< ヨブ 記 36 >

1 エリフは重ねて言った、
Ndipo Elihu anapitirira kuyankhula nati:
2 「しばらく待て、わたしはあなたに示すことがある。なお神のために言うべき事がある。
“Mundilole pangʼono pokha ndipo ndikuonetsani kuti zilipo zambiri zoti ziyankhulidwe mʼmalo mwa Mulungu.
3 わたしは遠くからわが知識を取り、わが造り主に正義を帰する。
Nzeru zanga ndimazitenga kutali; ndidzaonetsa kulungama kwa Mlengi wanga.
4 まことにわたしの言葉は偽らない。知識の全き者があなたと共にいる。
Ndithudi mawu anga si abodza; wanzeru zangwiro ali ndi inu.
5 見よ、神は力ある者であるが、何をも卑しめられない、その悟りの力は大きい。
“Mulungu ndi wamphamvu, koma sanyoza anthu; Iye ndi wamphamvu, ndipo ndi wokhazikika pa cholinga chake.
6 彼は悪しき者を生かしておかれない、苦しむ者のためにさばきを行われる。
Salola oyipa kuti akhalebe ndi moyo koma amapereka ufulu kwa anthu osautsidwa.
7 彼は正しい者から目を離さず、位にある王たちと共に、とこしえに、彼らをすわらせて、尊くされる。
Iye saleka kuyangʼanira anthu olungama; amawayika kuti alamulire pamodzi ndi mafumu ndipo amawalemekeza mpaka muyaya.
8 もし彼らが足かせにつながれ、悩みのなわに捕えられる時は、
Koma ngati anthu amangidwa ndi unyolo, ndipo akondwa ndi zingwe zamasautso,
9 彼らの行いと、とがと、その高ぶったふるまいを彼らに示し、
Iye amawafotokozera zomwe anachita, kuti iwo anachimwa modzikuza.
10 彼らの耳を開いて、教を聞かせ、悪を離れて帰ることを命じられる。
Mulungu amawatsekula makutu kuti amve malangizo ake ndipo amawalamula kuti alape zoyipa zawo.
11 もし彼らが聞いて彼に仕えるならば、彼らはその日を幸福に過ごし、その年を楽しく送るであろう。
Ngati iwo amumvera ndi kumutumikira, adzatsiriza masiku a moyo wawo mwamtendere, adzatsiriza zaka zawo mosangalala.
12 しかし彼らが聞かないならば、つるぎによって滅び、知識を得ないで死ぬであろう。
Koma ngati samvera, adzaphedwa ndi lupanga ndipo adzafa osadziwa kanthu.
13 心に神を信じない者どもは怒りをたくわえ、神に縛られる時も、助けを呼び求めることをしない。
“Anthu osapembedza amasunga mkwiyo mu mtima mwawo; akawalanga, safuwulira kwa Iye kupempha thandizo.
14 彼らは年若くして死に、その命は恥のうちに終る。
Amafa akanali achinyamata, pakati pa amuna achiwerewere a kumalo azipembedzo.
15 神は苦しむ者をその苦しみによって救い、彼らの耳を逆境によって開かれる。
Koma ovutika, Iye amawapulumutsa pa mavuto awo; Mulungu amawayankhula mʼmasautso awowo.
16 神はまたあなたを悩みから、束縛のない広い所に誘い出された。そしてあなたの食卓に置かれた物はすべて肥えた物であった。
“Iye akukukopani inu kuti muchoke mʼmasautso, kuti mupite ku malo aakulu kumene kulibe chokutchingani, kumalo a mpumulo kumene kuli chakudya chabwino kwambiri.
17 しかしあなたは悪人のうくべきさばきをおのれに満たし、さばきと公義はあなたを捕えている。
Koma tsopano inu mwapezeka wopalamula chifukwa cha kuyipa kwanu; chiweruzo ndi chilungamo chakugwerani.
18 あなたは怒りに誘われて、あざけりに陥らぬように心せよ。あがないしろの大いなるがために、おのれを誤るな。
Muchenjere kuti wina asakukopeni ndi chuma; musalole kuti chiphuphu chachikulu chikusocheretseni.
19 あなたの叫びはあなたを守って、悩みを免れさせるであろうか、いかに力をつくしても役に立たない。
Kodi chuma chanu kapena mphamvu zanu zonse zingakusungeni kotero kuti simungakhale pa masautso?
20 人々がその所から断たれるその夜を慕ってはならない。
Musalakalake kuti usiku ubwere, pakuti ndiyo nthawi imene anthu adzawonongeka.
21 慎んで悪に傾いてはならない。あなたは悩みよりもむしろこれを選んだからだ。
Muchenjere kuti musatembenukire ku uchimo, chifukwa uchimowo ndiwo unabweretsa kuzunzika kwanu.
22 見よ、神はその力をもってあがめられる。だれか彼のように教える者があるか。
“Taonani, Mulungu ndi wamkulu ndiponso ndi wamphamvu. Kodi ndi mphunzitsi uti amene angafanane naye?
23 だれか彼のためにその道を定めた者があるか。だれか『あなたは悪い事をした』と言いうる者があるか。
Kodi ndani amene anamuwuzapo Mulungu zoti achite, kapena kumuwuza kuti, ‘Inu mwachita chinthu cholakwa?’
24 神のみわざをほめたたえる事を忘れてはならない。これは人々の歌いあがめるところである。
Kumbukirani kutamanda ntchito zake zimene anthu amaziyamika mʼnyimbo.
25 すべての人はこれを仰ぎ見る。人は遠くからこれを見るにすぎない。
Anthu onse amaziona ntchitozo; anthuwo amaziona ali kutali.
26 見よ、神は大いなる者にいまして、われわれは彼を知らない。その年の数も計り知ることができない。
Ndithudi, Mulungu ndi wamkulu, sitimudziwa nʼpangʼono pomwe! Chiwerengero cha zaka zake nʼchosadziwika.
27 彼は水のしたたりを引きあげ、その霧をしたたらせて雨とされる。
“Mulungu ndiye amakweza timadontho tamadzi kuthambo, timene timasungunuka nʼkukhala mvula;
28 空はこれを降らせて、人の上に豊かに注ぐ。
mitambo imagwetsa mvulayo ndipo mvulayo imavumbwa pa anthu mokwanira.
29 だれか雲の広がるわけと、その幕屋のとどろくわけとを悟ることができようか。
Kodi ndani amene angadziwe momwe mitambo imayendera, momwe Iye amabangulira kuchokera kumalo ake?
30 見よ、彼はその光をおのれのまわりにひろげ、また海の底をおおわれる。
Taonani momwe amawalitsira zingʼaningʼani pa malo ake onse, zimafika ngakhale pansi pa nyanja.
31 彼はこれらをもって民をさばき、食物を豊かに賜い、
Umu ndi mmene Iye amalamulira mitundu ya anthu ndi kuwapatsa chakudya chochuluka.
32 いなずまをもってもろ手を包み、これに命じて敵を打たせられる。
Amadzaza manja ake ndi zingʼaningʼani, ndipo amazilamulira kuti zigwe pamalo pamene Iye akufuna.
33 そのとどろきは、悪にむかって怒りに燃える彼を現す。
Mabingu ake amalengeza za kubwera kwa mvula yamkuntho; ngʼombe nazo zimalengeza za kubwera kwake.

< ヨブ 記 36 >