< איוב 39 >
הידעת--עת לדת יעלי-סלע חלל אילות תשמר | 1 |
“Kodi iwe umadziwa nthawi imene mbalale yayikazi imaswera? Kodi umaonerera pamene nswala ikubala?
תספר ירחים תמלאנה וידעת עת לדתנה | 2 |
Kodi umawerenga miyezi imene zimakhala ndi bere? Kodi nthawi imene zimaswana iwe umayidziwa?
תכרענה ילדיהן תפלחנה חבליהם תשלחנה | 3 |
Zimakhala tsonga ndi kuswa ana awo; pamenepo ululu wobereka nʼkutha.
יחלמו בניהם ירבו בבר יצאו ולא-שבו למו | 4 |
Ana a nyamazi amakhala ndi mphamvu ndipo amakulira mʼthengo; kenaka amachoka ndipo sabwereranso.
מי-שלח פרא חפשי ומסרות ערוד מי פתח | 5 |
“Kodi bulu wakuthengo amamupatsa ndani ufulu wongodziyendera? Ndani amamasula zingwe zake?
אשר-שמתי ערבה ביתו ומשכנותיו מלחה | 6 |
Ine ndinamupatsa chipululu kuti chikhale mudzi wake, nthaka ya mchere kuti ikhale malo ake okhalamo
ישחק להמון קריה תשאות נגש לא ישמע | 7 |
Iye amakhala kutali ndi phokoso la mu mzinda; ndipo samva kufuwula kwa oyendetsa nyama zakatundu.
יתור הרים מרעהו ואחר כל-ירוק ידרוש | 8 |
Amayendayenda mʼmapiri kudya msipu ndipo amafunafuna msipu uliwonse wobiriwira.
היאבה רים עבדך אם-ילין על-אבוסך | 9 |
“Kodi njati ingavomere kukutumikira? Kodi ingagone mu gome lako usiku?
התקשר-רים בתלם עבתו אם-ישדד עמקים אחריך | 10 |
Kodi ungathe kuyimanga ndi zingwe kuti izilima? Kodi ingasalaze nthumbira mʼmunda mwako?
התבטח-בו כי-רב כחו ותעזב אליו יגיעך | 11 |
Kodi ungadalire njatiyo chifukwa champhamvu zake? Kodi ungayilekere kuti igwire ntchito zako zolemetsa?
התאמין בו כי-ישוב (ישיב) זרעך וגרנך יאסף | 12 |
Kodi ungadalire kuti idzakubweretsera tirigu wako ndi kumuyika ku malo opunthira?
כנף-רננים נעלסה אם-אברה חסידה ונצה | 13 |
“Nthiwatiwa imakupiza mapiko ake monyadira, koma mapikowo sangafanane ndi mapiko ndi nthenga za kakowa.
כי-תעזב לארץ בציה ועל-עפר תחמם | 14 |
Nthiwatiwa imakwirira mazira ake pansi ndipo amafundidwa ndi nthaka,
ותשכח כי-רגל תזורה וחית השדה תדושה | 15 |
nthiwatiwayo sidera nkhawa kuti mazira ake angathe kuswanyidwa, ndi kuti nyama zakuthengo zitha kuwaponda.
הקשיח בניה ללא-לה לריק יגיעה בלי-פחד | 16 |
Nthiwatiwa imachitira nkhanza ana ake ngati anawo si ake; Imayiwala zoti inavutika powabala.
כי-השה אלוה חכמה ולא-חלק לה בבינה | 17 |
Chifukwa Mulungu anayimana nzeru, simvetsa kanthu kalikonse.
כעת במרום תמריא תשחק לסוס ולרכבו | 18 |
Komatu nthiwatiwa ikadzambatuka ndi kuyamba kuthamanga, imamusiya kutali kavalo ndi wokwerapo wake.
התתן לסוס גבורה התלביש צוארו רעמה | 19 |
“Kodi ndiwe amene umamupatsa mphamvu kavalo kapena kumuveka chenjerere mʼkhosi mwake?
התרעישנו כארבה הוד נחרו אימה | 20 |
Kodi ndiwe amene umalipatsa dzombe ulemerero wolumphira, ukali wake nʼkumachititsa mantha?
יחפרו בעמק וישיש בכח יצא לקראת-נשק | 21 |
Iye amalumphalumpha moopseza, kukondwerera mphamvu zake, ndipo amapita ku nkhondo ndi mphamvu zake zonse.
ישחק לפחד ולא יחת ולא-ישוב מפני-חרב | 22 |
Iye sachita mantha, saopa chilichonse; sabwerera mʼmbuyo akaona lupanga.
עליו תרנה אשפה להב חנית וכידון | 23 |
Zida zankhondo zimachita kwichikwichi mʼchimake pambali pake pamodzi ndi mkondo wonyezimira ndi nthungo.
ברעש ורגז יגמא-ארץ ולא-יאמין כי-קול שופר | 24 |
Kavaloyo amanjenjemera ndi ukali ndi kulumphalumpha; satha kungoyima pamene wamva kulira kwa lipenga.
בדי שפר יאמר האח-- ומרחוק יריח מלחמה רעם שרים ותרועה | 25 |
Lipenga likalira amati, ‘Twee!’ Amamva fungo la nkhondo ali patali, kufuwula kwa anthu olamulira nkhondo ndi mfuwu wankhondo.
המבינתך יאבר-נץ יפרש כנפו לתימן | 26 |
“Kodi kabawi amawuluka ndi nzeru zako, ndi kutambasula mapiko ake kupita kummwera?
אם-על-פיך יגביה נשר וכי ירים קנו | 27 |
Kodi umalamulira chiwombankhanga ndiwe kuti chiziwuluka ndi kumanga chisa chake pamwamba penipeni?
סלע ישכן ויתלנן-- על שן-סלע ומצודה | 28 |
Chimakhala pa phiri ndipo chimakhala pamenepo usiku; chimakhala pa msonga penipeni pa mwala.
משם חפר-אכל למרחוק עיניו יביטו | 29 |
Chili pamenepo chimayangʼanayangʼana choti chigwire kuti chidye; maso ake amachionera patali chinthucho.
ואפרחו יעלעו-דם ובאשר חללים שם הוא | 30 |
Ana ake amayamwa magazi, ndipo kumene kuli mitembo ndiko chimapezeka.”