< Dagiti Proverbio 29 >

1 tao a namin-adu a natubngar ngem pasikkilenna ti tengngedna, madadael a dagus ket saanto nga umimbag.
Munthu amene amawumitsabe khosi lake atadzudzulidwa kwambiri, adzawonongeka mwadzidzidzi popanda chomuchiritsa.
2 Inton umadu dagiti agar-aramid iti umno, agrag-o dagiti tattao, ngem no ti nadangkes a tao ti mangiturturay, agsennaay dagiti tattao.
Anthu olungama akamalamulira mʼdziko anthu amakondwa, koma ngati dziko lilamulidwa ndi anthu oyipa mtima anthu amadandaula.
3 Siasinoman a mangayat iti kinasirib ket pagrag-oena ti amana, ngem ti makikadkadua kadagiti balangkantis ket daddaelenna ti kinabaknangna.
Munthu amene amakonda nzeru amasangalatsa abambo ake, koma woyenda ndi akazi achiwerewere amasakaza chuma chake.
4 Patakderen ti ari ti daga babaen iti hustisia, ngem dadaelen daytoy ti tao a dumawdawat iti pasuksok.
Mfumu imalimbitsa dziko poweruza mwachilungamo, koma mfumu imene imawumiriza anthu kuti ayipatse mphatso imawononga dziko.
5 Ti tao a mangpatpatiray-ok iti kaarrubana ket agiwaywayat iti iket para iti sakana.
Munthu woshashalika mnzake, akudziyalira ukonde mapazi ake.
6 Matiliw iti palab-og ti siasinoman a dakes a tao babaen iti bukodna a basol, ngem agkanta ken agrag-o ti tao nga agar-aramid iti umno.
Munthu woyipa amakodwa ndi machimo ake, koma wochita chilungamo amayimba lokoma.
7 Irupir ti agar-aramid iti nasayaat dagiti napanglaw; saan a maawatan ti nadangkes ti kasta a pannakaammo.
Munthu wolungama amasamalira anthu osauka, koma woyipa salabadira zimenezi.
8 Puoran dagiti maag ti siudad, ngem ikkaten dagiti nasirib ti gura.
Anthu onyoza atha kuwutsa ziwawa mu mzinda, koma anthu anzeru amaletsa ukali.
9 No makisinuppiat ti masirib kadagiti maag a tao, agpungtot ken agkatawa isuna, ken awanto ti inana.
Ngati munthu wanzeru atsutsana ndi chitsiru, chitsirucho chimachita phokoso ndi kumangoseka ndipo sipakhala mtendere.
10 Kagura dagiti mawaw ti dara ti awan basolna ket sapulenda ti biag dagiti nalinteg.
Anthu okhetsa magazi amadana ndi munthu wangwiro koma anthu olungama amasamalira moyo wake.
11 Ipakita ti tao a maag ti amin nga ungetna, ngem ti masirib a tao ket igawidna ti ungetna ken pakalmaenna ti bagina.
Munthu wopusa amaonetsa mkwiyo wake, koma munthu wanzeru amadzigwira.
12 No dengdenggen ti mangiturturay ti kinaulbod, agbalinto a nadangkes dagiti amin nga opisyalesna.
Ngati wolamulira amvera zabodza, akuluakulu ake onse adzakhala oyipa.
13 Agpada ti napanglaw ken ti mangidaddadanes a tao, ta agpada nga innikan ni Yahweh iti lawag dagiti matada.
Munthu wosauka ndi munthu wopondereza anzake amafanana pa kuti: Yehova ndiye anawapatsa maso onsewa.
14 No ukomen ti ari dagiti napanglaw babaen iti kinapudno, mapasingkedanto iti agnanayon ti tronona.
Ngati mfumu iweruza osauka moyenera, mpando wake waufumu udzakhazikika nthawi zonse.
15 Mangted iti sirib ti baot ken panangbabalaw, ngem ti ubing a saan a madisdisiplinaan ket ibabainna ti inana.
Ndodo ndi chidzudzulo zimapatsa nzeru koma mwana womulekerera amachititsa amayi ake manyazi.
16 Inton dagiti nadangkes a tao ti agturay, umadu ti basol, ngem makita dagiti agar-aramid iti umno ti pannakaabak dagiti nadangkes a tattao.
Oyipa akamalamulira zoyipa zimachuluka, koma anthu olungama adzaona kugwa kwa anthu oyipawo.
17 Disiplinaam ti anakmo ket paginanaennakanto, mangiyegto isuna iti ragsak iti biagmo.
Umulange mwana wako ndipo adzakupatsa mtendere ndi kusangalatsa mtima wako.
18 No awan ti naipadto a sirmata saan a matengngel dagiti tattao, ngem nagasat ti tao a mangsalsalimetmet iti linteg.
Ngati uthenga wochokera kwa Yehova supezeka anthu amangochita zofuna zawo; koma wodala ndi amene amasunga malamulo.
19 Saanto a mabagbagaan iti maysa a tagabu, ta uray no maawatanna, awanto ti sungbatna.
Munthu wantchito sangalangizidwe ndi mawu okha basi; ngakhale awamvetse mawuwo sadzatha kuchitapo kanthu.
20 Kitaen ti tao a darasudos iti saona? Ad-addu ti namnamma para ti maag ngem isuna.
Ngakhale munthu wa uchitsiru nʼkuti ndiponi popeza chikhulupiriro chilipo kuposa munthu wodziyesa yekha kuti ndi wanzeru poyankhula.
21 Ti mangpanuynoy iti tagabuna sipud pay iti kinaagtutubona, addanto ti parrikut iti kamaudiananna.
Ngati munthu asasatitsa wantchito wake kuyambira ali mwana, potsirizira adzapeza kuti wantchitoyo wasanduka mlowachuma wake.
22 Ti naunget a tao ket mangpataud iti ringgor ken makaaramid iti adu a basol ti amo a naunget.
Munthu wamkwiyo amayambitsa mikangano, ndipo munthu waukali amachita zolakwa zambiri.
23 Ti kinatangsit ti maysa a tao ket isu ti mangipababa kenkuana, ngem ti addaan iti napakumbaba nga espiritu ket mapadayawanto.
Kunyada kwa munthu kudzamutsitsa, koma munthu wodzichepetsa amalandira ulemu.
24 Ti tao a makibingay kadagiti agtatakaw ket kagurgurana ti bukodna a biag; mangmangegna ti lunod ket agulimek.
Woyenda ndi munthu wakuba ndi mdani wa moyo wake womwe; amalumbira koma osawulula kanthu.
25 Ti buteng ti tao ket isu’t pakaisiloanna, ngem maisalakan ti agtaltalek kenni Yahweh.
Kuopa munthu kudzakhala ngati msampha, koma aliyense amene amadalira Yehova adzatetezedwa.
26 Adu ti mangsapul iti rupa ti mangituray, ngem agtaud kenni Yahweh ti hustisia para kenkuana.
Anthu ambiri amafunitsitsa kuti wolamulira awakomere mtima, koma munthu amaweruzidwa mwachilungamo ndi thandizo la Yehova basi.
27 Ti tao a saan a nalinteg ket pakarurudan dagiti agar-aramid iti umno, ngem ti nalinteg ti dalanna ket makarimon kadagiti nadangkes a tattao.
Anthu olungama amanyansidwa ndi anthu achinyengo; koma anthu oyipa amanyansidwa ndi anthu a mtima wowongoka.

< Dagiti Proverbio 29 >