< Job 22 >
1 Alors, répondant, Eliphaz, le Thémanite, dit:
Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
2 Est-ce qu’un homme peut être comparé à Dieu, quand il serait d’une science parfaite?
“Kodi munthu nʼkukhala waphindu kwa Mulungu? Kodi munthu wanzeru angamupindulire Iye?
3 Que sert à Dieu que tu sois juste? ou quel bien lui fais-tu si ta voie est sans tache?
Kodi Wamphamvuzonse akanapeza chabwino chotani iweyo ukanakhala wolungama? Kodi iyeyo akanapeza phindu lanji makhalidwe ako akanakhala angwiro?
4 Est-ce en craignant qu’il t’accusera, et qu’il viendra avec toi en jugement,
“Kodi nʼchifukwa choti umamuopa, kuti azikudzudzula, kuti azifuna kukukokera ku mlandu?
5 Et non pas à cause de ta malice très grande et de tes infinies iniquités?
Kodi osati nʼchifukwa chakuti kuyipa kwako nʼkwakukulu? Kodi machimo ako si opanda malire?
6 Car tu as retenu le gage de tes frères sans raison, et tu as dépouillé de leurs vêtements ceux qui étaient nus.
Iwe unkawumiriza abale ako kuti akupatse chikole popanda chifukwa; umalanda anthu zovala zawo ndi kuwasiya amaliseche.
7 Tu n’as pas donné de l’eau à celui qui était épuisé de lassitude, et à celui qui avait faim tu as soustrait du pain.
Sunawapatse madzi anthu otopa, ndipo unawamana chakudya anthu anjala,
8 Par la force de ton bras tu possédais ta terre, et, étant le plus puissant, tu la conservais.
ngakhale unali munthu wamphamvu, wokhala ndi malo akeake, munthu waulemu wake, wokhala mʼdzikomo.
9 Tu as renvoyé les veuves les mains vides, et tu as brisé les bras des orphelins.
Ndipo akazi amasiye unawachotsa wopanda kanthu, ndipo unapondereza ana amasiye.
10 C’est pour cela que tu es environné de pièges, et qu’une frayeur soudaine te trouble.
Nʼchifukwa chake misampha yakuzungulira, nʼchifukwa chake tsoka ladzidzidzi lakuchititsa mantha,
11 Et tu pensais que tu ne verrais point de ténèbres, et que tu ne serais pas accablé par un impétueux débordement d’eaux.
nʼchifukwa chake kuli mdima kuti sungathe kuona kanthu, nʼchifukwa chakenso madzi achigumula akumiza.
12 Ne songes-tu pas que Dieu est plus élevé que le ciel, et qu’il est au-dessus du sommet des étoiles?
“Kodi Mulungu sali kutalitali kumwamba? Ndipo ona nyenyezi zili mmwamba kwambirizo, ona kutalika kwake pamene zililipo!
13 Et tu dis: Mais que connaît Dieu? car c’est comme à travers d’une profonde obscurité qu’il juge.
Komabe iweyo ukunena kuti, ‘Kodi Mulungu amadziwa chiyani? Kodi Iye amaweruza mu mdima woterewu?
14 Des nuées le cachent; il ne considère pas ce qui est de nous, et il parcourt les pôles du ciel.
Mitambo yakuda yamuphimba, kotero kuti Iye sakutiona pamene akuyendayenda pamwamba pa thambopo.’
15 Est-ce que tu désires suivre le sentier des siècles, qu’ont foulé des hommes iniques,
Kodi iwe udzayendabe mʼnjira yakale imene anthu oyipa ankayendamo?
16 Qui ont été enlevés avant leur temps, et dont un fleuve a renversé le fondement?
Iwo anachotsedwa nthawi yawo isanakwane, maziko awo anakokoloka ndi madzi achigumula.
17 Qui disaient à Dieu: Retire-toi de nous; et qui estimaient que le Tout-Puissant ne pouvait rien faire;
Anthuwo anati kwa Mulungu, ‘Tichokereni! Kodi Wamphamvuzonse angatichitire chiyani?’
18 Quoique ce fût lui qui eût rempli leurs maisons de biens. Que leur sentiment soit loin de moi!
Chonsecho ndi Iye amene anadzaza nyumba zawo ndi zinthu zabwino, choncho ine sindigwirizana ndi uphungu wa anthu oyipa.
19 Les justes les verront et ils se réjouiront, et l’innocent se moquera d’eux.
“Anthu olungama amaona kuwonongeka kwawo ndipo amakondwera; anthu osalakwa amangoseka, akamuona woyipa akulangidwa.
20 Est-ce que leur élévation n’a pas été entièrement détruite? et leurs restes, un feu ne les a-t-il pas dévorés?
Amanena kuti, ‘Ndithudi adani athu awonongeka ndipo moto wawononga chuma chawo!’
21 Soumets-toi donc à Dieu, et tu auras la paix; et par là tu auras des fruits excellents.
“Gonjera Mulungu kuti ukhale naye pamtendere; ukatero udzaona zabwino.
22 Reçois de sa bouche sa loi, et mets ses discours dans ton cœur.
Landira malangizo a pakamwa pake ndipo usunge mawu ake mu mtima mwako.
23 Si tu reviens au Tout-Puissant, tu seras rétabli, et tu éloigneras l’iniquité de ton tabernacle.
Ukabwerera kwa Wamphamvuzonse udzabwezeretsedwa; ukachotsa zoyipa zonse zimene zimachitika mʼnyumba mwako,
24 Il te donnera au lieu de terre, un rocher, et au lieu d’un rocher, des torrents d’or.
ndipo chuma chamtengowapatali nuchiona ngati fumbi, golide wa ku Ofiri numutaya ku miyala ya ku zigwa.
25 Et le Tout-Puissant sera contre tes ennemis, et l’argent sera mis en monceaux pour toi.
Pamenepo Wamphamvuzonseyo adzakhala golide wako, siliva wako wamtengowapatali.
26 Alors tu abonderas en délices dans le Tout-Puissant, et tu élèveras ta face vers Dieu.
Pamenepo udzakondwera naye Wamphamvuzonse ndipo udzakweza nkhope yako kwa Mulungu.
27 Tu le prieras, et il t’exaucera, et tu acquitteras tes vœux.
Udzamupempha ndipo adzakumvera, ndipo udzapereka zimene unalonjeza.
28 Tu décideras une chose, et elle se réalisera pour toi, et sur tes voies brillera la lumière.
Chimene watsimikiza kuti uchite, chidzachitikadi, kuwala kudzakuwunikira pa njira yako.
29 Car celui qui aura été humilié sera dans la gloire; et celui qui aura baissé les yeux, celui-là même sera sauvé,
Pamene anthu agwetsedwa pansi, iwe nʼkunena kuti, ‘Akwezeni!’ Pamenepo Iye adzapulumutsa anthu oponderezedwa.
30 L’innocent sera sauvé, mais il sera sauvé à cause de la pureté de ses mains.
Iye adzapulumutsa ngakhale munthu amene ndi wolakwa, ameneyo adzapulumutsidwa kudzera mʼkulungama kwako.”