzafanana nawo, chimodzimodzinso onse amene amadalira mafanowo.
9 이스라엘아, 여호와를 의지하라! 그는 너희 도움이시요 너희 방패시로다
Inu Aisraeli, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
10 아론의 집이여, 여호와를 의지하라! 그는 너희 도움이시요 너희 방패시로다
Iwe nyumba ya Aaroni, dalira Yehova; Iye ndiye thandizo lako ndi chishango chako.
11 여호와를 경외하는 너희는 여호와를 의지하라! 그는 너희 도움이시요 너희 방패시로다
Inu amene mumaopa Iye, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
12 여호와께서 우리를 생각하사 복을 주시되 이스라엘 집에도 복을 주시고 아론의 집에도 복을 주시며
Yehova watikumbukira ndipo adzatidalitsa: adzadalitsa nyumba ya Israeli, adzadalitsa nyumba ya Aaroni,
13 대소 무론하고 여호와를 경외하는 자에게 복을 주시리로다
adzadalitsa iwo amene amaopa Yehova; aangʼono ndi aakulu omwe.
14 여호와께서 너희 곧 너희와 또 너희 자손을 더욱 번창케 하시기를 원하노라
Yehova akuwonjezereni madalitso; inuyo pamodzi ndi ana anu.
15 너희는 천지를 지으신 여호와께 복을 받는자로다!
Mudalitsidwe ndi Yehova, Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
16 하늘은 여호와의 하늘이라도 땅은 인생에게 주셨도다
Kumwamba ndi kwa Yehova, koma dziko lapansi Iye walipereka kwa anthu.
17 죽은 자가 여호와를 찬양하지 못하나니 적막한 데 내려가는 아무도 못하리로다
Si anthu akufa amene amatamanda Yehova, amene amatsikira kuli chete;
18 우리는 이제부터 영원까지 여호와를 송축하리로다 할렐루야!
ndi ife amene timatamanda Yehova, kuyambira tsopano mpaka muyaya. Tamandani Yehova.

< 시편 115 >