< Job 21 >

1 Mais, répondant. Job dit:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 Ecoutez, je vous prie, mes paroles, et faites pénitence.
“Mvetserani bwino mawu anga; ichi chikhale chitonthozo changa chochokera kwa inu.
3 Supportez-moi, et moi je parlerai; et après, si bon vous semble, riez de mes paroles.
Ndiloleni ndiyankhule ndipo ndikatha kuyankhula munditonzetonze.
4 Est-ce contre un homme qu’est ma dispute, pour que je ne doive pas être justement contristé?
“Kodi ine ndikudandaulira munthu? Tsono ndilekerenji kupsa mtima?
5 Regardez-moi, et soyez dans l’étonnement, et mettez un doigt sur votre bouche:
Ndipenyeni ndipo mudabwe; mugwire dzanja pakamwa.
6 Et moi, quand je recueille mes souvenirs, je suis épouvanté, et le tremblement agite ma chair.
Ndikamaganiza zimenezi ndimachita mantha kwambiri; thupi langa limanjenjemera.
7 Pourquoi donc les impies vivent-ils, sont-ils élevés et affermis dans les richesses?
Chifukwa chiyani anthu oyipa amakhalabe ndi moyo, amakalamba ndi kusanduka amphamvu?
8 Leur race se perpétue devant eux, une troupe de leurs proches et de leurs petits enfants est en leur présence.
Amaona ana awo akukhazikika pamodzi nawo, zidzukulu zawo zikukula bwino iwo akuona.
9 Leurs maisons sont sûres et paisibles, et la verge de Dieu n’est pas sur eux.
Mabanja awo amakhala pa mtendere ndipo sakhala ndi mantha; mkwapulo wa Mulungu suwakhudza nʼkomwe.
10 Leur génisse a conçu et n’a pas avorté; leur vache a mis bas, et elle n’a pas été privée de son fruit.
Ngʼombe zawo zazimuna sizilephera kubereketsa; ngʼombe zawo zazikazi sizipoloza.
11 Leurs petits enfants, sortent comme les troupeaux, et leurs enfants sautent de joie au milieu de leurs jeux.
Amatulutsa ana awo ngati gulu la nkhosa; makanda awo amavinavina pabwalo.
12 Ils tiennent en main un tambour et une harpe, et ils se réjouissent au son d’un orgue.
Amayimba nyimbo pogwiritsa ntchito matambolini ndi azeze; amakondwa pakumva kulira kwa chitoliro.
13 Ils passent leurs jours dans le bonheur, et en un moment ils descendent dans les enfers. (Sheol h7585)
Zaka zawo zimatha ali mu ulemerero ndipo amatsikira ku manda mwamtendere. (Sheol h7585)
14 Ils ont dit à Dieu: Retire-toi de nous; nous ne voulons pas connaître tes voies.
Koma anthuwo amawuza Mulungu kuti, ‘Tichokereni!’ Ife tilibe chikhumbokhumbo chofuna kudziwa njira zanu.
15 Qui est le Tout-Puissant, pour que nous le servions? et que nous revient-il, si nous le prions?
Kodi Wamphamvuzonseyo ndani kuti timutumikire? Ife tipindula chiyani tikamapemphera kwa Iyeyo?
16 Mais cependant, puisque leurs biens ne sont pas en leur main, que le conseil des impies soit loin de moi.
Komatu ulemerero wawo suli mʼmanja mwawo, koma ine ndimakhala patali ndi uphungu wa anthu oyipa.
17 Combien de fois la lampe des impies s’éteindra, un déluge de maux leur surviendra, et Dieu leur distribuera les douleurs de sa fureur?
“Koma nʼkangati kamene nyale ya anthu oyipa imazimitsidwa? Nʼkangati kamene tsoka limawagwera? Nʼkangati kamene Mulungu amawakwiyira ndi kuwalanga?
