< Psalm 135 >

1 Hallelujah! Lobet den Namen des HERRN! Lobet ihn, ihr Knechte des HERRN,
Tamandani Yehova. Tamandani dzina la Yehova; mutamandeni, inu atumiki a Yehova,
2 die ihr stehet im Hause des HERRN, in den Vorhöfen des Hauses unsres Gottes!
amene mumatumikira mʼnyumba ya Yehova, mʼmabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.
3 Lobet den HERRN, denn gütig ist der HERR; singet seinem Namen, denn er ist lieblich!
Tamandani Yehova, pakuti Yehova ndi wabwino; imbani nyimbo zotamanda dzina lake, pakuti nʼkokoma kutero,
4 Denn der HERR hat sich Jakob erwählt, Israel zu seinem besonderen Eigentum.
Pakuti Yehova wasankha Yakobo kuti akhale wake, Israeli kuti akhale chuma chake chapamtima.
5 Denn ich weiß, daß der HERR groß ist; ja, unser Herr ist größer als alle Götter.
Ndikudziwa kuti Yehova ndi wamkulu, kuti Ambuye athu ndi wamkulu kuposa milungu yonse.
6 Alles, was er will, das tut der HERR im Himmel und auf Erden, im Meer und in allen Tiefen:
Yehova amachita chilichonse chimene chimamukomera, kumwamba ndi dziko lapansi, ku nyanja zazikulu ndi ku malo ake onse akuya.
7 Er führt Wolken herauf vom Ende der Erde, macht Blitze zum Regen und holt den Wind aus seinen Speichern hervor.
Iye amatulutsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi, amatumiza zingʼaningʼani pamodzi ndi mvula ndipo amatulutsa mphepo ku malo ake osungiramo.
8 Er schlug Ägyptens Erstgeburten, vom Menschen bis zum Vieh;
Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, ana oyamba kubadwa a anthu ndi nyama.
9 er sandte Zeichen und Wunder in deine Mitte, o Ägyptenland, gegen den Pharao und alle seine Knechte;
Iye anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa pakati pako, iwe Igupto, kutsutsana ndi Farao pamodzi ndi atumiki ake onse.
10 er schlug große Nationen und tötete mächtige Könige;
Iye anakantha mitundu yambiri ya anthu ndi kupha mafumu amphamvu:
11 Sihon, den König der Amoriter, und Og, den König zu Basan, und alle Könige Kanaans
Sihoni mfumu ya Aamori, Ogi mfumu ya Basani, ndi maufumu onse a ku Kanaani;
12 und gab ihr Land als Erbe, als Erbe seinem Volke Israel.
ndipo anapereka dziko lawo ngati cholowa, cholowa cha anthu ake Aisraeli.
13 O HERR, dein Name währt ewig; HERR, dein Gedächtnis bleibt für und für!
Dzina lanu, Inu Yehova, ndi losatha mpaka muyaya, mbiri yanu, Inu Yehova, idziwika mibado yonse.
14 Denn der HERR wird seinem Volke Recht schaffen und mit seinen Knechten Mitleid haben.
Pakuti Yehova adzaonetsa kuti anthu ake ngosalakwa, ndipo adzachitira chifundo atumiki ake.
15 Die Götzen der Heiden sind Silber und Gold, von Menschenhand gemacht.
Mafano a mitundu ya anthu ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
16 Sie haben einen Mund und reden nicht, Augen haben sie und sehen nicht;
Pakamwa ali napo koma sayankhula maso ali nawo, koma sapenya;
17 Ohren haben sie und hören nicht, auch ist kein Odem in ihrem Mund!
makutu ali nawo, koma sakumva ndipo mʼkamwa mwawo mulibe mpweya uliwonse.
18 Ihnen sind gleich, die sie machen, ein jeder, der auf sie vertraut.
Iwo amene amapanga mafanowo adzakhala ngati mafanowo, chimodzimodzinso iwo amene amadalira mafanowo.
19 Haus Israel, lobe den HERRN! Haus Aaron, lobe den HERRN!
Inu nyumba ya Israeli, tamandani Yehova; inu nyumba ya Aaroni, tamandani Yehova;
20 Haus Levi, lobe den HERRN! Die ihr den HERRN fürchtet, lobet den HERRN!
Inu nyumba ya Levi, tamandani Yehova; Inu amene mumaopa Iye, tamandani Yehova.
21 Gelobt sei der HERR von Zion aus, er, der zu Jerusalem wohnt! Hallelujah!
Wodalitsika ndi Yehova kuchokera mʼZiyoni, amene amakhala mu Yerusalemu. Tamandani Yehova.

< Psalm 135 >