< איוב 33 >

ואולם--שמע-נא איוב מלי וכל-דברי האזינה 1
“Koma tsopano, inu abambo Yobu chonde mverani mawu anga; mutcherere khutu zonse zimene ndinene.
הנה-נא פתחתי פי דברה לשוני בחכי 2
Tsopano ndiyamba kuyankhula; mawu anga ali pa msonga ya lilime langa.
ישר-לבי אמרי ודעת שפתי ברור מללו 3
Mawu anga akuchokera mu mtima wolungama; pakamwa panga pakuyankhula zoonadi zimene ndikuzidziwa.
רוח-אל עשתני ונשמת שדי תחיני 4
Mzimu wa Mulungu wandiwumba, mpweya wa Wamphamvuzonse umandipatsa moyo.
אם-תוכל השיבני ערכה לפני התיצבה 5
Mundiyankhe ngati mungathe; konzekani tsopano kuti munditsutse.
הן-אני כפיך לאל מחמר קרצתי גם-אני 6
Ine ndili monga inu pamaso pa Mulungu; nanenso ndinachokera ku dothi.
הנה אמתי לא תבעתך ואכפי עליך לא-יכבד 7
Musachite mantha ndipo musandiope ayi, Ine sindikupanikizani kwambiri ayi.
אך אמרת באזני וקול מלין אשמע 8
“Koma inu mwayankhula ine ndikumva, ndamva mawu anuwo onena kuti,
זך אני בלי-פשע חף אנכי ולא עון לי 9
‘Ndine wolungama mtima ndi wopanda tchimo; ndine woyera mtima ndipo ndilibe cholakwa.
הן תנואות עלי ימצא יחשבני לאויב לו 10
Komatu Mulungu wapeza zifukwa zoti anditsutsire nazo; Iye akundiyesa ngati mdani wake.
ישם בסד רגלי ישמר כל-ארחתי 11
Iyeyo wamanga mapazi anga mʼzigologolo, akulonda mayendedwe anga onse.’
הן-זאת לא-צדקת אענך כי-ירבה אלוה מאנוש 12
“Koma ine ndi kuti kwa inu, inuyo simukukhoza pa zimenezi, pakuti Mulungu ndi wamkulu kupambana munthu.
מדוע אליו ריבות כי כל-דבריו לא יענה 13
Chifukwa chiyani mukudandaula kwa Iye kuti sayankha mawu ena aliwonse a munthu?
כי-באחת ידבר-אל ובשתים לא ישורנה 14
Pajatu Mulungu amayankhula mwa njira zosiyanasiyana, ngakhale munthu sazindikira zimenezi.
בחלום חזיון לילה--בנפל תרדמה על-אנשים בתנומות עלי משכב 15
Mʼmaloto, mʼmasomphenya usiku, pamene anthu ali mʼtulo tofa nato pamene akungosinza chabe pa bedi,
אז יגלה אזן אנשים ובמסרם יחתם 16
amawanongʼoneza mʼmakutu ndi kuwaopseza ndi machenjezo ake,
להסיר אדם מעשה וגוה מגבר יכסה 17
kumuchotsa munthu ku zoyipa, ndi kuthetseratu kunyada kwake,
יחשך נפשו מני-שחת וחיתו מעבר בשלח 18
kumulanditsa munthu ku manda, kuti moyo wake usawonongeke ndi lupanga.
והוכח במכאוב על-משכבו וריב (ורוב) עצמיו אתן 19
“Mwina Mulungu amalanga munthu ndi matenda ndi ululu ali pa bedi pake, nthawiyo thupi lake lonse limangophwanya,
וזהמתו חיתו לחם ונפשו מאכל תאוה 20
kuti asakhalenso ndi chilakolako cha chakudya, ndipo amanyansidwa ndi chakudya chabwino chomwe.
יכל בשרו מראי ושפי (ושפו) עצמתיו לא ראו 21
Thupi lake limawonda ndipo mafupa ake, omwe anali obisika, tsopano amaonekera poyera.
ותקרב לשחת נפשו וחיתו לממתים 22
Munthuyo amayandikira ku manda, moyo wake umayandikira kwa amene amabweretsa imfa.
אם-יש עליו מלאך--מליץ אחד מני-אלף להגיד לאדם ישרו 23
“Koma patakhala mngelo ngati mthandizi, mmodzi mwa ambirimbiri oterewa, adzafotokoza zimene zili zoyenera,
ויחננו--ויאמר פדעהו מרדת שחת מצאתי כפר 24
kudzamukomera mtima ndi kunena kuti, ‘Mupulumutseni kuti asapite ku manda; ine ndapeza cholowa mʼmalo mwa moyo wake,’
רטפש בשרו מנער ישוב לימי עלומיו 25
pamenepo thupi lake lidzasanduka lasee ngati la mwana; ndipo adzabwezeretsedwanso kukhala ngati mʼmasiku a unyamata wake.
יעתר אל-אלוה וירצהו וירא פניו בתרועה וישב לאנוש צדקתו 26
Akapemphera kwa Mulungu, iyeyo adzalandiridwa. Mulungu adzamulandira mwa chimwemwe ndipo adzamubwezeretsa pamalo ake oyamba.
ישר על-אנשים ויאמר חטאתי וישר העויתי ולא-שוה לי 27
Ndipo adzabwera kwa anzake ndi kunena kuti, ‘Ndinachimwa ndipo sindinachite zolungama, koma sindinalangidwe koyenerana ndi kuchimwa kwanga.
פדה נפשי (נפשו) מעבר בשחת וחיתי (וחיתו) באור תראה 28
Iye anapulumutsa moyo wanga kuti usapite ku manda, ndipo ndidzakhala ndi moyo ndi kuonanso kuwala kwa dzuwa.’
הן-כל-אלה יפעל-אל-- פעמים שלוש עם-גבר 29
“Mulungu amachita zonsezi kwa munthu kawirikawiri,
להשיב נפשו מני-שחת-- לאור באור החיים 30
kupulumutsa moyo wa munthuyo ku manda, kuti athe kuonanso kuwala kwa moyo.
הקשב איוב שמע-לי החרש ואנכי אדבר 31
“Abambo Yobu, tcherani khutu ndipo mundimvere; khalani chete kuti ndiyankhule.
אם-יש-מלין השיבני דבר כי-חפצתי צדקך 32
Ngati muli nʼchoti munene, ndiyankheni; yankhulani, pakuti ine ndikufuna mupezeke wolungama.
אם-אין אתה שמע-לי החרש ואאלפך חכמה 33
Koma ngati sichoncho, mundimvere; khalani chete ndipo ine ndidzakuphunzitsani nzeru.”

< איוב 33 >