18 Ils seront comme des pailles à la face du vent, et comme de la cendre brûlante qu’un tourbillon disperse.
Nʼkangati kamene iwo amakhala ngati phesi lowuluka ndi mphepo, ngati mungu wowuluzika ndi kamvuluvulu?
19 Dieu gardera à ses fils la douleur du père; et lorsqu’il lui aura rendu selon son mérite, alors il comprendra.
Paja amati, ‘Mulungu amalanga ana chifukwa cha machimo abambo awo.’ Koma Mulungu amabwezera chilango munthuyo, kuti adziwe kuti Mulungu amalangadi.
20 Ses yeux verront sa ruine, et il boira de la fureur du Tout-Puissant.
Mulole kuti adzionere yekha chilango chake, kuti alawe ukali wa Wamphamvuzonse.
21 Car que lui importe sa maison après lui, lors même que le nombre de ses mois serait diminué de moitié?
Nanga kodi amalabadira chiyani zabanja lake limene walisiya mʼmbuyo, pamene chiwerengero cha masiku ake chatha?
22 Est-ce que quelqu’un enseignera la science à Dieu, qui juge ceux qui sont élevés?
“Kodi alipo wina amene angaphunzitse Mulungu nzeru, poti Iye amaweruza ngakhale anthu apamwamba?
23 Celui-ci meurt robuste et sain, riche et heureux.
Munthu wina amamwalira ali ndi mphamvu zonse, ali pa mtendere ndi pa mpumulo,
24 Ses entrailles sont pleines de graisse, et ses os sont arrosés de moelle.
thupi lake lili lonenepa, mafupa ake ali odzaza ndi mafuta.
25 Mais un autre meurt dans l’amertume de l’âme, sans aucune richesse.
Munthu wina amamwalira ali wowawidwa mtima, wosalawapo chinthu chabwino chilichonse.
26 Et cependant ils dormiront ensemble dans la poussière, et des vers les couvriront.
Olemera ndi osauka omwe amamwalira ndi kuyikidwa mʼmanda ndipo onse amatuluka mphutsi.
27 Certes, je connais vos pensées et vos jugements iniques contre moi.
“Ndikudziwa bwino zimene mukuganiza, ziwembu zanu zomwe mukuti mundichitire.
28 Car vous dites: Où est la maison d’un prince? et où sont les tabernacles des impies?
Inu mukuti, ‘Kodi nyumba ya mkulu uja ili kuti, matenti amene munkakhala anthu oyipa aja ali kuti?’
29 Interrogez le premier venu des passants, et vous reconnaîtrez qu’il comprend ces mêmes choses; à savoir:
Kodi munawafunsapo anthu amene ali pa ulendo? Kodi munaganizirapo zimene iwo amanena?
30 Que le méchant est réservé pour le jour de perdition, et qu’il sera conduit jusqu’au jour de la fureur.
Zakuti munthu woyipa amasungidwa chifukwa cha tsiku la tsoka, kuti amapulumutsidwa chifukwa cha tsiku la ukali wa Mulungu?
31 Qui le reprendra en face de sa voie? et qui lui rendra ce qu’il a fait?
Kodi ndani amadzudzula munthu wochimwayo? Ndani amamubwezera zoyipa zimene anachita?
32 Il sera conduit aux sépulcres, et il veillera au milieu du monceau des morts.
Iye amanyamulidwa kupita ku manda ndipo anthu amachezera pa manda ake.
33 Il a été agréable au gravier du Cocyte, et il entraînera tout homme après lui, et il y a devant lui une multitude innombrable.
Dothi la ku chigwa limamukomera; anthu onse amatsatira mtembo wake, ndipo anthu osawerengeka amakhala patsogolo pa chitanda chakecho.
34 Comment donc me donnezvous une vaine consolation, puisqu’il a été démontré que votre réponse répugne à la vérité.
“Nanga inu mudzanditonthoza bwanji ine ndi mawu anu opandapakewo palibe chimene chatsala kuti muyankhe koma mabodza basi!”

< Job 21 >