< תהילים 5 >

למנצח אל-הנחילות מזמור לדוד ב אמרי האזינה יהוה בינה הגיגי 1
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe zoyimbira za zitoliro. Salimo la Davide. Tcherani khutu ku mawu anga, Inu Yehova, ganizirani za kusisima kwanga
הקשיבה לקול שועי--מלכי ואלהי כי-אליך אתפלל 2
Mverani kulira kwanga kofuna thandizo, Mfumu yanga ndi Mulungu wanga, pakuti kwa Inu, ine ndikupemphera.
יהוה--בקר תשמע קולי בקר אערך-לך ואצפה 3
Mmawa, Yehova mumamva mawu anga; Mmawa ndimayala zopempha zanga pamaso panu ndi kudikira mwachiyembekezo.
כי לא אל חפץ רשע אתה לא יגרך רע 4
Inu si Mulungu amene mumasangalala ndi zoyipa; choyipa sichikhala pamaso panu.
לא-יתיצבו הוללים לנגד עיניך שנאת כל-פעלי און 5
Onyada sangathe kuyima pamaso panu; Inu mumadana ndi onse ochita zoyipa.
תאבד דברי כזב איש-דמים ומרמה יתעב יהוה 6
Mumawononga iwo amene amanena mabodza; anthu akupha ndi achinyengo, Yehova amanyansidwa nawo.
ואני--ברב חסדך אבוא ביתך אשתחוה אל-היכל-קדשך ביראתך 7
Koma Ine, mwa chifundo chanu chachikulu, ndidzalowa mʼNyumba yanu; mwa ulemu ndidzaweramira pansi kuyangʼana ku Nyumba yanu yoyera.
יהוה נחני בצדקתך--למען שוררי הושר (הישר) לפני דרכך 8
Tsogolereni Inu Yehova, mwa chilungamo chanu chifukwa cha adani anga ndipo wongolani njira yanu pamaso panga.
כי אין בפיהו נכונה--קרבם הוות קבר-פתוח גרנם לשונם יחליקון 9
Palibe mawu ochokera mʼkamwa mwawo amene angadalirike; mtima wawo wadzaza ndi chiwonongeko. Kummero kwawo kuli ngati manda apululu; ndi lilime lawo amayankhula zachinyengo.
האשימם אלהים-- יפלו ממעצותיהם ברב פשעיהם הדיחמו-- כי-מרו בך 10
Lengezani kuti ndi olakwa, Inu Mulungu! Zochita zawo zoyipa zikhale kugwa kwawo. Achotseni pamaso panu chifukwa cha machimo awo ambiri, pakuti awukira Inu.
וישמחו כל-חוסי בך לעולם ירננו-- ותסך עלימו ויעלצו בך אהבי שמך 11
Koma lolani kuti onse amene apeza chitetezo mwa Inu akondwere; lolani kuti aziyimba nthawi zonse chifukwa cha chimwemwe. Aphimbeni ndi chitetezo chanu, iwo amene amakonda dzina lanu akondwere mwa Inu.
כי-אתה תברך צדיק יהוה--כצנה רצון תעטרנו 12
Ndithu, Inu Yehova, mumadalitsa olungama; mumawazungulira ndi kukoma mtima kwanu ngati chishango.

< תהילים 5 >