< ヨブ 記 16 >

1 そこでヨブは答えて言った、
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 「わたしはこのような事を数多く聞いた。あなたがたは皆人を慰めようとして、かえって人を煩わす者だ。
“Ndinamvapo zambiri monga zimenezi; nonsenu ndinu anthu osatha kutonthoza mtima mnzanu.
3 むなしき言葉に、はてしがあろうか。あなたは何に激して答をするのか。
Kodi mawu anu ochulukawo adzatha? Kodi chikukuvutani nʼchiyani kuti muzingoyankhula mawu otsutsawa?
4 わたしもあなたがたのように語ることができる。もしあなたがたがわたしと代ったならば、わたしは言葉を練って、あなたがたを攻め、あなたがたに向かって頭を振ることができる。
Inenso ndikanatha kuyankhula monga inu, inuyo mukanakhala monga ndilili inemu; Ine ndikanatha kuyankhula mawu omveka bwino kutsutsana nanu ndi kukupukusirani mutu wanga.
5 また口をもって、あなたがたを強くし、くちびるの慰めをもって、あなたがたの苦しみを和らげることができる。
Ndipo mawu a pakamwa panga akanakulimbikitsani; chitonthozo chochokera pa milomo yanga chikanachepetsa ululu wanu.
6 たといわたしは語っても、わたしの苦しみは和らげられない。たといわたしは忍んでも、どれほどそれがわたしを去るであろうか。
“Koma ine ndikati ndiyankhule ululu wanga sukuchepa; ndipo ndikati ndikhale chete, ululu wanga sukuchokabe.
7 まことに神は今わたしを疲れさせた。彼はわたしのやからをことごとく荒した。
Ndithudi, Inu Mulungu mwanditha mphamvu; mwawononga banja langa lonse.
8 彼はわたしを、しわ寄らせた。これがわたしに対する証拠である。またわたしのやせ衰えた姿が立って、わたしを攻め、わたしの顔にむかって証明する。
Inu mwandimanga ndipo kundimangako kwakhala umboni; kuwonda kwanga kwandiwukira ndipo kukuchita umboni wonditsutsa.
9 彼は怒ってわたしをかき裂き、わたしを憎み、わたしに向かって歯をかみ鳴らした。わたしの敵は目を鋭くして、わたしを攻める。
Mulungu amabwera kwa ine mwankhanza ndipo amadana nane, amachita kulumira mano; mdani wanga amandituzulira maso.
10 人々はわたしに向かって口を張り、侮ってわたしのほおを打ち、ともに集まってわたしを攻める。
Anthu amatsekula pakamwa pawo kundikuwiza; amandimenya pa tsaya mwachipongwe ndipo amagwirizana polimbana nane.
11 神はわたしをよこしまな者に渡し、悪人の手に投げいれられる。
Mulungu wandipereka kwa anthu ochita zoyipa ndipo wandiponyera mʼmanja mwa anthu oyipa mtima.
12 わたしは安らかであったのに、彼はわたしを切り裂き、首を捕えて、わたしを打ち砕き、わたしを立てて的とされた。
Ine ndinali pamtendere, koma Mulungu ananditswanya; anandigwira pa khosi ndi kundiphwanya. Iye anandisandutsa choponyera chandamale chake;
13 その射手はわたしを囲む。彼は無慈悲にもわたしの腰を射通し、わたしの肝を地に流れ出させられる。
anthu ake oponya mauta andizungulira. Mopanda kundimvera chisoni, Iye akulasa impsyo zanga ndipo akutayira pansi ndulu yanga.
14 彼はわたしを打ち破って、破れに破れを加え、勇士のようにわたしに、はせかかられる。
Akundivulaza kawirikawiri, akuthamangira pa ine monga munthu wankhondo.
15 わたしは荒布を膚に縫いつけ、わたしの角をちりに伏せた。
“Ndasokerera chiguduli pa thupi langa ndipo ndayika mphamvu zanga pa fumbi.
16 わたしの顔は泣いて赤くなり、わたしのまぶたには深いやみがある。
Maso anga afiira ndi kulira, ndipo zikope zanga zatupa;
17 しかし、わたしの手には暴虐がなく、わたしの祈は清い。
komatu manja anga sanachite zachiwawa ndipo pemphero langa ndi lolungama.
18 地よ、わたしの血をおおってくれるな。わたしの叫びに、休む所を得させるな。
“Iwe dziko lapansi, usakwirire magazi anga; kulira kwanga kofuna thandizo kusalekeke!
19 見よ、今でもわたしの証人は天にある。わたしのために保証してくれる者は高い所にある。
Ngakhale tsopano mboni yanga ili kumwamba; wonditchinjiriza pa mlandu wanga ali komweko.
20 わたしの友はわたしをあざける、しかしわたしの目は神に向かって涙を注ぐ。
Wondipembedzera ndi bwenzi langa, pamene maso anga akukhuthula misozi kwa Mulungu;
21 どうか彼が人のために神と弁論し、人とその友との間をさばいてくれるように。
iye, mʼmalo mwanga, amamudandaulira Mulungu monga munthu amadandaulira bwenzi lake.
22 数年過ぎ去れば、わたしは帰らぬ旅路に行くであろう。
“Pakuti sipapita zaka zambiri ndisanayende mʼnjira imene sindidzabwerera.”

< ヨブ 記 16 >