< Job 39 >

1 Sais-tu le temps où les chamois mettent bas? As-tu observé quand les biches faonnent?
“Kodi iwe umadziwa nthawi imene mbalale yayikazi imaswera? Kodi umaonerera pamene nswala ikubala?
2 As-tu compté les mois de leur portée, et sais-tu le temps où elles mettent bas?
Kodi umawerenga miyezi imene zimakhala ndi bere? Kodi nthawi imene zimaswana iwe umayidziwa?
3 Elles se courbent, elles font sortir leurs petits, et se délivrent de leurs douleurs;
Zimakhala tsonga ndi kuswa ana awo; pamenepo ululu wobereka nʼkutha.
4 Leurs petits se fortifient, ils croissent en plein air, ils s'en vont et ne reviennent plus vers elles.
Ana a nyamazi amakhala ndi mphamvu ndipo amakulira mʼthengo; kenaka amachoka ndipo sabwereranso.
5 Qui a lâché l'onagre en liberté, et qui a délié les liens de cet animal farouche,
“Kodi bulu wakuthengo amamupatsa ndani ufulu wongodziyendera? Ndani amamasula zingwe zake?
6 A qui j'ai donné la steppe pour demeure, et la terre salée pour habitation?
Ine ndinamupatsa chipululu kuti chikhale mudzi wake, nthaka ya mchere kuti ikhale malo ake okhalamo
7 Il se rit du bruit de la ville; il n'entend pas les clameurs de l'ânier.
Iye amakhala kutali ndi phokoso la mu mzinda; ndipo samva kufuwula kwa oyendetsa nyama zakatundu.
8 Il parcourt les montagnes qui sont ses pâturages, il cherche partout de la verdure.
Amayendayenda mʼmapiri kudya msipu ndipo amafunafuna msipu uliwonse wobiriwira.
9 Le buffle veut-il te servir? Passe-t-il la nuit auprès de ta crèche?
“Kodi njati ingavomere kukutumikira? Kodi ingagone mu gome lako usiku?
10 Attaches-tu le buffle par la corde au sillon? Herse-t-il tes champs en te suivant?
Kodi ungathe kuyimanga ndi zingwe kuti izilima? Kodi ingasalaze nthumbira mʼmunda mwako?
11 Te fies-tu à lui parce que sa force est grande, et lui abandonnes-tu ton travail?
Kodi ungadalire njatiyo chifukwa champhamvu zake? Kodi ungayilekere kuti igwire ntchito zako zolemetsa?
12 Comptes-tu sur lui pour rentrer ton grain, et pour l'amasser sur ton aire?
Kodi ungadalire kuti idzakubweretsera tirigu wako ndi kumuyika ku malo opunthira?
13 L'aile de l'autruche s'agite joyeusement; est-ce l'aile et la plume de la cigogne?
“Nthiwatiwa imakupiza mapiko ake monyadira, koma mapikowo sangafanane ndi mapiko ndi nthenga za kakowa.
14 Non, car elle abandonne ses œufs à terre, elle les fait couver sur la poussière;
Nthiwatiwa imakwirira mazira ake pansi ndipo amafundidwa ndi nthaka,
15 Elle oublie qu'un pied peut les fouler, une bête des champs les écraser.
nthiwatiwayo sidera nkhawa kuti mazira ake angathe kuswanyidwa, ndi kuti nyama zakuthengo zitha kuwaponda.
16 Elle est dure envers ses petits, comme s'ils n'étaient pas siens. Son travail est vain, elle ne s'en inquiète pas.
Nthiwatiwa imachitira nkhanza ana ake ngati anawo si ake; Imayiwala zoti inavutika powabala.
17 Car Dieu l'a privée de sagesse, et ne lui a point départi d'intelligence.
Chifukwa Mulungu anayimana nzeru, simvetsa kanthu kalikonse.
18 Quand elle se lève, et bat des ailes, elle se moque du cheval et de son cavalier.
Komatu nthiwatiwa ikadzambatuka ndi kuyamba kuthamanga, imamusiya kutali kavalo ndi wokwerapo wake.
19 As-tu donné au cheval sa vigueur? As-tu revêtu son cou de la crinière frémissante?
“Kodi ndiwe amene umamupatsa mphamvu kavalo kapena kumuveka chenjerere mʼkhosi mwake?
20 Le fais-tu bondir comme la sauterelle? Son fier hennissement donne la terreur.
Kodi ndiwe amene umalipatsa dzombe ulemerero wolumphira, ukali wake nʼkumachititsa mantha?
21 De son pied il creuse la terre; il se réjouit en sa force; il va à la rencontre de l'homme armé;
Iye amalumphalumpha moopseza, kukondwerera mphamvu zake, ndipo amapita ku nkhondo ndi mphamvu zake zonse.
22 Il se rit de la crainte, il n'a peur de rien; il ne recule point devant l'épée.
Iye sachita mantha, saopa chilichonse; sabwerera mʼmbuyo akaona lupanga.
23 Sur lui retentit le carquois, la lance étincelante et le javelot.
Zida zankhondo zimachita kwichikwichi mʼchimake pambali pake pamodzi ndi mkondo wonyezimira ndi nthungo.
24 Bondissant et frémissant, il dévore l'espace; il ne peut se contenir dès que la trompette sonne;
Kavaloyo amanjenjemera ndi ukali ndi kulumphalumpha; satha kungoyima pamene wamva kulira kwa lipenga.
25 Dès qu'il entend la trompette, il hennit; il sent de loin la bataille, la voix tonnante des chefs et les clameurs des guerriers.
Lipenga likalira amati, ‘Twee!’ Amamva fungo la nkhondo ali patali, kufuwula kwa anthu olamulira nkhondo ndi mfuwu wankhondo.
26 Est-ce par ta sagesse que l'épervier prend son vol, et déploie ses ailes vers le Midi?
“Kodi kabawi amawuluka ndi nzeru zako, ndi kutambasula mapiko ake kupita kummwera?
27 Est-ce sur ton ordre que l'aigle s'élève, et qu'il place son aire sur les hauteurs?
Kodi umalamulira chiwombankhanga ndiwe kuti chiziwuluka ndi kumanga chisa chake pamwamba penipeni?
28 Il habite sur les rochers, il se tient sur la dent des rochers, sur les lieux inaccessibles.
Chimakhala pa phiri ndipo chimakhala pamenepo usiku; chimakhala pa msonga penipeni pa mwala.
29 De là, il découvre sa proie; ses yeux la voient de loin.
Chili pamenepo chimayangʼanayangʼana choti chigwire kuti chidye; maso ake amachionera patali chinthucho.
30 Ses petits sucent le sang, et partout où il y a des corps morts, il s'y trouve.
Ana ake amayamwa magazi, ndipo kumene kuli mitembo ndiko chimapezeka.”

< Job 39 >