< Nehemias 1 >

1 Dagiti sasao ni Nehemias a putot ni Hacalias: Ita, napasamak nga iti bulan ti Kislev, iti maika-duapulo a tawen, bayat nga addaak iti nasarekedkedan a siudad ti Susa,
Awa ndi mawu a Nehemiya mwana wa Hakaliya: Pa mwezi wa Kisilevi, chaka cha makumi awiri, pamene ndinali mu mzinda wa Susa,
2 ket immay ti maysa kadagiti kabsatko a lallaki a ni Hanani, a kaduana dagiti sumagmamano a tattao ti Juda, ket sinaludsodko kadakuada ti maipanggep kadagiti Judio a nakalibas, dagiti nabatbati a Judio nga adda sadiay, ken maipanggep iti Jerusalem.
Hanani mmodzi mwa abale anga, anabwera ndi anthu ena kuchokera ku Yuda, ndipo ine ndinawafunsa za Ayuda otsala amene sanatengedwe ukapolo, ndiponso za mzinda wa Yerusalemu.
3 Kinunada kaniak, “Dagiti adda iti probinsia a nakalasat iti pannakaibalud ket kasta unay ti panagsagaba ken pannakaibabainda gapu ta narba ti pader ti Jerusalem, ken napuoran dagiti ruangan daytoy.”
Anandiyankha kuti, “Amene sanatengedwe ukapolo aja ali pa mavuto aakulu ndipo ali ndi manyazi. Khoma la Yerusalemu ndilogamukagamuka ndipo zipata zake zinatenthedwa ndi moto.”
4 Ket apaman a nangngegko dagitoy a sasao, nagtugawak ket nagsangitak, adu nga aldaw a nagladladingitak, nagay-ayunar ken nagkarkararagak iti sangoanan ti Dios ti langit.
Nditamva zimenezi, ndinakhala pansi ndi kuyamba kulira. Ndinalira kwa masiku angapo. Ndinkasala zakudya ndi kumapemphera pamaso pa Mulungu Wakumwamba.
5 Kinunak, “O Yahweh, sika ti Dios ti langit, ti Dios a naindaklan ken nakakaskasdaaw, a napudno iti katulaganna ken kinamanangngaasina kadagiti mangipatpateg kenkuana ken mangtungtungpal kadagiti bilinna.
Ndinkati: “Inu Yehova, Mulungu wakumwamba, Mulungu wamkulu ndi woopsa. Mumasunga pangano ndi kuonetsa chikondi chosasinthika kwa onse amene amakukondani ndi kumvera malamulo anu.
6 Denggem ti kararagko ken lukatam dagiti matam tapno mangngegmo ti kararag ti adipenmo nga ikararagko ita iti sangoanam iti aldaw ken rabii para kadagiti tattao ti Israel nga adipenmo. Ak-aklonek dagiti basol dagiti tattao ti Israel, a nagbasolanmi kenka. Nagbasolak ken ti balay ti amak.
Tcherani khutu lanu ndi kutsekula maso anu kuti mumve pemphero la mtumiki wanune limene ndikupemphera usana ndi usiku pamaso panu kupempherera Aisraeli, atumiki anu. Ndikuvomereza machimo a Aisraeli amene tinakuchimwirani. Ndithu, ine ndi banja la makolo anga tinakuchimwirani.
7 Nagtignaykami a sidadangkes kenka, ken saanmi a tinungpal dagiti bilin, dagiti alagaden ken dagiti paglintegan nga imbilinmo kenni Moises nga adipenmo.
Ife tinakuchitirani zoyipa zambiri. Sitinamvere mawu anu, malamulo ndi malangizo anu amene munapereka kwa mtumiki wanu Mose.
8 Lagipem ti sao nga imbilinmo kenni Moises nga adipenmo, 'No agbalinkayo a saan a napudno, iwaraskayonto kadagiti nasion,
“Kumbukirani mawu amene munawuza mtumiki wanu Mose akuti, ‘Ngati mukhala osakhulupirika, ndidzakubalalitsani pakati pa mitundu ina.
9 ngem no agsublikayo kaniak ken surotenyo dagiti bilbilinko ken aramidenyo dagitoy, uray no naiwaras dagiti tattaoyo agingga iti kaadaywan a lugar, ummongekto ida manipud sadiay ket ipankonto ida iti dayta a lugar a pinilik a pagtalinaedan ti naganko.'
Koma mukabwerera kwa Ine, mukamvera malamulo anga ndi kuwatsatadi, ndiye kuti ngakhale anthu anu atabalalika kutali chotani, Ine ndidzawasonkhanitsa kuchokera kumeneko ndi kubwera nawo ku malo amene ndinasankha kuti azidzayitanira dzina langa.’
10 Ita, isuda dagiti adipenmo ken tattaom nga insalakanmo babaen iti naindaklan a pannakabalinmo ken iti bileg ti imam.
“Iwo ndi atumiki anu ndi anthu anu, amene munawawombola ndi mphamvu yanu yayikulu ndi dzanja lanu lamphamvu.
11 O Yahweh, agpakpakaasiak kenka, denggem ita ti kararag ti adipenmo, ken iti kararag dagiti adipenmo a naragsak nga agdayaw iti naganmo. Pagballigiem ti adipenmo ita nga aldaw ken ipaayam isuna ti asi iti imatang daytoy a tao.” Agserserbiak idi a kas mangimatmaton ti pannakaidasar iti arak ti ari.
Inu Ambuye tcherani khutu lanu kuti mumve pemphero la mtumiki wanune ndiponso pemphero la atumiki anu amene amakondwera kuchitira ulemu dzina lanu. Lolani kuti mtumiki wanune zinthu zindiyendere bwino lero ndi kuti mfumu indichitire chifundo.” Nthawi imeneyi nʼkuti ndili woperekera zakumwa kwa mfumu.

< Nehemias 1 >