< מִשְׁלֵי 12 >
אהב מוסר אהב דעת ושונא תוכחת בער | 1 |
Munthu amene amakonda mwambo amakonda kudziwa zinthu, koma amene amadana ndi chidzudzulo ndi wopusa.
טוב--יפיק רצון מיהוה ואיש מזמות ירשיע | 2 |
Munthu wabwino amapeza kuyanja pamaso pa Yehova, koma Yehova amatsutsa munthu wochita chinyengo.
לא-יכון אדם ברשע ושרש צדיקים בל-ימוט | 3 |
Munthu sangakhazikike bwino pochita zoyipa, koma maziko a anthu olungama sadzatekeseka.
אשת-חיל עטרת בעלה וכרקב בעצמותיו מבישה | 4 |
Mkazi wakhalidwe labwino ali ngati chipewa chaufumu kwa mwamuna wake, koma mkazi wochititsa manyazi ali ngati chilonda cha mafinya kwa mwamuna wake.
מחשבות צדיקים משפט תחבלות רשעים מרמה | 5 |
Maganizo a anthu olungama ndi owongoka, koma malangizo a anthu oyipa ndi achinyengo.
דברי רשעים ארב-דם ופי ישרים יצילם | 6 |
Mawu a anthu oyipa ndi ophetsa, koma mawu a anthu olungama amapulumutsa.
הפוך רשעים ואינם ובית צדיקים יעמד | 7 |
Anthu oyipa amagonjetsedwa ndipo amayiwalika, koma nyumba ya anthu olungama idzakhalabe.
לפי-שכלו יהלל-איש ונעוה-לב יהיה לבוז | 8 |
Munthu amatamandidwa malinga ndi nzeru zake, koma anthu amitima yokhota amanyozedwa.
טוב נקלה ועבד לו-- ממתכבד וחסר-לחם | 9 |
Nʼkwabwino kukhala munthu wonyozeka koma wodzigwirira ntchito nʼkukhala ndi zonse zofunika, kuposa kukhala wodzikuza koma ulibe ndi chakudya chomwe.
יודע צדיק נפש בהמתו ורחמי רשעים אכזרי | 10 |
Munthu wolungama amasamalira moyo wa ziweto zake, koma chifundo cha munthu woyipa ndi chakhanza.
עבד אדמתו ישבע-לחם ומרדף ריקים חסר-לב | 11 |
Wolima mʼmunda mwake mwakhama adzakhala ndi chakudya chochuluka, koma wotsata zopanda pake alibe nzeru.
חמד רשע מצוד רעים ושרש צדיקים יתן | 12 |
Munthu woyipa amalakalaka zofunkha za anthu oyipa, koma mizu ya anthu olungama imabereka zipatso.
בפשע שפתים מוקש רע ויצא מצרה צדיק | 13 |
Munthu woyipa amakodwa mu msampha wa mayankhulidwe ake oyipa; koma munthu wolungama amatuluka mʼmavuto.
מפרי פי-איש ישבע-טוב וגמול ידי-אדם ישוב (ישיב) לו | 14 |
Munthu amakhala ndi zabwino zambiri chifukwa cha mawu ake ndipo ntchito zimene munthu agwira ndi manja ake zimamupindulira.
דרך אויל ישר בעיניו ושמע לעצה חכם | 15 |
Zochita za chitsiru mwini wakeyo amaziona ngati zabwino, koma munthu wanzeru amamvera malangizo.
אויל--ביום יודע כעסו וכסה קלון ערום | 16 |
Mkwiyo wa chitsiru umadziwika nthawi yomweyo, koma munthu wanzeru sasamala kunyozedwa.
יפיח אמונה יגיד צדק ועד שקרים מרמה | 17 |
Woyankhula zoona amapereka umboni woona, koma mboni yabodza imafotokoza zonama.
יש בוטה כמדקרות חרב ולשון חכמים מרפא | 18 |
Munthu woyankhula mosasamala mawu ake amalasa ngati lupanga, koma mawu a munthu wanzeru amachiritsa.
שפת-אמת תכון לעד ועד-ארגיעה לשון שקר | 19 |
Mawu woona amakhala mpaka muyaya koma mawu abodza sakhalitsa.
מרמה בלב-חרשי רע וליעצי שלום שמחה | 20 |
Mʼmitima ya anthu amene amakonza zoyipa muli chinyengo; koma anthu olimbikitsa za mtendere amakhala ndi chimwemwe.
לא-יאנה לצדיק כל-און ורשעים מלאו רע | 21 |
Palibe choyipa chimene chimagwera munthu wolungama, koma munthu woyipa mavuto samuthera.
תועבת יהוה שפתי-שקר ועשי אמונה רצונו | 22 |
Pakamwa pa bodza pamamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi anthu oyankhula zoona.
אדם ערום כסה דעת ולב כסילים יקרא אולת | 23 |
Munthu wochenjera amabisa nzeru zake, koma munthu wopusa amaonetsa uchitsiru wake poyera.
יד-חרוצים תמשול ורמיה תהיה למס | 24 |
Ogwira ntchito mwakhama adzalamulira, koma aulesi adzakhala ngati kapolo.
דאגה בלב-איש ישחנה ודבר טוב ישמחנה | 25 |
Nkhawa imakhala ngati katundu wolemera mu mtima mwa munthu, koma mawu abwino amamusangalatsa.
יתר מרעהו צדיק ודרך רשעים תתעם | 26 |
Munthu wolungama amatsogolera mnansi wake, koma ntchito za anthu oyipa zimawasocheretsa.
לא-יחרך רמיה צידו והון-אדם יקר חרוץ | 27 |
Munthu waulesi sapeza chimene akufuna, koma munthu wakhama amapeza chuma chamtengo wapatali.
בארח-צדקה חיים ודרך נתיבה אל-מות | 28 |
Mʼnjira yachilungamo muli moyo; koma njira ya munthu woyipa imafikitsa ku imfa.