< מִשְׁלֵי 12 >

אהב מוסר אהב דעת ושונא תוכחת בער 1
Munthu amene amakonda mwambo amakonda kudziwa zinthu, koma amene amadana ndi chidzudzulo ndi wopusa.
טוב--יפיק רצון מיהוה ואיש מזמות ירשיע 2
Munthu wabwino amapeza kuyanja pamaso pa Yehova, koma Yehova amatsutsa munthu wochita chinyengo.
לא-יכון אדם ברשע ושרש צדיקים בל-ימוט 3
Munthu sangakhazikike bwino pochita zoyipa, koma maziko a anthu olungama sadzatekeseka.
אשת-חיל עטרת בעלה וכרקב בעצמותיו מבישה 4
Mkazi wakhalidwe labwino ali ngati chipewa chaufumu kwa mwamuna wake, koma mkazi wochititsa manyazi ali ngati chilonda cha mafinya kwa mwamuna wake.
מחשבות צדיקים משפט תחבלות רשעים מרמה 5
Maganizo a anthu olungama ndi owongoka, koma malangizo a anthu oyipa ndi achinyengo.
דברי רשעים ארב-דם ופי ישרים יצילם 6
Mawu a anthu oyipa ndi ophetsa, koma mawu a anthu olungama amapulumutsa.
הפוך רשעים ואינם ובית צדיקים יעמד 7
Anthu oyipa amagonjetsedwa ndipo amayiwalika, koma nyumba ya anthu olungama idzakhalabe.
לפי-שכלו יהלל-איש ונעוה-לב יהיה לבוז 8
Munthu amatamandidwa malinga ndi nzeru zake, koma anthu amitima yokhota amanyozedwa.
טוב נקלה ועבד לו-- ממתכבד וחסר-לחם 9
Nʼkwabwino kukhala munthu wonyozeka koma wodzigwirira ntchito nʼkukhala ndi zonse zofunika, kuposa kukhala wodzikuza koma ulibe ndi chakudya chomwe.
יודע צדיק נפש בהמתו ורחמי רשעים אכזרי 10
Munthu wolungama amasamalira moyo wa ziweto zake, koma chifundo cha munthu woyipa ndi chakhanza.
עבד אדמתו ישבע-לחם ומרדף ריקים חסר-לב 11
Wolima mʼmunda mwake mwakhama adzakhala ndi chakudya chochuluka, koma wotsata zopanda pake alibe nzeru.
חמד רשע מצוד רעים ושרש צדיקים יתן 12
Munthu woyipa amalakalaka zofunkha za anthu oyipa, koma mizu ya anthu olungama imabereka zipatso.
בפשע שפתים מוקש רע ויצא מצרה צדיק 13
Munthu woyipa amakodwa mu msampha wa mayankhulidwe ake oyipa; koma munthu wolungama amatuluka mʼmavuto.
מפרי פי-איש ישבע-טוב וגמול ידי-אדם ישוב (ישיב) לו 14
Munthu amakhala ndi zabwino zambiri chifukwa cha mawu ake ndipo ntchito zimene munthu agwira ndi manja ake zimamupindulira.
דרך אויל ישר בעיניו ושמע לעצה חכם 15
Zochita za chitsiru mwini wakeyo amaziona ngati zabwino, koma munthu wanzeru amamvera malangizo.
אויל--ביום יודע כעסו וכסה קלון ערום 16
Mkwiyo wa chitsiru umadziwika nthawi yomweyo, koma munthu wanzeru sasamala kunyozedwa.
יפיח אמונה יגיד צדק ועד שקרים מרמה 17
Woyankhula zoona amapereka umboni woona, koma mboni yabodza imafotokoza zonama.
יש בוטה כמדקרות חרב ולשון חכמים מרפא 18
Munthu woyankhula mosasamala mawu ake amalasa ngati lupanga, koma mawu a munthu wanzeru amachiritsa.
שפת-אמת תכון לעד ועד-ארגיעה לשון שקר 19
Mawu woona amakhala mpaka muyaya koma mawu abodza sakhalitsa.
מרמה בלב-חרשי רע וליעצי שלום שמחה 20
Mʼmitima ya anthu amene amakonza zoyipa muli chinyengo; koma anthu olimbikitsa za mtendere amakhala ndi chimwemwe.
לא-יאנה לצדיק כל-און ורשעים מלאו רע 21
Palibe choyipa chimene chimagwera munthu wolungama, koma munthu woyipa mavuto samuthera.
תועבת יהוה שפתי-שקר ועשי אמונה רצונו 22
Pakamwa pa bodza pamamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi anthu oyankhula zoona.
אדם ערום כסה דעת ולב כסילים יקרא אולת 23
Munthu wochenjera amabisa nzeru zake, koma munthu wopusa amaonetsa uchitsiru wake poyera.
יד-חרוצים תמשול ורמיה תהיה למס 24
Ogwira ntchito mwakhama adzalamulira, koma aulesi adzakhala ngati kapolo.
דאגה בלב-איש ישחנה ודבר טוב ישמחנה 25
Nkhawa imakhala ngati katundu wolemera mu mtima mwa munthu, koma mawu abwino amamusangalatsa.
יתר מרעהו צדיק ודרך רשעים תתעם 26
Munthu wolungama amatsogolera mnansi wake, koma ntchito za anthu oyipa zimawasocheretsa.
לא-יחרך רמיה צידו והון-אדם יקר חרוץ 27
Munthu waulesi sapeza chimene akufuna, koma munthu wakhama amapeza chuma chamtengo wapatali.
בארח-צדקה חיים ודרך נתיבה אל-מות 28
Mʼnjira yachilungamo muli moyo; koma njira ya munthu woyipa imafikitsa ku imfa.

< מִשְׁלֵי 12 >