< Job 40 >
1 Et le Seigneur continua à parler à Job:
Yehova anati kwa Yobu:
2 Est-ce que celui qui dispute avec Dieu se réduit si facilement au silence? Certainement celui qui reprend Dieu doit lui répondre.
“Kodi iwe ufuna kukangana ndi Wamphamvuzonse? Iwe amene unatsutsana ndi Mulungu umuyankhe Iyeyo!”
3 Répondant alors au Seigneur, Job dit:
Pamenepo Yobu anayankha Yehova:
4 Moi qui a parlé légèrement, que peux-je répondre? Je mettrai ma main sur ma bouche.
“Ine sindili kanthu konse, kodi ndingathe kukuyankhani chiyani? Ndagwira pakamwa panga.
5 J’ai dit une chose (plut à Dieu que je ne l’eusse pas dite!) et une autre; je n’y ajouterai rien de plus.
Ndinayankhula kamodzi, koma pano ndilibe yankho, ndinayankha kawiri, koma sindiwonjezeranso mawu ena.”
6 Or, répondant à Job du milieu d’un tourbillon, le Seigneur dit:
Ndipo Yehova anayankha Yobu mʼkamvuluvulu kuti,
7 Ceins tes reins comme un homme de cœur; je t’interrogerai, et réponds-moi.
“Tsopano vala dzilimbe ngati mwamuna; ndikufunsa mafunso ndipo iwe undiyankhe.
8 Est-ce que tu rendras vain mon jugement; et me condamneras-tu, pour que toi, tu sois justifié?
“Kodi iwe unganyoze chiweruzo changa cholungama? Kodi ungandidzudzule kuti iweyo ukhale wolungama?
9 Et as-tu un bras comme Dieu, et tonnes-tu d’une voix semblable?
Kodi uli ndi dzanja monga la Mulungu, ndipo mawu ako angagunde ngati mphenzi monga a Mulungu?
10 Environne-toi de majesté, et élève-toi dans les airs, et sois glorieux, et revêts-toi de splendides vêtements.
Ngati zili choncho udzikometsere ndi ulemerero ndi kukongola, ndipo udziveke ulemu ndi ulemerero waufumu.
11 Dissipe les superbes dans ta fureur, et d’un regard humilie tout arrogant.
Tsanula ukali wako wosefukirawo, uyangʼane aliyense wodzikuza ndipo umuchepetse,
12 Regarde tous les superbes et confonds-les; et brise les impies en leur lieu.
Uyangʼane aliyense wodzikweza ndipo umutsitse, uwapondereze oyipa onse pamalo pomwe alilipo.
13 Cache-les dans la poussière tous ensemble, et plonge leurs faces dans la fosse.
Onsewo uwakwirire pamodzi mfumbi; ukulunge nkhope zawo mʼmanda.
14 Et moi, je confesserai que ta droite peut te sauver.
Ukatero Ine ndidzakuvomereza kuti dzanja lako lamanja lakupulumutsadi.
15 Vois, Béhémoth que j’ai fait avec toi mangera du foin comme le bœuf.
“Taganiza za mvuwu, imene ndinayipanga monga momwe ndinapangira iwe, ndipo imadya udzu ngati ngʼombe.
16 Sa force est dans ses reins, et sa vertu dans le nombril de son ventre.
Mphamvu zake ndi zazikulu kwambiri, thupi lake ndi lanyonga kwambiri!
17 Il serre sa queue qui est semblable à un cèdre; les nerfs de ses cuisses sont entrelacés.
Mchira wake umayima tolotolo ngati mtengo wamkungudza; mitsempha ya ntchafu zake ndi yogwirana bwino.
18 Ses os sont des tuyaux d’airain, ses cartilages comme des lames de fer.
Mafupa ake ali ngati mapayipi amkuwa, nthiti zake zili ngati mipiringidzo yachitsulo.
19 C’est lui qui est le commencement des voies de Dieu; celui qui l’a fait appliquera son glaive.
Mvuwuyo ndi yayikulu mwa zolengedwa za Mulungu, komatu mlengi wake amatha kuyiopseza ndi lupanga lake.
20 C’est pour lui que les montagnes portent des herbes; toutes les bêtes de la campagne viendront se jouer là.
Imapeza chakudya chake ku mtunda ndipo nyama zakuthengo zonse zimasewera pambali pake.
21 Il dort sous l’ombre, dans le secret des roseaux et dans des lieux humides.
Imagona pa tsinde pa zitsamba za mipeta, imabisala mʼbango ndiponso pa thawale.
22 Des ombres couvrent son ombre, et les saules du torrent l’environneront.
Imaphimbika ndi mthunzi wazitsamba za mipeta; imazunguliridwa ndi misondozi ya mu mtsinje.
23 Voici qu’il absorbera un fleuve, et il ne s’en étonnera point; il a même la confiance que le Jourdain viendra couler dans sa bouche.
Madzi a mu mtsinje akakokoma, sichita mantha, iyo sitekeseka, ngakhale madzi a mu Yorodani afike mʼkhosi mwake.
24 On le prendra par les yeux comme à l’hameçon, et, avec des harpons, on percera ses narines.
Kodi alipo amene angathe kukola mvuwu ndi mbedza kapena kuyikola mu msampha?