< Proverbi 4 >

1 Ascoltate, o figli, l'istruzione di un padre e fate attenzione per conoscere la verità,
Ananu, mverani malangizo a abambo anu; tcherani khutu kuti mupeze nzeru zodziwira zinthu.
2 poiché io vi do una buona dottrina; non abbandonate il mio insegnamento.
Zimene ndikukuphunzitsani ndi zabwino. Choncho musasiye malangizo anga.
3 Anch'io sono stato un figlio per mio padre, tenero e caro agli occhi di mia madre.
Paja ndinalinso mwana mʼnyumba mwa abambo anga; mwana mmodzi yekha wapamtima pa amayi anga.
4 Egli mi istruiva dicendomi: «Il tuo cuore ritenga le mie parole; custodisci i miei precetti e vivrai.
Ndipo abambo anandiphunzitsa ndi mawu akuti, “Ugwiritse mawu anga pa mtima pako, usunge malamulo anga kuti ukhale ndi moyo.
5 Acquista la sapienza, acquista l'intelligenza; non dimenticare le parole della mia bocca e non allontanartene mai.
Upeze nzeru, upeze nzeru zomvetsa zinthu; usayiwale mawu anga kapena kutayana nawo.
6 Non abbandonarla ed essa ti custodirà, amala e veglierà su di te.
Usasiye nzeru ndipo idzakusunga. Uziyikonda ndipo idzakuteteza.
7 Principio della sapienza: acquista la sapienza; a costo di tutto ciò che possiedi acquista l'intelligenza.
Fundo yayikulu pa za nzeru ndi iyi: upeze nzeru. Kaya pali china chilichonse chimene ungapeze, koma upeze nzeru yomvetsa bwino zinthu.
8 Stimala ed essa ti esalterà, sarà la tua gloria, se l'abbraccerai.
Uyilemekeze nzeruyo ndipo idzakukweza; ikumbatire nzeruyo ndipo idzakupatsa ulemu.
9 Una corona di grazia porrà sul tuo capo, con un diadema di gloria ti cingerà».
Idzayika sangamutu yokongola yamaluwa pamutu pako; idzakupatsa chipewa chaufumu chaulemu.”
10 Ascolta, figlio mio, e accogli le mie parole ed esse moltiplicheranno gli anni della tua vita.
Mwana wanga, umvere ndi kuvomereza zimene ndikunena, ndipo zaka za moyo wako zidzakhala zochuluka.
11 Ti indico la via della sapienza; ti guido per i sentieri della rettitudine.
Ndakuphunzitsa njira yake ya nzeru. Ndakutsogolera mʼnjira zolungama.
12 Quando cammini non saranno intralciati i tuoi passi, e se corri, non inciamperai.
Pamene ukuyenda, mapazi ako sadzawombana; ukamadzathamanga, sudzapunthwa.
13 Attieniti alla disciplina, non lasciarla, pràticala, perché essa è la tua vita.
Ugwiritse zimene ndikukuphunzitsazi osazitaya ayi. Uwasamale bwino pakuti moyo wako wagona pamenepa.
14 Non battere la strada degli empi e non procedere per la via dei malvagi.
Usayende mʼnjira za anthu oyipa kapena kuyenda mʼnjira ya anthu ochimwa.
15 Evita quella strada, non passarvi, stà lontano e passa oltre.
Pewa njira zawo, usayende mʼmenemo; uzilambalala nʼkumangopita.
16 Essi non dormono, se non fanno del male; non si lasciano prendere dal sonno, se non fanno cadere qualcuno;
Pakuti iwo sagona mpaka atachita zoyipa; tulo salipeza mpaka atapunthwitsa munthu wina.
17 mangiano il pane dell'empietà e bevono il vino della violenza.
Paja chakudya chawo ndicho kuchita zoyipa basi ndipo chakumwa chawo ndi chiwawa.
18 La strada dei giusti è come la luce dell'alba, che aumenta lo splendore fino al meriggio.
Koma njira ya anthu olungama ili ngati kuwala kwa mʼbandakucha kumene kumanka kuwalirawalira mpaka dzuwa litafika pa mutu.
19 La via degli empi è come l'oscurità: non sanno dove saranno spinti a cadere.
Koma njira ya anthu oyipa ili ngati mdima wandiweyani; iwo sadziwa chomwe chimawapunthwitsa.
20 Figlio mio, fà attenzione alle mie parole, porgi l'orecchio ai miei detti;
Mwana wanga, mvetsetsa zimene ndikunena; tchera khutu ku mawu anga.
21 non perderli mai di vista, custodiscili nel tuo cuore,
Usayiwale malangizo angawa, koma uwasunge mu mtima mwako.
22 perché essi sono vita per chi li trova e salute per tutto il suo corpo.
Pakuti amapatsa moyo kwa aliyense amene awapeza ndipo amachiritsa thupi lake lonse.
23 Con ogni cura vigila sul cuore perché da esso sgorga la vita.
Ndipotu mtima wako uziwuyangʼanira bwino ndithu pakuti ndiwo magwero a moyo.
24 Tieni lungi da te la bocca perversa e allontana da te le labbra fallaci.
Usiyiretu kuyankhula zokhotakhota; ndipo ulekeretu kuyankhula zinthu zonyansa.
25 I tuoi occhi guardino diritto e le tue pupille mirino diritto davanti a te.
Maso ako ayangʼane patsogolo; uziyangʼana kutsogolo molunjika.
26 Bada alla strada dove metti il piede e tutte le tue vie siano ben rassodate.
Uzilingalira bwino kumene kupita mapazi ako ndipo njira zako zonse zidzakhala zosakayikitsa.
27 Non deviare né a destra né a sinistra, tieni lontano il piede dal male.
Usapatukire kumanja kapena kumanzere; usapite kumene kuli zoyipa.

< Proverbi 4 >