< Job 39 >

1 Est-ce que tu connais le temps de l’enfantement des chèvres sauvages dans les rochers? ou as-tu observé des biches lorsqu’elles enfantaient?
“Kodi iwe umadziwa nthawi imene mbalale yayikazi imaswera? Kodi umaonerera pamene nswala ikubala?
2 As-tu compté les mois de leur conception, et sais-tu le temps de leur enfantement?
Kodi umawerenga miyezi imene zimakhala ndi bere? Kodi nthawi imene zimaswana iwe umayidziwa?
3 Elles se courbent pour mettre bas leur faon, et elles enfantent, et elles poussent des hurlements.
Zimakhala tsonga ndi kuswa ana awo; pamenepo ululu wobereka nʼkutha.
4 Leurs petits se séparent et vont au pâturage; ils sortent et ne reviennent pas vers elles.
Ana a nyamazi amakhala ndi mphamvu ndipo amakulira mʼthengo; kenaka amachoka ndipo sabwereranso.
5 Qui a laissé aller l’onagre libre, qui a rompu ses liens?
“Kodi bulu wakuthengo amamupatsa ndani ufulu wongodziyendera? Ndani amamasula zingwe zake?
6 Je lui ai donné dans la solitude une maison, et ses lieux de retraite dans une terre de sel.
Ine ndinamupatsa chipululu kuti chikhale mudzi wake, nthaka ya mchere kuti ikhale malo ake okhalamo
7 Il méprise la multitude d’une ville, et il n’entend pas le cri d’un exacteur.
Iye amakhala kutali ndi phokoso la mu mzinda; ndipo samva kufuwula kwa oyendetsa nyama zakatundu.
8 Il regarde de tous côtés les montagnes, lieux de son pâturage, et il cherche tous les herbages verts.
Amayendayenda mʼmapiri kudya msipu ndipo amafunafuna msipu uliwonse wobiriwira.
9 Est-ce qu’un rhinocéros voudra te servir, ou demeurera-t-il à ton étable?
“Kodi njati ingavomere kukutumikira? Kodi ingagone mu gome lako usiku?
10 Est-ce que tu lieras un rhinocéros à tes traits, pour qu’il laboure? ou rompra-t-il les glèbes des vallons après toi?
Kodi ungathe kuyimanga ndi zingwe kuti izilima? Kodi ingasalaze nthumbira mʼmunda mwako?
11 Est-ce que tu auras confiance en sa grande force, et lui laisseras-tu tes travaux?
Kodi ungadalire njatiyo chifukwa champhamvu zake? Kodi ungayilekere kuti igwire ntchito zako zolemetsa?
12 Est-ce que tu croiras qu’il te rendra tes semailles et qu’il remplira ton aire?
Kodi ungadalire kuti idzakubweretsera tirigu wako ndi kumuyika ku malo opunthira?
13 L’aile de l’autruche est semblable aux ailes du héron et de l’épervier.
“Nthiwatiwa imakupiza mapiko ake monyadira, koma mapikowo sangafanane ndi mapiko ndi nthenga za kakowa.
14 Quand elle abandonne ses œufs sur la terre, sera-ce toi, par hasard, qui les réchaufferas dans la poussière?
Nthiwatiwa imakwirira mazira ake pansi ndipo amafundidwa ndi nthaka,
15 Elle oublie qu’un pied les foulera, ou que la bête des champs les écrasera.
nthiwatiwayo sidera nkhawa kuti mazira ake angathe kuswanyidwa, ndi kuti nyama zakuthengo zitha kuwaponda.
16 Elle est dure pour ses petits, comme s’ils n’étaient pas les siens, elle a rendu son travail inutile, en les abandonnant, aucune crainte ne l’y obligeant.
Nthiwatiwa imachitira nkhanza ana ake ngati anawo si ake; Imayiwala zoti inavutika powabala.
17 Car Dieu l’a privée de sagesse, et ne lui a pas donné l’intelligence.
Chifukwa Mulungu anayimana nzeru, simvetsa kanthu kalikonse.
18 Dans l’occasion, elle élève en haut ses ailes; elle se rit du cheval et de celui qui le monte.
Komatu nthiwatiwa ikadzambatuka ndi kuyamba kuthamanga, imamusiya kutali kavalo ndi wokwerapo wake.
19 Est-ce que tu donneras au cheval de la force, ou environneras-tu son cou de hennissements?
“Kodi ndiwe amene umamupatsa mphamvu kavalo kapena kumuveka chenjerere mʼkhosi mwake?
20 Est-ce que tu le feras bondir comme les sauterelles? La gloire de ses naseaux est la terreur.
Kodi ndiwe amene umalipatsa dzombe ulemerero wolumphira, ukali wake nʼkumachititsa mantha?
21 Il creuse de son sabot la terre, il s’élance avec audace; il court au-devant des hommes armés;
Iye amalumphalumpha moopseza, kukondwerera mphamvu zake, ndipo amapita ku nkhondo ndi mphamvu zake zonse.
22 Il méprise la peur, il ne cède pas au glaive.
Iye sachita mantha, saopa chilichonse; sabwerera mʼmbuyo akaona lupanga.
23 Sur lui retentira le bruit du carquois, la lance étincellera ainsi que le bouclier.
Zida zankhondo zimachita kwichikwichi mʼchimake pambali pake pamodzi ndi mkondo wonyezimira ndi nthungo.
24 Bouillonnant et frémissant il dévore la terre, et ne tient aucun compte du bruit de la trompette, lorsqu’elle sonne le retour.
Kavaloyo amanjenjemera ndi ukali ndi kulumphalumpha; satha kungoyima pamene wamva kulira kwa lipenga.
25 Dès qu’il entend le clairon, il dit: Oh! il sent de loin une guerre, l’exhortation des chefs, et les cris confus d’une armée.
Lipenga likalira amati, ‘Twee!’ Amamva fungo la nkhondo ali patali, kufuwula kwa anthu olamulira nkhondo ndi mfuwu wankhondo.
26 Est-ce par ta sagesse que l’épervier se couvre de ses plumes, étendant ses ailes vers le midi?
“Kodi kabawi amawuluka ndi nzeru zako, ndi kutambasula mapiko ake kupita kummwera?
27 Est-ce à ton ordre que l’aigle s’élèvera, et placera son nid dans les lieux les plus élevés?
Kodi umalamulira chiwombankhanga ndiwe kuti chiziwuluka ndi kumanga chisa chake pamwamba penipeni?
28 C’est dans des pierres qu’il demeure, et c’est sur des rocs escarpés et des rochers inaccessibles qu’il fait son séjour.
Chimakhala pa phiri ndipo chimakhala pamenepo usiku; chimakhala pa msonga penipeni pa mwala.
29 De là il contemple sa proie, et ses yeux voient de loin.
Chili pamenepo chimayangʼanayangʼana choti chigwire kuti chidye; maso ake amachionera patali chinthucho.
30 Ses petits lécheront le sang, et partout où est un cadavre, soudain il est présent.
Ana ake amayamwa magazi, ndipo kumene kuli mitembo ndiko chimapezeka.”

< Job 39 >