< Sprueche 1 >

1 Sprüche Salomos, des Sohnes Davids, des Königs von Israel,
Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
2 daß man Weisheit und Zucht erlerne und verständige Reden verstehe,
Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo; kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;
3 daß man Gedankenzucht erlange, Rechtssinn, Urteilskraft und Aufrichtigkeit;
kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru, akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.
4 damit den Einfältigen Klugheit, den Jünglingen Erkenntnis und Besonnenheit verliehen werde.
Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera, achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.
5 Wer weise ist, hört darauf und vermehrt seine Kenntnisse, und wer verständig ist, eignet sich Fertigkeiten an,
Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake, ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,
6 damit er Sprichwörter und bildliche Rede verstehe, die Worte der Weisen und ihre Rätsel.
kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo, mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.
7 Die Furcht des HERRN ist der Anfang der Erkenntnis; nur Toren verachten Weisheit und Zucht!
Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.
8 Höre, mein Sohn, die Unterweisung deines Vaters und verwirf nicht die Lehre deiner Mutter!
Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.
9 Denn sie sind ein schöner Kranz für dein Haupt und ein Geschmeide um deinen Hals.
Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.
10 Mein Sohn, wenn dich Sünder überreden wollen, so willige nicht ein,
Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa usamawamvere.
11 wenn sie sagen: «Komm mit uns, wir wollen auf Blut lauern, wir wollen dem Unschuldigen ohne Ursache nachstellen;
Akadzati, “Tiye kuno; tikabisale kuti tiphe anthu, tikabisalire anthu osalakwa;
12 wir wollen sie verschlingen wie der Scheol die Lebendigen, als sänken sie unversehens ins Grab! (Sheol h7585)
tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol h7585)
13 Wir wollen allerlei kostbares Gut gewinnen und unsre Häuser füllen mit Raub;
Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;
14 schließe dich uns auf gut Glück an, wir wollen gemeinsame Kasse führen!»
Bwera, chita nafe maere, ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”
15 Mein Sohn, geh nicht mit ihnen auf dem Wege, halte deinen Fuß zurück von ihrem Pfad!
Mwana wanga, usayende nawo pamodzi, usatsagane nawo mʼnjira zawozo.
16 Denn ihre Füße laufen zum Bösen und eilen Blut zu vergießen.
Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha, amathamangira kukhetsa magazi.
17 Denn vergeblich wird das Netz ausgespannt vor den Augen aller Vögel;
Nʼkopanda phindu kutchera msampha mbalame zikuona!
18 sie aber lauern auf ihr eigenes Blut und stellen ihrem eigenen Leben nach.
Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe; amangodzitchera okha msampha!
19 Dies ist das Schicksal aller, die nach [ungerechtem] Gewinn trachten: er kostet seinen Besitzern die Seele!
Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza; chumacho chimapha mwiniwake.
20 Die Weisheit ruft draußen laut, öffentlich läßt sie ihre Stimme hören;
Nzeru ikufuwula mu msewu, ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
21 im ärgsten Straßenlärm schreit sie, an den Pforten der Stadttore hält sie ihre Reden:
ikufuwula pa mphambano ya misewu, ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
22 Wie lange wollt ihr Einfältigen die Einfalt lieben und ihr Spötter Lust am Spotten haben und ihr Toren Erkenntnis hassen?
“Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti? Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti? Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
23 Kehret um zu meiner Zurechtweisung! Siehe, ich will euch meinen Geist sprudeln lassen, euch meine Worte kundtun!
Tamverani mawu anga a chidzudzulo. Ine ndikukuwuzani maganizo anga ndi kukudziwitsani mawu anga.
24 Darum, weil ich rufe und ihr mich abweiset, weil ich meine Hand ausstrecke und niemand darauf achtet,
Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera. Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.
25 weil ihr vielmehr allen meinen Rat verwerfet und meine Zurechtweisung nicht begehret,
Uphungu wanga munawunyoza. Kudzudzula kwanga simunakusamale.
26 so werde auch ich eures Unglücks lachen und euer spotten,
Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto; ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.
27 wenn das, was ihr fürchtet, wie ein Wetter über euch kommt und euer Schicksal euch wie ein Wirbelsturm überraschen wird, wenn euch Angst und Not überfällt.
Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe, tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu, mavuto ndi masautso akadzakugwerani.
28 Dann werden sie mich anrufen, aber ich werde nicht antworten; sie werden mich eifrig suchen und nicht finden,
“Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha; mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.
29 darum, daß sie die Erkenntnis gehaßt und die Furcht des HERRN nicht erwählt haben,
Popeza iwo anadana ndi chidziwitso ndipo sanasankhe kuopa Yehova,
30 daß sie meinen Rat nicht begehrt und alle meine Zurechtweisung verschmäht haben.
popeza iwo sanasamale malangizo anga ndipo ananyoza chidzudzulo changa.
31 Darum sollen sie von der Frucht ihres eigenen Weges essen und von ihren eigenen Ratschlägen genug bekommen!
Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.
32 Denn ihre Verirrung bringt die Einfältigen um, und ihre Sorglosigkeit stürzt die Toren ins Verderben.
Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo, ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.
33 Wer aber mir gehorcht, wird sicher wohnen und kein Unheil fürchten müssen.
Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata; adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”

< Sprueche 1 >