< Dagiti Salmo 73 >

1 Pudno unay a naimbag ti Dios iti Israel, kadagiti addaan iti nasin-aw a puso.
Salimo la Asafu. Mulungu ndi wabwino ndithu kwa Israeli, kwa iwo amene ndi oyera mtima.
2 Ngem no maipapan kaniak, ngan-nganin naikaglis ti sakak; ngan-nganiak a naitibkol
Koma kunena za ine, mapazi anga anali pafupi kuterereka; ndinatsala pangʼono kugwa.
3 gapu ta naapalak kadagiti napalangguad idi nakitak ti kinarang-ay dagiti nadangkes.
Pakuti ndinkachitira nsanje odzitamandira, pamene ndinaona mtendere wa anthu oyipa.
4 Ta awan ti sinagabada nga ut-ot agingga iti ipapatayda, ngem napigsa ken napakanda iti usto.
Iwo alibe zosautsa; matupi awo ndi athanzi ndi amphamvu.
5 Nawayada kadagiti dadagsen dagiti dadduma a tao; saanda a naburburiboran a kas kadagiti dadduma a tattao.
Saona mavuto monga anthu ena; sazunzika ngati anthu ena onse.
6 Ar-arkusan ida ti kinapalangguad a kas iti kuintas nga adda iti tengngedda; kawkawesan ida ti kinaranggas a kas kagay.
Nʼchifukwa chake kunyada kuli monga mkanda wa mʼkhosi mwawo; amadziveka chiwawa.
7 Manipud iti kasta a kinabulsek, rummuar ti basol; sumalpot ti dakes a kapanunotan kadagiti pusoda.
Mʼmitima yawo yokhota mumachokera zolakwa; zoyipa zochokera mʼmaganizo awo sizidziwa malire.
8 Pagang-angawanda ti mangibagbaga iti agkakadakes a banbanag; sipapalangguad nga agpangpangtada iti kinaranggas.
Iwowo amanyogodola ndi kumayankhula zoyipa; mwa kudzikuza kwawo amaopseza ena nʼkumati, “Tikuponderezani.”
9 Agsasaoda iti maibusor kadagiti langit, ken agdakdakiwas dagiti dilada iti entero a daga.
Pakamwa pawo pamayankhula monyoza Mulungu kumwamba ndipo lilime lawo limayenda pa dziko lapansi.
10 Mapan ngarud kadakuada dagiti tattao ti Dios ket dumngegda kadagiti sasaoda.
Nʼchifukwa chake anthu awo amapita kwa iwowo ndi kumwa madzi mochuluka.
11 Kunada, “Kasano koma nga ammo ti Dios? Ammo kadi ti Dios ti mapaspasamak?”
Iwo amati, “Kodi Mulungu angadziwe bwanji? Kodi Wammwambamwamba angadziwe kalikonse?”
12 Kitaem: nadangkes dagitoy a tattao; kanayon nga awan pakaburburiburanda, ken pabaknangda a pabaknang.
Umu ndi mmene oyipa alili; nthawi zonse ali pabwino ndipo chuma chawo chimachulukirachulukira.
13 Pudno a sinalsalluadak ti pusok iti awan kaes-eskanna ken binugbugoak dagiti imak iti kinaawan-ammo.
Ndithudi ine ndawusunga pachabe mtima wanga woyera; pachabe ndasamba mʼmanja mwanga mwa kusalakwa kwanga.
14 Ta iti agmalem, nagsagsagabaak ken iti binigat, mapalpalintegak.
Tsiku lonse ndapeza mavuto; ndakhala ndi kulangidwa mmawa uliwonse.
15 No naibagak nga, “Ibagak dagitoy a banbanag,” ket mabalin a ginulibak daytoy a henerasion dagiti annakmo.
Ndikanati, “Ndidzayankhula motere,” ndikanachita chosakhulupirika kwa ana anu.
16 Nupay pinadaskon nga awaten dagitoy a banbanag, nagbalin a narigat unay daytoy para kaniak.
Pamene ndinayesa kuti ndimvetse zonsezi, zinandisautsa kwambiri
17 Ket simrekak ngarud iti santuario ti Dios, sakonto naawatan ti nagbanaganda.
kufikira nditalowa mʼmalo opatulika a Mulungu; pamenepo ndinamvetsa mathero awo.
18 Sigurado nga ikabilmo ida kadagiti nagalis a disso; ipanmo ida iti pannakadadael.
Zoonadi Inu munawayika pa malo woterera; Mumawagwetsa pansi kuti awonongeke.
19 Anian ti panagbalinda a let-ang iti apagdarikmat! Dumtengda iti kanibusanan ken naggibusda iti kasta unay a buteng.
Mwamsangamsanga iwo amawonongedwa, amasesedwa kwathunthu ndi mantha!
20 Kasda la tagtagainep kalpasan nga agriing ti maysa a tao; O Apo, inton bumangonka, awanto koma ti malagipmo kadagidiay a tagtagainep.
Monga loto pamene wina adzuka, kotero pamene Inu muuka, Inu Ambuye, mudzawanyoza ngati maloto chabe.
21 Ta nagladingit ti pusok, ken nasugatanak iti kasta unay.
Pamene mtima wanga unasautsidwa ndi kuwawidwa mu mzimu mwanga,
22 Awan am-ammok ken kurangak iti pannakaammo; kaslaak ayup nga awan ti riknana iti sangoanam.
ndinali wopusa ndi wosadziwa; ndinali chirombo chopanda nzeru pamaso panu.
23 Nupay kasta, kankanayon a kaduaka; iggemmo ti makannawan nga imak.
Komabe ineyo ndili ndi Inu nthawi zonse; mumandigwira dzanja langa lamanja.
24 Tarabayennak babaen kadagiti balakadmo ket kalpasanna, awatennak iti gloriam.
Inu mumanditsogolera ndi malangizo anu ndipo pambuyo pake mudzanditenga ku ulemerero.
25 Adda aya masarakak sadi langit a kas kenka? Awan siasinoman ditoy daga a tarigagayko no di ket sika.
Kodi kumwamba ndili ndi yani kupatula Inu? Ndipo dziko lapansi lilibe chilichonse chimene ndimachilakalaka koposa Inuyo.
26 Kumapsot ti lasag ken pusok, ngem ti Dios ti pigsa ti pusok iti agnanayon.
Thupi ndi mtima wanga zitha kufowoka, koma Mulungu ndiye mphamvu ya mtima wanga ndi cholandira changa kwamuyaya.
27 Mapukawto dagidiay adayo kenka; dadaelemto amin dagiti saan a napudno kenka.
Iwo amene ali kutali ndi Inu adzawonongeka; Inu mumawononga onse osakhulupirika pamaso panu.
28 Ngem no maipapan kaniak, ti laeng masapul nga aramidek ket ti umasideg iti Dios. Pinagbalinko a kamangko ni Yahweh nga Apo. Iwaragawagko dagiti amin nga aramidmo.
Koma kunena za Ine ndi kwabwino kukhala pafupi ndi Mulungu. Ndatsimikiza kuti Ambuye Yehova ndiwo pothawirapo panga ndipo ndidzalalika ntchito zanu zonse.

< Dagiti Salmo 73 >